Saturday, November 30, 2024

LAMULUNGU LA 1 MU NYENGO YA ADVENTI – C

LAMULUNGU LA 1 MU NYENGO YA ADVENTI – C.

“Tikonzekere Kubwera Kwa Ambuye.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI YEREMIYA: YEREMIYA 33:14 – 16. (Ndidzaphukitsa nthambi yolungama kuchokera kubanja kwa Davide).

 

Chauta akutinso, “akubwera masiku pamene ndidzachitadi zimene ndidalonjeza anthu a ku Israele ndi aku Yuda. Masiku amenewo ndiponso pa nthawi yomweyo, ndidzaphukitsa nthambi zolungama kuchokera kubanja la Davide. Munthuyo adzachita zabwino ndi zolungama mdziko lonse. Nthawi imeneyo anthu a ku Yuda adzapulumuka, ndipo a ku Yerusalemu adzakhala pa mtendere. Motero mzindawo udzakhala ndi dzina loti, ‘Chauta ndiye chipulumutso chathu.’”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 24: 04 – 05, 08 – 09, 10, 14.  

 

Ndikupereka mtima wanga kwa Inu Chauta.

 

Mundidziwitse njira zanu, Inu Chauta,

Mundiphunzitse kuchita kufuna kwanu,

Munditsogolere m’choona chanu ndi kundilangiza,

Pakuti Inu ndinu Mulungu Mpulumutsi wanga,

Ndimadalira Inu Masiku onse.

 

Ndikupereka mtima wanga kwa Inu Chauta.

 

Chauta ndi wabwino ndi wolungama,

Nchifukwa chake amaphunzitsa ochimwa njira zake,

Amatsogolera anthu odzichepetsa kuti achite zolungama,

Amawaphunzitsa njira zake.

 

Ndikupereka mtima wanga kwa Inu Chauta.

 

Njira zonse za Chauta ndi za chikondi chosasinthika,

Nzokhulupirika kwa anthu osunga chipangano chake ndi malamulo ake,

Chauta amapalana chibwenzi ndi anthu omvera Iye,

Ndipo amawadziwitsa chipangano chake.

 

Ndikupereka mtima wanga kwa Inu Chauta.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA ATESALONIKA: 1 ATESALONIKA 03: 12 – 04. (Ambuye adzalimbitse mitima yanu kuti idzakhale yangwiro pamene Yesu adzabweranso).

 

Abale, Ambuye akulitsirekulitsire kukondana kwanu, ndiponso chikondi chanu cha pa anthu onse, monga momwe chikondi chathu cha pa inu chikukulirakulira. Motero Iye adzalimbitsa mitima yanu kuti idzakhale yangwiro ndi yoyera pamaso pa Mulungu Atate athu, pamene Ambuye Yesu adzabweranso pamodzi ndi oyera ake onse. Potsiriza tsono, abale, tifuna kukupemphani kanthu. Mudalandira kwa ife mau onena za m’mene muziyendera kuti mukondweretse Mulungu. Mukutsata mayendedwe otere kumene, koma tikukupemphani kolimba m’dzina la Ambuye Yesu kuti muchite zimenezi koposa kale. Pakuti mukudziwa malangizo amene tidakupatsani ochokera kwa Ambuye Yesu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – SALIMO 85:8.

Alleluia, Alleluia Tiwonetseni chikondi chanu chosasinthika, Inu Chauta, ndipo mutipulumutse. Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 21: 25 – 28, 34 – 36 (Chipulumutso chanu chayandikira).

 

Pa nthawi yomweyo, Yesu anati kwa ophunzira ake: “padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, pa mwezi ndi pa Nyenyezi. Pansi pano anthu a mitundu yonse adzada nkhawa nkutha nzeru, pomva kukokoma kwa nyanja ndi mafunde ake. Ena adzakomoka ndi mantha poyembekezera zimene zikudza pa dziko lonse lapansi, pakuti mphamvu zonse zakuthambo zidzagwedezeka. Pamenepo anthu adzaona Mwana wa Munthu akubwera pa mitambo, ali ndi mphamvu ndi ulemerero waukulu. Zimenezi zikadzayamba kuchitika, mudzaimirire nkukweza mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira. Chenjerani kuti mitima yanu ingapusitsidwe ndi maphwando, kuledzera, ndi kudera nkhawa za moyo uno, kuti tsikulo lingakufikireni modzidzimutsa. Pajatu lidzawagwera ngati nsampha anthu onse a pa dziko lonse lapansi. Muzikhala maso tsono, ndipo muzipepemphera nthawi zonse, kuti mukhale ndi mphamvu zopulumukira ku zonsezi zimene ziti zidzachitike, ndiponso kuti mukaimirire pamaso pa Mwana wa Munthu.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, Ambuye atiwuza kuti, tizikhala maso ndi kumapemphera nthawi zonse. Tiyeni tsono, tikweze mitima kumwamba, kuti Ufumu wa Mulungu udze m’dziko lonse lapansi:

 

1.     Tipempherere Mpingo woyera wa Mulungu, kuti maphunzitso ake ndinso ntchito zake ziwutse chikhulupiriro, m’mitima ya anthu onse.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Tipempherere anthu a mafuko onse kuti atsekule mitima yawo ndi kulandira Mthenga Wabwino.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Tipempherere anthu odwala ndi onse amene ali m’mavuto, kuti asataye mtima, koma apeze anzao achifundo owathandiza.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Tipempherere onse amene ali ndi ana, kuti ayesetse kuutsa chikhulupiriro m’mitima ya ana aowo, powafotokozera za kudza kwa Mpulumutsi.
Tikupemphani, mutivomereze.

5.     Tidzipempherere ife tomwe tili muno, kuti Mulungu akulitsirekulitsire kukondana kwathu, ndiponso chikondi chathu cha pa anthu onse.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Mulungu Atate athu, mutiphunzitse kuyembekeza mosafookera kubwera kwa Mwana wanu, kuti akadzagogoda pakhomo pathu, adzatipeze tili maso ndikupemphera. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, November 23, 2024

Chaka cha Yesu Khristu Mfumu – B.

Chaka cha Yesu Khristu Mfumu – B.

“Ndife ake a Yesu Khristu.”

 

MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI DANIELE: DANIELE 07: 13 – 14. (Ulamuliro wake ndi wamuyaya, sudzatha).

 

Pamene ndinkaonabe zinthu m’masomphenya usiku, ndidaona wina ngati mwana wa munthu akutsika ndi mitambo yakumwamba. Atayandikira Mkulu amene analipo chikhalire uja, ena adamperekeza Mkuluyo. Pamenepo adampatsa ulamuliro, ulemerero ndi ufumu, kuti anthu a mitundu yonse, a mafuko onse ndi a zilankhulo zosiyasiyana azimtumikira. Ulamuliro wake ndi wamuyaya, sudzatha. Ufumu wake ndi wosagawikana, ndipo sudzaonongedwa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 93: 01 – 02, 05.

 

Chauta ndiye Mfumu. Wavala za ulemerero.

 

Chauta ndiye mfumu,

Wavala ulemerero, wavala mphamvu ngati lamba,

Iye adakhazikitsa dziko lapansi,

Silidzagwedezeka konse.

 

Chauta ndiye Mfumu. Wavala za ulemerero.

 

Mpando wanu waufumu, Inu Chauta,

Mudaukhazikitsa kuyambira makedzana,

Inu ndinu amuyaya.

 

Chauta ndiye Mfumu. Wavala za ulemerero.

 

Malamulo anu ndi osasinthika, Inu Chauta,

Nyumba yanu ndi yoyera mpaka muyaya.

 

Chauta ndiye Mfumu. Wavala za ulemerero.

-------------------------------------------------------------------------

 

MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA CHIBVUMBULUTSO: CHIBVUMBULUTSO 01: 05 – 08. (Mfumu yolamula mafumu onse a pa dziko lapansi, adatisandutsa mafumu, kuti tizitumikira Mulungu ngati mtundu wa ansembe).

 

Akukomereninso mtima ndi kukupatsani mtendere Yesu Khristu, mboni yokhulupirika, amene ali woyambirira kulandira moyo waulemerero, amenenso ali Mfumu yolamula mafumu onse a padziko lapansi. Iyeyo amatikonda, ndipo ndi magazi ake adatimasula ku machimo athu. Iye adatisandutsa mafumu, kuti tizitumikira Mulungu Atate ake modzipereka ngati mtundu wa ansembe. Motero Yesu Khristuyo alandire ulemerero ndi mphamvu zolamulira mpaka muyaya. Amen. Mvetsetsani!  Akubwera pa mitambo! Aliyense adzamuona, amene adamubaya aja nawonso adzamuwona. Ndipo anthu a mitundu yonse pansi pano adzalira chifukwa cha Iye. Nzoonadi zimenezi. Ndithudi! Ine ndine Woyamba ndiponso Wotsiriza, akutero Ambuye Mulungu, Mphambe, amene alipo, amene analipo kale, amene alikudza.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MARKO 11: 09, 10.

 

Alleluia, Alleluia – Ngwodala amene alikudza m’dzina la Ambuye. Udalitsidwe Ufumu wa atate athu Davide umene ulikudza tsopano. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA: YOHANE 18: 33 – 37. (Mwanena nokha kuti ndine Mfumu.)

 

Pa nthawi yomweyo, Pilato adalowanso m’nyumba yake ija, naitana Yesu. Adamufunsa kuti, “kodi iwe, ndiwe Mfumu ya Ayuda?” Yesu adati, “kodi mukunena zimenezi mwa inu nokha, kapena ena adakuuzani za Ine?” Pilato adati, “ine ndi Myuda kodi? Anthu a mtundu wako womwe ndiponso akulu a ansembe ndiwo akupereka kwa ine. Udachita chiyani?” Yesu adayankha kuti, “ufumu wanga si wapansipano ai, Ufumu wanga ukadakhala wapansipano, bwenzi anyamata anga atamenya nkhondo kuti ndisaperekedwe kwa akulu a Ayuda. Komatu ai, ufumu wanga si wansipano.” Pilato adati, “tsono ndiye kuti ndiwedi Mfumu, ati?” Yesu adati, “Mwanena nokha kuti ndine Mfumu. Ine ndidabwera pansi pano ndipo ndidababwa kuti ndidzachitire umboni choona. Aliyense wokonda choona amamva mau anga.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, mogwirizana ndi Yesu Khristu mtsogoleri wathu, tipemphe Atate athu a Kumwamba kuti Ufumu wao udze m'dziko lonse lapansi:

 

1.     Atate, muthandize Mpingo wanu kuti uunikire anthu onse pakuwatumikira modzichepetsa, ndipo onse agonjere Ufumu wanu wachikondi.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atate, muwongolere akulu onse olamulira maiko, kuti ayesetse kukhazikitsa chilungamo ndi mtendere pakati pa anthu ao.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Atate, muchirikize akhristu amene akuzunzidwa chifukwa chokhulupirira Inu, kuti akondwere pozindikira kuti Ufumu wa Kumwamba ndi wao.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Atate, mutidalitse ife tomwe, kuti tikhale a mtima umodzi ndi Mwana wanu potumikira anthu anzathu, tigwirizane tonse mwa ubale.
Tikupemphani, mutivomereze.


Mulungu Atate athu, tonse tikuti, “Dzina lanu lilemekezedwe ponseponse ndipo Ufumu wanu ukhazikike m’mitima ya anthu onse.” Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, November 16, 2024

LAMULUNGU LA 33 PA CHAKA – B.

LAMULUNGU LA 33 PA CHAKA – B.

“Potha Dziko Lino Kudzaoneka Zotani?”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI DANIELE: DANIELE 12: 01 – 03. (Pa nthawiyo anthu ako adzapulumuka).

 

Mulungu adalankhulitsa mneneri Daniele kuti, “pa nthawi imeneyo Mikaele, mngelo wamkulu amene amalonda anthu akwanu, adzafika. Nthawi imeneyo idzakhala ya mavuto oopsa amene sadaonekepo nkale lonse, chilengere cha mtundu woyamba wa anthu mpaka nthawi imeneyo. Pa nthawiyo anthu ako adzapulumuka, onse amene maina ao adalembedwa m’buku. Ambiri mwa amene agona m’nthaka yafumbi adzauka. Ena adzapita ku moyo wosatha ena ku manyazi ndi ku chilango chosatha. Ndipo amene adatsogolera anthu kuti ambiri m’njira ya chilungamo adzawala ngati Nyenyezi mpaka muyaya.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 16: 05, 08 – 11.

 

Mundisunge Inu Mulungu, pakuti ndikuthawira kwa inu.

 

Chauta ndiye chuma changa ndi cholowa changa,

Tsogolo langa lili m’manja mwanu,

Nthawi zonse ndimalingalira za Chauta,

Popeza kuti ali ku dzanja langa lamanja,

Palibe amene angandiopse konse.

 

Mundisunge Inu Mulungu, pakuti ndikuthawira kwa inu.

 

Nchifukwa chake mtima wanga ukukondwa,

Ndipo m’katikati mwangamu ndikusangalala,

Thupi langanso lidzakhala pabwino,

Chifukwa simudzandisiya ku malo a anthu akufa,

Simudzalola kuti wokondedwa wanune ndikaole kumeneko.

 

Mundisunge Inu Mulungu, pakuti ndikuthawira kwa inu.

 

Mumandiwonetsa njira ya ku moyo,

Ndimapeza chimwemwe chachikulu kumene kuli Inu,

Ndidzasangalala mpaka muyaya ku dzanja lanu lamanja.

 

Mundisunge Inu Mulungu, pakuti ndikuthawira kwa inu.

-------------------------------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA AHEBRI: AHEBRI 10: 11 – 14, 18. (Mwa nsembe imodzi yomweyo wasandutsa angwiro kwamuyaya onse amene Iye akuwayeretsa).

 

Abale, wansembe aliyense amaimirira tsiku ndi tsiku nkumatumikira, ndipo amapereka nsembe imodzimodzi mobwerezabwereza. Komabe nsembe zimenezi sizingathe konse kuchotsa machimo. Koma Khristu adapereka nsembe imodzi yokha yochotsera machimo onse. Ndipo ataipereka, adakhala ku dzanja lamanja la Mulungu. Kumeneko akudikira tsono kuti Mulungu amsandutse adani ake kukhala ngati chopondapo mapazi ake. Mwa nsembe imodzi yomweyo wasandutsa angwiro kwamuyaya onse amene Iye akuwayeretsa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – LUKA 21: 36.

Alleluia, Alleluia – Muzikhala maso tsono, ndipo muzipemphera nthawi zonse, kuti mukhale ndi mphamvu ndiponso kuti mukaimirire pamaso pa Mwana wa Munthu. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 13: 24 – 32. (Iye adzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mbali zonse).

 

Yesu adawauza ophunzira ake kuti, “masiku amenewo, mavutowo atatha, dzuwa lidzada, mwezi uzaleka kuwala. Nyenyezi zidzagwa kuchokera kuthambo, ndipo mphamvu zamumlengalenga zidzagwedezeka. Pamenepo anthu adzaona Mwana wa Munthu akubwera pa mitambo, ali ndi mphamvu zazikulu ndi ulemerero. Tsono Iye adzatuma angelo ake kuti akasonkhanitse osankhidwa ake kuchokera ku mbali zonse, kuyambira ku malekezero ena a dziko lapansi mpaka ku malekezero ake enanso. Phunziraniko kwa mkuyu. Mukamaona kuti nthambi zake zayamba kukhala zanthete ndipo masamba akuphuka, mumadziwa kuti chilimwe chayandikira. Momwemonso mukadzaona zija ndanenazi zikuchitika, mudzadziwe kuti Mwana wa Munthu ali pafupi, ali pakhomo penipeni. Ndithu ndikunenetsa kuti zonsezi zidzaoneka anthu a mbadwo unowo asanamwalire onse. Thambo ndi dziko lapansi zidzatha, koma mau anga sadzatha mphamvu konse. Koma za tsiku lake kapena nthawi yake, palibe amene amadziwa. Angelo omwe akumwamba sadziwa. Ngakhale Ineyo Mwanane sindidziwa, amadziwa ndi Atate okha basi.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, tamva lero kuti Yesu adzabweranso ndi ulemerero. Tiyeni tipemphe Mulungu Atate athu kuti alimbitse chikhulupiriro m’mitima ya anthu onse:

 

1.     Tipempherere akhristu onse kuti aonetse anzao mtima wachifundo ndipo mayendedwe ao atsimikize kuti moyo wosatha ulipodi Kumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Anthu amene maso ao anaima pa zinthu za pansi pano, maso ao atsekuke, azindikire kuti kwao kwenikweni ndi Kumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu odwala ndi ena onse amene ali m’mavuto, akhale ndi chikhulupiriro cholimba, poyembekezera tsiku lodzabwera Ambuye.

Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tomwe, kuti tilimbikire kuchita ntchito zabwino, pozindikira kuti Ufumu wa Mulungu ulikukhazikikadi m’mitima ya athu.
Tikupemphani, mutivomereze.

Mulungu Atate athu, mutiwunikire ndi kuwala kwa Mzimu wanu Woyera kuti tikukondweretseni pa zonse, polakalaka kudza kwa Mpulumutsi wathu, Yesu Khristu Ambuye athu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, November 9, 2024

LAMULUNGU LA 32 PA CHAKA – B

LAMULUNGU LA 32 PA CHAKA – B.

“Ufulu Umaitana Ufulu Unzake.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LOYAMBA LA MAFUMU: 01 MAFUMU 17: 10 – 16. (“Pitani, mundiphikire kakeke.” Maiyo, nakachitadi monga momwe adaanenera Eliya).

 

Eliya adanyamuka napita ku Zarefati. Atafika pa chipata cha mzindawo, adangoona mai wamasiye akutola nkhuni. Tsono adaitana maiyo namuuza kuti, “patseniko madzi pang’ono, ndimwe.” Pamene mai uja ankapita kukatunga madziwo, Eliya adamuitananso namuuza kuti, “mundintengerekonso kabuledi.” Apo maiyo adati, “pali Chauta, Mulungu wanu, ine sindidaphike kanthu kalikonse, koma ndili ndi ufa pang’ono m’mbiya, ndi mafuta pang’ono m’nsupa. Tsono ndikutola nkhuni zoti ndikaphikire kaufako, kuti ndikadye ine ndi mwana wanga, kenaka kufa kukhala komweko.” Koma Eliya adauza maiyo kuti, “musade nkhawa. Pitani, mukachite monga mwaneneramo. Koma poyamba mutapeko kaufa pang’ono, mundiphikire kakeke, mubwere nako kuno. Pambuyo pake mukaphikenso kuti mudye inuyo ndi mwana wanu. Chauta, Mulungu wa Aisraele, akunena kuti, ‘ufa umene uli m’mbiyawo sudzatha, mafutanso amene ali m’nsupawo sadzatha, mpaka tsiku limene Chauta adzagwetse mvula pa dziko lapansi.’” Tsono maiyo adapita, nakachitadi monga momwe adaanenera Eliya. Maiyo ndi Eliya ndiponso onse a pa banja la maiyo adadya ufawo masiku ambiri. Ufa umene unali m’mbiyamo sudathe, mafuta amene anali m’nsupawo sadathenso, monga momwe Chauta adaalankhulira kudzera mwa Eliya.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 146: 07 – 10.

 

Mtima wanga, tamanda Chauta.

 

Amasunga malonjezo ake nthawi zonse,

Amachitira anthu opsinjidwa zolungama,

Amawapatsa chakudya anthu anjala,

Chauta amamasula am’ndende.

 

Mtima wanga, tamanda Chauta.

 

Chauta amatsekula maso a anthu osapenya,

Chauta amakweza anthu otsitsidwa,

Chauta amakonda anthu ochita chilungamo,

Chauta amateteza alendo.

 

Mtima wanga, tamanda Chauta.

 

Amachirikiza mkazi wamasiye ndiponso mwana wamasiye,

Koma njira za anthu oipa amazipotoza,

Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako, iwe Ziyoni,

Adzalamulira ku mibadwo yonse.

 

Mtima wanga, tamanda Chauta.

-------------------------------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA AHEBRI: AHEBRI 09: 24 – 38. (Khristu adaperekedwa nsembe kamodzi kokha, kuti asenze machimo a anthu).

 

Abale, Khristu sadalowe m’malo opatulika omangidwa ndi anthu, malo ongofanizira malo enieni opatulika a Kumwamba. Iye adapita Kumwamba kwenikweniko, kuti tsopano aziwonekera pamaso pa Mulungu chifukwa cha ife. Mkulu wa ansembe onse amalowa m’malo Opatulika Kopambana chaka ndi chaka atatenga magazi amene sali ake. Koma Khristu sadalowe Kumwamba kuti azidzipereka nsembe kawirikawiri. Zikadatero, akadayenera kumamva zowawa kawirikawiri chilengedwere cha dziko lapansi. Koma monga zilirimu, waoneka kamodzi kokha pakutha pake pa nthawi yotsiriza, kuti achotse uchimo pakudzipereka yekha nsembe. Munthu aliyense amafa kamodzi kokha, pambuyo pake nkumaweruzidwa. Momwemonso Khristu adaperekedwa nsembe kamodzi kokha, kuti asenze ndi kuchotsa machimo a anthu ambiri. Adzaonekanso kachiwiri, osati kuti adzachotsenso uchimo ai, koma kuti adzapulumutse anthu amene akumuyembekeza.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 05: 03.

Alleluia, Alleluia – Ngodala anthu amene ali osauka mumtima mwao, pakuti Ufumu wakumwamba ndi wao. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO 12: 38 – 44. (Mai wamasiye wosaukayu waponyamo koposa anthu ena onsewa).

 

Pamenepo Yesu ankawaphunzitsa, adati, “chenjera nawoni aphunzitsi a Malamulo. Amakonda kuyenda atavala mikanjo yaitali, ndi kuti anthu aziwalonjera mwaulemu pa misika. Amakonda mipando ya ulemu kwambiri m’nyumba zamapemphero, ndiponso malo olemekezeka pa maphwando. Koma amawadyera chuma chao azimai amasiye, nkumapemphera mapemphero ataliatali monyengezera. Anthu amenewa adzalangidwa koposa.” Tsiku lina Yesu adaakhala pansi nkuyang’anana ndi bokosi loponyamo ndalama zopereka ku Nyumba ya Mulungu. Ankayang’anitsitsa m’mene anthu ankaponyera ndalama zao. Anthu ambiri achuma ankaponyamo ndalama zambiri. Koma padafika mai wina wamasiye, wosauka. Iyeyu adangoponyamo tindalama tiwiri. Tsono Yesu adaitana ophunzira ake nawauza kuti, “ndithu ndikunenetsa kuti mai wamasiye wosaukayu waponyamo koposa anthu ena onsewa, amene akuponya ndalama m’bokosimu. Chifukwa ena onsewa angoponyamo zimene atapa pa zochuluka zimene ali nazo. Koma maiyu, mwa umphawi wake, waponyamo zonse zimene anali nazo, ngakhale zimene akadagulira chakudya.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pakuti Mulungu ngwachifundo, ifenso tiziwonetsa mtima womwewo pakupempherera anthu onse:

 

1.     Tipempherere atsogoleri a Eklezia kuti asenze udindo wao molimbika, azitumikira akhristu anzawo modzichepetsa ndi mosaopa zowawa.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Tipempherere akhristu onse kuti aonetse mtima wachifundo posamala Mpingo wa Mulungu ndi pothandiza anzawo mzosowa zawo.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Tipempherere madotolo, anesi ndi anamwino, kuti onse agwire ntchito yao modzipereka ndi mwachikondi.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Tidzipereke ife tomwe tili muno, kuti tikhale achangu pa ntchito zothandiza Mpingo wa Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.

Mulungu Atate athu, mutikomere mtima pomvera mapemphero athuwa. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, November 2, 2024

LAMULUNGU LA 31 PA CHAKA – B.

 

LAMULUNGU LA 31 PA CHAKA – B.

“Kodi Mwa Malamulo onse, Lamulo Loposa Nliti”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA DEUTORONOMO: DEUTORONOMO 06: 02 – 06. (“Mverani, Inu Aisraele, muzikonda Chauta, ndi mtima wanu wonse”).

 

Mose analankhula ndi anthu ake nawauza kuti, “muzikaopa Chauta, Mulungu wanu, ndipo muzikamvera malamulo ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsaniwa, kuti pakutero mukhale moyo nthawi yaitali. Inu Aisraele, mutchere khutu, ndipo muchenjere, mumveredi malamulowa. Tsono zinthu zidzakuyenderani bwino, ndipo mudzakhala mtundu wochuluka zedi ndi kumakhala m’dziko lamwanaalirenji, monga momwe Chauta, Mulungu wa makolo anu, adakulonjezerani. Mverani, Inu Aisraele, Chauta Mulungu wanu, ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse ndi mphamvu zanu zonse. Muziwasunga bwino mumtima mwanu malamulo amene ndikukupatsani lerowa.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 18: 02 – 04, 47, 51.

 

Ndimakukondani Chauta, Inu mphamvu zanga.

 

Ndimakukondani Chauta, inu mphamvu zanga,

Chauta ndiye thanthwe langa, linga langa ndi Mpulumutsi wanga,

Ndiye Mulungu wanga, ndi thanthwe langa limene ndimathawirako,

Ndiye chishango changa, ndiye Mtetezi wanga, ndiye linga langa,

Ndimaitana Chauta, amene ayenera kumtamanda,

Ndipo amandipulumutsa kwa adani anga.

 

Ndimakukondani Chauta, Inu mphamvu zanga.

 

Chauta ndi wamoyo. Litamandike thanthwe langa,

Alemekezeke Mulungu wondipulumutsa,

Amathandiza mfumu yake, kuti izipambana,

Amaonetsa chikondi chake chosasinthika kwa wodzozedwa wake.

 

Ndimakukondani Chauta, Inu mphamvu zanga.

-------------------------------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA AHEBRI: AHEBRI 07: 23 – 28. (Yesu ngwamuyaya, motero unsembe wake ngwosasinthika).

 

Abale, ansembe akale aja anali ambiri, chifukwa ankafa, sankatha kupitirira ndi udindo waowo. Koma Yesu ngwamuyaya, motero unsembe wake ngwosasinthika. Nchifukwa chake angathe kuwapulumutsa kwathunthu anthu amene akuyandikira kwa Mulungu kudzera mwa Iye, pakuti Iyeyo ali ndi moyo nthawi zonse kuti aziwapempherera. Tsono padaafunika kuti tikhale naye wotere mkulu wa ansembe: woyera mtima, wopanda choipa kapena chodetsa chilichonse, wosiyana ndi anthu ochimwa, ndiponso wokwezedwa kubzola zonse zakumwambaku. Yesu ameneyu sali ngati akulu a ansembe ena aja. Palibe chifukwa chakuti tsiku ndi tsiku azipereka nsembe poyamba chifukwa cha machimo ake, kenaka chifukwa cha machimo anthu. Zimenezi adachitiratu kamodzi kokha, pakudzipereka yekha ngati nsembe. Malamulo a Mose amaika anthu amene ali ndi zofooka, kuti akhale akulu a ansembe onse. Koma mau a lumbiro la Mulungu lija limene lidabwera pambuyo pa Malamulowo, adaika Mwana wake, amene wakhala wangwiro kwamuyaya kuti akhale mkulu wa ansembe onse.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 14: 23.

Alleluia, Alleluia – Ngati munthu andikonda, adzatsata zimene ndanena Ine. Atate anga adzamkonda, ndipo Ife tidzabwera nkukhazikika mwa iye. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO 12: 28 – 34. (Uzikonda Chauta, Mulungu wako. Uzikonda mnzako).

 

Mphunzitsi wina wa Malamulo adawamva akutsutsana. Ataona kuti Yesu wawayankha bwino Asaduki aja, adadza pafupi, namufunsa kuti, “kodi mwa malamulo onse, lalikulu ndi liti?” Yesu adamuyankha kuti, “lamulo lalikulu ndi ili, tamverani, inu Aisraele, Chauta, Mulungu wathu, Iye yekha ndiye Mulungu. Motero, uzikonda Chauta, Mulungu wakoyo, ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mphamvu zako zonse. Lamulo lachiwiri lake ndi ili, uzikonda mnzako monga momwe umadzikondera iwe wemwe. Palibe lamulo lina loposa malamulo amenewa.” Mphunzitsi wa Malamulo uja adati, “ai, mwayankha bwino, Aphunzitsi. Monga mwaneneramo, nzoonadi kuti Mulungu ndi mmodzi yekhayo, ndipo palibe winanso koma Iye yekha. Mwalondolanso ponena chinthu chopambana ndicho kumkonda Mulungu ndi mtima wonse, ndi nzeru zonse, ndi mphamvu zonse, ndiponso kukonda mnzako monga umadzikondera iwe wemwe. Kuteroko nkoposa kupereka nsembe zopsereza ndiponso nsembe zina zonse.” Yesu adaona kuti munthuyo wayankha mwanzeru. Tsono adamuuza kuti, “iwe suli kutali ndi Ufumu wa Mulungu.” Ndipo kuyambira apo panalibenso wina woti ayesere kumufunsa kanthu.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pakuti Mulungu amatikonda modabwitsa, timupemphe kuti adzaze mitima yathu ndi ya anthu onse ndi mzimu wake wachikondi:

 

1.     Tipempherere akhristu onse kuti aonetse mtima wachikondi pa moyo wao wonse, makamaka pomathandiza anzao osauka.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Tipempherere atsogoleri a Mpingo kuti aongolere anthu ao m’njira ya chikondi ndi kudzetsa ubale weniweni pakati pa anthu.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Tipempherere anthu odwala, ovulala ndi onse amene akuvutika kuti apeze anzao achifundo odzawasamala ndi kuwalimbitsa mtima.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tomwe a m'Parishi ino, kukondana kwathu kupite m’tsogolo, kusonyeza kuti Mbuye akukhaladi pakati pathu.
Tikupemphani, mutivomereze.

Mulungu wathu, popereka kwa Inu mapemphero athuwa, tikukutchulani kuti, “Atate” pokhulupirira chikondi chanu chosasinthika. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...