Saturday, July 13, 2024

LAMULUNGU LA 15 PA CHAKA – B.

LAMULUNGU LA 15 PA CHAKA – B.

“Yesu Khristu Akutituma Kukalalika Mthenga Wabwino.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI AMOSI: AMOSI 07: 12 – 15. (Pita, ukalalikire anthu anga, Aisraele).

 

Amaziya adauza Amosi kuti, “Mlosi iwe, choka kuno! Thawira ku dziko la Yuda! Uzikalosa kumeneko, ndipo anthu akumeneko azikakudyetsa. Koma usakalosenso ku Betele poti kumeneko ndi malo opatulika a mfumu, ndiponso ndi Nyumba ya Mulungu ya dziko lino.” Amosi adayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri konse, kapenanso wa m’gulu la aneneri. Inetu ndine woweta nkhosa, ndiponso wolima nkhuyu. Chauta adachita kukanditenga, kundileketsa ntchito yoweta nkhosa, nandiwuza kuti, pita, ukalalikire anthu anga, Aisraele.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 85: 09 – 14.

 

Tiwonetseni chikondi chanu chosasinthika, Inu Chauta, ndipo mutipulumutse.

 

Ndimve zimene Chauta adzalankhula,

Chifukwa adzalankhula za Mtendere kwa anthu ake,

Zoonadi, Mulungu ali wokonzeka kuti apulumutse amene amamuwopa,

Kuti ulemerero wake ukhale m’dziko lathu.

 

Tiwonetseni chikondi chanu chosasinthika, Inu Chauta, ndipo mutipulumutse.

 

Chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika zidzakumana,

Chilungamo ndi Mtendere zidzagwirizana,

Anthu ake adzakhala okhulupirika pansi pano,

Ndipo Mulungu wakumwamba adzawalungamitsa.

 

Tiwonetseni chikondi chanu chosasinthika, Inu Chauta, ndipo mutipulumutse.

 

Inde, Chauta adzapereka zabwino,

Ndipo dziko lathu lidzabereka zokolola zambiri,

Mulungu ndi wolungama chikhalire,

Chilungamo chake chimaongolera zochita zake zonse.

 

Tiwonetseni chikondi chanu chosasinthika, Inu Chauta, ndipo mutipulumutse.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AEFESO: AEFESO 01: 03 – 14. (Mulungu asanalenge dziko lapansi, adatisankhiratu mwa Khristu).

 

Abale, tiyamike Mulungu, Atate Ambuye athu Yesu Khristu. Mwa Khristu Iye adatipatsa madalitso onse auzimu Kumwamba. Mulungu asanalenge dziko lapansi, adatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi opanda cholakwa pamaso pake. Chifukwa chotikonda, adakonzeratu kuti mwa Yesu Khristu atilandire ngati ana ake. Adachita zimenezi chifukwa adaafuna kutero mwa kukoma mtima kwake. Adaafuna kuti tizitamanda ulemu wake chifukwa adatikomera mtima kopambana, pakutipatsa Mwana wake wokondedwa ngati mphatso yaulere. Ndi imfa ya Mwana wakeyo Mulungu adatipulumutsa, adatikhululukira machimo athu. Nzazikuludi mphatso zaulere zimene Mulungu adatipatsa mochuluka. Mwa luntha ndi nzeru adatiwululira chifuniro chake chimene kale chinali chobisika. Zimene adaati achite mwa kukoma mtima kwake ndi zomwe Iye mwini adaakonzeratu kale. Chimene Mulungu adalongosola kuti achite itakwana nthawi, nchakuti asonkhanitse pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za Kumwamba ndi zapansipano. Paja Mulungu amaongolera zinthu zonse monga momwe Iye wafunira ndi m’mene watsimikizira. Iye adatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale akeake. Adazikonzeratu kuti ziyenera kukhala choncho. Adafuna kuti ife, amene tinali oyamba kuyembekeza Khristu, tilemekeze ulemerero wake. Mwa Khristu, inunso mutamva mau oona, amene ali Uthenga Wabwino wokupulumutsani, mudaukhulupirira. Nchifukwa chake Mulungu adakusindikizani chizindikiro chotsimikizira kuti ndinu akedi, pakukupatsani Mzimu Woyera amene Iye adaalonjeza. Mzimu Woyerayo ndiye chikole chotsimikizira kuti tidzalandiradi madalitso onse amene Mulungu adalonjeza kupatsa anthu ake, ndipo kuti Mulungu adzapulumutsa kwathunthu anthu amene adawaombola kuti akhale ake enieni. Cholinga cha zonsezi ndi chakuti tilemekeze ulemerero wake.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – AEFESO 01: 17 – 18.

Alleluia, Alleluia – Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu akuunikireni m’mitima mwanu, kuti mudziwe zimene mungathe kuyembekezera kwa Mulungu amene adakuitanani. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 06: 07 – 13. (Yesu adaitana ophunzira ake khumi ndi awiri aja, nawatuma awiriawiri).

 

Pa nthawi yomweyo, Yesu adaitana ophunzira ake khumi ndi awiri aja, nawatuma awiriawiri. Adawapatsa mphamvu zotulutsira mizimu yoipitsa anthu. Adawalamula kuti, “musatenge kanthu kena kalikonse pa ulendo, koma ndodo yokha. Musatenge kamba, kapena thumba lapaulendo, kapena ndalama m’chikwama. Nsapato muvale inde, koma musakhale ndi mikanjo iwiri.” Adawauzanso kuti, “mukafika pa mudzi, mudzikhala nao kunyumba kumene mudafikirako, mpaka itakwana nthawi yoti muchoke kumudziko. Ngati kumudzi kwina anthu sakulandirani, nakana kumva mau anu, pochoka musanse fumbi la kumapazi kwanu. Chimenechi chidzakhala chizindikiro choti apalamula.” Ophunzira aja adapitadi, namakalalikira anthu kuti atembenuke mtima. Ankatulutsa mizimu yoipa yochuluka, ndiponso ankadzoza mafuta anthu odwala ambiri nkumawachiritsa.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, Mulungu adatipatsa Mzimu Woyera, natitsimikizira kuti tidzalandira madalitso onse amene Ambuye adalonjeza. Tiyeni, tikweze mapemphero athu kwa Atate athu a Kumwamba kuti atsire madalitsowo pa anthu onse:

 

1.     Atate, mulimbitse Apapa ndi Aepiskopi onse kuti akhazikitse akhristu ao m’chikhulupiriro choona, pakuwalalikira Mthenga Wabwino mwachangu.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atate, muunikire atsogoleri a maiko onse kuti atumikire anthu ao ndi kuwasamala mwachilungamo ndi mwachikondi.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Atate, musankhule ena mwa ana athu kuti alowe unsembe kapena m’zipani za mu Mpingo kuti azidzakutumikirani pa moyo wao wonse.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Atate, mutiwongolere ife tomwe tili muno, kuti mau athu ndinso ntchito zathu zotumikira anzathu, zisonyeze kukoma mtima kwanu kofuna kuwapulumutsa.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, pakuti zinthu zonse zimachitika monga momwe Inu mufunira, tikulemekeza ulememero wanu ndi kudala kokoma mtima kwanu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

No comments:

Post a Comment

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...