Saturday, November 25, 2023

CHAKA CHA YESU KHRISTU MFUMU CHAKA A

CHAKA CHA YESU KHRISTU MFUMU – A.

LAMULUNGU LOMALIZA LA PA CHAKA

“Ufumu wa Yesu Khristu ndi wachikondi.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI EZEKIELE; EZEKIELE 34: 11 – 12, 15 – 17. (Kunena za inu, nkhosa zanganu, Ine Ambuye Chauta ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa).

 

Zimene ndikunena Ine Ambuye Chauta ndi izi, Tsopano nkhosa zangazo ndidzazifunafuna ndekha mwiniwakene, ndipo ndidzazisamala. Monga m’busa amanka nafunafuna nkhosa zake, pamene zina zabalalikira kutali, Inenso ndidzatero, kunka ndikufunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa konse kumene zidamwazikira pa nthawi yamdima ndi yankhungu. Ineyo mwiniwake ndidzakhala m’busa wa nkhosa zanga. Ndipo Ine ndemwe ndizidzazipumulitsa. Ndikutero Ine Ambuye Chauta. Zotayika ndidzazifunafuna, zosokera ndidzazibweza, zopweteka ndidzazimanga mabala ake. Zofooka ndidzazilimbikitsa, koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosa zanga mwachilungamo. Tsono kunena za inu, nkhosa zanganu, Ine Ambuye Chauta ndikukuuzani kuti, Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zamphongo ndi atonde.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 23: 01 – 03, 05 – 06.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Chauta ndiye m’busa wanga,

Sindidzasowa kanthu,

Amandigoneka pa busa lamsipu.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako,

Amatsitsimutsa moyo wanga,

Amanditsogolera m’njira za chilungamo,

Malinga ndi ulemerero wa dzina lake.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Inu mumandikonzera chakudya,

Adani anga akuwona,

Mumandilandira bwino podzoza mutu wanga ndi mafuta,

Mumadzaza chikho changa mpaka kusefukira.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Zoonadi, zokoma zanu ndi chikondi chanu,

Zidzakhala ndi ine masiku onse a moyo wanga,

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu,

Moyo wanga wonse.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO; 01 AKORINTO 15: 20 – 26, 28. (Mwana wa Mulungu nayenso adzagonjera Mulungu, kuti Mulungu akhale wolamulira aliyense kwathunthu).

 

Abale, Khristu adauka ndithu kwa akufa. Pakati pa onse amene adafa, ndiye woyamba kuuka. Pakuti monga imfa idadza pansi pano kudzera mwa munthu wina, momwemonso kuuka kwa akufa kudadza kudzera mwa munthu wina. Monga anthu onse amamwalira chifukwa ndi ana a Adamu, momwemonso anthu onse adzauka chifukwa cholumikizana ndi Khristu. Koma aliyense adzauka pa nthawi yake: woyambirira ndi Khristu, ndipo pambuyo pake, pamene Khristuyo adzabwera, nawonso amene ali ake adzauka. Pamenepo chimalizo chidzafika. Khristu atathetsa ufumu wonse, ulamuliro wonse, ndi mphamvu zonse, adzapereka ufumu uja kwa Mulungu Atate. Paja Khristu ayenera kulamulira mpaka atagonjetsa adani ake onse. Mdani wotsiriza kumthetsa mphamvu, ndiye imfa. Koma pamene zonse zidzakhala zitagonjera Khristu, pamenepo Mwana wa Mulungu nayenso adzagonjera Mulungu, amene adamgonjetsera zinthu zonse. Adzachita zimenezi kuti Mulungu akhale wolamulira aliyense kwathunthu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MARKO 11: 09, 10.

 

Alleluia, AlleluiaNgwodala amene alikudza m’dzina la Ambuye. Udalitsidwe Ufumu wa atate athu Davide umene ulikudza tsopano. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 25: 31 – 46. (Adzakhala pa mpando wake wachifumu ndipo adzawalekanitsa monga momwe mbusa amalekanitsira nkhosa ndi mbuzi.).

 

Yesu adawauza ophunzira ake kuti: “Pamene Mwana wa Munthu adzabwera ndi ulemerero wake, pamodzi ndi angelo onse, adzachita kukhalira pa mpando wake wachifumu. Adzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse pamaso pake, ndipo adzawalekanitsa monga momwe m’busa amalekanitsira nkhosa ndi mbuzi. Nkhosa adzazikhazika ku dzanja lake lamanja, koma mbuzi ku dzanja lake lamanzere. Tsono Iyeyo ngati Mfumu adzauza a ku dzanja lamanjawo kuti,

‘Bwerani kuno inu odalitsidwa a Atate anga. Lowani mu ufumu umene adakukonzerani chilengedwere dziko lapansi. Paja Ine ndidaali ndi njala, inu nkundipatsa chakudya. Ndidaali ndi ludzu, inu nkundipatsa chakumwa. Ndidaali mlendo, inu nkundilandira kunyumba kwanu. Ndidaali wamaliseche, inu nkundiveka. Ndinkadwala, inu nkumadzandizonda. Ndidaali m’ndende, inu nkumadzandichezetsa.’ Apo olungama aja adzati, ‘Ambuye, ndi liti

tidaakuwonani muli ndi njala, ife nkukupatsani chakudya, kapena muli ndi ludzu, ife nkukupatsani chakumwa? Ndi liti tidaakuwonani muli mlendo, ife nkukulandirani kunyumba kwathu, kapena muli wamaliseche, ife nkukuvekani? Ndi liti tidaamvapo kuti mukudwala kapena kuti muli m’ndende, ife nkudzakuchezetsani?’ Mfumuyo idzawayankha kuti, ‘Ndithu ndikunenetsa kuti nthawi iliyonse pamene munkamuchitira zimenezi wina aliyense mwa

abale anga ngakhale otsika kwambiriwa, munkachitira Ine amene.’ Pambuyo pake Mfumuyo idzauzanso a ku dzanja lake lamanzere aja kuti, ‘Chokani apa, inu otembereredwa. Pitani ku moto wosatha, umene Mulungu adakonzera Satana ndi angelo ake. Ine ndidaali ndi njala, inu osandipatsa chakudya. Ndidaali ndi ludzu, inu osandipatsa chakumwa. Ndidaali mlendo, inu osandilandira kunyumba kwanu. Ndidaali wamaliseche, inu osandiveka. Ndinkadwala, ndidaalinso m’ndende, inu osadzandichezetsa.’ Apo nawonso adzati, ‘Ambuye, ndi liti tidaakuwonani muli ndi njala, kapena muli ndi ludzu, kapena wamaliseche, ndi liti tidaamvapo kuti mukudwala kapena kuti muli m’ndende, ife osachitapo kanthu?’ Mfumuyo idzawayankha kuti, ‘Ndithu ndikunenetsa kuti, nthawi iliyonse pamene munkakana kuthandiza wina aliyense mwa abale anga ngakhale otsika kwambiriwa, munkakana kuthandiza Ine amene.’ Pamenepo iwowo adzachoka kumapita ku chilango chosatha, olungama aja nkumapita ku moyo wosatha.”

 

Mthenga wa Ambuye…...…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pakuti ndife ake a Khristu, tiyeni tipemphe Atate athu a Kumwamba kuti Ufumu wao ukhazikike m’dziko lonse lapansi.

 

1.     Akhristu onse akondane ndi kuika mtima pa ntchito zachifundo, aonetse anthu onse kudza kwa Ufumu wa Kumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Mafumu ndi akulu olamulira maiko alimbikire kukhazikika pa chilungamo, chimvano ndi mtendere pakati pa anthu ao.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu amene akusauka ndi njala, odwala, olumala, omangidwa, ndi onse amene akuvutika m’mitima mwao, apeze anzao achifundo owachitira zabwino.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse tili muno tiwafewere mtima anzathu amene ali osowa, tiziwathandiza monga momwe tingathere osaopa kupereka moyo wathu womwe.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate popereka kwa Inu mapemphero athuwa, tikutamanda chifundo chanu chofuna kutisonkhanitsa tonse mu Ufumu wanu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, November 18, 2023

LAMULUNGU LA 33 PA CHAKA – CHAKA A

“Tizigwiritsa Ntchito Mphatso za Mulungu.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MIYAMBO; MIYAMBO 31: 10 – 13, 19 – 20, 30 – 31 (Kodi mkazi wolemerera angathe kumpeza ndani?).

 

Kodi mkazi wolemerera angathe kumpeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala ya yamtengowapatali. Mtima wa mwamuna wake umamkhulupirira, ndipo mwamunayo sadzasowa phindu. Masiku onse a moyo wake, mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino osati zoipa. Amanka nafunafuna ubweya ndi thonje, ndipo amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu. Thonje amadzilukira yekha, ndipo nsalu amadziwombera yekha. Anthu osauka amawachitira chifundo, amphawi amawapatsa chithandizo. Nkhope yachikoka ndi yonyenga, kukongola nkosakhalitsa, koma mkazi woopa Chauta ndiye woyenera kumtamanda. Muzimlemekeza chifukwa cha zochita zake, ntchito zake zizimpatsa ulemu ku mabwalo.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 127: 01 – 05.

 

Ngwodala aliyense woopa Chauta.

 

Ngwodala aliyense woopa Chauta,

Amene amayenda m’njira zake,

Udzadya zimene manja ako adzagwirira ntchito,

Udzasangalala, ndipo zinthu zidzakuyendera bwino.

 

Ngwodala aliyense woopa Chauta.

 

Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka,

M’kati mwa nyumba yako,

Ana ako adzakhala ngati tiziphukira taolivi,

Kuzungulira tebulo lako.

 

Ngwodala aliyense woopa Chauta.

 

Zoonadi, ndimo m’mene adzakhalire wodala munthu woopa Chauta,

Chauta amene amakhala ku Ziyoni akudalitse,

Uwone m’mene Yerusalemu zinthu zidzamuyendere bwino,

Masiku onse a moyo wako.

 

Ngwodala aliyense woopa Chauta.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA ATESALONIKA; 01 ATESALONIKA 05: 01 – 06 (Koma inu abale, simuli m’chimbulimbuli kuti tsikulo nkukudzidzimutsani ngati mbala).

 

Abale, za nthawi ndi nyengo yake yodzachitika zimenezi, nkosafunikira kuti ndichite kukulemberani. Inu nomwe mukudziwa bwino kuti tsiku la Ambuye likazafika ngati mbala yausiku. Pamene anthu azikati, Pali mtendere, tili pabwino, pamenepo chiwonongeko chidzawagwera modzidzimutsa. Chidzawadzidzimutsa monga momwe zowawa zimamchitira mkazi pa nthawi yoti achire; ndipo sadzatha konse kuchizemba. Koma inu abale, simuli m’chimbulimbuli kuti tsikulo nkukudzidzimutsani ngati mbala. Paja nonsenu zanu zonse ndi zam’kuwala, ndiye kuti zausana. Ife zathu si zausiku kapena zamumdima ai. Nchifukwa chake tsono tisagone tulo monga momwe amachitira anthu ena, ife tikhale maso, tikhale osaledzera.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 15: 04a, 05b.

Alleluia, Alleluia – Khalani mwa Ine, ndipo Inenso ndidzakhala mwa inu, atero Ambuye. Munthu wokhala mwa Ine amabereka zipatso zambiri. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 25: 14 – 30 (Popeza kuti udakhulupirika pa zinthu zochepa, bwera udzakondwere pamodzi ndi ine).

 

Yesu adawauza ophunzira ake fanizo ili: “Za Ufumu wakumwamba tingazifanizirenso motere: Munthu wina ankapita pa ulendo. Asananyamuke adaitana antchito ake, nawasiyira chuma chake. Wina adampatsa ndalama zisanu, wina ziwiri, wina imodzi. Aliyense adampatsa molingana ndi nzeru zake, iye nkuchokapo. Wantchito amene adaalandira ndalama zisanu uja adapita nakachita nazo malonda nkupindula ndalama zinanso zisanu. Chimodzimodzinso amene adaalandira ndalama ziwiri uja, adapindula ndalama zinanso ziwiri. Koma amene adaalandira ndalama imodzi uja, adapita nakaikumbira pansi ndalama ya mbuye wake ija. Patapita nthawi yaitali, mbuye wao uja adabwerako nawaitana antchito ake aja kuti amufotokozere za zimene

adaachita ndi ndalama zija. Wantchito amene adaalandira ndalama zisanu uja adabwera ndi zisanu zinanso nati, ‘Ambuye, mudaandisiyira ndalama zisanu. Onani, ndidapindula zisanu zinanso: izi.’ Mbuye wakeyo adamuuza kuti, ‘Udachita bwino kwabasi, ndiwe mtumiki wabwino ndi wokhulupirika. Tsono popeza kuti udakhulupirika pa zinthu zochepa, ndidzakuika kuti uziyang’anira zinthu zambiri. Bwera udzakondwere pamodzi ndi ine, mbuye wako.’ Nayenso wantchito amene adaalandira ndalama ziwiri uja, adabwera nati, ‘Ambuye, mudaandisiyira ndalama ziwiri. Onani, ndidapindula ziwiri zinanso: izi.’ Mbuye wakeyo adamuuza kuti,

‘Udachita bwino, ndiwe mtumiki wabwino ndi wokhulupirika. Tsono popeza kuti udakhulupirika pa zinthu zochepa, ndidzakuika kuti uziyang’anira zinthu zambiri. Bwera udzakondwere pamodzi ndi ine, mbuye wako.’ Nayenso amene adaalandira ndalama imodzi uja adabwera nati,

‘Ambuye, ine ndinkadziwa kuti inu ndinu munthu wankhwidzi. Mumakolola kumene simudabzale, ndipo mumasonkhanitsa dzinthu kumene simudafese mbeu. Ndiye ndinkachita mantha, choncho ndidaakaikumbira pansi ndalama yanu ija. Nayi tsono ndalama yanuyo.’ Apo mbuye wake uja adamuuza kuti, ‘Ndiwe wantchito woipa ndi waulesi. Kani unkadziwa kuti ineyo ndimakolola kumene sindidabzale, ndipo ndimasonkhanitsa dzinthu kumene sindidafese mbeu? Tsonotu udaayenera kukaika ku banki ndalama yangayo, ine pobwera ndikadadzailandira pamodzi ndi chiwongoladzanja chake. Mlandeni ndalamayi, muipereke kwa amene ali ndi ndalama khumiyo. Pajatu aliyense amene ali ndi kanthu, adzamuwonjezera zina, choncho adzakhala ndi zochuluka koposa. Koma amene alibe kanthu, ngakhale kamene ali nakoko adzamlandabe. Tsono mtumiki wopandapakeyu kamponyeni kunja ku mdima. Kumeneko azikalira ndi kukukuta mano.’”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, tsopano tikweze mitima yathu ndi mapemphero athu Kumwamba kuti mau a Ambuye agwire ntchito mwa ife ndi mwa anthu onse:

 

1.     Atsogoleri a Mpingo alimbikire kutumikira anthu ao modziiwala ndi modzichepetsa, pogwiritsa ntchito mphatso zomwe Mulungu adawaninkha.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akulu olamulamulira maiko asenze udindo wao mofatsa ndi molimba mtima, potsata ubwino wa anthu ao momwe Mulungu afunira.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Mabanja onse, eniake akhale a mtima umodzi pa ntchito zokometsera moyo wao, makamaka pa ntchito zolera bwino ana ao.

Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse tili muno tikhale anthu achangu pa ntchito zothandiza Mpingo wa Ambuye ndi pa ntchito zotukula moyo wa anthu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, musaleke kutilimbitsa ndi Mzimu wanu Woyera, kuti ntchito zathu zonse zikhale zokutsirani ulemu ndi zokulitsa chikondi chanu m’mitima ya anthu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, November 11, 2023

LAMULUNGU LA 32 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 32 PA CHAKA – CHAKA A.

“Simudziwa tsiku lake kapena nthawi yake.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA LUNTHA; LUNTHA 06: 12 – 16 (Luntha ndi lowala, lilibe mdima. Kwa olikonda, nkwapafupi kuliwona).

 

Luntha ndi lowala, lilibe mdima. Kwa olikonda, nkwapafupi kuliwona, olifunafuna amalipeza. Limadziwonetsa mwamsanga kwa anthu olifuna. Munthu wodzuka m’mamawa kuti alifune, sadzavutika, adzalipeza litakhala kale pakhomo pake. Kuikapo mtima pa za luntha ndiye kumvetsa bwino zinthu. Munthu wochita changu pofunafuna adzaona msanga mtendere wamumtima. Pajatu limayesayensa kufunafuna oyenera kulilandire, limadziwonetsa kwa iwowo m'njira zao, limapezekanso ndi m’maganizo ao omwe.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 63: 02 – 08.

 

Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu, Mulungu wanga.

 

Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, ndimakufunafunani,

Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu,

Thupi langa likulakalaka Inu,

Ngati dziko louma, loguga ndi lopanda madzi.

 

Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu, Mulungu wanga.

 

Ndikukhumbira kukuwonani m’malo anu oyera,

Ndi kuwona mphamvu zanu ndi ulemerero wanu,

Ndidzakutamandani chifukwa chikondi chanu nchabwino kupambana moyo,

Ndipo pakamwa panga padzakutamandani Inu.

 

Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu, Mulungu wanga.

 

Choncho ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,

Ndidzakweza manja anga kwa Inu mopemphera,

Mudzandikhutitsa ndi zonona,

Ndipo ndidzakutamandani ndi mau osangalala.

 

Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu, Mulungu wanga.

 

Ndikagona pabedi panga ndimalingalira za Inu,

Usiku wonse ndimasinkhasinkha za Inu,

Inu mwakhala chithandizo changa,

Motero ndikuimba ndi chimwemwe pansi pa mapiko anu.

 

Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu, Mulungu wanga.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA ATESALONIKA; 01 ATESALONIKA 04: 13 – 18 (Amene adamwalira akukhulupirira Yesu, iwonso Mulungu adzawaukitsa nkubwera nawo pamodzi ndi Yesuyo).

 

Abale, tifuna kuti mudziweko za anthu amene adamwalira, kuti chisoni chanu chisakhale ngati cha anthu ena amene alibe chiyembekezo. Paja ife timakhulupirira kuti Yesu adaamwalira naukanso. Motero timakhulupiriranso kuti anthu amene adamwalira akukhulupirira Yesu, iwonso Mulungu adzawaukitsa nkubwera nawo pamodzi ndi Yesuyo. Tsopano tikuuzeni mau a Ambuye mwini. Ife amoyofe, otsala mpaka kubwera kwa Ambuye, sikuti tidzawasiya kumbuyo amene adamwalira aja ai. Padzakhala mfuu wa mau a mngelo wamkulu ndi wa lipenga la Mulungu. Ndipo pamenepo Ambuye mwini adzatsika kuchokera Kumwamba. Anthu amene adafa akukhulupirira Khristu, adzayamba ndiwo kuuka. Pambuyo pake ife amoyofe, otsalafe, tidzatengedwa pamodzi nawo m’mitambo kuti tikakumane ndi Ambuye mu mlengalenga. Motero tidzakhala ndi Ambuye nthawi zonse. Nchifukwa chake tsono muzithuzitsana mtima pokambirana zimenezi.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 24: 42a, 44.

Alleluia, Alleluia – Khalani maso, chifukwa simudziwa tsiku limene Mwana wa Munthu adzabwera. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 25: 01 – 13 (Mkwati akubwera! Tulukani, kamchingamireni!).

 

Yesu adawauza ophunzira ake fanizo ili: “Pa nthawi imeneyo za Ufumu wakumwamba zidzafanafana ndi zimene zidaachitikira anamwali khumi. Iwowo adaatenga nyale zao nkumakachingamira mkwati. Asanu anali opusa, ndipo asanu enawo anali ochenjera. Asanu opusa aja adangotenga nyale zao, osatenga mafuta ena apadera. Koma asanu ochenjera aja adaatenga mafuta ena apadera m’nsupa zao. Popeza kuti mkwati adaachedwa, onse aja adayamba kuwodzera, nagona tulo. Tsono pakati pa usiku kudamveka kufuula kuti, ‘Mkwati akubwera! Tulukani, kamchingamireni!’ Anamwali khumi aja adadzuka, nkuyamba kukonza nyale zao zija. Opusa aja adapempha ochenjera aja kuti, ‘Tipatseniko mafuta, onani nyale zathu zikuzima.’ Koma ochenjera aja adati, ‘Hi, ai, tikatero satikwanira tonsefe. Bwanji osati mungopita ku sitoro mukagule anu.’ Pamene ankakagula, mkwati adafika. Amene anali okonzekeratu aja adalowa naye pamodzi m’nyumba yaphwando; pambuyo pake adatseka chitseko. Kenaka m’mbuyo mwalendo anamwali ena aja nawonso adabwera nati, ‘Bwana, Bwana, titsekulireni!’ Koma mkwatiyo adati, ‘Pepani, sindikukudziwani!’” Pomaliza Yesu adati, “Ndiyetu inu, muzikhala maso, poti simudziwa tsiku lake kapena nthawi yake?”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, ife amene tilikuyembekeza kubwera kwa Ambuye, tiyeni tipemphe Atate a Kumwamba kuti aike m’mitima mwathu ndi mwa anthu onse chikhulupiriro ndi chikondi choona:

 

1.     Apapa, Aepiskopi ndi ansembe onse, atsogolere akhristu ao m’njira yaungwiro ndi yachikondi, powakumbutsa za kukonzekera kubwera kwa Ambuye.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

2.     Anthu amene angokhulupirira zapansi pano adzidzimuke pakumva za chikondwerero chimene Mulungu wakonzera anthu ake Ufumu wa Kumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

3.     Akhristu ofooka ndi osokera, adzuke ndi kubwerera kwa Mulungu ndi mtima wolapa, podziwa kuti Ambuye adzabwera pa nthawi imene ife sitiyembekezako.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tomwe tilimbikire kuchita ntchito zachifundo ndi kumapemphera, kuwopa kuti mwina nyale zathu zingazime.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, mwa chifundo chanu mverani mapemphero athuwa. Mutikhazikitse m’chikondi chanu, kufikira tsiku limene adzatitenge. Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, November 4, 2023

LAMULUNGU LA 31 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 31 PA CHAKA – CHAKA A.

“Muli ndi Atate amodzi okha, ndiwo Atate anu a Kumwamba.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MALAKI; MALAKI 01: 14 – 02: 02. 08 – 10 (Koma inu ansembe mudasiya njira yanga. Mudaphunthwitsa anthu ambiri ndi zophunzitsa zanu).

 

Chauta Wamphamvuzonse akunena kuti, “Ine ndine Mfumu yaikulu, ndipo dzina langa nlochititsa mantha pakati pa anthu a mitundu yonse. Tsono ansembe inu, lamulo ili nlokhalira inu. Mukapanda kundimvera, mukapanda kulemekeza dzina langa, ndidzakutembererani. Zabwino zimene mumazilandira nazonso ndidzazitemberera. Ndithu, ndazitemberera kale chifukwa simudamvere ndi mtima wonse. Koma inu ansembe mudasiya njira yanga. Mudaphunthwitsa anthu ambiri ndi zophunzitsa zanu. Mudaipitsa chipangano changa ndi Alevi. Ndikutero Ine Chauta Wamphamvuzonse. Nchifukwa chake Inenso ndakusandutsani onyozeka ndi achabechabe pamaso pa anthu, popeza kuti simudatsate njira zanga, ndipo mwakhala mukukondera poweruza milandu.” Kodi tonsefe suja tili ndi bambo mmodzi? Kodi suja adatilenga ndi Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tsono tikuphwanya chipangano cha Mulungu ndi makolo athu posamakhulupirirana?

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 131.

 

Ambuye, sungani mtima wanga mwa mtendere.

 

Chauta, mtima wanga ndi wosadzikuza,

Maso anga ndi osanyada,

Sinditengeka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.

 

Ambuye, sungani mtima wanga mwa mtendere.

 

Koma ndautonthoza ndi kuukhalitsa chete mtima wanga,

Monga mwana amene mai wake amamtonthoza ndi bere.

Momwemo mtima wanga uli phe m’kati mwanga.

 

Ambuye, sungani mtima wanga mwa mtendere.

 

Iwe Israele, khulupirira Chauta,

Kuyambira tsopano mpaka muyaya.

 

Ambuye, sungani mtima wanga mwa mtendere.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA ATESALONIKA; 01 ATESALONIKA 02: 07 – 09, 13 (Tidatsimikiza zogawana nanu osati Uthenga Wabwino wa Mulungu wokha, komanso ngakhale moyo wathu womwe).

 

Abale, tidakhala ofatsa pakati panu ngati mai wosamalira ana ake. Tinkakukondani, ndipo chifukwa cha kukulakalakani kwambiri, tidatsimikiza zogawana nanu osati Uthenga Wabwino wa Mulungu wokha, komanso ngakhale moyo wathu womwe. Abale, simukumbukira nanga kuti tinkagwira ntchito kwambiri mpaka kutopa? Monse muja tinkakulalikirani Uthenga Wabwino wa Mulungu, tinkagwira ntchito zamanja usana ndi usiku, kuwopa kuti tingavutitse wina aliyense mwa inu. Pa mbali yathu, timathokoza Mulungu kosalekeza. Timatero chifukwa chakuti pamene mudamva mau a Mulungu amene tidakulalikirani, mudawalandira osati ngati mau a anthu chabe, koma monga momwe aliri ndithu, mau a Mulungu. Mauwo ndi omwe akugwira ntchito mwa inu okhulupirira.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 23: 9b, 10b.

Alleluia, Alleluia – Muli ndi Atate amodzi okha, ndiwo Atate anu akumwamba. Mphunzitsi wanu ndi mmodzi yekha, ndiye Khristu. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 23: 01 – 12 (Sachita zimene amaphunzitsa).

 

Pa nthawi yomweyo, Yesu adalankhula ndi gulu la anthu ochuluka pamodzi ndi ophunzira ake. Adawauza kuti, “Aphunzitsi a Malamulo ndi Afarisi ali ndi udindo wotanthauzira malamulo a Mose. Nchifukwa chake muzichita ndi kutsata zonse zimene iwo amakuphunzitsani. Komatu musamatsanzira zimene amachita, pakuti sachita zimene amaphunzitsa. Iwo amamanga katundu wosautsa kunyamula nkusenzetsa anthu, koma iwowo samukhudzako mpang’ono pomwe. Zonse zimene amachita amangozichita kuti anthu awaone. Amadzimangirira timapukusi tikulutikulu ta mau a Mulungu pa mphumi ndi pa mkono. Amatalikitsanso mphonje za zovala zao. Amakonda malo olemekezeka pa maphwando ndiponso mipando yaulemu kwambiri ku nyumba zamapemphero. Amakondanso kuti anthu aziwalonjera mwaulemu pa misika, ndipo kuti aziwatchula aphunzitsi. Koma inuyo anthu asati azikutchulani aphunzitsi, pakuti muli ndi

Mphunzitsi mmodzi yekha, ndipo nonsenu muli pa chibale. Musamatchulanso munthu pansi pano kuti atate, popeza kuti muli ndi atate amodzi okha, ndiwo Atate anu akumwamba. Anthu asatinso azikutchulani atsogoleri, popeza kuti Mtsogoleri wanu ndi mmodzi yekha, ndiye Khristu. Pakati panupa wamkulu akhale mtumiki wanu. Pajatu aliyense wodzikuza adzamchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamkuza.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pozindikira kuti tonse tili pachibale ndipo Yesu Mtsogoleri wathu waimirira pakati pathu, tiyeni tipempherere anthu onse:

 

1.     Ansembe ndi akulu onse a Mpingo asenze udindo wao mokhulupirika ndi modzichepetsa, pakutumikira anthu ao mwachifundo.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akhristu onse nawonso ayesetse kutsogolera anthu anzao pa njira ya chipulumutso, pakuwaphunzitsa ndi kuwaonetsa mtima wachikondi.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Akhristu amene akhumudwa ndi zitsanzo zoipa za atsogoleri ao, asati ataye mtima, koma ayesetse kulangiza atsogoleriwo mwaubale.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse osonkhana pano, tileke mtima wamantha, kuti tiziweruzana ndi kumalangizana mwachifundo, pofuna kukometsa makhalidwe a Mpingo.
Tikupemphani, mutivomereze.


Atate, mutiwongolere ndi Mzimu wanu Woyera, kuti tikutumikireni modzichepetsa polondola mapazi a Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...