Saturday, May 27, 2023

CHAKA CHA PENTEKOSITE – CHAKA A

                                            CHAKA CHA PENTEKOSITE – CHAKA A.

“Adawauzira Mpweya wopatsa moyo.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA NTCHITO ZA ATUMWI; NTCHITO 02: 01 – 11 (Onse aja adadzazidwa ndi Mzimu Woyera, ndipo adayamba kulankhula).

 

Pamene tsiku la chikondwerero cha Pentekoste lidafika, iwo onse anali pamodzi m'nyumba imodzi. Mwadzidzidzi kudamveka kuchokera kumwamba mkokomo ngati wa mphepo yaukali, nudzaza nyumba yonse imene ankakhalamo. Ndipo adaona ngati timalawi ta moto tooneka ngati malilime tikugawikana nkukhala pa iwo, aliyense kakekake. Onse aja adadzazidwa ndi Mzimu Woyera, ndipo adayamba kulankhula zilankhulo zachilendo, monga Mzimuyo ankawalankhulitsira. Tsono, m’Yerusalemu muja munali Ayuda ena, anthu okonda Mulungu, ochokera ku mayiko onse a pa dziko lapansi. Pamene mkokomo uja udamveka, anthu ambirimbiri adasonkhana. Onse adadodoma, chifukwa aliyense mwa iwo ankawamva akulankhula chilankhulo chake. Adadabwa, nathedwa nzeru ndipo adati, “Kodi onse akulankhulawa, si Agalileya? Nanga bwanji aliyense mwa ife akuwamva akulankhula chilankhulo chakwao? Ena mwa ife ndi Aparti ndi Amedi ndi Aelami, ena ndi okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya, ku Frijiya ndi ku Pamfiliya, ku Ejipito, ndi ku madera a Libiya kufupi ndi ku Kirene, ena ndi alendo ochokera ku Roma, ndiye kuti Ayuda ndi ena otsata za Chiyuda. Enanso ndi Akrete ndi Aarabu, komabe tonse tikuwamva anthuwa akulankhula m’zilankhulo zathu za ntchito zazikulu za Mulungu.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 104: 01, 24, 29 – 34.

 

Tumizani Mzimu wanu, Ambuye, ndipo muwalitsenso dziko lonse lapansi.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,

Inu Chauta, Mulungu wanga, ndinu aakulu kwambiri,

Inu Chauta ntchito zanu nzambiri,

Ndipo dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

 

Tumizani Mzimu wanu, Ambuye, ndipo muwalitsenso dziko lonse lapansi.

 

Mukazichotsera mpweya, zimafa nkubwerera ku fumbi,

Mukatumiza mpweya wanu zimalengedwa,

Ndipo mumakonzanso maonekedwe a dziko lapansi.

 

Tumizani Mzimu wanu, Ambuye, ndipo muwalitsenso dziko lonse lapansi.

 

Ulemerero wa Chauta ukhalebe mpaka muyaya,

Chauta akondwe nazo ntchito zakezo,

Mapemphero anga amkomere Chauta,

Popeza kuti ndimakondwa mwa Iye.

 

Tumizani Mzimu wanu, Ambuye, ndipo muwalitsenso dziko lonse lapansi.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORITO; 01 AKORITO 12: 03b – 07, 12 – 13 (Tidabatizidwa mwa Mzimu Woyera mmodzimodzi kuti tikhale thupi limodzi).

 

Abale, munthu amene Mzimu Woyera samtsogolera, sanganene kuti, ‘Yesu ndi Ambuye.’

Tsonotu pali mphatso zamitundumitundu, koma wozipereka ndi Mzimu Woyera m’modzimodzi. Pali njira zosiyanasiyana zotumikira, koma Ambuye amene timawatumikira ndi amodzimodzi. Pali mphamvu zosiyanasiyana, koma Mulungu ndi m’modzimodzi amene amagwiritsa ntchito mphamvu zonsezo mwa munthu aliyense. Mzimu Woyera amapatsa munthu aliyense mphatso yakuti yakuti yoti ayigwiritse ntchito yopindulitsa anthu onse. Khristu ali ngati thupi limodzi limene lili ndi ziwalo zambiri. Ngakhale ziwalozo nzambiri, komabe thupilo ndi limodzi lokha. Pajatu ngakhale ndife Ayuda kapena a mitundu ina, akapolo kapena mfulu, tidabatizidwa mwa Mzimu Woyera mmodzimodzi kuti tikhale thupi limodzi.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

Nyimbo ya Pentekoste (Sequence)

(Nyimboyi itha kunenedwa kapena kuyimbidwa)

 


Bwerani Mzimu Woyera

Tumizani kuwala kwanu

Kufumira kumwambako.

 

Bwerani, Tate wa amphawi

Bwerani, wopatsa mphatso

Inu muuni wa mitima.

 

Ndinu Msangalatsi ndithu

Woyendera mitima yathu

Kuti mudzaithunzitsa.

 

Pa ntchito ndinu Mpumulo

Mumatichotsera kutentha

Ndi kutsangula misozi yathu.

 

Ndinu kuwala kokoma

Dzazani mitima yathu

Ya ife anthu okumverani.

 

Mutapanda kudzamthandiza

Munthu sangapeze kanthu

Zonse zidzamuipira.

 

Tsukani zoipa zathu

Dzatsirireni zouma

Chiritsani mabala athu.

 

Dzafewetseni zolimba

Funditsani zozizira

Lungamitsani zokhota.

 

Tipatseni anthu anufe

Okhulupirira Inu

Mphatso zisanu ndi ziwiri.

 

Kometsani makhalidwe athu

Katifikitseni kumwamba

Kukadala nthawi zonse.

Amen.



--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO

 

Alleluia, Alleluia – Bwerani Mzimu Woyera, mudzaze mitima ya anthu okhulupirira ndipo chikondi chanu chikhazikike mwa iwo.  – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA YOHANE WOYERA; YOHANE 20: 19 – 23 (Monga Atate adandituma, Inenso ndikukutumani. Landirani Mzimu Woyera).

 

Madzulo kutada pa tsiku Lamulungu lomwelo, ophunzira aja anali pamodzi. Zitseko zinali zokhoma, chifukwa ankaopa akulu a Ayuda. Tsono Yesu adadza naimirira pakati pao nkunena kuti, “Mtendere ukhale nanu!” Atatero, adawaonetsa manja ake ndi m’thiti mwake, ndipo ophunzira aja adakondwa kwambiri powaona Ambuyewo. Yesu adatinso, “Mtendere ukhale nanu. Monga Atate adandituma, Inenso ndikukutumani.” Pambuyo pake adawauzira m’pweya nati, “Landirani Mzimu Woyera. Anthu amene mudzawakhululukira machimo ao, adzakhululukidwadi, koma amene simudzawakhululukira, sadzakhululukidwa ai.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, lero popempherera anthu onse, tikumbukire kuti Atate athu a Kumwamba salephera kupereka Mzimu Woyera kwa iwo amene amapempha:

 

1.     Eklezia afalitse Mthenga Wabwino ponseponse ndi mphamvu za Mzimu Woyera, ndipo atsogolere anthu m’njira ya ungwiro ndi ya chikondi.
Tumizani, Ambuye, Mzimu wanu Woyera.

 

2.     Akhristu onse ayesetse kukhala a mtima umodzi, Mzimu Woyera alunzitse mitima yao ndi kuwatsogolera m’choona chonse.
Tumizani, Ambuye, Mzimu wanu Woyera.

 

3.     Anthu onse amene adakali padera, Mzimu Woyera awaunikire ndi kuwalondoloza m’njira ya chipulumutso.
Tumizani, Ambuye, Mzimu wanu Woyera.

 

4.     Ife tonse tili muno, titumikire Mpingo wa Mulungu modzipereka, pakugwiritsa ntchito mphatso zomwe tidalandira kwa Mzimu Woyera.
Tumizani, Ambuye, Mzimu wanu Woyera.

 

Mulungu Atate athu, tikuthokozani chifukwa mwa Ubatizo Mzimu Woyera wanu adatisandutsa thupi limodzi limene mutu wake ndi Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, May 20, 2023

CHAKA CHAKUKWERA KWA AMBUYE KUMWAMBA – CHAKA A

CHAKA CHAKUKWERA KWA AMBUYE KUMWAMBA – CHAKA A.

“Inetu ndili nanu masiku onse.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA NTCHITO ZA ATUMWI; NTCHITO 01: 01 – 11 (Yesu adatengedwa kupita kumwamba, iwo akupenya).

 

A Teofilo, m’buku langa loyamba lija ndidakulemberani za zonse zimene Yesu ankachita ndi kuphunzitsa kuyambira pa chiyambi, kufikira tsiku limene adzatengedwa kupita kumwamba. Mwa mphamvu ya Mzimu Woyera, anali atauza atumwi amene adawasankha aja zoti iwowo adzachite. Iye ataphedwa, adadziwonetsa wamoyo kwa iwo mwa njira zambiri zotsimikizika. Adawaonekera nalankhula nawo za ufumu wa Mulungu masiku makumi anai. Pamene anali nawo pamodzi, Yesu adawalamula kuti, “musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate adalonjeza, monga ndidaakuuzani. Pajatu Yohane ankaabatiza ndi madzi, koma pasanapite masiku ambiri, inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.” Tsono atumwi aja atasonkhana, adafunsa Yesu kuti, “Ambuye, kodi ino ndiyo nthawi yoti mukhazikitse ufumu mu Israele?” Iye adati, “si ntchito yanu kuti mudziwe nthawi kapena nyengo pamene zidzachitike zimene Atate adakhazikitsa mwa mphamvu yao. Koma mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera akadzabwera pa inu, ndipo mudzakhala mboni zanga ku Yerusalemu, ku Yudeya ndi ku Samariya konse, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.” Atanena zimenezi, Yesu adatengedwa kupita kumwamba, iwo akupenya. Ndipo mtambo udamlandira nkumubisa, iwo osamuonanso. M’mene atumwi aja ankayang’anitsitsabe kumwamba, Iye akupita, mwadzidzidzi anthu awiri ovala zoyera adaimirira pambali pao. Anthuwo adawafunsa kuti, “Inu anthu a ku Galileya, mwatani mwangoti chilili pamenepa mukuyang’ana kumwamba? Yesuyu amene watengedwa kuchokera pakati panu kupita kumwamba, adzabwerenso monga momwe mwamuwoneramu akupita kumwambako.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 47: 02 – 03, 06 – 09.

 

Mulungu wakwera, anthu akumfuulira, Chauta wakwera, akumuimbira lipenga.

 

Ombani m’manja inu anthu a mitundu yonse,

Fulani kwa Mulungu poimba nyimbo zachimwemwe,

Paja Chauta Wopambanazonse ndi woopsa,

Ndiye mfumu yaikulu pa dziko lonse lapansi.

 

Mulungu wakwera, anthu akumfuulira, Chauta wakwera, akumuimbira lipenga.

 

Mulungu wakwera, anthu akumfuulira,

Chauta wakwera, akumuimbira lipenga,

Imbani nyimbo zotamanda Mulungu,

Imbani nyimbo zotamanda mfumu yathu.

 

Mulungu wakwera, anthu akumfuulira, Chauta wakwera, akumuimbira lipenga.

 

Mulungu ndiye Mfumu ya dziko lonse lapansi,

Imbani mwaluso nyimbo zotamanda,

Mulungu amalamulira mitundu ya anthu,

Mulungu amakhala pa mpando wake woyera waufumu.

 

Mulungu wakwera, anthu akumfuulira, Chauta wakwera, akumuimbira lipenga.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AEFESO: AEFESO 01: 17 – 23 (Iye wakhala kudzanja lamanja la Atate).

 

Abale, ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate aulemerero, akuninkheni Mzimu Woyera, amene adzakupatsani nzeru, nadzaulula Mulungu kwa inu, kuti mumdziwe kwenikweni. Ndimapemphera kuti Mzimu Woyerayo akuunikireni m’mitima mwanu, kuti mudziwe zimene mungathe kuyembekezera kwa Mulungu amene adakuitanani. Ndimafunanso kuti mudziwe kukula kwake kwa ulemerero ndi madalitso amene Mulungu amalonjeza kupatsa anthu ake. Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu yake yopitirira muyeso imene ikugwira ntchito mwa ife omkhulupirira. Mphamvuyi ndi yomwe ija yolimba koposa, imene Mulungu adaigwiritsa ntchito pamene adaukitsa Khristu kwa akufa, namkhazika ku dzanja la manja m’dziko la kumwamba. Adamkhazika pamwamba pa mafumu onse, aulamuliro onse ndi akuluakulu onse a kumwamba, ndiponso pamwamba pa maina ena onse amene anthu angawatchule nthawi ino kapenanso nthawi ilikudza. Mulungu adagonjetsa zonse kuti zikhale pansi pa mapazi a Khristu, ndipo adamkhazika pamwamba pa zonse kuti akhale mutu wa mpingo. Mpingowu ndi thupi la Khristu, ndipo ndi wodzazidwa ndi Khristuyo amene amadzaza zinthu zonse kotheratu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 28: 19a, 20b.

 

Alleluia, Alleluia – Pitani kwa anthu a mitundu yonse, mukawasandutse ophunzira anga. Ndipo ineyo ndili nanu masiku onse, mpaka kutha kwa dziko lino lapansi.  – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 28: 16 – 20 (Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi pansi pano).

 

Ophunzira khumi ndi mmodzi aja adapita ku Galileya kuphiri kumene Yesu adaapangana nawo kuti akakumane. Pamene adamuwona, adampembedza, koma ena ankakayika. Yesu adadza pafupi nawauza kuti, “mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine kumwamba ndi pansi pano. Nchifukwa chake inu pitani kwa anthu a mitundu yonse, mukawasandutse ophunzira anga. Muzikawabatiza m’dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera. Mudzikawaphunzitsa kusunga zonse zimene Ine ndidakulamulani. Ndipo Ineyo ndili nanu masiku onse, mpaka kutha kwa dziko lino lapansi.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, popeza Yesu Khristu ali nafe masiku onse, tiyeni, pamodzi naye tipemphe Atate athu a Kumwamba kuti Ufumu wao udze:

 

1.     Akhristu onse alimbikire kufalitsa Mthenga Wabwino pakati pa anzao, pokhala mboni zenizeni za Yesu Khristu.
Atate, Ufumu wanu udze!

 

2.     Achinyamata apezeke ambiri odzipereka ku ntchito yokalalikira mau a Mulungu ku maiko akunja.
Atate, Ufumu wanu udze!

 

3.     Anthu odwala ndi onse amene ali m’mavuto, alimbe mtima ndi kusangalala, pozindikira kuti Yesu ali nawo pafupi nthawi zonse.
Atate, Ufumu wanu udze!

4.     Ife tonse tili muno, mau athu ndi ntchito zathu zisonyeze kuti Yesu Khristu alikukhazikadi ufumu wake leroli ndi masiku onse.
Atate, Ufumu wanu udze!

 

Mulungu Atate athu, muunikire anthu onse ndi Mzimu wanu Woyera kuti azindikire ntchito zodabwitsa zimene mulikuchita ponseponse, kudzera mwa Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, May 13, 2023

LAMULUNGU LA 06 LA PASAKA – CHAKA A.

LAMULUNGU LA 06 LA PASAKA – CHAKA A.

“Adzakupatsani Nkhoswe ina.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA NTCHITO ZA ATUMWI; NTCHITO 08: 05 – 08, 14 – 17 (Adawasanjika manja, ndipo adalandira Mzimu Woyera).

 

Filipo adatsikira ku mzinda wa ku Samariya, namalalikira anthu akumeneko za Khristu, mpulumutsi wolonjezedwa uja. Makamu a anthu ndi mtima umodzi ankatchera makutu ku zimene Filipo ankanena. Onse ankamvetsera mau ake nkumaona zozizwitsa zimene iye ankachita. Pakuti mizimu yonyansa inkatuluka mwa anthu ambiri amene anali atagwidwa nayo, nimafuula kwambiri. Ndipo ambiri amene anali akufa ziwalo kapena opunduka, ankachira. Choncho munali chimwemwe chachikulu mumzinda muja. Pamene atumwi okhala ku Yerusalemu adamva kuti anthu aku Samariya alandira mau a Mulungu, adatumako Petro ndi Yohane. Iwowo atafika, adayamba kupempherera okhulupirira aja kuti alandire Mzimu Woyera. Nthawiyo nkuti Mzimu Woyera asanafike pa wina aliyense mwa iwo. Onsewo anali atangobatizidwa m’dzina la Ambuye Yesu. Tsono Petro ndi Yohane adawasanjika manja, ndipo adalandira Mzimu Woyera.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 66: 01 – 07, 16, 20.

 

Tamandani Mulungu ndi chimwemwe mokweza mau, inu anthu onse a pa dziko lapansi.

 

Tamandani Mulungu ndi chimwemwe mokweza mau,

Inu anthu onse a pa dziko lapansi,

Imbani nyimbo zoyamika dzina lake laulemerero,

Muuzeni Mulungu kuti, ntchito zanu nzodabwitsa kwambiri.

 

Tamandani Mulungu ndi chimwemwe mokweza mau, inu anthu onse a pa dziko lapansi.

 

Anthu onse a pa dziko lapansi amakupembedzani,

Amaimba nyimbo zotamanda Inu,

Amaimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita,

Ntchito zake nzodabwitsa pakati pa anthu.

 

Tamandani Mulungu ndi chimwemwe mokweza mau, inu anthu onse a pa dziko lapansi.

 

Adasandutsa nyanja kuti ikhale nthaka youma,

Anthu adaoloka mtsinje uja poyenda pansi,

Nchifukwa timukondwerere Iye,

Iye amalamula ndi mphamvu zake mpaka muyaya.

 

Tamandani Mulungu ndi chimwemwe mokweza mau, inu anthu onse a pa dziko lapansi.

 

Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita,

Koma zoona Mulungu wandimvera,

Wasamala mau a pemphero langa.

Mulungu atamandike chifukwa sadakane pemphero langa,

Sadachotse chikondi chake chosasinthika kwa Ine.

 

Tamandani Mulungu ndi chimwemwe mokweza mau, inu anthu onse a pa dziko lapansi.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PETRO WOYERA: 01 PETRO 03: 15 – 18 (Pa za thupi adaphedwa, koma pa za mzimu adapatsidwa moyo).

 

Abale, muzilemekeza Khristu m’mitima mwanu ngati Mbuye wanu. Khalani okonzeka nthawi iliyonse kuwayankha mofatsa ndi mwaulemu anthu okufunsani za zimene mumayembekeza. Khalani ndi mtima wopanda kanthu koutsata, kotero kuti anthu ena akamasinjirira mayendedwe anu abwino pamene mukutsata Khristu, achite manyazi ndi chipongwe chao. Nkwabwino kumva zowawa chifukwa chochita zabwino, ngati Mulungu wafuna choncho, koposa kumva zowawa chifukwa chochita zoipa. Paja nayenso Khristu adafera machimo a anthu kamodzi kokha; munthu wolungama kufa m’malo mwa anthu ochimwafe, kuti atifikitse kwa Mulungu. Pa za thupi adaphedwa, koma pa za mzimu adapatsidwa moyo.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 14: 23.

 

Alleluia, Alleluia – Yesu anati, “Ngati munthu andikonda, adzatsata zimene ndanena Ine, Atate anga adzamkonda, ndipo Ife tidzabwera nkukhazikika mwa iye.”  – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA; YOHANE 14: 15 – 21 (Ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina).

 

Yesu adauza ophunzira ake kuti, “Ngati mundikonda, mudzitsata malamulo anga. Pamenepo ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthawi zonse. Nkhosweyo ndi Mzimu wodziwitsa zoona. Anthu ongokonda zapansipano sangathe kumlandira ai, chifukwa samuwona kapena kumdziwa. Koma inu mumamdziwa, chifukwa amakhala ndi inu, ndipo adzakhala mwa inu. Sindidzakusiyani nokha kuti mukhale ana amasiye. Ndidzabweranso kwa inu. Kwangotsala kanthawi pang’ono, ndipo anthu ongokonda zapansipano sadzandiwonanso, koma inu mudzandiwona. Popeza kuti Ine ndili ndi moyo, inunso mudzakhala ndi moyo. Tsiku limenelo mudzadziwa kuti Ine ndimakhala mwa Atate, ndipo inu mumakhala mwa Ine, monga Ine ndimakhala mwa inu. “Munthu amene alandira malamulo anga nawatsata, ndiye amandikonda. Ndipo amene andikonda Ine, Atate anga adzamkonda. Inenso ndidzamkonda munthuyo, ndipo ndidzadziwonetsa kwa Iye.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, popeza kuti Ambuye Yesu alikukhala mwa ife, tingathe kupemphera mogwirizana ndi mosakaika, kuti “Ambuye, tumani Mzimu wanu Woyera!”

 

1.     Eklezia akhale chizindikiro chosonyeza anthu onse chifundo cha Mulungu chofuna kuwapulumutsa.
Ambuye, tumani Mzimu wanu Woyera.

 

2.     Ansembe apezeke ambiri olalikira Mthenga Wabwino ku maiko akunja.
Ambuye, tumani Mzimu wanu Woyera.

 

3.     Anyamata oyembekeza kulandira Sakramenti la Ulimbitso akhale okonzeka kuchitira Yesu Khristu umboni pa moyo wao Wonse.
Ambuye, tumani Mzimu wanu Woyera

 

4.     Ife tonse tili muno, tiyende molimbika m’njira ya ungwiro ndi ya chikondi.
Ambuye, tumani Mzimu wanu Woyera

 

Mulungu Atate athu, mwa chifundo chanu mverani mapemphero athuwa pamodzi ndi madandaulo a anthu onse. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, May 6, 2023

LAMULUNGU LA 05 LA PASAKA – CHAKA A.

“Ine ndine njira yopita kwa Atate."

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA NTCHITO ZA ATUMWI; NTCHITO 06: 01 – 07 (Pakati panupa sankhanipo amuna asanu ndi awiri odzazidwa ndi Mzimu Woyera).

 

Masiku amenewo ophunzira aja ankachulukirachulukira. Koma Ayuda olankhula Chigriki anali ndi dandaulo pa Ayuda olankhula Chiyuda kuti akazi ao amasiye sankasamalidwa bwino pamene zachifundo za tsiku ndi tsiku zinkagawidwa. Tsono atumwi khumi ndi awiri aja adasonkhanitsa gulu lonse la ophunzira, nawauza akuti, “sibwino kuti ife tizisiya kulalika mau a Mulungu nkumayang’anira za chakudya. Nchifukwa chake abale, pakati panupa sankhanipo amuna asanu ndi awiri, a mbiri yabwino, odzadzidwa Mzimu Woyera ndiponso nzeru. Tidzapatsa iwowo ntchitoyi. Koma ife tidzadzipereka ku ntchito ya kupemphera ndi kulalika mau a Mulungu.”  Mau amenewa adakomera gulu lonse lija, motero adasankha Stefano, munthu wodzadzidwa ndi chikhulupiriro ndiponso ndi Mzimu Woyera. Adasankhanso Filipo, Prokoro, Nikanore, Timoni, Parmenasi, ndi Nikolasi wa ku Antiokeya, yemwe kale anali atasiya chikunja kutsata chiyuda. Adawaimiritsa pamaso pa atumwi, ndipo atumwiwo adapemphera nawasanjika manja. Mau a Mulungu ankafalikira ponseponse, ndipo ophunzira ankachulukirachulukira ndithu ku Yerusalemu. Ansembe omwe ambirimbiri ankamvera chikhulupirirocho.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 33: 01 – 05, 18 – 19.

 

Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika chikhale pa ife, chifukwa timakhulupirira Inu.

 

Kondwerani mwa Chauta, inu anthu ake,

Zoonadi ochita zolungama azitamanda,

Tamandani Chauta ndi pangwe,

Muimbireni nyimbo ndi zeze wa nsambo khumi.

 

Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika chikhale pa ife, chifukwa timakhulupirira Inu.

 

Mau a Chauta ndi olungama,

Zochita zake zonse amazichita mokhulupirika,

Iye amachita zolungama ndi kuweruza mosakondera,

Amaonetsa chikondi chosasinthika pa dziko lonse lapansi.

 

Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika chikhale pa ife, chifukwa timakhulupirira Inu.

 

Chauta amayang’ana anthu omumvera,

Ndikudalira chikondi chake chosasinthika,

Iye amachita izi kuti awapulumutse ku imfa,

Ndi kuwasungira moyo anthuwo pa nthawi ya njala.

Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika chikhale pa ife, chifukwa timakhulupirira Inu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PETRO WOYERA: 01 PETRO 02: 04 – 09 (Inu ndinu fuko losankhidwa, ansembe achifumu).

 

Bwerani kwa Iye amene ali mwala wa moyo womwe anthu adaukana, koma Mulungu adausankha kuti ngwamtengowapatali. Inunso mukhale ngati miyala yamoyo yoti Mulungu amangire nyumba yake. M’menemo muzitumikira ngati nsembe zochokera ku mtima, zokomera Mulungu kudzera mwa Yesu Khristu. Paja m’malembo mudalembedwa kuti, “ndasankha mwala wamtengowapatali. Ndikuuika tsopano m’Ziyoni, ngati mwala wapangodya. Wokhulupirira Iye sadzachita manyazi.” Tsono kwa inu okhulupirira, Iye ndi wamtengowapatali. Koma kwa osakhulupirira, ndi monga momwe mau a Mulungu anenera kuti, “mwala womwe amisiri omanga nyumba adaukana, womwewo wasanduka mwala wapangodya.” Mau a Mulungu akutinso, “umenewu ndi mwala wokhumudwitsa anthu, ndi nthathwe lowagwetsa.” Amakhumudwa popeza kuti amakana kumvera mau a Mulungu, ndipo anali oyeneradi kuti adzaone zotere. Komatu inu ndinu fuko losankhidwa, ansembe achifumu, mtundu wopatulika, anthu akeake a Mulungu. Adakusankhani kuti mukalalike ntchito zamphamvu za Iye amene adakuitanani kuti mutuluke mu mdima, mukalowe m’kuwala kwake kodabwitsa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 14: 06.

 

Alleluia, Alleluia – Ineyo ndine njira, ndine Choona ndiponso Moyo. Palibe munthu angafike kwa Atate ngati sadzera mwa Ine. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA; YOHANE 14: 01 – 12 (Ineyo ndine njira, ndine choona ndiponso moyo).

 

Yesu adawauza ophunzira akewo kuti, “mtima wanu usavutike. Khulupirirani Mulungu, Khulupirirani inenso. M’nyumba mwa Atate anga muli malo ambiri okhalamo. Kukadakhala kuti mulibe malo, ndikadakuuzani. Ndikupita kukakukonzerani malo. Ndipo ndikapita kukakukonzerani malo, ndidzabweranso kudzakutengani, kuti inunso mukakhale kumene kuli Ine. Ndipo kumene ndikupita Ineko, njira yake mukuidziwa.” Tomasi adati, “Ambuye, sitikudziwa kumene mukupita, nanga njira yake tingaidziwe bwanji?” Yesu adamuyankha kuti, “Ineyo ndine njira, ndine choona ndiponso moyo. Palibe munthu angafike kwa Atate ngati sadzera mwa Ine. Mukadandidziwa Ine, Atate anganso mukadawadziwa. Kuyambira tsopano mukuwadziwa ndipo mwawaona.” Filipo adati, “Ambuye, tiwonetseni Atatewo, Mukatero tikhutira.” Yesu adamuyankha kuti, “Iwe Filipo, ndakhala nanu nthawi yonseyi, ndipo sunandidziwebe? Amene waona Ine, waonanso Atate. Nanga bwanji ukuti ‘tiwonetseni Atate?’ Kodi sukukhulupirira kuti Ine ndimakhala mwa Atate, ndipo Atate amakhala mwa Ine? Mau amene ndimakuuzani sachokera kwa Ine ndekha ai, koma Atate amene amakhala mwa Ine, ndiwo amagwira ntchito yao. Mundikhulupirire kuti Ine ndimakhala Atate ndipo Atate amakhala mwa Ine. Kupanda apo, khulupiriranitu chifukwa cha ntchito zanga zomwezo. Ndithu ndikunenetsa kuti amene amandikhulupirira, ntchito zomwe ndimachita Ine, nayenso adzazichita. Ndipo adzachita zoopsa pamenepa, chifukwa ndikupita kwa Atate.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pa Ubatizo tidasanduka anthu akeake a Mulungu. Tsono mogwirizana ndi Yesu Khristu, tipereke ulemu kwa Atate athu a Kumwamba popempha madalitso ao:

 

1.     Akhristu onse, akhale okondana ndi ogwirizana mwa Yesu Khristu, aoneke ngati miyala yamoyo yoti Mulungu amange nayo nyumba.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

2.     Adikoni ndi atsogoleri ena a Mpingo, asenze udindo wao molimbana ndipo atumikire anthu a mwachifundo.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

3.     Anthu amasiye ndi ena onse ali m’mavuto, alandire chisamaliro chokwanira kuchokera kwa anzao ndipo adziwe kuyamika chifundo cha Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

4.     Ife tonse a m’Parishi yathu ino, mayendedwe athu ndi ntchito zathu zotumikira anzathu, zisonyeze kuti Yesu Khristu ndiyedi njira yopita kwa Atate.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Mulungu Atate athu, mutiyang’ane ndi maso achifundo ndipo mumvere mapemphero athuwa, popeza kuti mwatiwonetsa kukoma mtima kwanu, mwa Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...