Saturday, July 6, 2024

LAMULUNGU LA 14 PA CHAKA – B

LAMULUNGU LA 14 PA CHAKA – B.

“Anthu a Kumudzi kwao Sadamkhulupirire.”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI EZEKIELE: EZEKIELE 02: 02 – 05. (Anthu ake ndi okanika; koma adzadziwa ndithu kuti mneneri wafikadi pakati pao).

 

Pamene ankalankhula, Mzimu wa Mulungu udalowa mwa ine nundiimiritsa, ndipo ndidamva Mulungu akulankhula. Adandiwuza kuti, “iwe mwana wa munthu, ndikukutuma kwa Israele, mtundu wa anthu aupandu amene andipandukira. Iwowo ndi makolo ao akhala akundichimwira mpaka lero lino. Anthu ake ndi okanika ndiponso achipongwe. Ndikukutuma kuti ukanene zimene Ine Ambuye Chauta ndikuwauza. Ndiye popeza kuti iwowo ngaupandu, kaya akamvera kaya akakana, (pakuti ndi anthu opanduka) koma adzadziwa ndithu kuti mneneri wafikadi pakati pao.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 123.

 

Timayang’anira ife kwa Chauta, mpaka atatichitira chifundo.

 

Ndikukweza maso anga kwa Inu,

Inu amene mumakhala pa mpando wachifumu kumwamba,

Monga momwe anyamata amayang’anira,

Ku dzanja la bwana wao.

 

Timayang’anira ife kwa Chauta, mpaka atatichitira chifundo.

 

Monga momwe adzakazi amayang’anira ku dzanja la dona wao,

Ndi momwemonso timayang’anira ife,

Kwa Chauta Mulungu wathu,

Mpaka atatichitira chifundo.

 

Timayang’anira ife kwa Chauta, mpaka atatichitira chifundo.

 

Mutichitire chifundo, Inu Chauta, mutichitire chifundo,

Pakuti adani athu atinyoza kopitirira malire,

Pa nthawi yaitali, anthu olemera akhala akutinyodola,

Anthu onyada akhala akutinyoza.

 

Timayang’anira ife kwa Chauta, mpaka atatichitira chifundo.

------------------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YACHIWIRI YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 02 AKORINTO 12: 07 – 10. (Ndidzanyadira kufooka kwanga, kuti mphamvu za Khristu zikhale mwa ine).

 

Abale, kuwopa kuti ndingamadzitukumule chifukwa cha zazikulu kwambiri zimene Ambuye adandiwululira, Mulungu adandipatsa cholasa ngati minga m’thupi. Adalola wamthenga wa Satana kuti azindimenya, kuti ndingamanyade kwambiri. Pamenepo ndidapempha Ambuye katatu kuti andichotsere chimenechi, koma Iwo adandiuza kuti, “chithandizo changa nchokukwanira. Mphamvu zanga zimaoneka kwenikweni mwa munthu wofooka.” Nchifukwa chake makamaka ndidzanyadira kufooka kwanga, kuti mphamvu za Khristu zikhale mwa ine. Tsono ndimakondwera pamene ndili wofooka, pamene anthu andinyoza, namandizunza, ndiponso pamene ndimva zowawa ndi kusautsidwa chifukwa cha Khristu. Pakuti pamene ndili wofooka, mpamene ndili ndi mphamvu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – LUKA 04:18.

Alleluia, Alleluia – Ambuye andidzoza kuti ndikalalikire amphawi Uthenga Wabwino. Wandituma kuti ndikalengeze kwa am’ndende kuti adzamasulidwa. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 06: 01 – 06. (Mneneri amalemekezeka kwina kulikonse, kupatula kumudzi kwao).

 

Yesu adachoka kumeneko, nakafika kumudzi kwao. Ophunzira ake adatsagana naye. Litafika tsiku la Sabata, Iye adayamba kuphunzitsa m’nyumba yamapemphero. Anthu ambiri amene ankamvetsera adadabwa kwambiri nkumanena kuti, “kodi Iyeyu zonsezi adazitenga kuti? Nzeru zimene adalandirazi nzotani? Akutha bwanji kuchita zinthu zamphamvu zotere? Kodi ameneyu si mmisiri wa matabwa uja, mwana wa Maria? Kodi abale ake si Yakobo, ndi Yose, ndi Yudasi, ndi Simoni? Kodi suja alongo ake ali nafe pompano?” Choncho adakhumudwa naye. Koma Yesu adawauza kuti, “mneneri amalemekezeka kwina kulikonse, kupatula kumudzi kwao, pakati pa achibale ake, ndiponso kubanja kwao.” Motero sadathe kuchita zinthu zamphamvu kumeneko. Adangosanjika manja pa odwala owerengeka, nkuwachiritsa. Ndipo adadabwa poona kuti anthu akumeneko sadamkhulupirire. Pambuyo pake Yesu adapita ku midzi yozungulira, namakaphunzitsa anthu.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, tamva lero m’mene Mulungu amatekesekera ndi chipulumutso cha anthu. Tiyeni, timupemphe kuti chithandizo chake chiwafikire anthu onse:

 

1.     Atate athu otikonda, mulimbikitse atsogoleri a Mpingo kuti asenze udindo wao mofatsa ndi mosakayika.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Atate a ufumu wonse, muwongolere akulu olamulira dziko lathu lino, kuti aliyendetse mwamtendere potsata ubwino wa anthu.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Atate a chifundo, mukulitse m’mitima ya akhristu chikondi chotumikira anzao, kuti alimbikire pa ntchito zotukula moyo wa anthu.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Atate a ufulu wonse, mutipatse ife amene tili muno chikhulupiriro cholimba, kuti tiphunzitse bwino ana athu za Ambuye Yesu Mpulumutsi.

Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, maso athu akuyang’ana kwa Inu, popeza kuti simuleka kuthandiza anthu amene akuzindikira umphawi wao. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

No comments:

Post a Comment

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...