Saturday, June 24, 2023

LAMULUNGU LA 12 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 12 PA CHAKA – CHAKA A.

“Yesu amapulumutsa onse omukhulupirira.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MNENERI YEREMIYA: YEREMIYAYA 20: 10 – 13 (Chauta, ndiye amapulumutsa osauka kwa adani ao).

 

Ndimamva ambiri akunong’ona. Zoopsa zili pa mbali zonse! Amati, “kamnenezeni! Tiyeni tikamneneze!” Amene adaali abwenzi anga amayembekeza kuti ndigwa pansi, amati, “mwina mwake adzatha kunyengedwa, tsono ife tidzamgwira ndi kulipsira pa iyeyo.” Koma Chauta ali nane, ndiye wankhondo woopsa. Nchifukwa chake anthu ondizunza adzakhumudwa, ndithu sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri, chifukwa cha kundilepherako, ndipo manyazi aowo sadzaiwalika konse. Inu Chauta Wamphamvuzonse, amene mumaweruza anthu molungama, amene mumapenya zamumtima, ndikupereka mlandu wanga kwa Inu. Ndikukupemphani kuti mundilipsire adani anga. Imbirani Chauta, mtamandeni Chauta! Ndiye amapulumutsa osauka kwa adani ao.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 69: 08 – 10, 14, 17, 33 – 35.

 

Mundiyankhe Inu Ambuye, chifukwa chikondi chanu nchachikulu.

 

Pakuti ndanyozedwa, nkhope yanga yagwidwa ndi manyazi chifukwa cha Inu,

Kwa abale anga ndasanduka mlendo, kwa ana a mai wanga ndili ngati wakudza,

Changu chochitira Nyumba yanu chandiphetsa,

Chipongwe cha anthu okunyozani chandigwera.

 

Mundiyankhe Inu Ambuye, chifukwa chikondi chanu nchachikulu.

 

Koma ine ndimapemphera kwa Inu Chauta,

Mundiyankhe pa nthawi yabwino, Inu Mulungu,

Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika,

Ndi chithandizo chanu chokhulupirika. mundiyankhe, Inu Chauta,

Pakuti chikondi chanu chosasinthika nchabwino.

Munditchere khutu, chifukwa cha chifundo chanu chachikulu.

 

Mundiyankhe Inu Ambuye, chifukwa chikondi chanu nchachikulu.

 

Ozunzika aone zimenezo ndipo asangalale,

Inu amene mumafunafuna Mulungu, mulimbenso mtima

Paja Chauta amamvera anthu osowa,

Sanyoza anthu ake omangidwa ndi unyolo.

Kumwamba ndi pansi pano,

Nyanja ndi zonse zoyenda m’menemo zitamande Iye.

 

Mundiyankhe Inu Ambuye, chifukwa chikondi chanu nchachikulu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA: AROMA  05: 12 – 15 (Sitingafananitse mphatso yaulere ya Mulungu ndi kuchimwa kwa Adamu ai).

 

Abale, uchimo udalowa m’dziko lapansi chifukwa cha munthu mmodzi, ndipo uchimowo udadzetsa imfa. Motero imfa idafalikira kwa anthu onse, popeza kuti onse adachimwa. Uchimo udaalipo pa dziko lapansi Mulungu asanapereke Malamulo. Koma pamene palibe malamulo, machimo a munthu sawerengedwa ai. Komabe kuyambira nthawi ya Adamu kufikira nthawi ya Mose, imfa inali ndi ulamuliro pa anthu onse. Inali ndi ulamuliro ngakhalenso pa amene kuchimwa kwao kunkasiyana ndi kuchimwa kwa Adamu, amene adaphwanya lamulo la Mulungu. Adamuyo amafanizira Iye uja amene Mulungu adaati adzabwerayu. Koma sitingafananitse mphatso yaulere ya Mulungu ndi kuchimwa kwa Adamu ai. Pajatu anthu ambiri adafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, koma kukoma mtima kwa Mulungu, ndiponso mphatso yake yaulere, zidaposa ndithu, chifukwa zidabweretsera anthu ambiri madalitso ochuluka. Mphatso imene Mulungu adaperekayo ndiye munthu mmodzi uja, Yesu Khristu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 15: 26b, 27a.

 

Alleluia, Alleluia – Mzimu wa choona akadzabwera, adzandichitira umboni. Inunso

mudzandichitira umboni. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA: MATEYO 10:  26 – 33 (Musamawaopa amene amapha thupi).

 

Ophunzira khumi ndi awiri amenewa Yesu adawatuma ndi mau akuti: “inu musamaopa anthu. Kanthu kalikonse kovundikirika kadzaululika, ndipo kalikonse kobisika kadzadziwika. Zimene ndikukuuzirani m’chibisibisi, inu mukazilankhulire poyera, ndipo zimene mukuzimvera m’manong’onong’o, inu mukazilalikire pa madenga. Musamawaopa amene amapha thupi, koma Mzimu sangathe kuupha. Makamaka muziwopa amene angathe kuwononga thupi ndi mzimu womwe m’Gehena. Suja amagulitsa atimba awiri kandalama kamodzi? Komabe palibe ndi m’modzi yemwe amene angagwe pansi, Atate anu osadziwa. Inuyotu ngakhale tsitsi lomwe la kumutu kwanu adaliwerenga lonse. Choncho musati muziopa ai. Ndinu a mtengo woposa atimba ambiri. Aliyense wondivomereza pamaso pa anthu, Inenso ndidzamuvomera pamaso pa Atate anga amene ali kumwamba. Koma aliyense wondikana pamaso pa anthu kuti Ine sandidziwa, Inenso ndidzamkana pamaso pa Atate anga amene ali kumwamba kuti sindimdziwa.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, lero popempherera anthu onse, tipereke kwa Mulungu Atate athu madandaulo ao, mavuto ndi nkhawa zao zonse:

 

1.     Atsogoleri a Mpingo agwire ntchito yao mosakayika ndi mopanda mantha, adziwe kuteteza akhristu ao ndi kuwalimbitsa mtima.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akhristu amene akuzunzidwa chifukwa cha chikhulupiriro chao asataye mtima, koma aonetse chamuna pomchitira Yesu Khristu umboni.

Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu odwala ndi ena onse amene akuyesedwa ndi zoipa, nawonso alimbe mtima pakuphatikizana ndi Yesu Khristu m’mavuto ao.

Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse osonkhana pano, tileke mtima wamantha: mau athu, mayendedwe athu ndi ntchito zathu zisonyeze kuti ndifedi anthu ake a Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, popereka kwa Inu mapemphero athuwa, tikuyamika kukoma mtima kwanu, chifukwa mwatipatsa mphamvu zogonjetsera zoipa zili zonse mwa Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, June 17, 2023

LAMULUNGU LA 11 PA CHAKA – CHAKA A

 

 
LAMULUNGU LA 11 PA CHAKA – CHAKA A.

“Ambuye atituma kwa anzathu.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA EKSODO: EKSODO 19: 02 – 06 (Ndipo inu mudzakhala anthu onditumikira Ine ngati ansembe, ndiponso ngati mtundu woyera).

 

Aisraele atachoka ku Refidimu adakafika ku chipululu cha Sinai, kumene adamangako mahema pafupi ndi phirilo. Mose adakwera phiri kukakumana ndi Mulungu, ndipo Mulungu adamuitana

M’phirimo namuuza kuti, “Uuze zidzukulu za Yakobo, ndiye kuti mtundu wonse wa Aisraele kuti, ‘Mudaona zimene ndidawachita Aejipito, ndiponso muja ndidakunyamulani monga m’mene mphungu imanyamulira ana ake pa mapiko ake, ndipo ndidakufikitsani kwa Ine. Tsono mukamandimvera ndi kusunga chipangano changa, mudzakhala anthu anga pakati pa makamu onse, pakuti dziko lonse lapansi ndi langa. Ndipo inu mudzakhala anthu onditumikira Ine

ngati ansembe, ndiponso ngati mtundu woyera.’ Tsono ukawauze mau amenewa Aisraele.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 100: 02 – 03, 05.

 

Ndife anthu ake, nkhosa za busa lake.

 

Fuulani kwa Chauta ndi chimwemwe, inu maiko onse,

Tumikirani Chauta mosangalala,

Bwerani pamaso pake mukuimba mokondwa.

 

Ndife anthu ake, nkhosa za busa lake.

 

Dziwani kuti Chauta ndiye Mulungu,

Ndiye amene adapanga ife, ndipo ifeyo ndife ake,

Ndife anthu ake, nkhosa za busa lake.

 

Ndife anthu ake, nkhosa za busa lake.

 

Paja Iye ndi wabwino,

Chikondi chake nchamuyaya,

Kukhulupirika kwake nkosatha.

 

Ndife anthu ake, nkhosa za busa lake.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA: AROMA 05: 06 – 11 (Tsono popeza kuti imfa ya Khristu idatiyanjanitsa ndi Mulungu, nanji tsono moyo wake, ndiye udzatipulumutsa kwenikweni).

 

Abale, pa nthawi imene Mulungu adaikonzeratu, pamene ife tikusowabe pogwira, Khristu adatifera anthu ochimwafe. Nchapatali kuti munthu afere munthu wina, ngakhale winayo akhale wolungama. Kaya kapena mwina munthu nkulimba mtima mpaka kufera munthu wabwino. Koma Mulungu adatsimikiza kuti amatikonda kwambiri, chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu adatifera. Ndiye popeza kuti tsopano chifukwa cha magazi ake tapezeka kuti ndife olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa pamenepo ku mkwiyo wa Mulungu. Ife tinali adani a Mulungu, koma imfa ya Mwana wake idatiyanjanitsa ndi Iye. Tsono popeza kuti imfa ya Khristu idatiyanjanitsa ndi Mulungu, nanji tsono moyo wake, ndiye udzatipulumutsa kwenikweni. Koma si pokhapo ai, timakondwera mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu, amene atiyanjanitsa ndi Mulungu tsopano.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MARKO 01: 15.

 

Alleluia, Alleluia – Nthawi yakwana, Ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwinowu. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA: MATEYO 09: 36 – 10: 08 (Adasonkhanitsa ophunzira ake khumi ndi awiri aja, nawatuma).

 

Pamene Yesu adaona makamu a anthu, adawamvera chifundo, chifukwa iwo anali olema ndi ovutika ngati nkhosa zopanda mbusa. Tsono adauza ophunzira ale kuti, “Dzinthu ndzochulukadi, achepa ndi antchito. Nchifukwa chake mupemphe Mwini dzinthu kuti atume antchito okatuta dzinthu dzakedzo. Yesu adasonkhanitsa ophunzira ake khumi ndi awiri aja, nawapatsa mphamvu pa mizimu yoipitsa anthu, kuti azitulutsa mwa anthuwo, ndiponso mphamvu zochiritsira nthenda zonse za anthu ndi zofooka zao zam’thupi. Atumwi khumi ndi awiriwo maina ao ndi awa: Woyamba ndi Simoni, wotchedwa Petro, ndipo mbale wake Andrea; Yakobo, mwana wa Zebedeo, ndi mbale wake Yohane; Filipo ndi Bartolomeo; Tomasi ndi Mateyo, wokhometsa msonkho uja; Yakobo, mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo; Simoni, wa m’chipani chandale cha Azelote; ndiponso Yudasi Iskariote, amene pambuyo pake adapereka Yesu kwa adani ake. Anthu khumi ndi awiri amenewa Yesu adawatuma ndi malamulo akuti, “Musapite kwa anthu a mitundu ina kapena kukalowa m’mudzi uliwonse wa Asamariya ai. Koma makamaka mupite kwa Aisraele amene ali ngati nkhosa zotayika. Pitani, muzikalalika kuti, Mulungu ali pafupi kukhazikitsa ufumu wake tsopano. Muzikachiritsa odwala, muzikaukitsa akufa, muzikachotsa khate, muzikatulutsa mizimu yoipa. Mwalandira mwaulere, kaperekeni mwaulere.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, poona kuti dzinthu ndzochuluka, koma antchito ngochepa, tiyeni tipemphe mwini dzinthu kuti atumize antchito okatuta dzinthu dzakezo:

 

1.     Ansembe ndi atsogoleri onse a Mpingo asenze udindo mwachangu ndi mogwirizana, pomamvera chifundo anthu onse amene ali olema ndi ovutika.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

2.     Akhristu onse popemphera adziwe kusinkhasikha za kukoma mtima kwa Mulungu Mpulumutsi wao, kuti iwonso aziwonetsa anzawo mtima womwewo pakuwatumikira mwachifundo.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

3.     Achinyamata apezeke ambiri odzipereka ku ntchito zotumikira Mpingo, pozindikira kuti anthu ambirimbiri ali olema ndi ovutika ngati nkhosa zopanda mbusa.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

4.     Ife tonse tili pano tiyesetse kusenza udindo wathu wachikhristu mosatopa, kuti ana athu ndi abale athu nawonso aphunzire kumanga moyo wao pa chikondi cha Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, popereka kwa Inu mapemphero athuwa, tikutamanda chifundo chanu chofuna kutisonkhanitsa tonse mu Ufumu wanu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Thursday, June 15, 2023

CHAKA CHA MTIMA WOYERA WA YESU – CHAKA A

CHAKA CHA MTIMA WOYERA WA YESU – CHAKA A

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA DEUTERONOMO: DEUTERONOMO 07: 06 – 11 (Mulungu adakukondani ndi kukusankhani inu).

 

Mose adauza anthu ake kuti, “Inu ndinu mtundu wopatulika wa Chauta, Mulungu wanu. Mulungu adasankha inu kuti mukhale anthu ake pakati pa anthu onse a pa dziko lapansi. Mulungu pokukondani ndi kukusankhani inu, sadachitire kuti munkaposa anthu ena onse pakuchuluka. Paja mudaali ochepa ndinuyo pakati pa mitundu yonse. Koma Chauta adakukondani, ndipo adafunadi kusunga malumbiro amene adaachita ndi makolo anu. Nchifukwa chake adakupulumutsani ndi mphamvu zake, nakusandutsani mfulu, kukuchotsani m’dziko laukapolo kwa mfumu ya ku Ejipito ija. Nchifukwa chake mudziwe kuti Chauta, Mulungu wanu, ndiye yekha Mulungu, ndipo ndi Mulungu wokhulupirika. Iye adzasungadi chipangano chake ndipo adzaonetsa chifundo chake chosasinthika kwa anthu a mibadwo zikwi zambirimbiri amene amakonda Iye namamvera malamulo ake. Koma onse amene amadana ndi Mulungu, adzawabwezera pakuwaononga. Sadzamlekerera munthu wodana naye, koma adzamubwezera pakumlanga ndithu. Motero, muzimvera mosamala malangizo ndi malamulo amene ndikukulamulani lerowa.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 103: 01 – 04, 06 – 08, 10.

 

Chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omuwopa.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,

Moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera,

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,

Ndipo usaiwale zabwino zake zonse.

 

Chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omuwopa.

 

Ndiye amene amakhululukira machimo ako onse,

Ndi kuchiritsa matenda ako onse,

Ndiye amene amapulumutsa moyo wako ku manda,

Amakuveka chikondi chake chosasinthika,

Ndiponso chifundo chake ngati chisoti chaufumu.

 

Chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omuwopa.

 

Chauta amaweruza mwachilungamo onse opsinjidwa,

Amawachitira zolungama,

Adadziwitsa Mose njira zake,

Adaonetsa Aisraele ntchito zake.

 

Chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omuwopa.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima, ndi wosakwiya msanga,

Ndipo chikondi chake chosasinthika nchachikulu,

Satilanga moyenerera machimo athu,

Satibwezera molingana ndi zolakwa zathu.

 

Chikondi cha Chauta nchamuyaya kwa anthu omuwopa.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA YOHANE WOYERA: 01 YOHANE 04: 07 – 16 (Mulungu adaonetsa chikondi chake kwa ife).

 

Inu okondedwa, tizikondana, pakuti chikondi nchochokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi, ndi mwana wa Mulungu, ndipo amadziwa Mulungu. Koma munthu wopanda chikondi sadziwa Mulungu, pakuti Mulungu ndiye chikondi chimene. Mulungu adaonetsa chikondi chake kwa ife motere: Iye nkukhala ndi Mwana mmodzi yekha, koma adamtuma pansi pano, kuti mwa Iye tikhale ndi moyo. Chikondi chenicheni ndi ichi, chakuti sindife tidakonda Mulungu ai, koma Mulungu ndiye adatikonda ifeyo, natuma Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu. Inu okondedwa, ngati Mulungu adatikonda kwambiri chotere, ifenso tiyenera kumakondana. Palibe munthu amene adaona Mulungu. Koma tikamakondana, Mulungu amakhala mwa ife, ndipo chikondi chake chafika pake penipeni mwa ife. Tikudziwa kuti limakhala mwa Mulungu, ndipo Iyenso amakhala mwa ife, chifukwa adatipatsa Mzimu wake Woyera. Ife taona, ndipo tikuchita umboni, kuti Atate adatuma Mwana wake kuti adzakhale Mpulumutsi wa anthu a pa dziko lonse lapansi. Aliyense wovomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye, ndipo iye amakhala mwa Mulungu. Motero ife timadziwa ndipo timakhulupirira ndithu kuti Mulungu amatikonda. Mulungu ndiye chikondi, ndipo munthu wokhala ndi moyo wachikondi, amakhala mwa Mulungu, Mulungunso amakhala mwa iye.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 11: 29ab.

 

Alleluia, Alleluia – Senzani goli langa, ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wa mtima wodzichepetsa. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA YOHANE WOYERA: YOHANE 19: 31 – 37 (Koma mmodzi mwa asilikali aja adamubaya m’nthiti mwake ndi mkondo, ndipo nthawi yomweyo mudatuluka magazi ndi madzi).

 

Linali tsiku lokonzekera chikondwerero cha Pasaka. Akulu a Ayuda sadafune kuti mitemboyo ikhalebe pa mtanda pa tsiku la Sabata, chifukwa Lasabata limenelo linali lalikulu. Nchifukwa chake adakapempha Pilato kuti alamule kuti akathyole miyendo ya anthu opachikidwa aja, nkuwachotsa. Tsono asilikali adabwera, nathyola miyendo ya mmodzi mwa awiri aja amene adaapachikidwa pamodzi ndi Yesu. Adateronso ndi mnzake uja. Koma pamene adafika pa Yesu, poona kuti wafa kale, sadathyole miyendo yake. Koma mmodzi mwa asilikali aja adamubaya m'nthiti mwake ndi mkondo, ndipo nthawi yomweyo mudatuluka magazi ndi madzi. Amene adaona zimenezi ndiye akuzichitira umboni, kuti inunso mukhulupirire. Umboni wakewo ngwoona, ndipo mwiniwakeyo akudziwa kuti zimene akunena nzoona. Izi zidaatero kuti zipherezere zimene Malembo adanena kuti, “Sadzathyola fupa lake ndi limodzi lomwe.” Ndipo penanso Malembo akuti, “Anthu azidzamuyang’ana amene iwo adamubaya.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Pokhala a mtima umodzi ndi Yesu Khristu, tiyeni tipempherere anthu onse, poyamika Atate athu a Kumwamba:

 

1.     Ansembe ndi akulu onse a Mpingo, atsogolere anthu ao m’njira ya chikondi, powaphunzitsa za kukoma mtima kwa Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Asistere, Abrazala ndi ena onse okhala m’zipani za Mulungu, ayende molimbika m’njira ya ungwiro polondola mapazi a Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Akhristu ofooka ndi otayika adzidzimuke m’mitima mwao ndi kubwerera kwa Mulungu, pozindikira chifundo chake chofuna kuwapulumutsa.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tomwe tili muno tikhale ophunzira enieni a Yesu Khristu pomayesetsa kutengera maganizo ake ndi makhalidwe ake.
Tikupemphani, mutivomereze.

Atate, tikupereka kwa Inu mapemphero athuwa pamodzi ndi zosowa za anthu onse, poyamika chifundo chanu chosasinthika. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

 

Saturday, June 10, 2023

CHAKA CHA UKARISTIA [CORPUS CHRISTI] – CHAKA A

 

CHAKA CHA UKARISTIA [CORPUS CHRISTI] – CHAKA A

“Ine ndine chakudya chopatsa moyo.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA DEUTERONOMO; DEUTERONOMO 08: 02 – 03, 14b – 16a (Adakupatsani mana oti mudye, chakudya chimene

makolo anu anali asanadyepo).

 

Mose adauza anthu ake kuti, “Kumbukirani m’mene Chauta, Mulungu wanu, adakutsogolerani m’chipululu, pa ulendo wa pa zaka zonse makumi anai zapitazi. Adakuvutani nakuyesani ndi zowawa, kuti adziwe zimene zinali m’mitima mwanu, ndipo kuti aone ngati mudzamvera malamulo kapena ai. Adakutsitsani pokukhalitsani ndi njala, komanso adakupatsani mana kuti mudye. Inu ndi makolo anu simunadyepo ndi kale lonse chakudya chimenechi. Adachita zimenezi kuti akuphunzitseni kuti munthu sakhala ndi moyo ndi chakudya chokha ai, koma ndi mau onse otuluka m’kamwa mwa Mulungu. Pamenepo musadzadyade ndi kuiwala Chauta, Mulungu wanu, amene adakutulutsani ku Ejipito kumene mudali akapolo. Iye adakutsogolerani, mpaka mudabzola chipululu chachikulu ndi choopsa chija, m’mene munali njoka za ululu woopsa ndi zinkhanira. Adakupatsani mana oti mudye, chakudya chimene makolo anu anali asanadyepo.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 147: 12 – 15, 19 – 20.

 

Tamanda Mulungu, iwe Yerusalemu

 

Tamanda Chauta, iwe Yerusalemu,

Tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,

Paja amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako,

Amadalitsa anthu amene ali mwa iwe.

 

Tamanda Mulungu, iwe Yerusalemu

 

Amadzetsa mtendere m’malire a dziko lako,

Amakudyetsa pokupatsa ufa wa tirigu wosalala,

Akapereka lamulo pa dziko lapansi,

Mau ake amayenda mwaliwiro.

 

Tamanda Mulungu, iwe Yerusalemu

 

Amadziwitsa Yakobe mau ake,

Amaphunzitsa Israele malamulo ake ndi malangizo ake,

Sadachitepo zimenezi ndi mtundu wina uliwonse wa anthu,

Iwo sadziwa malangizo ake.

 

Tamanda Mulungu, iwe Yerusalemu

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORITO: 01 AKORIRTO  10: 16 – 17 (Popeza kuti mkate ndi umodzi wokha, ife tonse, ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi).

 

Abale, nanga chikho chimene timachidalitsa mothokoza Mulungu, kodi suja timaphatikizana ndi magazi a Khristu tikamweramo? Nanga mkate umene timaunyema, kodi suja timaphatikizana ndi thupi la Khristu tikaudya? Popeza kuti mkate ndi umodzi wokha, ife tonse, ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, chifukwa tonse timagawana mkate umodzi womwewo.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 06: 51.

 

Alleluia, Alleluia – Ine ndine chakudya chamoyo chimene chidatsika kuchokera Kumwamba. Munthu wodya chakudyachi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

Nyimbo ya Ukaristia (Sequence)

 

O SIYONI UYAMIKE

Mbusa wabwino, Buledi weniweni,

Mbuye Yesu, mutichitire chisoni.

Muteteze, nkulowetsa Nkhosa zanufe kumwamba.

 

1.     Siyoni, uyamike,
Mpulumutsi wako, Mbuye,
Mfumu ndinso Mbusa wako.

2.     Sudzafika kuimbira,
Mlungu wako mokwanira,
Ukwezetu mawu ako.

3.     Nkofunika ndithu lero,
Kutama Buledi wamoyo,
Ngwopatsa moyo womwewo.

4.     Tidziwa mosapeneka,
Kuti Yesu anapatsa,
Bulediyu kwa apositoli.

5.     Tsono tisankhule nyimbo,
Zokoma kwambiri lero,
Ndi kuimba mwachimwemwe.

6.     Misa itibweretsera,
Tsiku lomwe la kupanga,
Phwando loyerayerali.

7.     Ndi Pasaka yatsopano,
Ya Mfumu yatsopanonso,
Miyambo yakale yatha.

8.     Zalero zibadiritsa,
Zakale, monga kuyera,
M’mawa kuchotsatu mdima.

9.     Yesu anatilamula,
Kubwereza zomwe zija,
Anazichita tsikuli.

10.  Pomvera Yesu ifenso,
Tisandutsa buledi m’vinyo,
Pa nsembe yopulumutsa.

11.  Buledi asanduka Thupi,
Ndiponso vinyo Magazi,
A Khristu, Ambuye athu.

12.  Sitimvetsa, sitiona,
Koma ndithu tizimvera,
Zozizwitsa zimenezi.

13.  Buledi ndinso vinyo ali,
Chizindikiro chophimba,
Zazikulu zobisika.

14.  Tidya Thupi la Ambuye,
Ndi kumwa Magazi ake:
Akhala muziwirizi.

15.  Aliyense amlandira,
Wathunthudi, wosasweka,
Ndi wosagawika konse.

16.  Nayo Buledi wa anjelo,
Ngwa alendofe tsopano,
Manna wotipatsa nyonga.

17.  Mulungu wamphamvuzonse,
Ndiponso wodziwa zonse,
Inu mutidyetsa pano.

18.  Mutidyetsenso Kumwamba,
M’phwando la anthu oyera.
Amen. Amen. Aleluya.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA YOHANE WOYERA; YOHANE 06: 51 – 58 (Thupi langa ndi chakudya chenicheni, ndipo magazi anga ndi chakumwa chenicheni).

 

Yesu adati kwa makamu a Ayuda, “Ine ndine chakudya chamoyo chimene chidatsika kuchokera kumwamba. Munthu wodya chakudyachi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya. Ndipo chakudyacho chimene Ine ndidzapereka ndi thupi langa, limene ndikupereka kuti anthu a pa dziko lapansi akhale ndi moyo.” Pamenepo Ayuda adayamba kukangana okhaokha, ankati, “Munthu ameneyu angathe bwanji kutipatsa thupi lake kuti tidye?” Yesu adati, “Ndithu ndikunenetsa kuti ngati simudya thupi la Mwana wa Munthu ndi kumwa magazi ake, simungakhale ndi moyo mwa inu. Aliyense wodya thupi langa ndi kumwa magazi anga, ali ndi moyo wosatha, ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. Pakuti thupi ndi chakudya chenicheni, ndipo magazi anga ndi chakumwa chenicheni. Aliyense wodya thupi langa ndi kumwa magazi anga amakhala mwa Ine, ndipo Ine ndimakhala mwa iyeyo. Monga Atate amoyo adandituma, ndipo Ine ndili ndi moyo pokhala mwa Iwo, momwemonso aliyense wodya Ine, adzakhala ndi moyo pokhala mwa Ine. Chakudya chimene chidatsika kuchokera kumwamba nchimenechi. Nchosiyana ndi mana aja amene makolo anu ankadya koma nkufabe. Wodya chakudya chimenechi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, Ukaristia ukusonyeza umodzi wathu ndi Yesu Khristu. Tiyeni pamodzi ndi Iyeyo tiyamike Mulungu popempherera anthu onse:

 

 

1.     Akhristu onse apeze m’sakramenti la Ukaristia gwero la moyo wa ungwiro, ndinso chifundo chokondana mwaubale, polumikizana ndi Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

2.     Makolo achikhristu adziwe kuphunzitsa bwino ana ao za Ambuye Yesu, ndipo autse m’mitima mwao chifundo chofunitsa kulandira Ukaristia.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

3.     Ansembe onse asenze udindo wao mokhulupirika ndi mwachangu, aziwonetsa chitsanzo chabwino kwa anthu ao powatsogolera m’njira ya ungwiro.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

4.     Ife tomwe tili muno tikhale amodzi ndi okondana mwaubale pakulandira Ukaristia kawirikawiri.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate a chifundo, tikukuthokozani chifukwa chotiitana tonse ku phwando lanu, Inu amene mufuna kutisonkhanitsa tonse mu Ufumu wanu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

LAMULUNGU LA 3 MU NYENGO YA ADVENT—A

LAMULUNGU LA 3 MU NYENGO YA ADVENT—A [Gaudete Sunday] “Bwerani Ambuye, mudzatipulumutse.”   MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA M’N...