LAMULUNGU LA 31 PACHAKA (CYCLE C)
MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LUNTHA; LUNTHA 11: 22 – 12: 02. (Mumawachitira chifundo anthu onse, chifukwa mumakonda kwambiri chamoyo chilichonse.)
Pamaso panu dziko lonse lapansi lili ngati kamchenga kopendeketsa sikelo, ngati dontho la mame am’mamawa logwa pa nthaka. Komabe chifukwa mungathe kuchita zinthu zonse, mumawachitira chifundo anthu onse. Mumapsinya maso dala kuti musaone machimo a anthu, kuti apeze mpata wotembenukira mtima. Mumakonda zolengedwa zonse, palibe ncholengedwa chimodzi chomwe chimene chingakunyanseni. Mukadadana ndi kanthu, bwezi mutaleka kukalenga. Kanthu kalikonse kakadakhala moyo bwanji, mukadapanda kukasunga? Koma zinthu zonse mumazichitira chifundo, chifukwa zonse nzanu, Inu Ambuye, amene mumakonda kwambiri chamoyo chilichonse. Mzimu wanu wosafa umakhala m’zinthu zonse. Nchifukwa chake anthu akakunyozani, mumawalanga pang’onopang’ono. Mumawakumbutsa machimo ao ndi kuwachenjeza kuti asiye zoipa ndi kukhulupirira inu, Ambuye.
Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu
---------------------------------------
NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 145: 01 – 02, 08 – 11, 13, 14.
Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga.
Ndidzakuyamikani, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga,
Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse mpaka muyaya,
Ndidzakuthokozani tsiku ndi tsiku,
Ndidzatamanda dzina lanu mpaka muyaya.
Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga,
Chauta ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
Wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi chosasinthika,
Chauta ndi Wabwino kwa onse,
Amachitira chifundo Zamoyo zonse zimene adazilenga.
Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga.
Zamoyo zonse zidzakuthokozani, Inu Chauta,
Anthu anu onse oyera mtima adzakutamandani,
Adzalankhula za ulemerero wa ufumu wanu,
Adzasimba za mphamvu zanu.
Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga.
Chauta ndi wokhulupirika pa mau ake onse,
Ndi wokoma mtima pa zochita zake zonse,
Chauta Amachirikiza onse ogwa m’mavuto,
Amakweza onse otsitsidwa.
Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga.
--------------------------------------
MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YACHIWIRI YA PAULO WOYERA KWA ATESALONIKA; 02 ATESALONIKA 01: 11 – 02: 02. (Dzina la Ambuye athu Yesu lidzalemekezedwa mwa inu, ndipo inu mudzalemekezedwa mwa Iye.)
Nchifukwa chake timakupemphererani nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akusandutseni oyenera moyo umene iye adakuitanirani. Timapemphanso kuti ndi mphamvu zake akulimbikitseni kuchita zabwino zonse zimene mumalakalaka kuzichita, ndiponso Ntchito zotsimikizira chikhulupiriro chanu. Motero dzina la Ambuye athu Yesu lidzalemekezedwa mwa iye. Zonsezi zidzachitika chifukwa cha kukoma mtima kwa Mulungu wathu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu. Pazakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, ndiponso za kusonkhana kwathu kuti tikakumane naye, tifuna kukupemphani kanthu, abale. Maganizo anu asasokonezeke mnsanga, ndipo musaopsezedwe ndi mau akuti, “tsiku la Ambuye lafika,” ngakhale anene kuti mauwo ngochokera kwa Mzimu Woyera, kapena kuti tawanena ndife, kapena tachita kuwalemba m’kalata.
Mau a Ambuye……...Tithokoze Mulungu.
--------------------------------------
NYIMBO YA MTHENGA WABWINO. – Yohane 03:16.
Alleluia, Alleluia – Mulungu adawakonda kwambiri anthu apa dziko lonse lapansi. Anali naye Mwana mmodzi yekha, koma adampereka kuti aliyense wokhulupirira Iyeyo akhale ndi moyo wosatha. – Alleluia, Alleluia.
--------------------------------------
MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 19: 01 – 10. (Mwana wa Munthu adabwera kudzafunafuna ndi kudzapulumutsa amene adatayika.)
Yesu adalowa m’Yeriko, ulendo wake wobzola mzindawo. Kudafika munthu wina, dzina lake Zakeyo. Iyeyo anali mkulu wa okhometsa msonkho, ndipo anali wolemera. Ankafunitsitsa kuwona Yesu kuti ngwotani. Koma pakuti Zakeyoyo anali wamfupi, adalephera kumuwona chifukwa cha kuchuluka kwa anthu. Tsono adathamangira kutsogolo nakakwera mu mkuyu kuti amuwone, chifukwa Yesu ankayenera kudzera pamenepo. Ndipo pamene Yesu adafika pamalopo, adayang’ana m’mwamba., namuuza kuti, “Zakeyo, fulumira, tsika chifukwa lero ndikuyenera kukakhala nao kunyumba kwako.” Pomwepo Zakeyo adafulumira, natsika, kenaka nkukamlandira Yesu mokondwa kwambiri. Poona zimenezi, anthu onse adayamba kung’ung’uza. Adati, “Wakakhala kunyumba kwa munthu wochimwa.” Koma Zakeyo adaimirira nauza Ambuye kuti, “Ambuye, ndithudi ndidzapereka hafu la chuma changa kwa amphawi. Ndipo ngati ndidalandira kanthu kwa munthu aliyense monyenga, ndidzamubwezera kanai.” Apo Yesu adamuuza kuti, “chipulumutso chafika m’banja lino lero, popeza kuti ameneyunso ndi mwana wa Abrahamu. Pajatu mwana wa munthu adabwerta kudzafunafuna ndi kudzapulumutsa amene adatayika.”
Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.
#Pax_et_Gaudium_in_Domino.
Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295