Saturday, July 20, 2024

LAMULUNGU LA 16 PA CHAKA – B.

LAMULUNGU LA 16 PA CHAKA – B.

“Yesu Yekha Ndi Mtsogoleri Woona Wokhulupirika.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI YEREMIYA: YEREMIYA 23: 01 – 06. (Ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, ndidzazipatsa abusa oziweta bwino).

 

“Tsoka kwa abusa amene amaononga ndi kumwaza nkhosa za pabusa panga,” akutero Chauta. Nchifukwa chake Chauta, Mulungu wa Israele, ponena za abusa oyang’anira anthu ake, akuti, “mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga, simudazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu. Pambuyo pake Mwiniwakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kudzichotsa ku malo onse amene ndidazimwazira. Ndidzazibwezera ku ubusa lakwao, ndipo zidzaswana ndi kuchuluka. Ndidzazipatsa abusa oziweta bwino. Sizidzaopanso kapena kuchita mantha, kapena kusokera,” akutero Chauta. Chauta akunena kuti, “akubwera masiku pamene ndidzaphukitsira Davide nthambi yoongoka imene idzakhala mfumu yanzeru ndi yoweruza m’dzikomo mwachilungamo ndi mosakondera. Pa masiku akewo Yuda adzapulumuka, ndipo Israele adzakhala pabwino. Adzamutcha dzina lake lakuti, ‘Chauta ndiye chilungamo chathu.”’

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 23.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu,

Amandigoneka pa busa lamsipu,

Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako,

Amatsitsimutsa moyo wanga.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Amanditsogolera m’njira za chilungamo,

Malinga ndi ulemerero wa dzina lake,

Ngakhale ndiyende m’chigwa chamdima wabii, sindidzaopa choipa chilichonse,

Pakuti Inu Ambuye mumakhala nane, chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditeteza.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Inu mumandikonzera chakudya, adani anga akuwona,

Mumandilandira bwino podzoza mutu wanga,

Mumadzaza chikho changa mpaka kusefukira.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Zoonadi, zokoma zanu ndi chikondi chanu,

Zidzakhala ndi ine masiku onse a moyo wanga,

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu moyo wanga onse.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AEFESO: AEFESO 02: 13 – 18. (Khristu mwini wake ndiye Mtendere wathu. Iye adasasandutsa Ayuda ndi anthu a mitundu ina kuti akhale amodzi).

 

Abale, tsopano, mwa Khristu Yesu, inu amene kale lija munali kutali ndi Mulungu, mwakhala pafupi, chifukwa cha imfa ya Khristu. Khristu ndiye mwini wake wa mtendere wathu. Iye adasandutsa Ayuda ndi anthu a mitundu ina kuti akhale amodzi. Pakupereka thupi lake, adagamula khoma la chidani limene linkatilekanitsa. Iye adathetsa Malamulo a Mose pamodzi ndi malangizo ake ndi miyambo yake. Adachita zimenezi kuti kuchokera ku mitundu iwiri ija, alenge mtundu umodzi watsopano, wokhala mwa Iye, kuti choncho adzetse mtendere. Khristu adafa pa mtanda kuti athetse chidani, ndipo kuti mwa mtandawo aphatikize pamodzi m’thupi limodzi mitundu iwiriyo, ndi kuiyanjanitsa ndi Mulungu. Khristu adadzalalika Uthenga Wabwino wa mtendere kwa inu a mitundu inanu, amene munali kutali ndi Mulungu, ndiponso kwa Ayuda, amene anali pafupi naye. Tsopano kudzera mwa Khristu ife tonse, Ayuda ndi a mitundu ina, tingathe kufika kwa Atate mwa Mzimu Woyera mmodzi yemweyo.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 10: 27.

Alleluia, Alleluia – Nkhosa zanga zimamva mau anga, atero Ambuye. Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsatira. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 06: 30 – 34. (Anali ngati nkhosa zopanda mbusa woziyang’anira).

 

Atumwi aja adabwerera kwa Yesu namufotokozera zonse zimene adaachita ndi kuphunzitsa. Yesu adawauza kuti, “tiyeni tipite kwatokha kumalo kosapitapita anthu, kuti mukapumule pang’ono.” Adaatero chifukwa anthu anali piringupiringu, Mwakuti iwo sankatha kupeza ndi mpata wodyera womwe. Tsono adalowa m’chombo napita kwaokha kumalo kosapita anthu. Komabe anthu ambiri adawaona akupita, nawazindikira. Motero adathamanga pa mtunda kuchokera ku mizinda yonse, nakafika kumaloko, Yesu ndi ophunzira ake aja asanafike. Pamene Yesu adatuluka m’chombomo, adaona chikhamu chachikulu cha anthu. Adawamvera chifundo anthuwo, chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mbusa, choncho adayamba kuwaphunzitsa zambiri.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, tiyeni tipereke mapemphero athu kwa Mulungu, Mbusa wathu wamkulu; tiyamike chifundo chake chotisamalira:

 

1.     Atate, muthandize akulu a Mpingo kuti atsate chitsanzo cha Ambuye Yesu, Mbusa wabwino, posamala akhristu ao.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atate, thandizani atsogoleri athu kuti ayendetse bwino dziko lathu, potsata chitsanzo cha Yesu Khristu, Mbusa wawo.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Atate, muthandize akatekumeni ndi akunja onse, kuti avomere kutsata Yesu Khristu, Mbusa wolondola nkhosa zotayika.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Atate, muthandize akhristu onse akugwa, kuti abwerere kwa Mbusa wao, Yesu Khristu, amene akufuna kuti pakhale khola limodzi lokha.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, tikukupemphani modzichepetsa, mumvere mapemphero athuwa kuti nkhosa zanu zonse zikhale pamodzi. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

No comments:

Post a Comment

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...