Saturday, June 25, 2022

 

LAMULUNGU LA 13 PA CHAKA (CYCLE C)

(Wofuna kutsata Yesu asamayang’anenso zakumbuyo.)

MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LOYAMBA LA MAFUMU: 01 MAFUMU 19: 16b, 19 – 21. (Pambuyo pake adanyamuka namayenda ndi Eliya ndi kumamtumikira.)

Chauta adamuuza Eliya kuti, “Elisa, mwana wa Safati wa ku Abele-Mehola, ukamdzoze kuti akhale mneneri wolowa m’malo mwako.” Eliya atachoka kumeneko, adakapeza Elisa akulima ndi pulawo yokokedwa ndi ng’ombe. Panali magoli khumi ndi awiri, mwiniwakeyo nkumayenda ndi goli lotsiriza. Eliya adabwera kumene kunali iyeko, namuveka mwinjiro wake. Pomwepo Elisa adasiya ng’ombe zakezo, adathamangira Eliya uja nampempha kuti, “mundilore kuti ndikatsanzike bambo wanga ndi mayi wanga, ndipo pambuyo pake ndidzakutsatani.” Eliya adamuyankha kuti, “Chabwino, pita. Ndakuletsa ngati?” Apo Elisha adabwerera, ndipo adatenga ng’ombe zake ziwiri nazipha. Kenaka adatenga magoli a ng’ombezo nasonkhera moto nkuphikira nyamayo, ndipo adaipereka kwa anthu kuti adye. Pambuyo pake adanyamuka namayenda ndi Eliya ndi kumamtumikira.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 16: 01 – 02, 05, 07 – 11.

Chauta ndiye chuma changa ndi cholowa changa.

Mundisunge Inu Mulungu, pakuti ndikuthawira kwa Inu.

Ndimamuuza Chauta kuti, “Inu ndinu Ambuye anga.”

Chauta ndiye chuma changa ndi cholowa changa.

Tsogolo langa lili m'manja mwanu.

Chauta ndiye chuma changa ndi cholowa changa.

Ndikutamanda Chauta amene ali phungu wanga.

Mtima wanga umandilangiza ndi usiku womwe.

Nthawi zina ndimalingalira za Chauta.

Popeza kuti ali ku dzanja langa lamanja,

palibe amene angandiopse konse.

Chauta ndiye chuma changa ndi cholowa changa.

Nchifukwa chake mtima wanga ukukondwa,

Ndipo m’katikati mwangamu ndikusangalala,

Thupi langanso lidzakhala pabwino,

Chifukwa simudzandisiya ku malo a anthu akufa,

Simudzalola kuti wokondedwa wanune ndikaole kumeneko.

Chauta ndiye chuma changa ndi cholowa changa.

Mumandiwonetsa njira ya ku moyo.

Ndimapeza chimwemwe chachikulu kumene kuli Inu,

Ndidzasangalala mpaka muyaya ku dzanja lanu lamanja.

Chauta ndiye chuma changa ndi cholowa changa.

--------------------------------------

MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA A GALATIYA; AGALATIYA 05: 01, 13 – 18. (Mulungu adakuitanani kuti mukhale mfulu)

Abale, Khristu adatimasula kuti tikhale mfulu ndithu. Muzichilimikira tsono, osalola kumangidwanso m’goli la ukapolo. Inu abale, Mulungu adakuitanani kuti mukhale mfulu. Koma chenjerani kuti ufulu wanu umenewu usapatse mpata khalidwe lanu lokonda zoipa. Kwenikweni muzitumikirana mwachikondi. Paja malamulo onse a Mulungu amaundidwa mkota pa lamulo limodzi lija lakuti, “uzikonda mnzako monga momwe umazikondera iwe wemwe.” Koma ngati muyamba kulumana ndi kukadzulana, muchenjere kuti mungaonongane kotheratu. Chimene ndikufuna kunena ndi ichi: Mulole Mzimu Woyera kuti azikutsogolerani. Mukatero, pamenepo simuzachita zimene khalidwe lanu lokonda zoipa limalakalaka. Pakuti khalidwelo limalakalaka zotsutsana ndi zimene Mzimu Woyera afuna, ndipo zimene Mzimu Woyera afuna zimatsutsana ndi zimene khalidwe lokonda zoipalo limafuna. Ziwirizi zimadana, kotero kuti simungachite zimene mufuna kuchita. Koma ngati Mzimu Woyera akutsogolerani, ndiye kuti sindinunso akapolo a Malamulo a Mose.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO.

Alleluia, Alleluia – Lankhulani, Inu Ambuye, poti mtumiki wanune ndilikumva. Muli nawo ndinu mau opatsa moyo wosatha. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAWU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; 09: 51 – 62. (Ndizikutsatani kulikonse kumene muzipita.)

Pamene masiku ankayandikira oti Yesu atengedwe kunka kumwamba, Iye adatsimikiza ndithu zopita ku Yerusalemu. Motero adatuma amithenga kuti atsogole, akalowe m’mudzi wina wa Asamariya kukamkonzera malo. Koma anthu a m’mudzimo sadafune kumulandira, chifukwa iye ankapita ku Yerusalemu. Ophunzira ake, Yakobe ndi Yohane ataona zimenezi adati, “Ambuye, bwanji tiitane moto kuchokera kumwamba kuti udzawapsereze anthu amenewa?” Koma Yesu adacheuka nadzudzula ophunzirawo. Pambuyo pake onse pamodzi adapita ku mudzi wina. Pamene iwo anali panjira, munthu wina adauza Yesu kuti, “ndidzikutsatani kulikonse kumene muzipita.” Yesu adamuyankha kuti, “nkhandwe zili ndi michembo yake, mbalame zili ndi zisa zake, koma mwana wa munthu alibe mpogoneka mutu womwe.” Pambuyo pake Yesu adauza munthu wina kuti, “Iwe, unditsate!” Iyeyo adati, “Ambuye mundilole ndiyambe ndakaika maliro a Atate anga.” Yesu adamuuza kuti, “aleke akufa aziika akufa anzao. Koma iwe, kalalike Ufumu wa Mulungu.” Munthu winanso adauza Yesu kuti, “ndidzakutsani, Ambuye, koma mundilole ndiyambe ndakatsanzikana ndi anthu kunyumba.” Yesu adati, “munthu amene wayambapo kulima, tsono nkumacheukiranso kumbuyo, Mulungu alibe naye ntchito mu ufumu wake.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, June 18, 2022

 

CHAKA CHA UKARISTIA [CORPUS CHRISTI] – CYCLE C

(Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.)

 

MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (CHIYAMBI); GENESIS 14: 18 – 20. (Adatenga buledi ndi vinyo.)

Ndipo Melkizedeki, mfumu ya ku Salemu, wansembe wa Mulungu Wopambanazonse, adabwera kwa Abramu atatenga Buledi ndi Vinyo. Adadalitsa Abramuyo, adati, “Mulungu Wopambanazonse, Mlengi wa kumwamba ndi dziko lapansi, akudalitse iwe Abramu. Atamandike Mulungu Wopambanazonse, amene adakupatsa mphamvu zogonjetsera adani ako onse.” Pamenepo Abramu adapereka kwa Melkizedeki chigawo chachikhumi cha zinthu zimene adaalandira.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 110: 01 – 04.

Ndiwe wansembe mpaka muyaya, unsembe wake wonga uja wa Melkizedeki.

Chauta adauza Mbuye wanga kuti,

“Khala ku dzanja langa lamanja,

mpaka nditasandutsa adani ako

kukhala ngati chopondapo mapazi ako.”

Ndiwe wansembe mpaka muyaya, unsembe wake wonga uja wa Melkizedeki.

Chauta adzakuza ufumu wako wamphamvu

kuchokera ku Ziyoni.

Adzati, “Khala mfumu yolamulira adani ako.”

Ndiwe wansembe mpaka muyaya, unsembe wake wonga uja wa Melkizedeki.

Anthu ako adzadzipereka mwaufulu.

pa tsiku limene udzaonetse mphamvu zako pa phiri loyera.

Anyamata ako adzabwera kwa iwe mu unyinji wao,

monga m'mene mame amabwerera m'mamawa.

Ndiwe wansembe mpaka muyaya, unsembe wake wonga uja wa Melkizedeki.

Chauta walumbira

ndipo sadzasintha maganizo ake akuti,

“Ndiwe wansembe mpaka muyaya,

unsembe wake wonga uja wa Melkizedeki.”

Ndiwe wansembe mpaka muyaya, unsembe wake wonga uja wa Melkizedeki.

--------------------------------------

MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO; 01 AKORINTO 11: 23 – 26. (Nthawi zonse mukamadya mkate umenewu, ndi kumwa chikho chimenechi, mumalalika imfa ya Ambuye.)

Inetu zimene ndidalandira kwa Ambuye ndi zimene nanenso ndidazipereka kwa inu, zakuti usiku umene adaperekedwa uja, Ambuye Yesu adaatenga mkate. Ndipo atathokoza Mulungu, adaunyemanyema nati, “ili ndi thupi langa limene likuperekedwa chifukwa cha inu. Muzichita zimenezi kuti muzindikumbukira.’’ Momwenso atatha kudya, Ambuye Yesu adatenga chikho nati, “Chikhochi ndi chipangano chatsopano chotsimikizika ndi magazi anga. Nthawi zonse mukamamwa chikho chimenechi, muzindikumbukira.’’ Pakuti nthawi zonse mukamadya mkate umenewu, ndi kumwa chikho chimenechi, mumalalika imfa ya Ambuye, mpaka adzabwerenso.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO.

Alleluia, Alleluia – Ine ndine chakudya chamoyo chimene chidatsika kuchokera Kumwamba. Munthu wodya chakudyachi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya. – Alleluia, Alleluia.

---------------------------------------

NYIMBO YA UKARISTIA (SEQUENCE)

 

O SIYONI UYAMIKE

Mbusa wabwino, Buledi weniweni,

Mbuye Yesu, mutichitire chisoni.

Muteteze, nkulowetsa

Nkhosa zanufe kumwamba.

 

1. O Siyoni, uyamike

Mpulumutsi wako, Mbuye,

Mfumu ndinso Mbusa wako.

 

2. Sudzafika kuimbira

Mlungu wako mokwanira.

Ukwezetu mawu ako.

 

3. Nkofunika ndithu lero

Kutama Buledi wamoyo,

Ngwopatsa moyo womwewo.

 

4.Tidziwa mosapeneka

Kuti Yesu anapatsa

Bulediyu kwa apositoli.

 

5. Tsono tisankhule nyimbo

Zokoma kwambiri lero

Ndi kuimba mwachimwemwe.

 

6. Misa itibweretsera

Tsiku lomwe la kupanga

Phwando loyerayerali.

 

7. Ndi Pasaka yatsopano

Ya Mfumu yatsopanonso

Miyambo yakale yatha.

 

8. Zalero zibadiritsa

Zakale, monga kuyera

M'mawa kuchotsatu mdima.

 

9. Yesu anatilamula

Kubwereza zomwe zija

Anazichita tsikuli.

 

10. Pomvera Yesu ifenso

Tisandutsa buledi n'vinyo

Pa nsembe yopulumutsa.

 

11. Buledi asanduka Thupi

Ndiponso vinyo Magazi

A Khristu, Ambuye athu.

 

12. Sitimvetsa, sitiona,

Koma ndithu tizimvera

Zozizwitsa zimenezi.

 

13. Buledi ndinso vinyo ali

Chizindikiro chophimba

Zazikulu zobisika.

 

14. Tidya Thupi la Ambuye

Ndi kumwa Magazi ake:

Akhala muziwirizi.

 

15. Aliyense amlandira

Wathunthudi, wosasweka,

Ndi wosagawika konse.

 

16. Nayo Buledi wa anjelo

Ngwa alendofe tsopano

Manna wotipatsa nyonga.

 

17. Mulungu wamphamvuzonse

Ndiponso wodziwa zonse,

Inu mutidyetsa pano.

 

18. Mutidyetsenso Kumwamba

M'phwando la anthu oyera.

Amen. Amen. Aleluya.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAWU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 09: 11b – 17. (Anthu onse aja adadya nakhuta.)

Anthu ambirimbiri ataona zimenezi, adamtsatira. Iye adawalandira bwino nayamba kulankhula nawo za ufumu wa Mulungu, nkumachiritsa odwala. Dzuwa lili pafupi kulowa, ophunzira khumi ndi awiri aja adadzauza Yesu kuti, “bwanji anthuwa azinyamuka tsopano, apite ku midzi ndi ku miraga ili pafupiyi, kuti akapeze malo ogona ndiponso chakudya, chifukwatu kuno nkuthengo.’’ Koma Yesu adawauza kuti, “inuyo apatseni chakudya.’’ Iwo adati, “tili ndi buledi msanu ndi nsomba ziwiri zokha. Kaya kapena tipite tikawagulire anthu onsewa chakudya?’’ Ndiye kuti amuna okha adaalipo ngati zikwi zisanu. Tsono Yesu adauza ophunzira ake kuti, “auzeni anthuwa akhale pansi m’magulumagulu, gulu lililonse anthu ngati makumi asanu.’’ Ophunzira aja adawakhalitsadi anthu onse aja pansi. Pambuyo pake Yesu adatenga buledi msanu uja ndi nsomba ziwiri zija, nayang’ana kumwamba, nkuthokoza Mulungu. Kenaka atanyemanyema bulediyo, adazipereka kwa ophunzira ake kuti agawire anthuwo. Anthu onse aja adadya nakhuta. Ndipo ophunzira aja adatola zotsala, nkudzaza madengu khumi ndi awiri.

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, June 11, 2022


CHAKA CHA UTATU WOYERA – CYCLE C
(Tiyamike Mulungu Atate ndi Mwana ndinso Mzimu Woyera.)

MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MIYAMBO; MIYAMBO 08: 22 – 31. (Lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake, Ine ndinalipo kale.)

Nzeru ya Mulungu imafuula kuti: “Chauta adandilenga ine nzeru pa chiyambi cha ntchito zake. Mwa ntchito zake zakalekale woyambilira ndinali ine. Ndidapangidwa masiku akalekale, pachiyambiyambi, dziko lapansi lisanalengedwe. Nyanja zozama zisanalengedwe, padakalibe akasupe odzaza ndi madzi, nkuti ine nditabadwa kale. Mapiri asanaumbidwe, magomo asanakhalepo, Mulungu anali atandilenga ineyo; lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake, lisanakhaleponso dothi loyamba la dziko lapansi. Ine ndinalipo kale, pamene ankakhazikitsa zakumwamba, pamene ankalemba mzere wa malire anyanja yozama, pamene ankaika thambo m'malo mwake, pamene ankatsekula akasupe a m’nyanja yozama, pamene ankaika malire a nyanja kuti madzi ake asabzole malirewo, pamene ankaika maziko a dziko lapansi. Nthawiyo nkuti ndili pambalipa ngati mmisiri wake, ndikumkondweretsa tsiku ndi tsiku, ndikusangalala pamaso pake nthawi zonse. Ndinkasangalala m’dziko lake lokhalamo anthu, ndi kumakondwa nawo ana a anthu.”

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 08: 04 – 05, 06 - 07, 08 – 09.

Chauta, Ambuye athu, dzina lanu ndi lotchuka pa dziko lonse lapansi.

Ndikamayang’ana ku thambo lanu limene mudapanga ndi manja anu,

Ndikamaona mwezi ndi nyenyezi zimene mudazikhazika kumeneko, ndimadzifunsa kuti,

“Kodi munthu nchiyani kuti muzimkumbukira, mwana wa munthu nchiyani kuti muzimsamalira?”

 

Chauta, Ambuye athu, dzina lanu ndi lotchuka pa dziko lonse lapansi.

Ndiyetu mudamlenga mochepera pang’ono kwa Mulungu amene,

Mudampatsa ulemerero ndi ulemu wachifumu,

Mudampatsa ulamuliro pa ntchito za manja anu,

Mudamgonjetsera zolengedwa zonse.

 

Chauta, Ambuye athu, dzina lanu ndi lotchuka pa dziko lonse lapansi.

Nkhosa, ng’ombe ndi nyama zakuthengo,

Mbalame zamumlengalenga, nsomba za m’nyanja,

Ndi zonse zoyenda pansi pa nyanja.

 

Chauta, Ambuye athu, dzina lanu ndi lotchuka pa dziko lonse lapansi.

 --------------------------------------

MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA 05: 01 – 05. (Tili pa mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.)

Abale, popeza kuti pakukhulupilira tapeza kuti ndife olungama pamaso pa Mulungu, ndiye kuti tili pa Mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Iyeyo ndiye amene adatitsekulira njira kuti pakukhulupilira tilandire mwai uwu umene Mulungu amapatsa mwaulere, umene takhazikikamo tsopano. Motero timakondwerera chiyembekezo chathu chakuti tidzalandilako ulemelero wa Mulungu. Koma sipokhapo ai, timakondweranso m’masautso athu. Pakuti tikudziwa kuti masautso amaphunzitsa munthu kupirira, kupirira kumabweretsa makhalidwe ovomerezedwa ndi Mulungu, ndipo makhalidwe ovomerezedwawo amabweretsa chiyembekezo. Chiyembekezo chimenechi munthu sichingamugwiritse fuwa la moto ai, pakuti Mulungu mwa Mzimu Woyera amene Iye adatipatsa, adadzaza mitima yathu ndi chikondi chake.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO.

Alleluia, Alleluia – Ulemu ukhale kwa Atate ndi Mwana ndi Mzimu Woyera, Mulungu amene alipo, amene analipo, amene alikudza. Alleluia, Alleluia.

-------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA; YOHANE 16: 12 – 15. (Zonse za Atate nzanga. Nchifukwa chake ndanena kuti adzakutenga zochokera kwa Ine, nadzakudziwitsani inu.)

Yesu adawauza ophunzira ake kuti: “ndili nawo mau ena ambiri oti ndikuuzeni, koma simungathe kuwamvetsa tsopano ayi. Koma akadzafika Mzimu wodziwitsa zoona uja adzakuphunzitsani zoona zonse. Pakuti sadzalankhula zochokera kwa Iye yekha ayi, koma zilizonse zimene Atate adzamuuze, ndizo zimene adzalankhula. Ndipo adzakudziwitsani zinthu zam’tsogolo. Adzandilemekeza, pakuti adzatenga zochokera kwa Ine nadzakudziwitsani. Zonse za Atate nzanga. Nchifukwa chake ndanena kuti adzatenga zochokera kwa ine, nadzakudziwitsani inu.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Friday, June 3, 2022


CHAKA CHA PENTEKOSTE – C

(Adawauzira mpweya wopatsa moyo)

MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA NTCHITO ZA ATUMWI: NTCHITO 02: 01 – 11. (Onse aja adadzazidwa ndi Mzimu Woyera, ndipo adayamba kulankhula.)

Pamene tsiku la chikondwerero cha Pentekoste lidafika, iwo onse anali pamodzi m’nyumba imodzi. Mwadzidzidzi kudamveka kuchokera kumwamba mkokomo ngati wa mphepo yaukali, nudzaza nyumba yonse imene ankakhalamo. Ndipo adaona ngati timalawi ta moto tooneka ngati malilime tikugawikana nkukhala pa iwo, aliyense kakekake. Onse aja adadzazidwa ndi Mzimu Woyera, ndipo adayamba kulankhula zilankhulo zachilendo, monga Mzimuyo ankawalankhulitsira. Tsono, m’Yerusalemu muja munali Ayuda ena, anthu okonda Mulungu, ochokera ku maiko onse a pa dziko lapansi. Pamene mkokomo uja udamveka, anthu ambirimbiri adasonkhana. Onse adadodoma, chifukwa aliyense mwa iwo ankawamva akulankhula chilankhulo chake. Adadabwa, nathedwa nzeru ndipo adati, “kodi onse akulankhulawa, si Agalileya? Nanga bwanji aliyense mwa ife akuwamva akulankhula chilankhulo chakwawo? Ena mwa ife ndi Aparti ndi Amedi ndi Aelami, ena ndi okhala ku Mesapotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya, Ku Frijiya ndi ku Pamfiliya, ku Ejipito, ndi ku madera a Libiya kufupi ndi ku Kirene, ena ndi alendo ochokera ku Roma, ndiye kuti Ayuda ndi ena otsata za Chiyuda. Enanso ndi Akrete ndi Aarabu, komabe tonse tikuwamva anthuwa akulankhula m’zilankhulo zathu za ntchito zazikulu za Mulungu.”

Mawu a Ambuye…Tithokoze Mulungu.

-------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 104: 01, 24, 24, 29 – 31. 

Tumizani Mzimu wanu, Ambuye, ndipo muwalitsenso dziko lonse lapansi.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,

Inu Chauta, Mulungu wanga, ndinu aakulu kwambiri,

Inu Chauta ntchito zanu zambiri,

Ndipo dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu

 

Tumizani Mzimu wanu, Ambuye, ndipo muwalitsenso dziko lonse lapansi.

 

Mukazichotsera mpweya, zimafa nkubwerera ku fumbi,

Mukatumiza mpweya wanu zimalengedwa,

Ndipo mumakonzanso maonekedwe a dziko lapansi.

 

Tumizani Mzimu wanu, Ambuye, ndipo muwalitsenso dziko lonse lapansi.

 

Ulemerero wa Chauta ukhalebe mpaka muyaya,

Chauta akondwe nazo ntchito zakezo,

Mapemphero anga amkomere Chauta,

Popeza kuti ndimakondwa mwa Iye.

 

Tumizani Mzimu wanu, Ambuye, ndipo muwalitsenso dziko lonse lapansi.

-------------------------

MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA: AROMA 08: 08 – 17. (Onse amene Mzimu wa Mulungu amawatsogolera, amenewo ndi ana a Mulungu.)

Abale, anthu oika mtima pa khalidwe limenelo, sangathe kukondweretsa Mulungu. Koma inu simulamulidwanso ndi khalidwe lanu lopendekera ku zoipa. Mumalamulidwa ndi Mzimu Woyera, ngati Mzimu wa Mulungu akhaladi mwa inu. Koma ngati munthu aliyense alibe Mzimu wa Khristu, iyeyu sali wake wa Khristu. Khristu akakhala mwa inu, ngakhale thupi lanu lidzafadi chifukwa cha uchimo, komabe mzimu wanu udzakhala ndi moyo, popeza kuti Mulungu wakuwonani kuti ndinu olungama pamaso pake. Ndipo Mzimu wa Mulungu, amene adaukitsa Yesu kwa akufa, akamakhala mwa inu, pamenepo, mwa Mzimu wake yemweyo, Mulungu adzapatsanso moyo matupi anu otha kufawa. Motero abale, tili ndi ngongole, komatu ngongole yake si yakuti tizigonjera khalidwe lathu lokonda zoipa, ndi kumachita chifuniro chake. Pakuti ngati m’moyo mwanu mutsata khalidwelo, mudzafa. Koma ngati ndi chithandizo cha Mzimu Woyera mupha zilakolako zanu zathupi, mudzakhala ndi moyo. Onse amene Mzimu wa Mulungu amawatsogolera, amenewo ndi ana a Mulungu. Pajatu Mzimu amene mudalandira, sakusandutsani akapolo, kuti muzikhalanso amantha ai. Koma Mzimuyo amakusandutsani ana a Mulungu, ndipo mwa mphamvu yake, popemphera kwa Mulungu timati, ‘Abba! Atate!’ Mzimu Woyera mwiniwakeyo ndi amene amavomerezana ndi mitima yathu kutsimikiza kuti ndife ana a Mulungu. Tsono ngati ndife ana a Mulungu, tidzalandira nso madalitso amene Iye akusungira anthu ake. Pamodzi ndi Khristu ifenso tidzalandira madalitso amene Mulungu anali atamsungira. Pakuti ngati timva zowawa pamodzi ndi Khristu, tidzalandiranso ndi ulemerero womwe pamodzi naye.

Mawu a Ambuye…Tithokoze Mulungu.

-------------------------

NYIMBO YA PENTEKOSTE (SEQUENCE) [Nyimboyi itha kunenedwa kapena kuyimbidwa]

 

1.      Bwerani Mzimu Woyera,

Tumizani kuwala kwanu,

Kufumira kumwambako.

 

2.      Bwerani, Tate wa amphawi,

Bwerani, wopatsa mphatso,

Inu muuni wa mitima.

 

3.      Ndinu Msangalatsi ndithu,

Woyendera mitima yathu,

Kuti mudzaithuzitsa.

 

4.      Pa ntchito ndinu Mpumulo,

Mumatichotsera kutentha,

Ndi kutsangula misozi yathu.

 

5.      Ndinu kuwala kokoma,

Dzazani mitima yathu,

Ya ife anthu okumverani.

 

6.      Mutapanda kudzamthandiza,

Munthu sangapeze kanthu,

Zonse zidzamuipira.

 

7.      Tsukani zoipa zathu,

Dzatsirireni zouma,

Chiritsani mabala athu.

 

8.      Dzafewetseni zolimba,

Funditsani zozizira,

Lungamitsani zokhota.

 

9.      Tipatseni anthu anufe,

Okhulupirira Inu,

Mphatso zisanu ndi ziwiri.

 

10.  Kometsani makhalidwe athu,

Katifikitseni kumwamba,

Kukadala nthawi zonse,

Amen.

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO.

Alleluia, Alleluia – Bwerani Mzimu Woyera, mudzaze m’mitima ya anthu okhulupirira ndipo chikondi chanu chikhazikike mwa iwo. – Alleluia, Alleluia.

-------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA: YOHANE 14: 15 – 16, 23 – 26. (Mzimu Woyera ndiye adzakuphunzitseni zonse.)

Yesu adawauza ophunzira ake kuti: “Ngati mundikonda, muzidzatsata malamulo anga. Pamenepo ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthawi zonse.” Yesu adati, “Ngati munthu andikonda, adzatsata zimene ndanena Ine. Atate anga adzamkonda, ndipo Ife tidzabwera nkukhazikika mwa ife. Munthu amene sandikonda, satsata zimene ndanena Ine. Mau amene mulikumvawa si angatu ai, koma ndi a Atate amene adandituma. Zimenezi ndakuuzani ndikadali nanu. Koma Nkhoswe ija, Mzimu Woyera amene Atate adzamtuma m’dzina langa, ndiye adzakuphunzitseni zonse, ndipo adzakukumbutsani zonse zimene ndidakuuzani.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...