Saturday, January 28, 2023


LAMULUNGU LA 04 PA CHAKA
– A

“Ngwodala iwo amene azindikira umphawi wao.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MNENERI ZEFANIYA; ZEFANIYA 02: 03; 03: 12 – 13. (Pakati panu ndidzasiya anthu odzichepetsa ndi otsika.)

 

Funafunani Chauta, inu nonse odzichepetsa, inu amene mumamvera malamulo ake. Chitani zolungama, khalani odzichepetsa. Mwina mwake mudzatha kupulumuka pa tsiku la mkwiyo wa Chauta. Pakati panu ndidzasiya anthu odzichepetsa ndi otsika. Iwowo adzafunafuna populumukira m’dzina la Chauta. Otsala a mu Israelewa sadzalakwanso, sadzalankhulanso zabodza, sadzachitanso zonyenga. Adzakhala pabwino mwamtendere, popanda wina wowaopsa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 146: 07 – 10.

 

Ngwodala iwo amene ali wosauka mu uzimu chifukwa ufumu wa kumwamba ndi wawo.

 

Chauta amasunga malonjezo ake nthawi zonse.

Amachitira anthu opsinjidwa zolungama,

Amawapatsa chakudya anthu anjala.

Chauta amamasula am’ndende.

 

Ngwodala iwo amene ali wosauka mu uzimu chifukwa ufumu wa kumwamba ndi wawo.

 

Chauta amatsekula maso a anthu osapenya,

Chauta amakweza anthu otsitsidwa,

Chauta amateteza alendo,

Amachirikiza mkazi wamasiye ndiponso mwana wamasiye.

 

Ngwodala iwo amene ali wosauka mu uzimu chifukwa ufumu wa kumwamba ndi wawo.

 

Chauta amakonda anthu ochita chilungamo,

Koma njira za anthu oipa amazipotoza,

Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako, iwe Ziyoni, adzalamulira ku mibadwo yonse.

 

Ngwodala iwo amene ali wosauka mu uzimu chifukwa ufumu wa kumwamba ndi wawo.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 01: 26 – 31. (Mulungu adasankha zimene anthu amaziyesa zopusa.)

 

Abale, taganizani m’mene munaliri pamene Mulungu adakuitanani. Pakati panu panalibe ambiri amene anthu ankawayesa anzeru. Panalibenso ambiri amphamvu, kapena obadwa m’mabanja omveka. Koma Mulungu adasankha zimene anthu amaziyesa zopusa, kuti Iye anyazitse nazo anthu anzeru. Adasankhanso zimene anthu amaziyesa zofooka, kuti Iye anyazitse nazo anthu amphamvu. Ndipo zimene anthu amaziyesa zachabe, zonyozeka ndi zosakhala zenizeni, Mulungu adazisankha kuti athetse mphamvu zinthu zimene iwowo amayesa kuti ndiye zenizeni. Mulungu adachita zimenezi kuti pasakhale wina aliyense woti nkumadzitukumula pamaso pake. Mulungu ndiye adakulunzanitsani ndi Khristu Yesu, ndipo adamsandutsa kuti akhale nzeru yathu. Chifukwa cha Yesu, timapezeka olungama pamaso pa Mulungu. Ndi Yesuyo amene amatisandutsa anthu akeake a Mulungu, ndiye amatipulumutsa. Nchifukwa chake, monga Malembo anenera, Wofuna kunyada, anyadire Ambuye.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO –

Alleluia, Alleluia – Atate, Mwini kumwamba ndi dziko lapansi, ndikukuyamikani kuti zinthuzi mudaaululira anthu osaphunzira. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 05: 01 – 12a. (Ngodala anthu amene ali osauka mumtima mwao.)

 

Yesu poona chikhamu cha anthu chija, adakwera pa phiri. Iye atakakhala pansi, ophunzira ake adamtsatira pomwepo. Kenaka adayamba kuwaphunzitsa, adati, “Ngodala anthu amene ali osauka mumtima mwao, pakuti Ufumu wakumwamba ndi wao. Ngodala anthu amene akumva chisoni, pakuti Mulungu adzawasangalatsa. Ngodala anthu ofatsa, pakuti Mulungu adzawapatsa dziko la pansi pano kuti likhale lao. Ngodala anthu amene akumva njala ndi ludzu lofuna chilungamo, pakuti Mulungu adzakwaniritsa zofuna zao. Ngodala anthu ochitira anzao chifundo, pakuti iwonso Mulungu adzawachitira chifundo. Ngodala anthu oyera mtima, pakuti adzaona Mulungu. Ngodala anthu odzetsa mtendere, pakuti Mulungu adzawatcha ana ake. Ngodala anthu ozunzidwa chifukwa cha kuchita chilungamo, pakuti Ufumu wakumwamba ndi wao. Ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani ndi kukunyengezerani zoipa zamitundumitundu chifukwa cha Ine. Sangalalani, kondwerani, chifukwa mphotho yanu ndi yaikulu Kumwamba. Paja ndi m’menenso anthu ankazunzira aneneri amene analipo kale inu musanabadwe.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, popeza kuti timadalira Mulungu pa zonse, tiyeni timupemphe thandizo lake m’zosowa zathu ndi za anthu onse:

 

1. Eklezia wa Mulungu aunikire anthu onse ndi maphunziro ake, ndipo chifundo chake chosamalira amphawi chidzetse Ufumu wa Mulungu pakati pa anthu.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

2. Akhristu amene akuzunzika chifukwa cha Mthenga Wabwino, alimbikire m’chikhulupiriro ndi kukondwera, podziwa kuti mphotho yao njaikulu kumwamba.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

3. Iwo amene amayesetsa kudzetsa chilungamo, mtendere ndi umodzi pakati pa anthu, apitirize ntchito yao mwakhama, podziwa kuti Mulungu adzawatcha ana ake.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

4. Ife tonse amene takomana muno, moyo wathu pansi pano ukhale wodziletsa, wokomera Mulungu ndi wodzaza ndi ntchito zachifundo.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, Inu mufuna kuti anthu onse alowe m’chikondwerero chanu. Mulimbitse chikhulupiriro chathu, mutikhazikitse m’chikondi chanu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, January 21, 2023


LAMULUNGU LA 03 PA CHAKA (CYCLE A)

“Adandituma kuti ndilalike Mthenga Wabwino.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MNENERI YESAYA; YESAYA 08: 23 – 09: 01 – 04. (M’dziko la Galilea, anthu aona kuwala kwakukulu.)

 

Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu adaanyozetsa dziko la Zebuloni ndi la Nafutali, koma kutsogolo kuno adzalisandutsa laulemu dera lonseli, kuyambira ku Nyanja yaikulu kuzambwe mpaka kukafika ku dziko la patsidya pa mtsinje wa Yordani, ndiye kuti dziko la Galilea, dziko la anthu a mitundu ina. Anthu amene ankayenda mumdima aona kuwala kwakukulu. Amene ankakhala m’dziko la mdima wandiweyani, kuwala kwawaonekera. Inu Chauta, mwauchulukitsa mtundu wanu, mwaonjezera kukondwa kwa anthu anu. Iwo akukondwa pamaso panu monga m’mene anthu amakondwera nthawi ya masika, monganso m’mene anthu amakondwera pogawana zofunkha. Pakuti inu mwathyola goli limene linkawalemera, ndodo zimene ankamenyera mapewa ao, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza, monga mudachitira pogonjetsa Amidiyani.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 27: 01, 04, 13 – 14.

 

Chauta ndiye muuni wanga ndi chipulumutso changa.

 

Chauta ndiye muuni wanga ndi chipulumutso changa.

Ndidzaopa yani?

Chauta ndiye linga la moyo wanga,

Nanga ndichitirenji mantha?

 

Chauta ndiye muuni wanga ndi chipulumutso changa.

 

Ndapempha chinthu chimodzi chokha kwa Chauta, chinthu chofunika kwambiri,

Chakuti ndizikhala m’Nyumba ya Chauta masiku onse a moyo wanga,

Kuti ndizikondwera ndi kukoma kwake kwa Chauta ndi kuti ndizipembedza lye m'Nyumba mwakemo.

 

Chauta ndiye muuni wanga ndi chipulumutso changa.

 

Ndikhulupirira kuti ndidzaona ubwino wake wa Chauta m’dziko la amoyo.

Tsono khulupirira Chauta,

Khala wamphamvu, ndipo ulimbe mtima,

Ndithu, khulupirira Chauta.

 

Chauta ndiye muuni wanga ndi chipulumutso changa.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO; 01 AKORINTO 01: 10 – 13, 17. (Pasakhale kupatulana pakati panu, koma muzimvana kwenikweni.)

 

Abale, ndikukupemphani m’dzina la Ambuye athu Yesu Khristu, kuti muzivomerezana pa zimene munena. Pasakhale kupatulana pakati panu, koma muzimvana kwenikweni pokhala a mtima umodzi ndi a maganizo amodzi. Pakuti ena a m’banja la Koloe andifotokozera kuti pali kukangana pakati panu, abale anga. Chimene ndikufuna nchakuti aliyense mwa inu akungonena zakezake. Wina akuti, “ine ndi wa Paulo,” winanso akuti, “ine ndine wa Apolo,” wina akuti, “ndine wa Kefa,” winanso akuti, “ine ndine wa Khristu.” Kodi Khristu wagawika? Kodi adakuferani pamtanda ndi Paulo? Kodi mudabatizidwa m’dzina la Paulo? Paja Khristu adandituma, osati kuti ndizibatiza ai, koma kuti ndizilalika uthenga wabwino. Ndipo ndiyenera kumaulalika mosagwiritsa ntchito luso lake la ulaliki, kuwopa kuti mtanda wa Khristu ungatheretu mphamvu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – Mateyo 04: 23.

Alleluia, Alleluia – Yesu adalalika Uthenga Wabwino wonena za ufumu wakumwamba. Ankachiritsanso nthenda zonse za anthu ndi zofooka zao. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 04: 12 – 23. (Anakakhala ku Kapernao monga mneneri Yesaya adaanena.)

 

Yesu atamva kuti Yohane adamponya m’ndende, adabwera ku Galileya. Adachokako ku Nazarete, nakakhala ku Kapernao, Mzinda wina wa m’mbali mwa Nyanja ku dera la Zebuloni ndi Nafutali. Zidaatero kuti zipherezere zimene mneneri Yesaya adaanena kuti, “iwe dziko la Zebuloni ndi iwe dziko la Nafutali, njira yakunyanja, patsidya pa Yordani, iwe Galileya, dziko la anthu akunja! Anthu okhala mu mdima aona kuwala kwakukulu. Anthu okhala m’dziko la mdima wabii wa imfa, kuwala kwawaonekera.” Kuyambira nthawi imeneyo Yesu adayamba kulalika kuti, “tembenukani mtima, chifukwa ufumu wakumwamba wayandikira.” Yesu akuyenda m’mbali mwa Nyanja ya Galileya, adaona anthu awiri pachibale pao: Simoni wotchedwa Petro, ndi mbale wake Andrea, akuponya khoka m'nyanjamo, popeza kuti anali asodzi. Yesu adawauza kuti, “inu, munditsate, ndikusandutseni asodzi a anthu.” Pomwepo iwo adasiya makoka ao, namamtsatadi. Atapitirira pamenepo, Yesu adaona enanso awiri pachibale pao: Yakobe ndi Yohane, ana a Zebedeo. Iwo anali m’chombo pamodzi ndi bambo waoyo, akukonza makoka ao, Yesu nkuwaitana. Pomwepo iwowo adasiya chombo chao ndi bambo wao uja, namatsata Yesu. Yesu adayendera dziko lonse la Galileya akuphunzitsa m’nyumba zamapemphero ndi kulalika uthenga wabwino wonena za ufumu wakumwamba. Ankachiritsanso nthenda zonse za anthu ndi zofooka zao zam’thupi.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

Mapemphero a Akhristu

 

Abale, Yesu Khristu watiitana tonse ku ntchito yake. Tsono tiyeni tipemphere mogwirizana, kuti ufumu wa Mulungu ukhazikike mwa ife ndi mwa anthu onse.

 

1. Apapa ndi Aepiskopi onse, akhale a mtima umodzi polalika mthenga wa Khristu, ndipo atsogolere anthu ao m’njira ya ungwiro.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

2. Akhristu ofooka ndi otayika, atembenuke mtima ndi kubwerera kwa Mulungu, pakumva mau a Mthenga Wabwino.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

3. Anyamata ndi atsikana oitanidwa, atembenukire ku ntchito zotumikira Mpingo, alimbikire pa maphunziro ao, ndipo alondole mapazi a Yesu Khristu mosacheukira m’mbuyo.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

4. Ife tonse osonkhana pano, tisenze udindo wachikhristu modzipereka ndi mogwirizana, potsogolera anzathu m’njira ya chikondi.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, Inu mukudziwa zosowa za munthu aliyense. Mutigawireko zokoma za ufumu wanu, kuti tiyende molimba m’njira ya chipulumutso. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, January 14, 2023


LAMULUNGU LA 02 PA CHAKA – A.

“Umboni wa Yohane Mbatizi”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MNENERI YESAYA; YESAYA 49: 03, 05 – 06. (Ndidzakusandutsa kuwala kounikira mitundu in ya anthu, kuti chipulumutso changa chikafike mpaka ku mathero a dziko lapansi).

 

Chauta adandiuza kuti, “iwe Israele ndiwe mtumiki wanga. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.” Chauta ndi amene adandiwumba m’mimba mwa amai anga kuti ndikhale mtumiki wake, kuti ndibweze fuko la Yakobe kwa Iye, ndipo kuti ndisonkhanitse Aisraele pafupi ndi Iye. Choncho ndimalemekezeka m’maso mwa Chauta, ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga. Chautayo akunena kuti, “nchinthu chochepa kwambiri kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobe ndi kuwabweza kwao Aisraele amene adapulumuka. Ndidzakusandutsa kuwala kounikira mitundu ina ya anthu, kuti chipulumutso changa chikafike mpaka ku mathero a dziko lapansi.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 40: 02, 04, 07 – 10.

 

Ndilipo, ndikubwera. Ndimakonda kuchita zimene mumafuna.

 

Ine ndidayembekeza Chauta ndi mtima wokhulupirira kuti adzandithandize,

Adaweramira pansi kuyang’ana kwa ine, namva kulira kwanga,

Mulungu waika nyimbo yatsopano m’kamwa mwanga,

Nyimbo yake yotamanda Iye.

 

Ndilipo, ndikubwera. Ndimakonda kuchita zimene mumafuna.

 

Simudafune nsembe ndi zopereka,

Koma mwandipatsa makutu oti ndizimvera,

Simudapemphe nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo,

Tsono ndidati, “ndilipo, ndikubwera.”

 

Ndilipo, ndikubwera. Ndimakonda kuchita zimene mumafuna.

 

Monga zidalembedwa za ine m’buku la malamulo,

Ndimakonda kuchita zimene mumafuna,

Inu Mulungu wanga,

Malamulo anu ali mumtima mwanga.

 

Ndilipo, ndikubwera. Ndimakonda kuchita zimene mumafuna.

 

Ndalalika uthenga wabwino wa chipulumutso chanu,

Pa msonkhano waukulu,

Sindidatseke pakamwa,

Monga mukudziwa, Inu Chauta.

 

Ndilipo, ndikubwera. Ndimakonda kuchita zimene mumafuna.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO; 01 AKORINTO 01: 01 – 03. (Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu akukomereni mtima ndi kukupatsani mtendere).

 

Abale, ndine, Paulo, amene mwa kufuna kwa Mulungu ndidaitanidwa kuti ndikhale mtumwi wa Khristu Yesu. Ndili pamodzi ndi mbale wathu, Sostene. Tikulembera mpingo wa Mulungu umene uli ku Korinto. Mulungu adakupatulani mwa Khristu Yesu, ndipo adakuitanani kuti mukhale anthu akeake, pamodzi ndi anthu onse amene ponseponse amatama dzina la Ambuye Yesu Khristu mopemba. Iye ndi Mbuye wathu ndi Mbuye waonso. Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu akukomereni mtima ndi kukupatsani mtendere.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – Yohane 01:14a, 12a.

 

Alleluia, Alleluia – Wotchedwa Mau uja adasanduka munthu, nadzakhala pakati pathu; kwa amene adaamlandira nakhulupirira dzina lake, Iye adawapatsa mphamvu zoti akhale ana a Mulungu.  – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA; YOHANE 01: 29 – 34. (Suuyu Mwanawankhosa wa Mulungu uja, wochotsa machimo a anthu).

 

M’mawa mwake Yohane adaona Yesu akubwera kwa iye, ndipo adati, “Suuyu Mwanawankhosa wa Mulungu uja, wochotsa machimo a anthu a pa dziko lapansi. Iyeyu ndi amene ndinkanena uja kuti, ‘pambuyo panga pakubwera munthu wopambana ine, pakuti ine ndisanabadwe, Iye alipo,’ Inenso sindinkamudziwa, koma ndidabwera kudzabatiza ndi madzi kuti Aisraele amdziwe.” Yohane adachitanso umboni, adati, “ndidaona Mzimu Woyera akutsika kumwamba ngati nkhunda, nakhazikika pa Iye. Ine sindinkamudziwa, koma Mulungu amene adandituma kudzabatiza ndi madzi, ndiye adaandiwuza kuti, ‘amene udzaone Mzimu Woyera akutsika ndi kukhazikika pa Iye, ndi Iyeyo wobatiza mwa Mzimu Woyera.’ Ineyo ndidazionadi, ndipo ndikuchita umboni kuti ameneyu ndi Mwanadi wa Mulungu.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu

 

Abale, Mulungu adatipatula natiyeretsa mwa Yesu Khristu kuti tikhale anthu akeake. Tiyeni tipemphe Atate athu a Kumwamba, kuti adalitse anthu onse ndi kuwapatsa mtendere:

 

1. Eklezia, Mpingo wa Yesu, aonetse makhalidwe a ungwiro, akhale ngati nyale younikira onse ndi chizindikiro chosonyeza chipulumutso.

Tikupemphani…, mutivomereze.

 

2. Anthu a mafuko onse okhala mu mdima, Mulungu awaunikire mpaka adzazindikire kuwala kwa Yesu Khristu ndi chifundo chake chofuna kuwapulumutsa.

Tikupemphani…, mutivomereze.

 

3. Apapa ndi Aepiskopi onse, akhale a mtima umodzi, pokumbukira Mwana wa Nkhosa wa Mulungu amene adadzachotsa machimo a anthu onse.

Tikupemphani…, mutivomereze.

 

4. Ife tonse tili muno, timchitire Ambuye Yesu umboni pa moyo wathu wa tsiku ndi tsiku, makamaka pakutumikira anzathu ndi mtima wachikondi.

Tikupemphani…, mutivomereze.

 

Atate, pamodzi ndi anthu onse amene amatamanda Yesu Khristu, tikuyamika kukoma mtima kwanu, chifukwa mwa Mwana wanuyo mudatipatsa madalitso onse. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

--------------------------------------

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, January 7, 2023

CHAKA CHA EPIFANIYA WA AMBUYE YESU – A

Yesu Mpulumutsi adadzera anthu a mitundu yonse.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MNENERI YESAYA; YESAYA 60: 01 – 06. (Ulemerero wa Chauta udzawonekera).

Iwe Yerusalemu dzuka, wala, kuwala kwako kwayamba. Ulemerero wa Chauta wakuwalira. Mdima udzaphimba dziko lapansi, mdima wandiweyani udzagwa pa anthu a mitundu ina. Koma iwe, Chauta adzakuwalira, ulemerero wake udzaoneka pa iwe. Anthu a mitundu ina adzatsata kuwala kwako, mafumu adzalondola kunyezimira kwako konga dzuwa limene likutuluka kumene. Yang’ana pozungulira, uwone zimene zikuchitika. Onse akusonkhana kuti abwere kwa iwe. Ana ako aakazi adzatengedwa m’manja ngati ana. Udzaona zimenezi, ndipo udzakondwa, mtima wako udzalumpha ndi chimwemwe. Chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe. Chuma cha maiko onse chidzabwera kwa iwe. Kudzafika mtindiri wa ngamira, ngamira zing’onozing’ono, kuchokera ku Midiyani ndi ku Efa. Onse a ku Sheba adzabwera. Adzakhala atatenga golide ndi lubani, ndipo adzatamanda Chauta mokweza mau.

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 72: 01 – 02, 07 – 08, 10 – 13.

Mafumu onse adzakugwadirani ndipo mitundu yonse ya anthu idzakutumikirani, Ambuye.

 

Inu Mulungu, patsaniko mfumu nzeru zoweruzira,

Patsaniko mwana wa mfumu mtima wokonda chilungamo,

Motero mfumuyo idzaweruza anthu anu molungama,

Ndiponso anthu anu osauka mosakondera.

 

Mafumu onse adzakugwadirani ndipo mitundu yonse ya anthu idzakutumikirani, Ambuye.

 

Mafumu a ku Tarisisi ndi akuzilumba adzaipatsa mitulo,

Mafumu a ku Sheba ndi a ku Seba adzabwera ndi mphatso,

Mafumu onse adzaigwadira,

Ndipo mitundu yonse ya anthu idzaitumikira.

 

Mafumu onse adzakugwadirani ndipo mitundu yonse ya anthu idzakutumikirani, Ambuye.

 

Ndithu iyo idzalanditsa anthu osowa amene amaiitana,

Idzapulumutsa anthu osauka ndiponso opanda wowathandiza,

Idzamvera chisoni anthu ofooka ndi osowa,

Ndipo idzapulumutsa moyo wa anthu aumphawi.

 

Mafumu onse adzakugwadirani ndipo mitundu yonse ya anthu idzakutumikirani, Ambuye.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AEFESO; AEFESO 03: 02 – 03, 05 – 06. (Chinsinsicho nchakuti anthu a mitundu ina nawonso ngoyenera kulandira madalitso a Mulungu pamodzi ndi Ayuda.)

Abale, kumva munamva za ntchito imene mwa ufulu wake Mulungu adandipatsa, yolalika pakati panu za kukoma mtima kwake. Adandiwululira chinsinsi chake, monga ndidakulemberani mwachidule posachedwapa. Chinsinsi chimenechi anthu a mibadwo yakale sadachidziwe, koma Mulungu wachiwulula tsopano mwa Mzimu Woyera kwa atumwi ake oyera mtima, ndiponso kwa aneneri ake. Chinsinsicho nchakuti mwa uthenga wabwino anthu a mitundu ina nawonso ngoyenera kulandira madalitso a Mulungu pamodzi ndi Ayuda. Pamodzinso ndi Ayuda ali ziwalo za thupi limodzi, ndipo mwa Khristu Yesu amalandira nao lonjezo la Mulungu.

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – Mateyo 02: 02.

Alleluia, Alleluia – Ife tidaona nyenyezi ikutuluka kuvumaku, motero tabwera kudzampembedza Ambuye. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 02: 01 – 12. (Ife tidaona nyenyezi ikutuluka kuvumaku, motero tabwera kudzampembedza Ambuye).

Yesu adabadwira m’mudzi wa Betelehemu, m’dziko la Yudeya, pa nthawi imene Herode anali mfumu ya Dzikolo. Ndiye kudabwera akatswiri ena a Nyenyezi ku Yerusalemu kuchokera kuvuma. Iwowo ankafunsa kuti, “ali kuti mwana amene adabadwa kuti adzakhale Mfumu ya Ayuda? Ife tidaona Nyenyezi yake ikutuluka kuvumaku, motero tabwera kudzampembedza.” Mfumu Herode atamva zimenezi, adavutika kwambiri ndipo anthu ena onse a m’Yerusalemu nawonso adavutika nazo. Tsono Herode yo adasonkhanitsa akulu onse a ansembe ndi Aphunzitsi onse a Malamulo a Mose, nawafunsa kuti, “kodi paja adati Mpulumutsi wolonjezedwa ndi Mulungu uja adzabadwira kuti?” Iwo adati, “m’mudzi wa Betelehemu ku Yudeya. Pajatu mneneri adalemba kuti, ‘iwe Betelehemu wa m’dziko la Yuda, sindiwe wamng’ono konse pakati pa akulu olamulira Yuda. Pakuti kwa iwe kudzachokera mtsogoleri pamene adzalamulira anthu anga Aisraele.’” Pamenepo Herode adawaitanira paseri akatswiri a Nyenyezi aja, nawafunsitsa za nthawi yeniyeni imene adaaiwonera Nyenyezi yo. Kenaka adawatumiza ku Betelehemu nkuwaudza kuti, “Pitani, kafunsitseni za mwanayo. Mukakampeza, mudzandidziwitse, kuti inenso ndidzapite kukampembedza.” Anthu aja atamva mau a mfumu, adanyamuka. Nyenyezi imene adaaiwona kuvuma ija idawatsogolera mpaka idakafika nkukaima pamwamba pa malo amene panali mwanayo. Ataiwona nyenyeziyo, adasangalala kwabasi. Adalowa m’nyumba, naona mwanayo ali ndi Maria mai wake, ndipo Adagwada nampembedza. Kenaka adamasula chuma chao, nampatsa mitulo ya golide, lubani ndi mafuta onunkhira a mure. Mulungu adawachenjeza m’maloto kuti asadzerenso kwa Herode kuja. Motero adadzera njira ina pobwerera kwao.

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...