Saturday, July 29, 2023

LAMULUNGU LA 17 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 17 PA CHAKA – CHAKA A.

“Chuma changa ndiye Mulungu Mwini.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LOYAMBA LA MAFUMU; 01 MAFUMU 03: 05, 07 – 12 (Wapempha nzeru zolamulira anthu bwino).

 

Ku Gibiyoniko Chauta adamuwonekera Solomoni m’maloto usiku, namuuza kuti, “Upemphe chilichonse chimene ufuna kuti ndikupatse. Solomoni adati, “Inu Chauta Mulungu wanga, mwaika mtumiki wanune pa malo a Davide bambo wanga, ngakhale ndine mwana wamng’ono chabe, ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yanga. Tsono ine mtumiki wanu ndikukhala pakati pa anthu amene mudawasankha, mtundu waukulu, anthu ake ochuluka, oti nkosatheka kuwawerenga. Nchifukwa chake mundipatse mtumiki wanune nzeru zolamulira anthu anu, kuti ndizidziwa kusiyanitsa zabwino ndi zoipa. Nanga popanda nzeruzo ndani angathe kulamulira mtundu waukulu chotere wa anthu anu?” Zidawakomera Ambuye kuti Solomoni adapempha zimenezi. Tsono Mulungu adauza Solomoni kuti, “Chifukwa chakuti wapempha zimenezi, osapempha moyo wautali kapena chuma kapena imfa ya adani ako, koma nzeru zolamulira anthu bwino, ndiye Ine ndikuchitira zimene wapempha. Zoona, ndikupatsa mtima wanzeru ndi waluntha, kotero kuti sadaonekepo kale lonse wina wofanafana nawe, ndipo sadzaonekanso wina wolingana nawe, iweyo utafa.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 119: 57, 72, 76 – 77.

 

Ambuye, ndimakonda malamulo anu.

 

Inu Chauta, ndikulonjeza kumvera mau anu,

Malamulo a pakamwa panu amandikomera,

Kuposa ndalama zikwizikwi zagolide ndi zasiliva.

 

Ambuye, ndimakonda malamulo anu.

 

Chikondi chanu chosasinthika chindisangalatse ine mtumiki wanu,

Monga momwe mudalonjezera,

Mundichitire chifundo kuti ndikhale ndi moyo,

Pakuti malamulo anu amandikondwetsa.

 

Ambuye, ndimakonda malamulo anu.

 

Koma ine ndimasamala malamulo anu,

Kupambana golide, golide wosungunula bwino,

Malamulo anu onse amalungamitsa mayendedwe anga,

Ndimadana ndi njira iliyonse yonyenga.

 

Ambuye, ndimakonda malamulo anu.

 

Malamulo anu ndi abwino,

Nchifukwa chake ndimawatsata ndi mtima wanga wonse,

Kufotokozera mau anu kumakhala ngati kuwala,

Kumapatsa nzeru za kumvetsa kwa anthu opanda nzeru.

 

Ambuye, ndimakonda malamulo anu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA 08: 28 – 30 (Mulungu adawapatulanso kale kuti akhale monga Mwana wake).

 

Abale, tikudziwa kuti Mulungu amayendetsa zinthu mwa njira yoti zonse ziwakomere anthu omukonda ndipo apindulepo. Anthuwo ndi amene Iye amawaitana monga momwe Iye adazikonzera. Pakuti anthu amene Mulungu adawasankhiratu, Iye adawapatulanso kale kuti akhale monga Mwana wake, kuti choncho Mwanayo akhale woyamba mwa abale ambiri. Mulungu sadangowapatula, komanso adawaitana. Sadangowaitana, komanso adawaona kuti ngolunga pamaso pake. Ndipo sadangoona kuti ngolunga pamaso pake, komanso adawagawirako ulemerero wake.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 11: 25.

 

Alleluia, Alleluia – Atate, Mwini kumwamba ndi dziko lapansi, ndikukuyamikani kuti zinthuzi mudaululira anthu osaphunzira. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 13: 44 – 52 (Amakagulitsa zonse zimene ali nazo, nkukagula munda).

 

Yesu adauza khamu la anthu kuti: “Ufumu wakumwamba uli ngati chuma chobisika m’munda. Munthu wina atachitumba, amachibisanso. Kenaka mokondwa amakagulitsa zonse zimene ali nazo, nkukagula munda uja. Ndiponso Ufumu wakumwamba uli ngati munthu wamalonda wonka nafunafuna ngale zokongola zamtengowapatali. Atapeza ngale imodzi yamtengowapatali kwambiri, amakagulitsa zonse zimene ali nazo, nkukagula ngale ija. Ufumu wakumwamba ulinso ngati khoka limene anthu amaliponya m’nyanja, ndipo limagwira nsomba za mitundu yonse. Likadzaza, anthu amalikokera ku mtunda. Tsono amakhala pansi, nsomba zabwino nkumaziika m’madengu, zachabe nkumangozitaya. Zidzateronso pa kutha kwa dziko lino lapansi. Angelo adzabwera nadzachotsa anthu ochimwa pakati pa anthu olungama, nkumawaponya m’ng’anjo ya moto. Kumeneko adzalira ndi kukukuta mano.” Yesu adawafunsa anthu aja kuti, “Mwazimvetsa zonsezi kodi?” Iwo adati, “Inde.” Apo Iye adawauza kuti, “Nchifukwa chaketu mphunzitsi aliyense wa Malamulo, amene adaphunzira za Ufumu wakumwamba, ali ngati mwinibanja amene amatulutsa zinthu zatsopano ndi zinthu zakale m’nkhokwe ya chuma chake.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale monga mfumu Solomoni uja, ifenso popempherera anthu onse tipemphe nzeru yozindikira zokoma zimene Mulungu adatikonzera mu Ufumu wake:

 

1.     Ansembe ndi akulu a Mpingo, aonetse anthu onse chifundo cha Mulungu chofuna kuwagawirako moyo wake ndi chikondi chake.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Anthu amene maganizo ao angoima pa zinthu za pansi pano, maso ao atsekuke ndipo mitima yao ikopedwe ndi zinthu zakumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Achinyamata amene Mulungu awaitana ku ntchito yake, avomere kuitanako ndi mtima wonse, pozindikira kukoma kwa Ufumu wa Kumwamba.

Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse tili muno, titsate molimbika malamulo onse a Ambuye‚ podziwa kuti chikondi cha Mulungu ndi chuma cha mtengowapatali chotipatsa moyo wosatha.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

Mulungu Atate athu, mverani mapemphero athuwa ndipo mutikhazikitse m’chikondi chanu, popeza kuti Inu nomwe mudzakhala mphotho yathu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, July 22, 2023

LAMULUNGU LA 16 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 16 PA CHAKA – CHAKA A.

“Inu, Ambuye, ndinu wachifundo ndi woleza mtima.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA LUNTHA; LUNTHA 12: 13, 16 – 19 (Mumakhululukira anthu ochimwa).

 

Pajatu Mulungu ndinu nokha, palibenso wina. Ndinu nokha amene mumasamala anthu onse. Palibenso wina amene muyenera kumufotokozera ngati chigamulo chanu ndi cholungama.

Mphamvu zanu ndiye gwero la chilungamo chanu, choncho popeza kuti ndinu mwini anthu onse, mumawachitira chifundo onse. Anthu amene amakayika kuti ndinu Mulungu Wamphamvuzonse,

mumawaonetsa mphamvu zanu. Anthu amene amadziwa zimenezi nkukuchitanibe chipongwe, mumawachititsa manyazi. Koma ngakhale ndinu mwini mphamvu, mumawaweruza mofatsa. Mumatilamula ndi mtima wachifundo, poti mukangofuna, mumaonetsa mphamvu zanu. Pochita ntchito zanu zoterezi, mudaphunzitsa anthu anu kuti wolungama ayenera kukhala wachifundo, mudadzaza ana anu ndi chikhulupiriro, chifukwa mumakhululukira anthu ochimwa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 86: 05 – 06, 09 – 10, 15 – 16.

 

Inu, Ambuye, ndinu abwino ndipo mumakhululukira anthu anu.

 

Inu Ambuye ndinu abwino, ndipo mumakhululukira anthu anu,

Chikondi chanu chosasinthika ndi chachikulu, kwa onse amene amakupembedzani,

Tcherani khutu, Inu Chauta, kuti mumve pemphero langa,

Mverani kulira kwanga kopemba.

 

Inu, Ambuye, ndinu abwino ndipo mumakhululukira anthu anu.

 

Mitundu yonse ya anthu imene mwailenga idzabwera, idzakuweramirani, Inu Ambuye,

Ndipo idzalemekeza ukulu wanu,

Pakuti Inu ndinu wamkulu, mumachita zinthu zodabwitsa,

Inu nokha ndinu Mulungu.

 

Inu, Ambuye, ndinu abwino ndipo mumakhululukira anthu anu.

 

Koma Inu Ambuye, ndinu Mulungu wachifundo,

Ndinu Mulungu wokoma mtima,

Wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi chosasinthika,

Mundiyang’ane ndipo mundichitire chifundo.

 

Inu, Ambuye, ndinu abwino ndipo mumakhululukira anthu anu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA 08: 26 – 27 (Mzimu Woyera mwiniwake amatipempherera ndi madandaulo osafotokozeka).

 

Abale, momwemonso Mzimu Woyera amatithandiza. Ndife ofooka, osadziwa m’mene tiyenera kupempherera. Nchifukwa chake Mzimu Woyera mwiniwake amatipempherera ndi madandaulo

osafotokozeka. Ndipo Mulungu amene amayang’ana za m’kati mwa mitima ya anthu, amadziwa zimene Mzimu Woyera afuna, pakuti Mzimuyo amapempherera anthu a Mulungu monga momwe Mulungu afunira.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 11: 25.

 

Alleluia, Alleluia – Atate, Mwini kumwamba ndi dziko lapansi, ndikukuyamikani kuti zinthuzi mudaaululira anthu osaphunzira. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 13: 24 – 43 (Zilekeni zikulire pamodzi zonse mpaka nyengo yodula).

 

Yesu adawaphera fanizo linanso. Adati, “Za Ufumu wakumwamba tingazifanizire motere: Munthu wina adaafesa mbeu zabwino m’munda mwake. Koma anthu onse ali m’tulo, mdani wake adabwera, nkufesa namsongole pakati pa tirigu, nachokapo. Tsono pamene mmera udakula nkuyamba kuchita njere, namsongole uja nayenso adayamba kuwoneka. Antchito a mwinimunda uja adadzamufunsa kuti, ‘Bwana, kodi suja mudaafesa mbeu zabwino m’munda mwanu? Nanga bwanji mukuwonekanso namsongole?’ Iye adawayankha kuti, ‘Ndi mdani amene wachita zimenezi.’ Antchito aja adamufunsa kuti, ‘Bwanji tikamzule?’ Koma iye adati, ‘Iyai, mungakazulire kumodzi ndi tirigu pozula namsongoleyo. Zilekeni zikulire pamodzi zonse mpaka nyengo yodula. Pa nthawi imeneyo ndidzauza odula kuti, Yambani mwazula namsongole, mummange m’mitolo kuti mukamtenthe. Kenaka musonkhanitse tirigu ndi kukamthira m’nkhokwe yanga.’” Yesu adawaphera fanizo linanso. Adati, “Ufumu wakumwamba uli ngati njere ya mbeu ya mpiru imene munthu adakaifesa m’munda mwake. Ndi yaing’ono kwambiri mukaiyerekeza ndi njere zina zonse. Komabe mbeu yake ikakula, imapambana zitsamba zina zonse. Imasanduka mtengo, mbalame zamumlengalenga nkumabwera kudzamanga zisa pa nthambi zake.” Yesu adawaphera fanizo linanso. Adati, “Ufumu wakumwamba ulinso ngati chofufumitsira buledi, chimene mai wina adachisanganiza ndi ufa wokwanira miyeso itatu, mpaka mtanda wonse udafufuma.” Zonsezi Yesu adalankhula ndi anthu aja m’mafanizo. Sadalankhule nawo kanthu popanda fanizo. Zidaatero kuti zipherezere zimene mneneri adaanena kuti, “Ndidzalankhula nawo m’mafanizo. Ndidzaulula zimene zinali zobisika chilengedwere dziko lapansi.” Pambuyo pake Yesu adawasiya anthu ambirimbiri aja, nakalowa m’nyumba. Tsono ophunzira ake adadzampempha kuti, “Tatimasulirani fanizo la namsongole wam’munda lija.” Yesu adati, “Wofesa mbeu zabwino uja ndi Mwana wa Munthu. Munda uja ndi dziko lino lapansi. Mbeu zabwino zija ndi anthu ake a Ufumu wakumwamba. Namsongole uja ndi anthu ake a Woipa uja. Mdani wodzafesa namsongole uja ndi Satana. Kudula kuja nkutha kwake kwa dziko lino lapansi, ndipo odula aja ndi angelo. Monga momwe adaazulira namsongole uja nkumutentha pa moto, zidzateronso pa kutha kwa dziko lino lapansi. Mwana wa Munthu adzatuma angelo ake kudzachotsa mu Ufumu wake anthu onse ochimwitsa anzao, ndi ena onse ochita zoipa, nadzawaponya m’ng’anjo ya moto. Kumeneko adzalira ndi kukukuta mano. Tsono anthu olungama adzawala ngati dzuwa mu Ufumu wa Atate ao. Amene ali ndi makutu, amve!”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, Mzimu Woyera amatitsogolera potidziwitsa m’mene tiyenera kupempherera, tiyeni titembenukire kwa Atate athu a Kumwamba poyang’ana zosowa zathu ndi za Mpingo wonse:

 

1.     Atsogoleri a Mpingo aongolere anthu ao mofatsa, moleza mtima ndi mopanda tsankho.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atsogoleri olamulira milandu asenze udindo wao mokhulupirika ndi mosakondera, ndipo adzetse chiyanjano ndi mtendere pakati pa anthu ao.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Akulu oweruza milandu asenze udindo wao mokhulupirika ndi mosakondera, ndipo adzetse chiyanjano ndi mtendere pakati pa anthu.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse a m’Parishi yathu ino tileke makhalidwe a kukwiyirana ndi a kuganizirana zoipa, podziwa kuti tonse ndife ana ake a Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate oleza mtima, titumizireni Mzimu wanu Woyera kuti tilondole mapazi a Mwana wanu pokhala anthu ofatsa ndi achifundo. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/


 

Saturday, July 15, 2023

LAMULUNGU LA 15 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 15 PA CHAKA – CHAKA A.

“Mbeu zogwera pa nthaka yabwino zimabereka.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MNENERI YESAYA; YESAYA 55: 10 – 11 (Mvula imapatsa alimi mbeu ndi chakudya).

 

Chauta akunena kuti: “Mvula ndi chisanu chambee zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko, koma zimathirira nthaka. Zimameretsa ndi kukulitsa zomera, kenaka nkupatsa alimi mbeu ndi chakudya. Ndimonso amachitira mau ochokera m’kamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine popanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo zimene ndidawatumira zidzayenda bwino.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 65: 10 – 14.

 

(Luka 8:8) Mbewu ina idagwera pa nthaka yabwino ndipo idabereka zokolola zambiri.

 

Tsono Inu mumadalitsa dziko lapansi ndi kulithirira,

Ndipo mumalilemekeza kwambiri,

Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi,

Inu mumawapatsa anthu dzinthu.

 

Mbewu ina idagwera pa nthaka yabwino ndipo idabereka zokolola zambiri.

 

Pakuti ndimo m’mene mwalikonzera dzikolo,

Inu mumathirira kwambiri makwawa am’mizere,

Mumasalaza nthumbira zake, mumafewetsa nthaka ndi mvula,

Ndipo mumadalitsa mbeu.

 

Mbewu ina idagwera pa nthaka yabwino ndipo idabereka zokolola zambiri.

 

Pakutha pa chaka mumapereka zokolola zambiri mwa ubwino wanu,

Kulikonse kumene Inu mupita,

Kumapezeka dzinthu dzambiri,

Ngakhale ku mabusa akuchipululu kumamera msipu wambiri.

 

Mbewu ina idagwera pa nthaka yabwino ndipo idabereka zokolola zambiri.

 

Ndipo mapiri amadzazidwa ndi chimwemwe,

Madambo adzaza ndi zoweta,

Zidikha zadzaza ndi dzinthu,

Zonsezo zikufuula ndi kuimbira limodzi mwachimwemwe.

 

Mbewu ina idagwera pa nthaka yabwino ndipo idabereka zokolola zambiri.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA 08: 18 – 23 (Zolengedwa zonse zikudikira molakalaka kuti Mulungu aonetse ana ake poyera).

 

Abale, Ine ndikutsimikiza kuti masautso amene tikuwamva tsopano salingana mpang’ono pomwe ndi ulemerero umene Mulungu adakonza kuti adzatiwonetse m’tsogolo muno. Zolengedwa zonse zikudikira molakalaka kuti Mulungu aonetse ana ake poyera. Pakuti zolengedwazo zidaasanduka zogonjera zopanda pake, osati chifukwa zidaafuna kutero ai, koma chifukwa Mulungu adaagamula choncho. Komabe zili ndi chiyembekezo ichi, chakuti izonso zidzamasulidwa ku ukapolo wa kuwola, ndi kulandirako ufulu ndi ulemerero wa ana a Mulungu. Tikudziwa kuti mpaka tsopano zolengedwa zonse zakhala zikubuula ndi kumva zowawa, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira. Tsonotu si zolengedwa zokhazi zikubuula ai. Koma ngakhale ifenso amene tili ndi mphatso zoyamba za Mzimu Woyera, tikubuula mu mtima, podikira kuti Mulungu atilandire ngati ana ake, ndi kupulumutsa matupi athu omwe.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO –

 

Alleluia, Alleluia – Mbeu ija ndiye mau a Mulungu, Yesu Khristu ndiye wofesa uja; aliyense wopeza mbeu ija adzakhala mwa lye mpaka muyaya. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 13: 01 – 09, 18 – 23 (Munthu wina adaapita kukafesa mbeu).

 

Tsiku lomwelo Yesu adatuluka m’nyumba nakakhala pansi m’mbali mwa nyanja. Anthu ambirimbiri adasonkhana kumene kunali Iye. Tsono Yesu adalowa m’chombo nakhala pansi, anthu onse aja ataima pa munda. Yesu adalankhula nawo zambiri m’mafanizo. Adati, “Munthu wina adaapita kukafesa mbeu. Akufesa choncho, mbeu zina zidagwera m’njira, ndipo mbalame zidabwera nkuzitolatola. Mbeu zina zidagwera pa nthaka yamiyala, pamene panalibe dothi lambiri. Zidamera msanga chifukwa nthakayo inali yosazama. Koma pamene dzuwa lidakwera, zidapserera kenaka zidauma, chifukwa zinali zosazika mizu. Mbeu zina zidagwera pa zitsamba zaminga. Zitsambazo pokula zidalanda chakudya cha mbeu zija. Koma mbeu zina zidagwera pa nthaka yabwino, ndipo zidabereka. Ngala zina zinali ndi njere makumi khumi, zina makumi asanu ndi limodzi, zina makumi atatu.” Tsono Yesu adati, “Amene ali ndi makutu, amve! Tsono inu mumvetse bwino tanthauzo lake la fanizo la munthu wofetsa mbeu lija. Munthu aliyense akamva mau onena za Ufumu wakumwamba, koma osawamvetsa, Woipa uja amabwera nkudzalanda zimene zidafesedwa mumtima mwake. Zimenezi ndiye mbeu zogwera m’njira zija. Mbeu zofesedwa pa nthaka yamiyala zija zikutanthauza munthu amene amamva mau a Mulungu, nthawi yomweyo nkuwalandira ndi chimwemwe. Tsono popeza kuti alibe mizu yozama, amangolimbika kanthawi pang’ono chabe. Mwakuti pakangofika mavuto kapena masautso chifukwa cha mau aja, nthawi yomweyo munthuyo amabwerera m’mbuyo. Mbeu zofesedwa pa zitsamba za minga zija zikutanthauza munthu amene amamva mau a Mulungu. Koma kutanganidwa ndi za pansi pano ndi kukondetsa chuma kumafooketsa mau aja, motero sabereka konse zipatso. Koma mbeu zofesedwa pa nthaka yabwino zija zikutanthauza munthu amene amamva mau a Mulungu nawamvetsa. Munthu wotere amaberekadi zipatso, mwina makumi khumi, mwina makumi asanu ndi limodzi, mwina makumi atatu.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pakuti tidalandira Mzimu Woyera, tingathe kupempherera anthu onse mosakayika, podziwa kuti Mulungu salephera kukwaniritsa malonjezo ake.

 

1.     Atsogoleri olalika Mau a Mulungu, alimbikire kufalitsa Mthenga Wabwino ponseponse.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akatekumeni ndi ena onse amene adakali padera, atsekulire Mulungu mitima yao polandira bwino mau ake.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Makolo a ana atsogolere ana ao m’njira yachikhristu, pakuwaphunzitsa Mau a Mulungu kunyumba.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tomwe amene tasonkhana pano, Mau a Mulungu akhazikike m’mitima mwathu ndi kubereka zipatso zokondweretsa Ambuye.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, tikukuyamikani kuti mau anu ndi opatsa moyo wosatha. Mutithandize kuwasunga ndi kuwagwiritsa ntchito pa moyo wathu wa tsiku ndi tsiku. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, July 8, 2023

LAMULUNGU LA 14 PA CHAKA – CHAKA A

 

LAMULUNGU LA 14 PA CHAKA – CHAKA A.

“Phunzirani kwa Ine: ndine wodzichepetsa mtima.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MNENERI ZEKARIYA: ZEKARIYA 09: 09 – 10 (Onani, mfumu yanu ikudza kwa inu).

 

Chauta akunena kuti: “Kondwani kwambiri, inu anthu a ku Ziyoni. Fuulani kwambiri, inu anthu a ku Yerusalemu. Onani, mfumu yanu ikudza kwa inu. Ikubwera ili yopambana ndi yogonjetsa adani. Ndi yodzichepetsa ndipo yakwera pa bulu, bulu wake kamwana tsono. Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efuremu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu. Uta wankhondo adzauthyola. Mfumu yanu idzachititsa mtendere pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndiponso kuchokera ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku mathero a dziko lapansi.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 145: 01 – 02, 08 – 11, 13 – 14.

 

Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu Mfumu.

 

Ndidzakuyamikani, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga,

Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse mpaka muyaya,

Ndidzakuthokozani tsiku ndi tsiku,

Ndidzatamanda dzina lanu maka muyaya.

 

Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu Mfumu.

 

Chauta ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

Wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi chosasinthika,

Chauta ndi wabwino kwa onse,

Amachitira chifundo zamoyo zonse zimene adazilenga.

 

Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu Mfumu.

 

Zamoyo zonse zidzakuthokozani, Inu Chauta,

Anthu anu onse oyera mtima adzakutamandani,

Adzalankhula za ulemerero wa ufumu wanu,

Adzasimba za mphamvu zanu.

 

Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu Mfumu.

 

Chauta ndi wokhulupirika pa mau ake onse,

Ndi wokoma mtima pa zochita zake zonse,

Chauta amachirikiza onse ogwa m'mavuto,

Amakweza onse otsitsidwa.

 

Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu Mfumu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA: AROMA  08: 09, 11 – 13 (Ngati ndi chithandizo cha Mzimu Woyera mupha zilakolako zanu zathupi, mudzakhala ndi moyo).

 

Abale, inu simulamulidwanso ndi khalidwe lanu lopendekera ku zoipa. Mumalamulidwa ndi Mzimu Woyera, ngati Mzimu wa Mulungu akhaladi mwa inu. Koma ngati munthu aliyense alibe Mzimu wa Khristu, iyeyu sali wake wa Khristu. Ndipo Mzimu wa Mulungu, amene adaukitsa Yesu kwa akufa, akamakhala mwa inu, pamenepo, mwa Mzimu wake yemweyo, Mulungu adzapatsanso moyo matupi anu otha kufawa. Motero abale, tili ndi ngongole, komatu ngongole yake si yakuti tizigonjera khalidwe lathu lokonda zoipa, ndi kumachita chifuniro chake. Pakuti ngati m’moyo mwanu mutsata khalidwelo, mudzafa. Koma ngati ndi chithandizo cha Mzimu Woyera mupha zilakolako zanu zathupi, mudzakhala ndi moyo.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 11: 25.

 

Alleluia, Alleluia – Atate, Mwini kumwamba ndi dziko lapansi, ndikukuyamikani kuti zinthuzi mudaaululira anthu osaphunzira. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA: MATEYO 11: 25 – 30 (Ndine wofatsa ndi wa mtima wodzichepetsa).

 

Pa nthawi imeneyo Yesu adati, “Atate, Mwini kumwamba ndi dziko lapansi, ndikukuyamikani kuti zinthuzi mudaululira anthu osaphunzira, nkubisira anthu anzeru ndi ophunzira. Chabwino Atate, pakuti mudafuna kutero mwa kukoma mtima kwanu. Atate adaika zonse m’manja mwanga. Palibe wina wodziwa Mwana kupatula Atate okha. Palibenso wina wodziwa Atate kupatula Mwana yekha, ndiponso amene Mwanayo akufuna kumuululira. Bwerani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa, ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo. Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wa mtima wodzichepetsa; mukatero mudzapeza mpumulo m’mitima mwanu. Pajatu goli limene ndimakoleka Ine nlosavuta, ndipo katundu amene ndimasenzetsa Ine ngwopepuka.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Pamodzi ndi Yesu Khristu, tiyamike Atate a Kumwamba amene adatiwululira chifundo chake chofuna kupulumutsa anthu onse:

 

1.     Eklezia wa Mulungu, aunikire anthu a mafuko onse powalalikira Mthenga Wabwino, ndipo adzetse mtendere m’mitima ya anthu.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

2.     Akatekumeni ndi anthu onse amene ali padera, mitima yao ikopedwe ndi maphunziro a Yesu ndi kumvera malamulo ake.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

3.     Anthu onse amene ali otopa ndi olemedwa atembenukire kwa Yesu Khristu, pozindikira kuti Iye angapatse anthu mtendere weniweni.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

4.     Ife tonse tili muno tikhale anthu odzetsa mtendere pakati pa anthu powatumikira mofatsa ndi modzichepetsa mtima.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, okoma mtima, mverani mapemphero athuwa, ndipo mutiwongolere ndi Mzimu wanu Woyera kuti tipeze mpumulo weniweni polondola mapazi a Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...