LAMULUNGU LA 11 PA CHAKA – B.
“Mulungu salephera kukhazikitsa Ufumu wake.”
MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI EZEKIELE: EZEKIELE 17: 22 – 24. (Ndine Chauta amene ndimatalikitsa mitengo yaifupi).
Ambuye Chauta akunena izi: “Ine ndemwe ndidzatenga kanthambi ka ku nsonga yapamwamba ya mtengo wa mkungudza, ndipo ndidzakabzala. Pa tinthambi tapamwamba ndidzathyoloka kena kanthete ndipo ndidzakabzala pa phiri lalitali kwambiri. Kadzaphuka ndi kubala zipatso zake. Motero kadzasanduka mkungudza wokoma. Mbalame za mitundu yonse yam’dzikomo idzadziwa kuti ndine Chautane amene ndimafupikitsa mitengo yaitali, ndiponso kutalikitsa mitengo yaifupi. Ndimaumitsa mitengo yobiriwira, ndi kubiriwiritsa mitengo youma. Ine Chauta ndanena zimenezi, ndipo ndidzazichitadi.”
Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.
---------------------------------------
NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 92: 02 – 03, 13 – 16.
Nkwabwino kuthokoza Chauta.
Nkwabwino kuthokoza Chauta,
Kuimba nyimbo zotamanda dzina lanu, Inu Wopambanazonse,
Nkwabwino m’mawa kulalika,
Za chikondi chanu chosasinthika,
Ndipo usiku kusimba za kukhulupirika kwanu.
Nkwabwino kuthokoza Chauta.
Anthu okondwetsa Mulungu,
Zinthu zimawayendera bwino ngati mitengo ya mgwalangwa,
Amakula ngati mikungudza ya ku Lebanoni,
Ali ngati mitengo yookedwa m’Nyumba ya Chauta.
Nkwabwino kuthokoza Chauta.
Mitengoyi imabalabe zipatso ngakhale itakalamba,
Nthawi zonse imakhala ndi madzi ndipo imabiriwira,
Imaonetsa kuti Chauta ndi wolungama,
Iye ndiye thanthwe langa, mwa Iye mulibe chokhota.
Nkwabwino kuthokoza Chauta.
------------------------------------------------
MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YACHIWIRI YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 02 AKORINTO 05: 06 – 10. (Ngakhale tikhalebe kuno, kapena kwa Ambuye, timayesetsa kuwakondweretsa Ambuye).
Abale, nchifukwa chake timalimba mtima masiku onse, ndipo tikudziwa kuti nthawi yonse pamene tikukhala m’thupi, ngati kwathu, ndiye kuti tili kutali ndi Ambuye. Pakuti timatsata chikhulupiriro, osati zopenya ndi maso. Ndithu tikulimba mtima, ndipo makamaka tikadakonda kutuluka m’thupi lathu lino ndi kukakhala kwa Ambuye. Nchifukwa chake, ngakhale tikhalebe kuno, kapena tikakhale kwa Ambuye, timayesetsa kuwakondweretsa Ambuyewo. Pakuti tonsefe tiyenera kukaimirira poyera pamaso pa Khristu kuti atiweruze. Kumeneko aliyense adzalandira zomuyenera, molingana ndi zimene adachita pansi pano, zabwino kapena zoipa.
Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.
--------------------------------------
NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 12: 31b – 32.
Alleluia, Alleluia – Mbeu ija ndi mau a Mulungu, amene Khristu anawafesa; amene angapeze mbeuyo adzakhala mwa Iye mpaka muyaya. – Alleluia, Alleluia.
--------------------------------------
MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MARKO WOYERA: MARKO 04: 26 – 34 (Pamene aifesa m’nthaka, ndi yaing’ono kwambiri. Koma ikukula ndithu kupambana zitsamba zina zonse).
Yesu adawauzanso kuti, “za Ufumu wa Mulungu tingazifanizire motere: munthu afesa mbeu m’munda. Iyeyo atha kumangogona usiku, m’mawa nadzuka, nthawi yonseyo mbeu adafesa zija zikumera ndi kukula, mwiniwakeyo osadziwa m’mene zonsezi zikuchitikira. Paja nthaka imabereketsa mbeuzo yokhayokha. Umayamba ndi mmera, kenaka ngala, pambuyo pake njere m’ngala muja zimakhwima, Tsono mbeuzo zikacha, munthu uja amatenga mpeni wodulira, pakuti nyengo yokolola yafika.” Yesu adatinso, “kodi Ufumu wa Mulungu tingauyerekeze ndi chiyani? Kaya tiwufanizire ndi chiyani? Uli ngati njere ya mbeu ya mpiru. Pamene aifetsa m’nthaka, ndi yaing’ono kwambiri mukaiyerekeza ndi njere zina pansi pano. Koma akaifetsa, imamera, mbeu yake nkukula ndithu kupambana zitsamba zina zonse. Imachita nthambi zazikulu, kotero kuti mbalame zimatha kudzamanga zisa mumthunzi mwake.” Yesu ankaphunzitsa anthu ndi mafanizo ambiri onga amenewa, polinganiza ndi nzeru za anthuwo. Sankawaphunzitsa popanda mafanizo. Koma ankati akakhala payekha ndi ophunzira ake, ankawatanthauzira zonse.
Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.
--------------------------------------
Mapemphero a Akhristu.
Abale, pakuti Mau a Mulungu salephera kuutsa chikhulupiriro m’mitima ya anthu, tiyeni, tipempherere anthu onse.
1. Tipempherere atsogoleri olalika Mau a Mulungu, kuti alimbikitse kufalitsa Mthenga Wabwino ponseponse.
Tikupemphani, mutivomereze.
2. Tipempherere akatekumeni ndi anthu onse amene adakali kunja, kuti atsekulire Mulungu mitima yao polandira bwino mau ake.
Tikupemphani, mutivomereze.
3. Tipempherere akhristu onse amene ali pabanja kuti atsogolere ana awo m’njira ya chipulumutso, pakuwaphunzitsa za Ambuye Yesu.
Tikupemphani, mutivomereze.
4. Tizipemphererana ife tomwe, kuti mau a Mthenga Wabwino akhazikike m’mitima mwathu ndi kulimbitsa chikhulupiriro chathu.
Tikupemphani, mutivomereze.
Atate, tikukuyamikani chifukwa mau anu ndi opatsa moyo. Mutithandize kuwasunga ndi kuwagwiritsa ntchito kuti tiyende M’chikondi chanu masiku onse. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.
#Pax_et_Gaudium_in_Domino.
Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295
No comments:
Post a Comment