Saturday, August 31, 2024

LAMULUNGU LA 22 PA CHAKA – B.

LAMULUNGU LA 22 PA CHAKA – B.

“Anthuwa Amangondilemekeza Pakamwa Pokha.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA DEUTORONOMO: DEUTORONOMO 04: 01 – 02, 06 – 08 (Musaonjezerepo kanthu kena pa zimene ndikulamulani ndipo muzimvera malamulo amene ndakupatsani).

 

Tsono inu Aisraele, muzimvera malamulo ndi malangizo onse amene ndikukuphunzitsani, kuti mukhale ndi moyo. Ndipo mudzalowa ndi kukhazikika m’dziko limene Chauta, Mulungu wa makolo anu, akukupatsani. Musaonjezerepo kanthu kena pa zimene ndakulamulani, ndipo musachotserepo kanthu. Muzimvera malamulo a Chauta, Mulungu wanu, amene ndakupatsani. Mukawasunge ndi kuwatsata, ndipo chimenechi chidaonetsa anthu a mitundu ina kuti ndinu anthu anzeru ndi omvetsa zinthu bwino. Akadzamva malamulo onsewa, iwowo adzati, “mtundu umenewo ndi waukulu, wanzeru ndi womvetsa zinthu bwino.” Palibe mtundu wina uliwonse, kaya ndi waukulu chotani, umene uli ndi Mulungu wokhala pafupi nawo, monga m’mene Mulungu wathu amakhalira ndi ife. Nthawi zonse tikamuitana, amatiyankha. Palibe mtundu wina uliwonse kaya ndi waukulu chotani, umene ali ndi malamulo ndi malangizo achilungamo onga awa amene ndakupatsani lerowa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 15: 02 – 05.

 

Munthu wochita zolungama amakhala pa phiri la Chauta.

 

Inu Chauta, kodi ndani angathe kukhala pa phiri lanu loyera?

Ndi munthu amene amayenda mosalakwa,

Amene amachita zolungama nthawi zonse,

Amene amalankhula zinthu ndi mtima woona.

 

Munthu wochita zolungama amakhala pa phiri la Chauta.

 

Ndi amene sasinjirira ndipo sachita anzake zoipa,

Kapena kumafalitsa mbiri yoipa ya anzake,

Ndi amene amanyoza munthu womkana Mulungu,

Koma amamlemekeza anthu omvera Chauta.

 

Munthu wochita zolungama amakhala pa phiri la Chauta.

 

Ndi amene amachitadi zimene walonjeza,

Ngakhale zikhale zowawa chotani,

Ndi amene salandira chiphuphu kuti azunze munthu osalakwa,

Munthu wochita zimenezi, palibe chilichonse chimene chidzamgwedeze.

 

Munthu wochita zolungama amakhala pa phiri la Chauta.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA YAKOBE: YAKOBE 01: 17 – 18, 21 – 22, 27. (Muzichita zimene mau akukuuzani).

 

Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera Kumwamba, ndipo Atate a zofunikira zonse zakuthambo. Iwo sasinthika konse, ndipo kuwala kwao sikutsitirika mpang’ono pomwe. Mwa kufuna kwake mwiniwakeyo, adatipatsa moyo kudzera mwa mau ake oona, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, ife tikhale ngati zipatso zoyamba zimene Iye wadzipatulira. Nchifukwa chake siyani chizolowezi chilichonse chonyansa, ndiponso kuipamtima kulikonse. Muwalandire mofatsa mau amene Mulungu adabzala m’mitima mwanu, pakuti ndiwo angathe kukupulumutsani. Musamadzinyenga pakungomva chabe mau a Mulungu, koma muzichita zimene mauwo anena. Chipembedzo choona ndi changwiro pamaso pa Mulungu amene Chipembedzo choona ndi changwiro pamaso pa Mulungu amene ali Atate, ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto ao, ndiponso kudzisunga bwino, kuwopa kudetsedwa ndi zoipa za m’dziko lapansi.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YAKOBE 01: 18.

Alleluia, Alleluia – Mwa kufuna kwake mwiniwakeyo, adatipatsa moyo kudzera mwa mau ake oona, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, ife tikhale ngati zipatso zoyamba zimene Iye wadzipatulira. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 07: 01 – 08, 14 – 15, 21 – 23. (Inu mumasiya Malamulo a Mulungu, nkumasunga miyambo ya anthu).

 

Tsiku lina Afarisi ena pamodzi ndi aphunzitsi ena a Malamulo, amene adaachokera ku Yerusalemu, adasonkhana kwa Yesu. Iwo adaaona kuti ophunzira ake ena ankangodya chakudya osasamba m’manja moyenera (ndiye kuti mosasamala mwambo wosamba m’manja). Pajatu Afarisi ndi Ayuda ena onse saadya asanasambe m’manja mwa njira yoyenera. Amatero kuti asunge mwambo wa makolo. Ndipo akachokera ku msika, saadya osasamba m’manja. Amasunganso miyambo ina yambiri imene makolo ao adawasiyira, monga kutsuka zikho, miphika, ndi ziwiya zamkuwa [ndi mabedinso]. Choncho Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo aja adamufunsa Yesu kuti, “chifukwa chiyani ophunzira anu sasunga mwambo wa makolo, koma amangodya chakudya osasamba m’manja moyenera?” Yesu adawayankha kuti, “inu anthu achiphamaso, ndithu mneneri Yesaya adaanenadi zoona muja adaalemba kuti, ‘anthu awa amangondilemekeza ndi pakamwa chabe, koma mtima wao uli kutalitali ndi Ine. Amandipembedza inde, koma kupembedza kwaoko nkopanda phindu, chifukwa zimene amaphunzitsa ngati zophunzitsa zenizeni, ndi malamulo a anthu chabe.’” Kenaka Yesu adati, “inu mumasiya Malamulo a Mulungu, nkumasunga miyambo ya anthu.” Pambuyo pake Yesu adaitananso anthu aja kuti adze pafupi, ndipo adawauza kuti, “mverani nonsenu, ndipo mumvetsetse bwino. Palibe chinthu chochokera kunja ndi kulowa m’kati mwa munthu chimene chingathe kumuipitsa. Koma zimene zimatuluka mwa munthu ndizo zimamuipitsa. Chifukwa m’kati mwa mitima ya anthu ndiye mumatuluka maganizo oipa, za chiwerewere, za kuba, za kuphana, zigololo, masiriro, kuipa mtima, kunyenga, zonyansa, kaduka, kunyoza, kudzikuza, ndiponso kupusa. Zoipa zonsezi zimachokera m’kati mwa munthu, ndipo ndizo zimamuipitsa.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.


Mapemphero a Akhristu


Abale, mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera Kumwamba kwa Atate. Tiyeni, tipemphe Mulungu kuti mawu ake ndi malamulo ake alowe ndi kuzika mizu m’mitima ya anthu onse:


1. Tipempherere akulu amene ali ndi udindo mu Mpingo, kuti atsogolere anthu awo moona ndi modzichepetsa mtima, pa njira ya kuyera ndi ya chikondi.

Tikupemphani, mutivomereze.


2. Tipempherere akhristu onse kuti kuyera kwao ndi kukondana kwao kuunikire anzao akunja ndi kuwakokera kwa Ambuye.

Tikupemphani, mutivomereze.


3. Tipempherere anthu osauka, odwala ndi amasiye, kuti azindikire kukoma mtima kwa Mulungu, powayendera anzao achikhristu.

Tikupemphani, mutivomereze.


3. Tidzipempherere ife tomwe, kuti chipempbedzo chathu chikhale choona ndi changwiro pamaso pa Mulungu ndi pamaso pa anzathu.

Tikupemphani, mutivomereze.


Atate, musaleke kuyeretsa mitima yathu ndi kuchotsamo kunyenga kulikonse, kuti mawu athu amveke Kumwamba, ndipo ntchito zathuzikome pamaso panu. Mwana Yesu Khristu Ambuye athu. Amen.


#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/ 

Saturday, August 24, 2024

LAMULUNGU LA 21 PA CHAKA – B.

“Muli nawo Mau Opatsa Moyo Wosatha.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA YOSWA: YOSWA 24: 01 – 02, 15 – 18. (Nafenso tidzatumikira Chauta, chifukwa ndiye Mulungu wathu).

 

Yoswa adasonkhanitsa mafuko onse a Aisraele ku Sekemu. Adaitana akuluakulu, atsogoleri, aweruzi ndi akapitao Aisraele, ndipo onsewo adafika pamaso pa Mulungu. Adauza anthu onsewo kuti, “zimene Chauta, Mulungu wa Aisraele, akunena ndi izi, akuti, ‘kale makolo anu ankakhala pa mbali ina ya mtsinje wa Yufurate, ndi kumapembedza milungu ina. Mmodzi mwa makolo amenewa anali Tera, bambo wa Abrahamu ndi Nahori.’ Tsono ngati simufuna kutumikira Chauta, sankhani lero lomwe lino amene mudzamtumikire, kapena milungu ya Aamori amene mukukhala nawo m’dziko mwao. Koma ine pamodzi ndi banja langa lonse, tidzatumikira Chauta.” Apo anthuwo adayankha kuti, “zoti nkusiya Chauta ndi kumakatumikira mulungu ina ndiye ai, ife sitingathe kuchita zotere mpang’ono pomwe. Chauta, Mulungu wathu, ndiye amene adatulutsa makolo athu pamodzi ndi ife tomwe mu ukapolo, ku dziko la Ejipito. Ndipo tidaonanso ndi maso athu zinthu zazikulu zimene adachita. Ife tikufika, Chauta ankapirikitsa Aamori amene ankakhala m’dziko lino. Motero nafenso tidzatumikira Chauta, chifukwa ndiye Mulungu wathu.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 34: 02 – 03, 16 – 23.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Ndidzayamika Chauta nthawi zonse,

Pakamwa panga padzatamanda Iye kosalekeza,

Moyo wanga umanyadira Chauta,

Anthu Ozunzika amve ndipo akondwere.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Koma Chauta amawakwiyira anthu ochita zoipa,

Anthuwo sadzakumbukiranso pansi pano,

Chauta samakwiiyira anthu ochita zolungama,

Ndipo amamvera zopempha zawo.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Pamene anthu ake akulira kuti awathandize,

Chauta amamva nawapulumutsa m’mavuto ao onse,

Chauta amakhala pafupi ndi anthu a mtima wosweka,

Amapulumutsa otaya mtima.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Anthu a Mulungu amaona masautso ambiri,

Komabe Chauta amawapulumutsa m’mavuto awo onse,

Chauta amasunga thupi la munthuyo,

Palibe fupa limene limasweka.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Choipa chitsata mwini,

Anthu odana ndi munthu wa Mulungu adzalangidwa,

Chauta amaombola moyo wa atumiki ake,

Palibe wothawira kwa Iye amene adzalangidwe.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AEFESO: AEFESO 05: 21 – 32. (Chinsinsicho nchokhudza Khristu ndi Mpingo.)

 

Abale, inu amene mumaopa Khristu, muzimverana. Inu akazi, muzimvera amuna anu, monga mumamvera Ambuye. Paja mwamuna ndi mutu wa mkazi wake, monga momwe Khristu ali mutu wa mpingo, umene uli thupi lake, ndipo Iye mwini ndi Mpulumutsi wa Mpingowo. Tsono monga Mpingo umamvera Khristu, momwemonso akazi azimvera amuna ao pa zonse. Inu amuna, muzikonda akazi anu, monga momwe Khristu adakondera Mpingo, nadzipereka chifukwa cha Mpingowo. Adachita zimenezi kuti aupatule ukhale wakewake, atauyeretsa pakuutsuka ndi madzi ndiponso ndi mau ake. Adafuna kuti akauimike pamaso pake uli waulemerero, wopanda banga kapena makwinya, kapena kanthu kena kalikonse kouipitsa, koma uli woyera ndi wangwiro kotheratu. Momwemonso amuna azikonda akazi ao, monga momwe eni akewo amakondera matupi ao. Amene amakonda mkazi wake ndiye kuti amadzikonda iye yemwe. Palibiretu munthu amene amadana ndi thupi lake, ndipo ife ndife ziwalo zake. Paja mau a Mulungu akuti, “nchifukwa chake mwamuna adzasiye atate ndi amai ake, nkukaphatikizana ndi mkazi wake, kuti awiriwo asanduke thupi limodzi.” Mau amenewa akutiwululira chinsinsi chozama, ndipo ndikuti chinsinsicho nchokhudza Khristu ndi Mpingo.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 06: 60 – 69.

Alleluia, Alleluia – Mau anu, Ambuye, ndiwo amapatsa Mzimu wa Mulungu ndiponso moyo. Muli nawo ndinu mau opatsa moyo wosatha. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA YOHANE WOYERA: YOHANE 06: 60 – 69. (Ambuye, nanga tingapitenso kwa yani? Muli nawo ndinu mau opatsa moyo wosatha).

 

Ophunzira ambiri a Yesu atamva zimenezi adati, “mau amenewa ngapatali. Angathe kuwavomera ndani?” Yesu adaadziwa mumtima mwake kuti ophunzira ake akung’ung’udza za zimenezi. Tsono adawafunsa kuti, “kodi zimenezi mukukhumudwa nazo? Nanga mudzatani mukadzaona Mwana wa Munthu akukwera kunka kumene anali kale? Mzimu wa Mulungu ndiwo umapatsa moyo, mphamvu ya munthu siipindula konse. Mau amene ndalankhula nanu ndiwo amapatsa mzimu wa Mulungu ndiponso moyo. Koma pali ena mwa inu amene sakukhulupirira.” (Pakuti Yesu adaadziwiratu mpachiyambi pomwe amene sadzakhulupirira, adaamudziwiratunso amene analikudzampereka kwa adani ake.) Tsono adati, “nchifukwa chake ndinakuuzani kuti palibe munthu amene angabwere kwa Ine ngati Atate sampatsa mphamvu zobwerera kwa Ine.” Kuchokera pamenepo ophunzira ambiri a Yesu adamsiya, osayenda nayenso. Tsono Yesu adafunsa ophunzira khumi ndi awiri aja kuti, “nanga inu, kodi inunso mukufuna kuchoka?” Simoni Petro adati, “Ambuye, nanga tingapitenso kwa yani? Muli nawo ndinu mau opatsa moyo wosatha. Ife ndiye tikukhulupirira ndipo tikudziwa kuti ndinu Woyera uja wochokera kwa Mulungu.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, tiyeni tipereke mapemphero athu kwa Mulungu kuti mau a Mthenga Wabwino aunikire anthu onse:

 

1.     Atate, mupatse nzeru ndi mphamvu kwa akulu a Eklezia kuti aonetse chikhulupiriro cholimba potsogolera mbumba yanu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

2.     Atate, mulimbitse ansembe ndi onse okhala m'zipani, kuti akutumikireni mokhulupirika ndi mwakhama, potsata malonjezo ao.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

3.     Atate, muunikire anthu amene akuyenda mu mdima nakhala okayikakayika, kuti aweramuke ndi kuyang’ana Mwana wanu Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

4.     Atate, mudalitse mabanja onse kuti eni ake akhale okhulupirika wina kwa m’nzake, ndipo akondane monga momwe Mwana wanu adakondera Mpingo wake.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Mulungu wathu, mverani mapemphero athuwa, ndipo mutiwonjezere chikhulupiriro, kuti tilondole mosakayika mapazi a Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, August 17, 2024

 LAMULUNGU LA 20 PA CHAKA – B.

“Ndine Chakudya Chopatsa Moyo.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MIYAMBO: MIYAMBO 09: 01 – 06 (Bwera, dzadyeko chakudya changa, ndipo udzamweko vinyo amene ndakonza).

 

Nzeru idamanga nyumba yake, idaimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri. Idapha ziweto zake, idakonza vinyo wake, nkuyala tebulo lake. Idatuma adzakazi ake kuti akakhalire pa malo apamwamba mu minda ndipo akalengeze kuti, “Munthu wamba aliyense abwere kuno!” Kwa munthu wopanda nzeru imati, “Bwera, dzadyeko chakudya changa, ndipo udzamweko vinyo amene ndakonza. Leka kupulukira kwako, kuti ukhale ndi moyo, uziyenda m’njira ya nzeru.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 34: 02 – 03, 10 – 15.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Ndidzayamika Chauta nthawi zonse,

Pakamwa panga padzatamanda Iye kosalekeza,

Moyo wanga umanyadira Chauta,

Anthu ozunzika amve ndipo akondwere.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Muzimvera Chauta, inu anthu ake oyera mtima,

Pakuti amene amamumvera sasowa kanthu,

Ngakhale anaamkango amasowa chakudya ndipo amakhala anjala,

koma anthu amene amalakalaka Chauta, sasowa zinthu zabwino.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Bwerani ana anga, mundimvere,

Ndidzakuphunzitsani kuwopa Chauta,

Ndani mwa inu amakhumba moyo ndi kulakalaka kuti akhale masiku ambiri,

Kuti asangalale ndi zinthu zabwino?

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Ngati ufunadi moyo, usalankhule zoipa,

Pakamwa pako pasakambe zonyenga,

Lewa zoipa, ndipo uchite zabwino,

Funafuna mtendere ndi kuulondola.

 

Yesani ndipo mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AEFESO: AEFESO 05: 15 – 20 (Dziwani zimene Ambuye afuna kuti muchite).

 

Abale, samalirani bwino mayendedwe anu. Musayende monga anthu opanda nzeru, koma monga anthu anzeru. Mukhale achangu, osataya nthawi yanu pachabe, pakuti masiku ano ngoipa. Nchifukwa chake musakhale opusa, koma dziwani zimene Ambuye afuna kuti muchite. Musaledzere vinyo, kumeneko nkudzitaya, koma mudzazidwe ndi Mzimu Woyera. Muzichezerana ndi mau a masalimo ndi a nyimbo za Mulungu ndi zauzimu. Ndipo muziimbira Ambuye mopolokezana ndi mtima wanu wonse. Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, m’dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 6:56

Alleluia, Alleluia – Aliyense wodya thupi langa ndi kumwa magazi anga, amakhala mwa Ine, ndipo Ine ndimakhala mwa iyeyo. Atero Ambuye.  – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA YOHANE WOYERA: YOHANE 06: 51 – 58 (Thupi langa ndi chakudya chenicheni, ndipo magazi anga ndi chakumwa chenicheni).

 

Yesu adauza khamu la anthu kuti: “Ine ndine chakudya chamoyo chimene chidatsika kuchokera Kumwamba. Munthu wodya chakudyachi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya. Ndipo chakudyacho chimene Ine ndidzapereka ndi thupi langa, limene ndikulipereka kuti anthu a pa dziko lonse lapansi akhale ndi moyo.” Pamenepo Ayuda aja adayamba kukangana okhaokha, ankati, “Munthu ameneyu angathe bwanji kutipatsa thupi lake kuti tidye?” Yesu adati, “Ndithu ndikunenetsa kuti ngati simudya thupi la Mwana wa Munthu ndi kumwa magazi ake, simungakhale ndi moyo mwa inu. Aliyense wodya thupi langa ndi kumwa magazi anga, ali ndi moyo wosatha, ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. Pakuti thupi langa ndi chakudya chenicheni, ndipo magazi anga ndi chakumwa chenicheni. Aliyense wodya thupi langa ndi kumwa magazi anga amakhala mwa Ine, ndipo Ine ndimakhala mwa iyeyo. Monga Atate amoyo adandituma, ndipo Ine ndili ndi moyo pokhala mwa Iwo, momwemonso aliyense wodya Ine, adzakhala ndi moyo pokhala mwa Ine. Chakudya chimene chidatsika kuchokera Kumwamba nchimenechi. Nchosiyana ndi mana aja amene makolo anu ankadya koma nkufabe. Wodya chakudya chimenechi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pokhala a mtima umodzi ndi Yesu Khristu amene akutitsogolera, tiyamike Atate a Kumwamba popempherera anthu onse:

 

1.     Ansembe onse ayesetse kuphatikizana kwenikweni ndi Yesu Khristu popereka nsembe ya Ukaristia, kuti azisenza udindo wao molimbika ndi mokhulupirika.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akhristu onse azindikire kuti Ukaristia ndi maziko a moyo wao, poti Ambuye amafuna kukhala mwa iwowo ndi kuwalunzitsa onse m’chikondi chao.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Akhristu amene ali ndi ana ayesetse ndithu kuphunzitsa ana awo za Ambuye Yesu, ndipo autse m’mitima mwao njala yofunitsa kulandira Ambuye m’sakramenti la Ukaristia.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse opemphera pano tikhale ndi mtima wosirira kulandira Ambuye kawirikawiri, kuti tikhazikike m’chikondi chao ndi kumagwirizana tonse mwa ubale.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, popereka kwa Inu mapemphero athuwa, tikukuyamikani kuti mwatikonzera phwando mu Ufumu wanu, kuti tizikondwera tonse pamaso panu mpaka muyaya. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, August 10, 2024

LAMULUNGU LA 19 PA CHAKA – B.

LAMULUNGU LA 19 PA CHAKA – B.

“Yesu Khristu Ndiye Chakudya Chopatsa Moyo.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LOYAMBA LA MAFUMU: 01 MAFUMU 19: 04 – 08. (Motero adapeza Mphamvu zoyendera, mpaka adakafika ku Sinai, phiri la Mulungu).

 

Eliya mwini wake adayenda ulendo wa tsiku limodzi m’chipululu, nakakhala pansi patsinde pa kamtengo ka tsache. Tsono adapempha kuti afe, adati, “zandikola! Inu Chauta, bwanji ndingofa basi! Ine sindingapambane makolo anga.” Atatero adagona tulo patsinde pa kamtengo ka tsache pomwepo. Mwadzidzidzi mngelo adamkhudza namuuza kuti, “dzuka, udye.” Eliya atapenya, adangoona kuti kumutu kwake kuli buledi wootcha pa makala, ndiponso mkhate wa madzi. Adadya, namwera, nkugonanso. Mngelo wa Chauta uja adabweranso kachiwiri, namkhudza nati, “dzuka, udye kuti ulendowu ungakukanike.” Eliya uja adadzuka, nadya nkumwera. Motero adapeza mphamvu zoyendera. Adayenda masiku makumi anai usana ndi usiku mpaka ku Sinai, phiri la Mulungu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 34: 02 – 09.

 

Yesani ndipo Mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Ndidzayamika Chauta nthawi zonse,

Pakamwa panga padzatamanda Iye kosalekeza,

Moyo wanga umanyadira Chauta,

Anthu Ozunzika amve ndipo akondwere.

 

Yesani ndipo Mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Lalikani pamodzi nane ukulu wa Chauta,

Tiyeni limodzi tiyamike dzina lake,

Ndidapemphera kwa Chauta ndipo adandiyankha,

Adandipulumutsa kwa zonse zimene ndinkaziwopa.

 

Yesani ndipo Mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Ozunzikawo atayang’ana kwa Chauta,

Nkhope zao zidasangalala, sadachite manyazi,

Munthu wosaukayu adalira, ndipo Chauta adamumva,

Nampulumutsa m’mavuto ake onse.

 

Yesani ndipo Mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

 

Mngelo wa Chauta amatchinjiriza anthu omvera Iye,

Ndipo amawapulumutsa,

Yesani ndipo Mudzaona kuti Chauta ndi wabwino,

Ngwodala munthu wothawira kwa Chauta.

 

Yesani ndipo Mudzaona kuti Chauta ndi wabwino.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AEFESO: AEFESO 04: 30 – 05:02. (Muzikondana, monga Khristu adatikonda ife).

 

Abale, musamvetse chisoni Mzimu Woyera amene Mulungu adakusindikizani chizindikiro chake chotsimikizira kuti ndinu ake pa tsiku limene Mulunguyo adzatipulumutsutse kwathunthu. Muchotseretu pakati panu kuzondana, kukalipa, ndiponso kupsa mtima. Musachitenso chiwawa, kapena kulankhula mau achipongwe, tayani kuipa konse. Muzikomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, ndipo muzikhululukirana monga momwe Mulungu mwa Khristu adakukhululukirani inunso. Tsono popeza kuti ndinu ana okondedwa a Mulungu, muziyesa kumtsanzira. Muzikondana, monga Khristu adatikonda ife, nadzipereka kwa Mulungu chifukwa cha ife. Adadzipereka ngati chopereka ndi nsembe ya fungo lokondweretsa Mulungu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 06: 51.

Alleluia, Alleluia – Ine ndine Chakudya chamoyo chimene chidatsika kuchokera Kumwamba. Munthu wodya chakudyachi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya. Atero Ambuye. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA YOHANE WOYERA: YOHANE 06: 41 – 51. (Ine ndine chakudya chotsika kuchokera kumwamba).

 

Pamenepo Ayudawo adayamba kung’ung’udza chifukwa Yesu adaati, “Ine ndine chakudya chotsika kuchokera kumwamba.” Iwo ankanena kuti, “kodi ameneyu si Yesu, mwana wa Yosefe uja? Bambo wake ndi mai wake suja tikuwadziwa? Nanga tsono anganene bwanji kuti, ‘ndidatsika Kumwamba?’” Yesu adawayankha kuti, “musang’ung’udze inu. Palibe munthu amene angabwere kwa Ine, ngati Atate amene adandituma samkoka. Ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. Paja aneneri adalemba kuti, ‘onse adzakhala ophunzitsidwa ndi Mulungu.’ Munthu aliyense womva Atate, nkuphunzira kwa Iwo, amadza kwa Ine. Sindiye kutitu wina aliyense adaona Atate ai, koma Ine ndekha amene ndidachokera kwa Mulungu; Ineyo ndi amene ndidaona Atate. Ndithu ndikunenetsa kuti wokhulupirira Ine, ali nawo moyo wosatha. Ine ndine chakudya chopatsa moyo. Makolo anu ankadya mana m’chipululu muja, komabe adafa. Koma chakudya chimene ndikunenachi ndi chimene chidatsika kuchokera Kumwamba, kuti munthu atachidya asafe. Ine ndine chakudya chamoyo chimene chidatsika kuchokera Kumwamba. Munthu wodya chakudyachi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya. Ndipo chakudyacho chimene Ine Ndidzapereka ndi thupi langa, limene ndikulipereka kuti anthu a pa dziko lonse lapansi akhale ndi moyo.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, Yesu adadzipereka kuti anthu a pa dziko lonse lapansi akhale ndi moyo. Tsono, tiyeni, tiwapempherere anthu onse:

 

1.     Tipempherere ansembe onse kuti akhale a mtima umodzi ndi Yesu Khristu, popereka nsembe yake, ndiponso pa moyo wao wonse.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Tipempherere akhristu amene adaleka kulandira kuti azindikire umphawi wao, azidzidzimuka m’mitima mwao ndi kubwerera kwa Ambuye ndi mtima wolapa.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Tipempherere mabanja a chikhristu kuti eni ake ayesetse kuutsa m’mitima ya ana ao njala yofunitsa kulandira Ambuye m’sakramenti la Ukaristia.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse tili muno tipemphererane kuti tisunge umodzi wathu ndi kumakondana mwaubale, pakulandira Ambuye kawirikawiri m’sakramenti la Ukaristia.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, popereka kwa Inu mapemphero athuwa, tikuyamika chifundo chanu chofuna kutisonkhanitsa tonse pamodzi, kuti tikhale amodzidi mwa Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...