Saturday, September 28, 2024

LAMULUNGU LA 26 PA CHAKA – B

LAMULUNGU LA 26 PA CHAKA – B.

“Tileke Makhalidwe Akaduka ndi Akudzikonda.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA NUMERI: NUMERI 11: 25 – 29. (Kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikadakondwa anthu onse a Chauta akadakhala aneneri).

 

Chauta adatsika mu mtambo nayamba kulankhula ndi Mose. Ndipo adatengapo mzimu umene unali pa Moseyo nauika pa akuluakulu makumi asanu ndi awiriwo. Koma sadapitirire kulosako. Anthu awiri adatsalira m’mahema, wina anali Elidadi, wina Meladi, ndipo mzimu udakhala pa iwowo. Anali nao m’gulu la olembedwa aja, koma sadapite nao ku chihema chamsonkhano, motero ankalosera m’mahema. Ndiye mnyamata wina adathamanga nakauza Mose kuti, “Elidadi ndi Meladi akulosa kumahemaku.” Apo Yoswa, mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose, mmodzi mwa anthu ake osankhidwa aja, adati, “Mbuyanga Mose, aletseni amenewo.” Koma Mose adamuuza kuti, “kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikadakondwa anthu onse a Chauta akadakhala aneneri, ndipo Chauta akadaika mzimu wake pa iwo.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 19: 08, 10, 12 – 14.

 

Malangizo a Chauta amasangalatsa mtima.

 

Malangizo a Chauta ndi olungama,

Amasangalatsa mtima,

Malamulo a Chauta ndi olungama,

Amapatsa mtima womvetsa.

 

Malangizo a Chauta amasangalatsa mtima.

 

Kuwopa Chauta ndiye chinthu changwiro,

Chimakhala mpaka muyaya,

Chiweruzo cha Chauta nchoona,

Ncholungama nthawi zone.

 

Malangizo a Chauta amasangalatsa mtima.

 

Malamulo anu amandiwunikira ine mtumiki wanu,

Powasunga ndimalandira mphotho yaikulu,

Nanga ndani angathe kudziwa zolakwa zonse?

Inu Chauta, mundichotsere zolakwa zanga zobisika.

 

Malangizo a Chauta amasangalatsa mtima.

 

Musalole kuti ine mtumiki wanu ndizichimwa dala,

Kulakwa koteroku ndisakutsate,

Tsono ndidzakhala wangwiro wopanda mlandu wa uchimo waukulu.

 

Malangizo a Chauta amasangalatsa mtima.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA YAKOBE: YAKOBE 05: 01 – 06. (Chuma chanu chaola).

 

Mverani tsono, inu anthu achumanu. Lirani ndi kufuula chifukwa cha zovuta zimene zikudzakugwerani. Chuma chanu chaola, ndipo njenjete zadya zovala zanu. Golide wanu ndi siliva zachita dzimbiri, ndipo dzimbirilo lidzakhala mboni yokutsutsani. Lidzaononga thupi lanu ngati moto. Mwadziwunjikira chuma pa masiku ano amene ali otsiriza. Antchito okolola m’minda mwanu simudawalipire. Ndalama zamalipirozo zikulira mokutsutsani. Ndipo kufuula kwa okololawo kwamveka m’makutu a Chauta Mphambe. Mwakhala mukuchita maphwando, ndipo mwalidyera dziko lino lapansi. Mwadzinenepetsa pa tsiku lopha anthu. Mwamuweruza kuti ngwolakwa ndipo mwamupha munthu wolungama, iye osalimbalimba.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – Cf. YOHANE 17: 17b, 17a.

Alleluia, Alleluia – Mau anuwo ngoona zedi, Ambuye, mutipatule ndi mau anu kuti tikhale anthu anu. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 09: 38 – 43, 45, 47 – 48. (Wosatsutsana nafe, ndi wogwirizana nafe ameneyo).

 

Yohane adauza Yesu kuti, “aphunzitsi, ife tinaona munthu wina akutulutsa mizimu yoipa potchula dzina lanu, ndiye ife tinayesa kumletsa chifukwa sayenda nafe.” Koma Yesu adati, “musamletse ai, chifukwa munthu sangati atachita zamphamvu m’dzina langa, nthawi yomweyo nkundinyoza. Chifukwa wosutsana nafe, ndi wogwirizana nafe ameneyo. Aliyense amene akupatsani chikho cha madzi chifukwa chakuti ndinu ake a Khristu, ndithu ndikunenetsa kuti ameneyo sadzalephera kulandira mphotho yake. Aliyense wochimwitsa ngakhale mmodzi mwa ana okhulupirira Inewa, ameneyo kukadakhala kwabwino koposa kuti ammangirire chimwala cha mphero m’khosi ndi kukamuponya m’nyanja. Tsono ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi bwino kuti ukalowe ku moyo wosatha uli woduka dzanja, kupambana kuti ukalowe uli ndi manja onse awiri ku Gehena, kwa moto wosazimika. Ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi bwino kuti ukalowe ku moyo wosatha uli woduka phazi, kupambana kuti ukaponyedwe ku Gehena uli ndi miyendo yonse. Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi bwino kuti ukalowe mu Ufumu wa Mulungu uli ndi diso limodzi lokha, kupambana kuti akakuponye ku Gehena uli ndi maso onse awiri. Kumeneko mphutsi zowazunza sizifa, moto wakenso wowatentha suzima.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, tikweze mapemphero athu kwa Mulungu amene afuna kupulumutsa anthu onse, nagwira ntchito mu mtima wa aliyense:

1.     Atate, musaleke kuyeretsa ndi kuwongolera Mpingo wanu kuti anthu ake akhale oyera mtima monga Inu nomwe Atate muli oyera.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atate, mupatse atsogoleri onse mtima wodzichepetsa, kuti asenze udindo wao modziiwala, potsata ubwino wa anthu onse.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Atate, mufewetse mitima ya anthu opata kuti asaumirire chuma, koma adziwe kuthandiza anzao amene ali m’mavuto.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Atate, mutithandize ife tomwe kuleka maganizo a kunyada ndi a kudzikonda, kuti mayendedwe athu akhale ogwirizana ndi Mthenga Wabwino.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate achifundo, muunike m’mitima ya anthu onse, muwaongolere ndi Mzimu wanu Woyera, kuti azindikire chipulumutso chanu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, September 21, 2024

LAMULUNGU LA 25 PA CHAKA – B.

LAMULUNGU LA 25 PA CHAKA – B.

“Wamkulu Adzisandutse Wamng’ono, Wotumukira Anthu Onse.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA LUNTHA: LUNTHA 02: 12, 17 – 20. (Timpereke ku imfa yochititsa manyazi).

 

Tsono timukhalizire munthu wolungama, popeza kuti amativutitsa, ndipo amatsutsana ndi ntchito zathu. Amatidzudzula chifukwa chopandulira malamulo, amatinena kuti timanyoza mwambo. Tiyeni tiwone ngati mau ake ndi oona, tiwone zimene zidzamufikire pakutha pa moyo wake. Ngati wolungamayo ndi mwanandi wa Mulungu, Mulungu adzamuthandiza, adzampulumutsa kwa adani ake. Timuyese pakumusautsa ndi kumunyoza, kuti tiwone ngati ndi wofatsa, ngati ndi wodziwa kupirira. Timpereke ku imfa yochititsa manyazi, paja iye akuti Mulungu adzamteteza.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 54: 03 – 06, 08.

 

Ambuye ndiwo amachirikiza moyo wanga.

 

Inu Mulungu, pulumutsani ndi dzina lanu,

Onetsani ndi mphamvu zanu kuti ndine wosalakwa,

Inu Mulungu, Imvani pemphero langa,

Tcherani khutu kuti mumve mau a pakamwa panga.

 

Ambuye ndiwo amachirikiza moyo wanga.

 

Anthu onyada andiwukira,

Anthu ankhalwe amafunafuna moyo wanga,

Iwo saganizako za Inu Mulungu.

 

Ambuye ndiwo amachirikiza moyo wanga.

 

Komatu, Mulungu ndiye amandithandiza,

Ambuye ndiwo amachirikiza moyo wanga,

Ndidzapereka nsembe kwa Inu mwaufulu,

Ndidzatamanda dzina lanu, popeza kuti ndinu abwino.

 

Ambuye ndiwo amachirikiza moyo wanga.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA YAKOBE: YAKOBE 03: 16 – 04: 03. (Chilungamo ndiye chipatso cha mbeu zimene anthu adzetse mtendere amafesa mu mtendere).

 

Pajatu pamene pali kaduka ndi kudzikonda, pomweponso pali chisokonezo ndi ntchito yoipa ya mtundu uliwonse. Koma nzeru zochokera Kumwamba, poyamba nzangwiro, kuwonjeza apo nzamtendere, zofatsa ndi zomvera bwino. Ndi za chifundo chambiri, ndipo zipatso zake zabwino nzochuluka. Nzeruzo sizikondera kapena kuchita chiphamaso. Ndipo chilungamo ndiye chipatso cha mbeu zimene anthu odzetsa mtendere amafesa mu mtendere. Kodi nkhondo zimachokera kuti? Kukangana pakati panu kumachokera kuti? Kodi suja zimachokera ku zilakolako zanu zathupi, zimene zimachita nkhondo mwa inu? Mumalakalaka zinthu, koma zimakusowani, nchifukwa chake mumapha munthu. Mumasirira zinthu, koma simungathe kuzipeza, nchifukwa chake mumamenyana, nkumachita nkhondo. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu. Ndipo ngakhale mupemphe, simulandira, chifukwa mumapempha molakwa. Zimene mumapempha, mumafuna kungozimwazira pa zokukondweretsani basi.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – Cf. 02 ATESALONIKA 02: 14.

Alleluia, Alleluia – Mulungu adakuitanani kudzera mwa Uthenga Wabwino kuti mulandire nao ulemerero wa Ambuye athu Yesu Khristu. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 09: 30 – 37. (Ngati wina afuna kukhala wamkulu, adzisandutse wotumikira onse).

 

Atachoka kumeneko, Yesu ndi ophunzira ake ankadutsa m’dziko la Galileya. Koma Iye sadafune kuti anthu adziwe, chifukwa ankaphunzitsa ophunzira ake. Ankawauza kuti, “Mwana wa Munthu akudzaperekedwa kwa anthu, ndipo iwowo adzamupha. Koma atamupha, Iye adzauka patapita masiku atatu.” Ophunzira ake sadamvetse mau amenewa, komabe ankaopa kumufunsa. Yesu ndi ophunzira ake adafika ku Kapernao. Atalowa m’nyumba, Iye adawafunsa kuti, “kodi panjira paja mumatsutsana zotani?” Ophunzira adangoti chete. Ndiye kuti zimene ankatsutsana panjirapo zinali zakuti wamkulu ndani pakati pao. Yesu adakhala pansi, nawaitana ophunzira khumi ndi awiri aja. Ndipo adawauza kuti, “ngati wina afuna kukhala wamkulu, adzisandutse wamng’ono, wotumikira onse.” Atatero adatenga mwana, namkhazika pakati pao nkumufungata, nawauza kuti, “aliyense wolandira bwino mwana wonga ngati uyu chifukwa cha ine, ndiye kuti akulandira bwino Ine amene. Ndipo wondilandira Ine bwino, ndiye kuti akulandira bwino osati Ineyo, koma Atate amene adandituma.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, monga ana amadalira chifundo cha bambo ndi mai, ifenso tsopano tipereke mapemphero athu kwa Atate athu a Kumwamba:

 

1.     Tipempherere akhristu onse, kuti avomere kutumikira Mpingo wa Yesu Khristu, osamangoganiza zao zokha.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Tipempherere atsogoleri onse, kuti asenze udindo wao mosamala ndi modzichepetsa mtima.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Tipempherere anthu opata, kuti asanyadire chuma chao, koma akumbukire kuthandiza anzao m’zosowa zao.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Tidzipempherere ife tomwe kuti tikhale ofatsa ndi a mtima wodzichepetsa monga Yesu analili pa moyo wawo wonse.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, polandira mapemphero athuwa, muwamvere chifundo ana anu onse amene ali m’mavuto. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, September 14, 2024

LAMULUNGU LA 24 PA CHAKA – B

LAMULUNGU LA 24 PA CHAKA – B.

“Wotaya Moyo Wake Chifukwa Cha Ine Adzausunga.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI YESAYA: YESAYA 50: 05 – 09. (Ndidapereka msana wanga kwa ondimenya).

 

Ambuye Chauta anditsekula makutu, ndipo sindidawanyoze kapena kuwapindukira. Ndidapereka msana wanga kwa ondimenya, ndiponso masaya anga kwa ondimwetula ndevu. Sindidawabisire nkhope ondinyoza ndi ondithira malovu. Koma kunyoza kwao sindikuvutika nako, chifukwa Ambuye Chauta amandithandiza. Nchifukwa chake ndalimbitsa mtima wanga ngati mwala. Ndikudziwa kuti sadzandichititsa manyazi. Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso angandiimbe mlandu? Tipitire limodzi ku bwalo lamilandu. Wofuna kutsutsana nane ndani? Nabwere pafupi. Ambuye Chauta ndi amene amandithandiza, ndani anganene kuti ndine wopalamula? Ndithu, onse ondizenga mlandu adzatheratu. Kutha kwake ngati chovala chodyewa ndi njenjete.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 115: 01 – 06, 08 – 09.

 

Ndimayenda pamaso pa Chauta m’dziko la amoyo.

 

Ndimakonda Chauta chifukwa amamva mau anga omupempha,

Iye amatchera khutu kuti andimve,

Nchifukwa chake ndidzampempha nthawi zonse pamene ndili moyo.

 

Ndimayenda pamaso pa Chauta m’dziko la amoyo.

 

Misampha ya imfa idandizinga, zoopsa za m’dziko la akufa zidandigwera,

Ndidaona mavuto, nkugwidwa ndi nthumazi,

Tsono ndidapemphera potchula dzina la Chauta kuti,

Chauta ndikukupemphani, pulumutsani moyo wanga.

 

Ndimayenda pamaso pa Chauta m’dziko la amoyo.

 

Chauta ndi wokoma mtima ndi wolungama,

Mulungu wathu ndi wachifundo,

Chauta amasunga a mtima wodzichepetsa,

Pamene ndidagwa m’zoopsa, Iye Adandipulumutsa.

 

Ndimayenda pamaso pa Chauta m’dziko la amoyo.

 

Pakuti Inu Chauta, mwandipulumutsa ku imfa,

Mwaletsa misozi yanga,

Mwanditeteza kuti ndisaphunthwe,

Ndimayenda pamaso pa Chauta m’dziko la amoyo.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA YAKOBE: YAKOBE 02: 14 – 18. (Chikhulupiriro pachokha, nchopanda ntchito zake, nchakufa basi).

 

Abale anga, pali phindu lanji, ngati munthu anena kuti, ndili ndi chikhulupiriro, koma popanda chimene akuchitapo? Kodi chikhulupiriro chotere chingampulumutse? Mwachitsanzo: mbale wina kapena mlongo ali ndi usiwa, ndipo masiku onse alibe chakudya chokwanira. Tsono wina mwa inu angowauza kuti, pitani ndi mtendere, mukafundidwe ndipo mukakhute, koma osawapatsa zimene akusowazo, pamenepo phindu lake nchiyani? Choncho, chikhulupiriro pachokha, chopanda ntchito zake, nchakufa basi. Koma kapena wina anganene kuti, inuyo muli ndi chikhulupiriro, ineyo ndili ndi ntchito zabwino. Pamenepo ine nkumuyankha kuti, uyesetse kundiwonetsa chikhulupiriro chako chopanda ntchito zakecho, ine ndi ntchito zanga ndikuwonetsa chikhulupiriro changa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – AGALATIYA 06: 14.

Alleluia, Alleluia – Koma ine sindinganyadire kanthu kena kalikonse, koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu. Popeza kuti tsopano zapansipano kwa ine zili ngati zakufa, ndipo inenso kwa zapansipano, ndili ngati wopachikidwa. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 08: 27 – 35. (Mwana wa Munthu adzayenera kuzunzidwa kwambiri).

 

Yesu ndi ophunzira ake adapita ku midzi ya ku Kesareya-Firipi. Pa njira Yesu adafunsa ophunzira akewo kuti, “kodi anthu amati Ine ndine yani?” Iwo adayankha kuti, “ena amati ndi Yohane Mbatizi, ena amati ndinu Eliya, enanso amati ndinu mmodzi mwa aneneri.” Apo Yesu adawafunsa kuti, “nanga inuyo, mumati ndine yani?” Petro adamuyankha kuti, “inu ndinu Mpulumutsi wolonjezedwa uja.” Yesu adawalamula kuti asauze munthu wina aliyense za Iye. Yesu adayamba kuphunzitsa ophunzira ake kuti, “mwana wa Munthu adzayenera kuzunzidwa kwambiri. Akulu a Ayuda, ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi a Malamulo adzamkana. Iye adzaphedwa, koma patapita masiku atatu adzauka.” Zimenezi adazinena mosabisa konse. Apo Petro adamtengera pambali, nayamba kumdzudzula. Koma Yesu adacheuka, nayang’ana ophunzira ake ena aja, ndipo adadzudzula Petro. Adati, “choka apa, iwe Satana! Maganizo akowa si maganizo a Mulungu ai, ndi maganizo a anthu chabe.” Pambuyo pake Yesu adaitana khamu la anthu pamodzi ndi ophunzira aja kuti adze pafupi naye, ndipo adawauza kuti, “munthu wofuna kutsata Ine, adzikane mwiniwakeyo, ndipo asenze mtanda wake nkumanditsata. Chifukwa wofuna kupulumutsa moyo wake, adzautaya, koma wotaya moyo wake chifukwa cha Ine ndi Uthenga Wabwino, adzaupulumutsa.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, popereka kwa Mulungu mapemphero athuwa tiperekenso zowawa zonse zimene anthu akuzimva m’dziko lino lapansi:

 

1.     Atate, mulimbitse mtima atsogoleri a Mpingo kuti asenze udindo wao mwakhama. Asaope kusauka ndi kutaya moyo wawo omwe chifukwa cha akhristu ao.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atate, mukumbukire akhristu onse amene azunzidwa chifukwa chokhulupirira Mthenga Wabwino. Muwachirikize, azizindikira kuti Ufumu wa Kumwamba ndi wao.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Atate, mudalitse odwala ndi ena onse amene akuvutika m’mitima mwao. Apeze mphamvu zopirira mavuto ao pokumbukira imfa ya Yesu Mpulumutsi.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Atate, mutipatse ife tonse chikhulupiriro cholimba, kuti titumikire anzathu modziiwala tokha, osaopa kumva zowawa.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Inu Chauta Mulungu wathu, landirani mapemphero athuwa, ndipo mutiphunzitse kumanga moyo wathu pa chikondi cha Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, September 7, 2024

LAMULUNGU LA 23 PA CHAKA – B

LAMULUNGU LA 23 PA CHAKA – B.

“Makutu a Agonthi Adzatsekuka.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI YESAYA: YESAYA 35: 04 – 07. (Makutu a agonthi adzatsekuka, ndipo osalankhula adzaimba mokondwa).

 

Muuze onse a mtima wamantha kuti, “limbani mtima, musachite mantha. Mulungu wanu akubwera kudzalipsira ndi kulanga adani anu. Akubwera kudzakupulumutsani.” Pamenepo maso a anthu akhungu adzaphenyuka, ndipo makutu a agonthi adzatsekuka. Opunduka adzalumpha ngati mphoyo, ndipo osalankhula adzaimba mokondwa. Akasupe adzatumphuka m’chipululu, ndipo mitsinje idzayenda m’dziko louma. Mchenga wotentha udzasanduka nyanja, ndipo dziko louma lidzasanduka la akasupe. Pamene panali mbuto za nkhandwe padzamera udzu ndi bango.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 146: 07 – 10.

 

Tamanda Chauta iwe Mtima wanga.

 

Chauta amasunga malonjezo ake nthawi zonse,

Amachitira anthu opsinjidwa zolungama,

Amawapatsa chakudya anthu anjala,

Chauta amamasula am’ndende.

 

Tamanda Chauta iwe Mtima wanga.

 

Chauta amatsekula maso a anthu osapenya,

Chauta amakweza anthu otsitsidwa,

Chauta amakonda anthu ochita chilungamo,

Chauta amateteza alendo.

 

Tamanda Chauta iwe Mtima wanga.

 

Chauta amachirikiza mkazi wamasiye ndiponso mwana wamasiye,

Koma njira za anthu oipa amazipotoza,

Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako, iwe Ziyoni, adzalamulira ku mibadwo yonse.

 

Tamanda Chauta iwe Mtima wanga.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA YAKOBE: YAKOBE 02: 01 – 05. (Mulungu adasankha amphawi kuti alandire madalitso amene Iye adalonjeza anthu omukonda).

 

Abale anga, popeza kuti mumakhulupirira Ambuye athu Yesu Khristu, Ambuye aulemerero, musamakondera. Mwachitsanzo: munthu wina alowa mumsonkhano wanu atavala mphete zagolide m’manja, alinso ndi zovala zokongola. Winanso nkulowa, koma ali mmphawi, nsanza zili wirawira. Tsono inu pofuna kusamala kwambiri wovala zokongolayo, mumuuza kuti, ‘khalani apa pabwinopa,’ mmphawi uja nkumuuza kuti, ‘iwe, kaimirire apo, kapena dzakhale pansi kumapazi kwangaku.’ Limenelotu ndi tsankho pakati pa inu nokhanokha, ndipo inuyo mwasanduka oweruza a maganizo oipa. Mwerani, abale anga okondedwa, kodi suja Mulungu adasankha ooneka amphawi m’maso mwa anthu, kuti akhale olemera pa chikhulupiriro, ndi kuti alandire madalitso amene Iye adalonjeza anthu omukonda?

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 04: 23.

Alleluia, Alleluia – Yesu adalalika Uthenga Wabwino wonena za ufumu wakumwamba. Ankachiritsanso nthenda zonse za anthu ndi zofooka zao zam’thupi. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 07: 31 – 37. (Agonthi amawachiritsa nkumamva, ndipo osalankhula amawalankhulitsa).

 

Yesu adachokanso ku dera lija la ku Tiro, namayenda kudutsa dera la ku Sidoni, kupita ku nyanja ya ku Galileya, kudzera pakati pa dera la Mizinda Khumi. Anthu ena adabwera kwa Iye ndi munthu yemwe anali gonthi ndi wolunkhula movutikira. Anthuwo adapempha Yesu kuti amchiritse pomusanjika manja munthuyo. Yesu adatengera munthu uja pambali kumchotsa pa khamu la anthu. Adapisa zala m’makutu a munthuyo, nalavula malovu, nkukhudza lilime la munthu uja. Adayang’ana kumwamba, nadzuma, nkumuuza kuti, “Efata!” ndiye kuti “Tsekuka!” Pomwepo makutu a munthuyo adatsekuka, ndipo chimene chinkamanga lilime lake chidamasuka, mpaka adayamba kulankhula bwino lomwe. Yesu adalamula anzake a munthuyo kuti, “musakauzetu wina aliyense zimenezi.” Koma ngakhale adawaletsa mwamphamvu choncho, iwo adanka nalengeza ndithu zimenezi. Ndipo anthu adazizwa kopitirira ndithu. Adati, “ameneyu amachita zonse bwino. Ngakhale agonthi amawachiritsa nkumamva, ndipo osalankhula amawalankhulitsa.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, tsopano tipereke mapemphero athu kwa Mulungu kuti anthu onse amve Mthenga Wabwino ndi kulandira chipulumutso pakukhulupirira Yesu Khristu:

 

1.     Atate, muwongolere Mpingo wanu kuti usonyeze kukoma mtima kwanu kwa anthu onse, pakuwaphunzitsa mau anu ndi Kuwatumikira mwachifundo.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atate, mulimbitse atsogoleri olamulira maiko kuti asamale ubwino wa anthu ao, ndipo ayesetse kutukula miyoyo ya anthu osauka.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Atate, mudalitse adokotala, anesi ndi onse ogwira ntchito m’zipatala, kuti awonetse mtima wachifundo kwa odwala onse, mopanda tsankho.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Atate, mutidzaze ndi Mzimu wanu wachikondi, kuti ifenso tidzetse chimwemwe cha chipulumutso chanu m’mitima ya anthu osauka, pakuwathandiza mwaufulu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Inu Chauta Mulungu wathu, mutikomere mtima polandira mapemphero athuwa, ndipo ife tidzakuyamikani ndi kutamanda chifundo chanu masiku onse. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...