Saturday, February 22, 2025

LAMULUNGU LA 7 PA CHAKA – C

LAMULUNGU LA 7 PA CHAKA – C

“Kondani adani anu, muwachitire zabwino.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LOYAMBA LA SAMUELE: 1 SAMUELE 26:2. 7-9.12-13,22-23. (Chauta anakuperekani m' manja mwanga lero, koma sindidaphe munthu wodzozedwa ufumu).

 

Saulo adanyamuka napita ku chipululu cha Zifi atatenga ankhondo 3,000 osankhidwa, kuti akafunefune Davide kuchipululuko. Choncho Davide ndi Abisai adakalowa ku zithando zankhondo usiku. Saulo anali gone m'chithando chake, atazika mkondo wake pansi cha kumutu kwake. Abinere ndi ankhondo onse adaagona momzungulira. Abisai adauza Davide kuti, “Mulungu wapereka mdani wanu kwa inu lero. Bwanji tsono mundilole kuti ndimbaye ndi mkondo kamodzinkamodzi ndi kumkhomerera pansi, sindichita kumbaya kawiri.” Koma Davide adamuuza kuti, “Ai, usamuphe. Ndani angathe kupweteka wodzozedwa wa Chauta nakhala wosachimwa?” Motero Davide adatenga mkondo ndi mtsuko wa madzi, zimene zinali kumutu kwa Saulo, nachokapo. Palibe amene adaona zimenezo ngakhale kuzidziwa, ndipo panalibe wina aliyense amene adadzuka. Onse anali m'tulo, chifukwa chakuti Chauta adaawagonetsa tulo tofa nato. Pambuyo pake Davide adakwerera mbali ina nakaimirira pamwamba pa phiri, pakati nkusiya mpata waukulu. Apo Davide adayankha kuti, “Suwu mkondo wanu, mfumu. Tumani mmodzi mwa ankhondowo adzatenge. Chauta amadalitsa munthu wokhulupirika ndi wochita zabwino. Chauta anakuperekani m' manja mwanga lero, koma sindidaphe munthu wodzozedwa ufumu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 103:1-4,8,10,12-13.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,

Moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera,

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,

Ndipo usaiwale zabwino zake zonse.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima.

 

Ndiye amene amakhululukira machimo ako onse,

Ndi kuchiritsa matenda ako onse,

Ndiye amene amapulumutsa moyo wako ku manda,

Amakuveka chikondi ndiponso chifundo chake, ngati chisoti chaufumu.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima, ndi wosakwiya msanga,

Ndipo chikondi chake chosasinthika nchachikulu,

Satilanga moyenerera machimo athu,

Satibwezera molingana ndi zolakwa zathu.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima.

 

Monga kuvuma kuli kutali ndi kuzambwe,

Ndi momwenso amachotsera zolakwa zathu,

Monga bambo amachitira chifundo ana ake,

Ndi momwenso Chauta amawachitira chifundo omulemekeza.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima.

---------------------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 1 AKORINTO 15:45-49. (Monga takhala ofanafana ndi Adamu, munthu wopangidwa ndi dothi uja, momwemonso tidzakhala ofanafana ndi Khristu, munthu wa Kumwamba).

 

Abale, Malembo akuti, “Munthu woyamba uja, Adamu, adachita kusanduka chinthu chamnofu chokhala ndi moyo.” Koma Adamu wotsiriza adakhala chinthu chauzimu chopatsa moyo. Loyamba sithupi lauzimu ai. Loyamba ndi lamnofu, pambuyo pake lauzimu. Adamu woyamba uja anali wochokera ku dothi, anali wapansipano, Koma Khristu, Adamu wachiwiri uja, anali wochokera Kumwamba. Anthu onse apansipano ali ngati Adamu wopangidwa ndi dothi uja. Ndipo onse amene ali a Kumwamba, ali ngati Khristu wa Kumwamba. Monga takhala ofanafana ndi Adamu, munthu wopangidwa ndi dothi uja, momwemonso tidzakhala ofanafana ndi Khristu, munthu wa kumwamba.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 13:34.

 

Alleluia, Alleluia Ndikukupatsani lamulo latsopano, lakuti muzikondana; monga momwe Ine ndidakukonderani, inunso muzikondana, atero Ambuye. Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 6:27-38 (Monga Atate anu akumwamba ali achifundo, inunso mukhale achifundo).

 

Yesu adawauza ophunzira ake kuti, “Koma inu amene mukumva mau anga, ndikukuuzani kuti, Muzikonda adani anu, muziwachitira zabwino amene amadana nanu. Muziwafunira madalitso amene amakutembererani, muziwapempherera amene amakuvutitsani. Ngati munthu akumenya pa tsaya, uperekere linalonso. Ndipo munthu akakulanda mwinjiro wako, umlole atenge ndi mkanjo womwe. Munthu akakupempha kanthu, uzimpatsa. Ndipo munthu akatenga zinthu zako, usamlamule kuti abweze. Zomwe mukufuna kuti anthu akuchitireni, inuyo muwachitire zomwezo. Ngati mukonda okhawo amene amakukondani, mungayembekeze kulandira mphotho yanji? Pajatu ngakhale anthu ochimwa amakondanso amene amawakonda. Ngati muchitira zabwino okhawo amene amakuchitirani zabwino, mungayembekeze kulandira mphotho yanji? Pajatu ngakhale anthu ochimwa amachita chimodzimodzi. Ndipo ngati mukongoza okhawo amene mukudziwa kuti adzakubwezerani, mungayembekeze kulandira mphotho yanji? Pajatu ngakhale anthu ochimwa amakongoza anzao ochimwa, kuti akalandirenso momwemo. Iyai, inu muzikonda adani anu, muzichita zabwino, ndipo muzikongoza osayembekeza kulandirapo kanthu. Mukatero mudzalandira mphotho yaikulu, ndiye kuti mudzakhala ana a Mulungu Wopambanazonse. Pajatu Iye amachitira zabwino anthu osayamika ndi oipa omwe. Monga Atate anu akumwamba ali achifundo, inunso mukhale achifundo. Musamaweruza anthu ena kuti ngolakwa, ndipo Mulungu sadzakuweruzani. Musamaimba ena mlandu, ndipo Mulungu

sadzakuimbani mlandu. Muzikhululukira ena, ndipo Mulungu adzakukhululukirani. Muzipereka moolowa manja, ndipo Mulungu adzakuchitirani momwemo: adzakupatsirani m'thumba mwanu

muyeso wabwino, wotsendereka, wokhutchumuka ndi wosefukira. Chifukwatu muyeso womwe mumagwiritsa ntchito poweruza ena, Mulungu adzagwiritsa ntchito womwewo pokuweruzani inu.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

Abale, podziwa kuti chifundo cha Mulungu nchopanda malire, tiyeni tipemphe Atate athu a Kumwamba kuti adzaze mitima yathu ndi ya anthu onse ndi Mzimu wao wachikondi:

 

1.     Tipempherere Akhristu onse, kuti kukondana kwao kupite m’tsogolo, ndipo adziwe kugonjetsa zoipa pakuchita zabwino.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Tipempherere anthu a mafuko onse, kuti alekeretu kukangana, ndipo choncho mtendere ukhazikike pakati pa maiko ndi pakati pa magulu a anthu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

3.     Tipempherere mabanja onse kuti eni ake akhale a mtima umodzi ndipo adziwe kumakhululukirana mwamsanga chifukwa chokhulupirira Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tomwe tipemphererane kuti timange moyo wathu pa chikondi chimene Ambuye amatikonda nacho, pomaonetsa anzathu mtima wachifundo.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, popereka kwa Inu mapemphero athuwa, tikuyamika chikondi chanu chosasinthika ndi chifundo chanu chopanda malire. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://business.facebook.com/latest/home?asset_id=109826477067295&business_id=1326098184199637&nav_ref=profile_plus_profile_left_nav_button Blog: https://www.blogger.com/blog/posts/2477989519106302629?hl=en-GB

Saturday, February 15, 2025

LAMULUNGU LA 6 PA CHAKA – C

LAMULUNGU LA 6 PA CHAKA – C

“Kodi munthu wodala ndani?”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA M’PROFETI YEREMIYA: YEREMIYA 17:5-8. (Tsoka kwa munthu wodalira munthu mnzake; ndi wodala munthu wokhulupirira Chauta).

 

Chauta akunena kuti, “tsoka kwa munthu wodalira munthu mnzake, amene amagonera

pa munthu mnzake kuti amthandize, pamene mtima wake wafulatira Chauta. Woteroyo adzakhala ngati chitsamba m'chipululu, ndipo sadzapeza zabwino. Adzakhala m'chipululu mopanda madzi, m'dziko lamchere m'mene anthu sangathe kukhalamo. Koma ndi wodala munthu wokhulupirira Chauta, amene amagonera pa Chautayo. Adzakhala ngati mtengo wobzalidwa m'mphepete mwa mtsinje, umene umatambalitsa mizu yake m'mbali mwamadzi. Suwopa kukamatentha, chifukwa masamba ake safota. Pa chaka chachilala sukuda nkhawa, ndipo suleka kubala zipatso.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 1:1-4.6.

 

Ngwodala munthu amene amadalira Chauta.

 

Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa,

Wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa,

Wosakhala nawo m’gulu la anthu onyoza Mulungu,

Koma wokondwerera kumvera malamulo a Chauta,

Nkumasinkhasinkha za malamulowo usana ndi usiku.

 

Ngwodala munthu amene amadalira Chauta.

 

Munthuyo ali ngati mtengo

Wobzalidwa m'mbali mwa mtsinje wa madzi.

Ngati mtengo wobereka zipatso pa nthawi yake,

Umene masamba ake safota konse.

Zochita zake zonse zimamuyendera bwino.

 

Ngwodala munthu amene amadalira Chauta.

 

Anthu oipa sali choncho,

Ali ngati mungu wouluzika ndi mphepo.

Paja Chauta amawasamalira anthu ake.

koma anthu ochimwa adzaonongeka.

 

Ngwodala munthu amene amadalira Chauta.

---------------------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 1 AKORINTO 15: 12,16-21. (Ngati Khristu sadauke, chikhulupiriro chanu nchopanda pake).

 

Abale, popeza kuti chimene timalalika ndi chakuti Khristu adauka kwa akufa, bwanji ena mwa inu akunena kuti, “Anthu akufa sadzaukanso”? Pakuti ngati akufa sauka, Khristunso sadauke. Ndipotu ngati Khristu sadauke, chikhulupiriro chanu nchopanda pake, ndipo mukadali m'machimo anu. Pamenepo nawonso amene adamwalira ali okhulupirira Khristu, adatayika ndithu. Ngati taika chikhulupiriro chathu mwa Khristu chifukwa cha moyo uno wokha, ndiye kuti ndife omvetsa chisoni koposa anthu ena onse. Koma ai, Khristu adauka ndithu kwa akufa. Pakati pa onse amene adafa, ndiye woyamba kuuka.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – LUKA 06: 23ab.

Alleluia, Alleluia Sangalalani ndi kuvina ndi chimwemwe, chifukwa mphotho yanu ndi yaikulu Kumwamba Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 6:17,20-26. (Ndinu odala, inu osaukanu. Koma ndinu atsoka, anthu achumanu).

 

Yesu adatsika phiri pamodzi ndi ophunzira ake, naima pa chidikha. Panali khamu lalikulu la ophunzira ake, ndi anthu ena ambirimbiri ochokera ku dera lonse la Yudeya ndi ku Yerusalemu, ndi kumbali yakunyanja, ku Tiro, ndi Sidoni. Yesu adayang’ana ophunzira ake, nawauza kuti, “Ndinu odala, inu Osaukanu, Ufumu wa Mulungu ndi wanu. Ndinu odala, inu amene mukumva njala tsopano, chifukwa mudzakhuta. Ndinu odala, inu amene mukulira tsopano, chifukwa mudzakondwa. Ndinu odala anthu akamadana nanu, akamakusalani ndi kukuchitani chipongwe, ndipo akamaipitsa dzina lanu chifukwa cha Ine Mwana wa Munthu. Nthawi imeneyo sangalalani ndi kuvina ndi chimwemwe chifukwa mphotho yanu ndi yaikulu Kumwamba. Paja ndi zomwenso makolo ao ankawachita aneneri kale. Koma ndinu atsoka, anthu achumanu, chifukwa mwalandiriratu zokusangalatsani. Ndinu atsoka, amene mukukhuta tsopanonu, chifukwa mudzamva njala. Ndinu atsoka, amene mukukondwa tsopanonu, chifukwa mudzamva chisoni ndiponso mudzalira. Ndinu atsoka, anthu onse akamakuyamikani. Paja makolo ao ankachitira aneneri onama akale zomwezi.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pakuti tikudalira Mulungu pa zonse, tiyeni timupemphe chithandizo chake pokumbukira zosowa zathu ndi za anthu onse:

 

1.     Tipempherere Eklezia wa Yesu kuti mau ake ndi chifundo chake chosamala amphawi zidzetse ufumu wa Mulungu m’mitima ya anthu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

2.     Tipempherere akhristu amene akuzunzika chifukwa cha Mthenga Wabwino, kuti alimbe mtima ndi kukondwera, podziwa kuti mphoto yao njaikulu kumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Tipempherere anthu amene amangofuna za pansi pano zokha, kuti azindikire kulakwa kwao ndipo atembenukire kwa Mulungu ndi mtima wolapa.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Tizipempherere ife tomwe kuti moyo wathu pansi pano ukhale wodziletsa, wokomera Mulungu ndi wochitira anzathu zachifundo zambiri.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate okoma mtima, mverani mapemphero athu ndipo mutipatse ife tonse mtima wokhulupirira chikondi chanu chosasinthika. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://business.facebook.com/latest/home?asset_id=109826477067295&business_id=1326098184199637&nav_ref=profile_plus_profile_left_nav_button

Blog: https://www.blogger.com/blog/posts/2477989519106302629?hl=en-GB

Saturday, February 8, 2025

LAMULUNGU LA 5 PA CHAKA – C

LAMULUNGU LA 5 PA CHAKA – C

“Ambuye! Ndilipo, munditume.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA M’PROFETI YESAYA: YESAYA 6:1-8. (Ndilipo ineyo, tumeni).

 

Chaka chimene mfumu Uziya adamwalira, ndidaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu wautali ndi wokwezedwa. Mkanjo wao unali wautali kwambiri, kotero kuti udadzaza Nyumba yao yonse. Pamwamba pao padaaimirira Aserafi. Aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri ophimbira kumaso, awiri ophimbira mapazi, awiri oulukira. Aserafiwo ankafuulirana kuti, “ngwoyera, ngwoyera, ngwoyera Chauta Wamphamvuzonse, ulemerero wake wadzaza dziko lonse lapansi. Chifukwa cha kufuulako maziko onse ndi ziwundo adagwedezeka ndipo m’Nyumba ya Chautamo mudangoti utsi pha. Apo ine ndidati: “Tsoka langa ine! Ndatayika. Pakuti ndine munthu wa pakamwa poipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poipa. Komabe maso anga aona Mfumu, Chauta Wamphamvuzonse.” Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja adaulukira kwa ine, ali ndi khala lamoto m’manja mwake. Khalalo adalichotsa pa guwa la nsembe ndi mbaniro. Ndipo adandikhuza pakamwa ndi khala lamotolo nati, “taona, ndakukhudza milomo ndi khalali. Kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.” Kenaka ndidamva mau a Ambuye akuti, “kodi ndidzatuma yani, ndani adzatipitire?” Apo ndidati, “ndilipo ineyo, tumeni.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 138:1-5, 7-8.

 

Ndidzakutamandani, Inu Chauta.

 

Ndikukuthokozani Inu Chauta ndi mtima wanga wonse,

Ndikuimba nyimbo zokutamandani pamaso pa milungu,

Ndikugwada mowerama,

Kunyumba kwa Nyumba yanu yoyera.

 

Ndidzakutamandani, Inu Chauta.

 

Ndikutamanda dzina lanu,

Chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika,

Chifukwanso cha kukhulupirika kwanu,

Pa tsiku limene ndidakuitanani, Inu mudandiyankha,

Mumandilimbitsa mtima ndi mphamvu zanu.

 

 

Ndidzakutamandani, Inu Chauta.

 

Mafumu onse a m’dziko adzakutamandani, Inu Chauta,

Chifukwa amva mau a pakamwa panu,

Adzaimba nyimbo zotamanda njira za Chauta,

Pakuti ulemerero wa Chauta ndi waukulu.

 

Ndidzakutamandani, Inu Chauta.

 

Mumatambasula dzanja lanu kuletsa adani anga okwiya,

Dzanja lanu lamanja limandipulumutsa,

Chikondi chanu, Inu Chauta, nchamuyaya,

Muipitirize ntchito imene mwaiyambayo.

 

Ndidzakutamandani, Inu Chauta.

---------------------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 1 AKORINTO 15:1-11. (Zimene timalalika ndi zomwezo, zimene mudakhulupirira ndi zomwezonso).

 

Abale, ndifuna kukukumbutsani Uthenga Wabwino umene ndidakulalikirani. Mudaulandira, ndipo mudakhazikitsapo chikhulupiriro chanu molimba. Mulungu adzakupulumutsani ndi Uthenga Wabwinowu, ngati musunga bwino mau ake monga ndidakulalikirani. Popanda kutero, bwenzi mutangokhulupirira pachabe. Pajatu mau aakulu amene ndidakupatsani ndi omwewo amene inenso ndidalandira. Mauwo ndi akuti Khristu adafera machimo athu, monga Malembo anenera. Adaikidwa m’manda, mkucha wake adauka, monga Malembo anenera. Motero adaonekera Kefa, kenaka atumwi khumi ndi awiri aja. Pambuyo pake adaonekera abale opitirira mazana asanu pa nthawi imodzi. Ambiri mwa iwowo akalipo, ena adamwalira. Ndipo adaonekera Yakobo, kenaka atumwi onse. Potsiriza, pambuyo pa onse adandiwonekeranso ineyo, ngakhale ndili ngati mpolo chabe. Inetu ndine wamng’onong’onodi mwa atumwi onse. Sindine woyenera konse kuti ndizitchedwa mtumwi, pakuti ndinkazunza Mpingo wa Mulungu. Koma chifukwa chakuti Mulungu adandikomera mtima, ndili monga ndilirimu. Ndipo kukoma mtima kwakeko sikunali kopanda phindu, popeza kuti ndidagwira ntchito koposa atumwi ena onse. Komabe si ndine ndidaigwira, koma mphamvu za Mulungu zimene zikundilimbikitsa. Motero kaya ndi ineyo kaya ndi iwowo, zimene timalalika ndi zomwezo, zimene mudakhulupirira ndi zomwezonso.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 4:19.

 

Alleluia, Alleluia Inu, munditsate, atero Ambuye, ndikakusandetseni asodzi a anthu Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 5:1-11. (Adasiya zonse namatsata Yesu).

 

Tsiku lina Yesu adaimirira pamphepete pa nyanja ya Genesarete, anthu ambirimbiri nkumamupanikiza kuti amve mau a Mulungu. Iye adaona zombo ziwiri pamphepetepo. Asodzi anali atatulukamo, ndipo ankatsuka makoka ao. Yesu adalowa m’chombo chimodzi, chimene chinali cha Simoni, nampempha kuti asunthire pang’ono ku nyanja. Adakhala pansi, ndipo ali m’chombo momwemo, adayamba kuwaphunzitsa anthuwo. Atatsiriza kulankhula, adauza Simoni kuti, “Sunthirani kozamako, muponye makoka anu kuti muphe nsomba.” Simoni adati, “Aphunzitsi, usiku wonsewu takhalira kugwira ntchito, osapha kanthu, koma chifukwa Inuyo mwatero, chabwino ndiponya makoka.” Tsono iwo adaponyadi makoka, napha nsomba zambirimbiri, kotero kuti makokawo ankayamba kung’ambika. Adachita kukodola anzao a m’chombo china chija kuti adzawathandize. Iwo adabwera, ndipo adadzaza zombo ziwiri zonse zija mpaka zinali pafupi kumira. Pamene Simoni Petro adaona zimenezo, adagwada nkuwerama kwambiri pamaso pa Yesu nati, “Pepani Ambuye, mundichokere, ndine munthu wochimwa.” Adaatero popeza kuti iye, pamodzi ndi onse amene anali naye, adaazizwa nako kuchuluka kwa nsomba zimene adaaphazo. Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedeo, anzake a Simoni, nawonso adaazizwa. Tsono Yesu adauza Simoni kuti, “Usaope, kuyambira tsopano udzakhala msodzi wa anthu.” Motero, atakokera zombozo ku mtunda, adasiya zonse namatsata Yesu.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, popeza kuti Mulungu saleka kuitana anthu ku ntchito yake, tiyeni, timudziwitse zosowa zathu ndi za anthu onse:

 

1.     Atate, mudalitse Apapa, Aepiskopi ndi ansembe onse kuti asenze udindo molimbika, azitsogolera bwino anthu ao pa njira ya chipulumutso.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atate, muitane anyamata ndi atsikana ambiri kuti adzipereke ndi mtima wonse ku ntchito yodziwitsa anzao Mthenga wanu Wabwino.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Atate, muunikire nzeru za akhristu onse, kuti azindikire udindo wao ndipo ayesetse kukokera anzao mu ufumu wanu.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Atate, mutithandize ife tomwe kuti tikhale akhristu achangu pomatekeseka ndi chipulumutso cha anzathu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Mulungu Atate athu, sindife oyenera konse kuti tikhale atumwi anu. Komabe tikukhulupirira Inu, muzitithandiza kukutumikirani moyenera. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://business.facebook.com/latest/home?asset_id=109826477067295&business_id=1326098184199637&nav_ref=profile_plus_profile_left_nav_button

Blog: https://www.blogger.com/blog/posts/2477989519106302629?hl=en-GB

Sunday, February 2, 2025

CHAKA CHA KUPEREKEDWA KWA AMBUYE YESU KU TEMPILE

 


CHAKA CHA KUPEREKEDWA KWA AMBUYE YESU KU TEMPILE

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI MALAKI: MALAKI 3:1-4 (Chauta amene mukumfunafuna adzafika ku Nyumba yake).

 

Chauta Wamphamvuzonse akunena kuti, “Ndidzatuma wamthenga wanga kuti akandikonzere njira. Kenaka mwadzidzidzi Chauta amene mukumfunafuna adzafika ku Nyumba yake. Wamthenga wa chipangano, amene mukumuyembekeza, suuyu akubwera. Kodi ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Kodi ndani adzatha kulimbikira iye akadzafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wapang’anjo, ndiponso ngati sopo wa munthu wochapa. Adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri wapang’anjo woyeretsa siliva, ndipo adzayeretsa Alevi monga amayeretsera golide ndi siliva, mpaka kuti azidzapereka nsembe zoyenera kwa Chauta. Choncho nsembe za Yuda ndi za Yerusalemu zidzakondweretsa Chauta, monga zidaaliri masiku amakedzana.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 24:7-10.

 

Kodi mfumu ya ulemereroyo ndani?

 

Kankhani zipata za mzinda,

tsekulani zitseko zakalekalezo,

kuti Mfumu yaulemerero ilowe.

 

Kodi mfumu ya ulemereroyo ndani?

 

Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?

Ndi Chauta wanyonga ndi wamphamvu,

Chauta ndiye ngwazi pa nkhondo.

 

Kodi mfumu ya ulemereroyo ndani?

 

Kankhani zipata za mzinda,

tsekulani zitseko zakalekalezo,

kuti Mfumu yaulemerero ilowe.

 

Kodi mfumu ya ulemereroyo ndani?

 

Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?

Ndi Chauta Wamphamvuzonse.

Iyeyo ndiye Mfumu yaulemerero.

 

Kodi mfumu ya ulemereroyo ndani?

 

---------------------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA KWA AHEBRI: AHEBRI 2:14-18 (Iye adaayenera kusanduka wofanafana ndi abale ake pa zonse).

 

Abale, popeza kuti anawo ndi anthu, okhala ndi magazi ndi mnofu, Yesu yemwe adasanduka munthu wonga iwowo. Adachita zimenezi kuti ndi imfa yake aononge Satana amene anali ndi mphamvu yodzetsa imfa. Pakutero adafunanso kuti awamasule amene pa moyo wao wonse anali ngati akapolo chifukwa choopa imfa. Paja nchodziwikiratu kuti sadatekeseke ndi angelo ai koma ndi zidzukulu za Abrahamu. Nchifukwa chake adaayenera kusanduka wofanafana ndi abale ake pa zonse, kuti akhale mkulu wa ansembe onse wachifundo ndi wokhulupirika potumikira Mulungu, ndipo kuti pakutero achotse machimo a anthu. Tsono popeza kuti iye yemwe adazunzikapo ndi kuyesedwapo, ndiye kuti angathe kuwathandiza anthu amene amayesedwa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – LUKA 2:32.

Alleluia, Alleluia “Mwapereka kuwala kodzaunikira anthu a mitundu ina, kudzakhala ulemerero wa anthu anu Aisraele.” – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 2:22-40 (Ndi maso angawa ndachiwonadi chipulumutso).

 

Idafika nthawi yoti Yosefe ndi Maria achite mwambo wakuyeretsedwa potsata Malamulo a Mose. Tsono mwanayo adapita naye ku Yerusalemu kuti akampereke kwa Ambuye. Pajatu m'Malamulo a Ambuye muli mau akuti, “Mwana aliyense wamwamuna, woyamba kubadwa, apatulidwe kuti akhale wao wa Ambuye.” Adakaperekanso nsembe potsata Malamulo a Ambuye akuti, “Apereke njiwa ziwiri kapena maunda awiri.”

 

Ku Yerusalemuko kunali munthu wina, dzina lake Simeoni. Anali munthu wolungama ndi woopa Mulungu. Ankayembekezera nthawi yoti Mulungu adzapulumutse Aisraele, ndipo Mzimu Woyera anali naye. Mzimu Woyerayo adaamuululira kuti sadzafa asanaone Mpulumutsi amene Mulungu adaalonjeza. Tsiku lina Mzimu Woyera adamlamula kuti apite ku Nyumba ya Mulungu. Makolo a Yesu adalowanso m’Nyumbamo ndi mwana waoyo kukamchitira mwambo potsata Malamulo a Mose. Pamenepo Simeoni adalandira mwanayo m'manja mwake, nayamba kutamanda Mulungu ndi mau akuti, “Ambuye, tsopano mundilole ine mtumiki wanu, ndipite ndi mtendere, pakuti mwachitadi zija mudaalonjezazi. Ndi maso angawa ndachiwonadi chipulumutso chija, chimene mudakonza kuti anthu a mitundu yonse achiwone. Mwapereka kuwala kodzaunikira anthu a mitundu ina, kodzakhala ulemerero wa anthu anu Aisraele.”

 

Atate ndi amai a mwanayo ankangodabwa nazo zimene Simeoni ankanena za mwanayo. Kenaka Simeoniyo adawadalitsa, nauza Maria, mai wa mwanayo, kuti, “Mwanayu Mulungu wamuika kuti Aisraele ambiri adzagwe, ambirinso adzadzuke, chifukwa cha iyeyu. Adzakhala chizindikiro chochokera kwa Mulungu, chimene anthu ambiri adzatsutsana nacho, kuti choncho maganizo amene ali m’mitima ya anthu ambiri adzaonekere poyera. Ndipo inunso mai, chisoni chidzabaya mtima wanu ngati lupanga.”

 

Kunalinso mneneri wina wamkazi, dzina lake Anna, mwana wa Fanuwele, wa fuko la Asere. Anali wokalamba kwambiri. Anali atakhala pa banja zaka zisanu ndi ziwiri zokha, pambuyo pake nkukhala wamasiye kufikira msinkhu wa zaka 84. Sankachokatu ku Nyumba ya Mulungu, ankakonda kudzatumikira Mulungu usana ndi usiku pakupemphera ndi kusala zakudya. Iye adafikako nthawi yomweyo, nayamba kuyamika Mulungu, nkumakamba za Mwanayo ndi anthu onse amene ankayembekezera nthawi yoti Mulungu adzapulumutse Yerusalemu. Yosefe ndi Maria atachita zonse potsata Malamulo a Ambuye, adabwerera ku Galileya, kumudzi kwao ku Nazarete. Mwanayo ankakula, nasanduka wamphamvu nkukhalanso wa nzeru zabasi. Ndipo Mulungu ankamudalitsa.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://business.facebook.com/latest/home?asset_id=109826477067295&business_id=1326098184199637&nav_ref=profile_plus_profile_left_nav_button

Blog: https://www.blogger.com/blog/posts/2477989519106302629?hl=en-GB



Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...