Saturday, October 28, 2023

LAMULUNGU LA 30 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 30 PA CHAKA – CHAKA A.

“Uzikonda mnzako, kusonyeza Mulungu kuti umamukondadi.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA EKSODO; EKSODO 22: 20 – 26 (Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye. Mukamawazunza, Ine ndidzakukwiyirani).

 

Chauta adamuuza Mose kuti, “Muwauze ana a Israele kuti, ‘Musazunze mlendo kapena kumkhalitsa m’phanthi, poti paja inunso munali alendo ku dziko la Ejipito. Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye. Mukamawazunza, Ine ndidzawamva iwowo akamalira kwa Ine. Ndidzakukwiyirani, ndipo ndidzakuphani ku nkhondo. Akazi anu adzasanduka amasiye, ndipo ana anunso adzasanduka amasiye. Mukakongoza ndalama munthu wina aliyense waumphawi pakati panupo, musamachita monga momwe amachitira anthu okongoza, musamuumirize kupereka chiwongoladzanja. Mukatenga mwinjiro wa munthu wina ngati chigwiriro kuti adzakulipireni, muubweze dzuwa lisanalowe, poti chofunda nchokhacho, ndicho chotetezera thupi lake. Nanga adzafunda chiyani? Akalira kwa Ine iyeyu kuti ndimthandize, ndidzamuyankha chifukwa ndine wachifundo.’”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 18: 02 – 04, 47, 51.

 

Ndimakukondani Chauta, Inu mphamvu zanga.

 

Ndimakukondani Chauta, Inu mphamvu zanga.

Chauta ndiye linga langa ndi mpulumutsi wanga,

Ndiye Mulungu wanga, ndi thanthwe langa limene ndimathawirako,

Ndimaitana Chauta, amene ayenera kumtamanda, ndipo amandipulumutsa kwa adani anga.

 

Ndimakukondani Chauta, Inu mphamvu zanga.

 

Chauta ndi wamoyo. Litamandike thanthwe langa, alemekezeke Mulungu wondipulumutsa

Mulungu amathandiza mfumu yake,

kuti izipambana nthawi ndi nthawi,

Amaonetsa chikondi chake kwa wodzozedwa wake.

 

Ndimakukondani Chauta, Inu mphamvu zanga.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA ATESALONIKA; 01 ATESALONIKA 01: 05 – 10 (Mudasiyira mafano ndi kutembenukira kwa Mulungu, kuti muzimtumikira: tsopano mukudikira Mwana wake).

 

Abale, Uthenga Wabwino umene tidadza nawo kwa inu sunali wapakamwa chabe, koma tinkaulalika ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndiponso mosakayika konse. Mukudziwa m’mene tinkakhalira pakati panu pofuna kuti tikuthandizeni. Inu mwakhala mukutsata chitsanzo chathu ndi cha Ambuye. Ngakhale mudapeza masautso ambiri, mudalandira mau athu mwa chimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera. Motero nanunso mudakhala chitsanzo kwa okhulupirira onse a ku Masedoniya ndi a ku Akaiya. Inde kuchokera kwa inu mau a Ambuye adakafika ku Masedoniya ndi ku Akaiya, ndipo kuwonjezera apo mbiri yakuti mudakhulupirira Mulungu idawanda ponseponse. Motero palibe chifukwa chakuti ife nkunenapo kanthu. Iwo amakamba okha za m’mene mudatilandirira, ndi za m’mene mudasiyira mafano ndi kutembenukira kwa Mulungu weniweni wamoyo, kuti muzimtumikira. Tsopano mukudikira

Mwana wake kuti abwerenso kuchokera Kumwamba. Mwana wakeyo ndi Yesu, amene Mulungu adamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ulikudza.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 14: 23.

Alleluia, Alleluia – Ngati munthu andikonda, adzatsata zimene ndanena Ine. Atate

anga adzamkonda, ndipo Ife tidzabwera nkukhazikika mwa iye. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 22: 34 – 40 (Uzikonda Chauta, Mulungu wako, ndipo uzikonda mnzako

monga momwe umadzikondera iwe wemwe).

 

Afarisi atamva kuti Yesu adatsutsa Asaduki, adasonkhana. Tsono mmodzi mwa iwo, katswiri wa Malamulo adafunsa Yesu funso kuti amutape m’kamwa. Adati, “Aphunzitsi, kodi mwa malamulo onse a Mulungu, lalikulu ndi liti?” Yesu adamuyankha kuti, “Uzikonda Chauta, Mulungu wako, ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse. Limeneli ndiye lamulo lalikulu ndi loyamba ndithu. Lachiwiri lake lofanana nalo ndi ili: Uzikonda mnzako monga momwe umadzikondera iwe wemwe. Malamulo onse a Mose ndiponso zonse zimene aneneri adaphunzitsa zagona pa malamulo awiriwa.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pakuti Mulungu amakonda anthu kwambiri timupemphe kuti aike chikondi chake chomwecho m’mitima mwathu ndi mwa anthu onse:

 

1.     Akhristu onse alimbikire kuchita ntchito zachifundo ndi kusonyeza chikondi choona kwa anthu anzawo.
Tikupemphani, mutivomereze.


 

2.     Atsogoleri a mipingo yachikhristu aongolere akhristu ao m’njira yachikondi, pokumbukira kuti ili ndi lamulo la Ambuye.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu odwala, ovulala ndi onse amene akuvutika, apeze anzao achifundo owasamala ndi owalimbitsa mtima.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse a m’Parishi yathu ino, kukondana kwathu kupite m’tsogolo kusonyeza kuti ndifedi abale ake a Yesu ndipo kuti Iye akukhaladi pakati pathu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, ife tazindikira chikondi chanu poona kuti Mwana wanu adapereka moyo wake chifukwa cha ife. Mudzaze mitima yathu ndi chikondi chanu chomwecho, nafenso tidziwe kupereka moyo wathu chifukwa cha abale athu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, October 21, 2023

LAMULUNGU LA 29 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 29 PA CHAKA – CHAKA A.

“Perekani kwa Mulungu zake za Mulungu.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MPROFETI YESAYA; YESAYA 45: 01, 04 – 06 (Chauta adamgwira Kirusi padzanja lamanja, kuti agonjetse mitundu ina ya anthu).

 

Chauta akulankhula ndi wodzozedwa wake Kirusi amene adamgwira dzanja lamanja, kuti agonjetse mitundu ina ya anthu, awathe mphamvu mafumu, ndi kutsekula zitseko kuti zipata zisatsekeke. Akunena kuti, “Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israele, ndikukuitana potchula dzina lako, ndikukupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa. Chauta ndine, palibenso wina, kupatula ine palibe Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu ngakhale sukundidziwa. Ndidzachita zimenezi kuti kuchokera kuvuma mpaka kuzambwe aliyense adziwe kuti palibe wina koma Ine ndekha.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 96: 01, 03 – 05, 07 – 10.

 

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta.

 

Imbirani Chauta nyimbo yatsopano!

Imbirani Chauta, anthu a m’dziko lonse lapansi!

Lengezani za ulemerero wake kwa anthu a mitundu yonse,

Simbani za ntchito zake zodabwitsa kwa anthu a m'maiko onse.

 

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta.

 

Chauta ngwamkulu, ngwoyenera kumtamanda kwambiri,

Ngwoyenera kumuwopa kupambana milungu yonse,

Paja milungu yonse ya mitundu ina ya anthu ndi mafano chabe,

Koma Chauta ndiye adalenga zakumwamba.

 

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta.

 

Tamandani, inu anthu a mitundu yonse,

Vomerezani kuti ulemerero ndi mphamvu, zonse nzake.

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta,

Bwerani ndi zopereka, ndipo mulowe m’mabwalo a Nyumba yake.

 

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta.

 

Pembedzani Chauta waulemerero ndi woyera,

Njenjemerani pamaso pake, inu anthu onse a pa dziko lapansi,

Uzani mitundu ya anthu kuti, ‘Chauta ndiye Mfumu,

Adzaweruza mitundu yonse ya anthu mwachilungamo.’

 

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA ATESALONIKA; 01 ATESALONIKA 01: 01 – 05 (Timakumbukira kosalekeza za chikhulupiriro chanu, chikondi chanu ndi chiyembekezo chanu).

 

Abale, ndife, Paulo, Silivano ndi Timoteo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli wake wa Mulungu Atate, ndiponso wa Ambuye Yesu Khristu. Mulungu akukomereni mtima ndi kukupatsani mtendere. Timathokoza Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu nonse ndi kumakutchulani m’mapemphero athu. Timakumbukira kosalekeza pamaso pa Mulungu Atate athu za m’mene mumatsimikizira chikhulupiriro chanu mwa ntchito zanu, za m’mene chikondi chanu chimakuthandizirani kugwira ntchito kolimba, ndiponso za m’mene mumachitira khama poyembekeza Ambuye athu Yesu Khristu. Abale athu, inu amene Mulungu amakukondani, tikudziwa kuti Iye adakusankhani kuti mukhale ake. Paja Uthenga Wabwino umene tidadza nawo kwa inu sunali wapakamwa chabe, koma tinkaulalika ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndiponso mosakayika konse. Mukudziwa m’mene tinkakhalira pakati panu pofuna kuti tikuthandizeni.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – AFILIPI 02: 15d, 16a.

Alleluia, Alleluia – Pakati pa anthu mumawala monga momwe zimaonekera nyenyezi pa dziko lapansi pakuwauza mau opatsa moyo. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 22: 15 – 21 (Perekani kwa Mfumu zake za Mfumuyo, ndiponso kwa Mulungu zake za Mulungu).

 

Nthawi ina Afarisi adakapangana zodzatapa Yesu m’kamwa. Adatuma ophunzira ao ena pamodzi ndi ena a m’chipani cha Herode kwa Yesu. Iwowa adauza Yesu kuti, “Aphunzitsi, tikudziwa kuti Inu mumanena zoona, mumaphunzitsa malamulo a Mulungu moona, ndipo simuwopa munthu aliyense. Paja Inu simuyang’anira kuti uyu ndani. Ndiye timati mutiwuze zimene mukuganiza. Kodi Malamulo a Mulungu amatilola kuti tizikhoma msonkho kwa Mfumu ya ku Roma, kapena ai?” Koma Yesu podziwa maganizo ao oipa, adati, “Bwanji kodi mukundiyesa dala, anthu achiphamasonu? Tandiwonetsani ndalama yamsonkho.” Iwo adampatsadi ndalamayo. Pamenepo Iye adawafunsa kuti, “Kodi nkhopeyi ndi ya yani, ndipo dzinali ndi la yani?” Iwo aja adati, “Zonse ndi za Mfumu ya ku Roma.” Apo Yesu adawauza kuti, “Tsono perekani kwa Mfumu zake za Mfumuyo, ndiponso kwa Mulungu zake za Mulungu.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pokumbukira kuti Ufumu wa Mulungu uyambirira pansi pano pomwe, m’mitima ya anthu, tiyeni tiwapempherere anthu onse:

 

1.     Atsogoleri a Mpingo asaope kulankhula mau ndi kuteteza anthu ao pamene paoneka zina ndi zina zotsutsana ndi chilungamo, ufulu ndinso mtendere.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akulu a boma ndi akulu ena osenza maudindo osiyanasiyana, asenze udindo wao mokhulupirika ndi mosakondera potsata ubwino wa anthu onse.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Akhristu onse adzipereke kwathunthu ku ntchito zotukula moyo wa anthu anzao, podziwa kuti pakutero alikudzetsa Ufumu wa Mulungu m’mitima mwao.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse osonkhana pano, chikhristu chathu chiziwonekera poyera, osati lamulungu lokha, komanso m’zochita zathu za masiku onse.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, mwa chifundo chanu mumvere mapemphero athuwa, ndipo mutiwongolere kuti ntchito zathu zonse zikhale zogwirizana ndi zimene mufuna Inu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, October 14, 2023

LAMULUNGU LA 28 PA CHAKA – CHAKA A

 LAMULUNGU LA 28 PA CHAKA – CHAKA A.

“Mulungu amaitana anthu onse ku chikondwerero chosatha.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MPROFETI YESAYA; YESAYA 25: 06 – 10 (Chauta Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse

phwando ndipo adzapukuta misozi m’maso mwa aliyense).

 

Pa phiri ili la Ziyoni Chauta Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse phwando la zakudya zokoma ndi la vinyo wabwino, phwando la nyama yonona ndi la vinyo amene wafikapo. Pa phiri limeneli adzachotsa chisoni chimene chaphimba anthu a mitundu yonse, chimene chakuta mafuko onse. Chauta adzathetsa imfa mpaka muyaya, adzapukuta misozi m’maso mwa aliyense, ndipo adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi. Watero Chauta. Tsiku limenelo aliyense adzati, Uyu ndiye Mulungu wathu! Tidamkhulupirira kuti adzatipulumutsa. Iyeyu ndiye Chauta. Tidamkhulupirira, tsopano tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa choti watipulumutsadi. Chauta adzateteza phirili ndi dzanja lake.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 23.

 

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu, Ambuye, moyo wanga wonse.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu,

Amandigoneka pa busa lamsipu,

Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako,

Amatsitsimutsa moyo wanga,

Amanditsogolera m’njira za chilungamo malinga ndi ulemerero wa dzina lake.

 

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu, Ambuye, moyo wanga wonse.

 

Ngakhale ndiyende m’chigwa chamdima wabii,

Sindidzaopa choipa chilichonse,

Pakuti Inu Ambuye mumakhala nane,

Chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditeteza.

 

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu, Ambuye, moyo wanga wonse.

 

Inu mumandikonzera chakudya, adani anga akuwona,

Mumandilandira bwino podzoza mutu wanga ndi mafuta,

Mumadzaza chikho changa mpaka kusefukira.

 

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu, Ambuye, moyo wanga wonse.

 

Zoonadi, zokoma zanu ndi chikondi chanu,

Zidzakhala ndi ine masiku onse a moyo wanga,

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu moyo wanga wonse.

 

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu, Ambuye, moyo wanga wonse.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AFILIPI; AFILIPI 04: 12 – 14, 19 – 20 (Ndingathe kuchita zonse chifukwa Khristu amandipatsa mphamvu).

 

Abale, kukhala wosauka ndimakudziwa, kukhala wolemera ndimakudziwanso. Pa zonse ndidaphunzira chinsinsi chake cha kukhala wokhutitsidwa, pamene ndapeza chakudya kapena ndili ndi njala, pamene ndili ndi zambiri kapena ndili wosoweratu. Ndingathe kuchita zonse chifukwa Khristu amandipatsa mphamvu. Komabe mudaachita bwino kundithandiza pa zovuta zanga. Mulungu wanga ali ndi chuma chochuluka, ndipo mwa Khristu Yesu adzakupatsani

zonse zimene mukusowa. Mulungu Atate athu alemekezedwe mpaka muyaya. Amen.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – AEFESO 01: 17 – 18.

Alleluia, Alleluia – Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu akuunikireni m’mitima mwanu, kuti mudziwe zimene mungathe kuyembekezera kwa Mulungu amene adakuitanani. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 22: 01 – 14 (Mukaitane aliyense amene mukampeze, kuti abwere kuno ku phwando laukwati).

 

Yesu adalankhulanso ndi anthu aja m’mafanizo. Adati, “Za Ufumu wakumwamba tingazifanizire motere: Mfumu ina idaakonzera mwana wake phwando laukwati. Idatuma antchito ake kuti akawauze anthu amene adaaitanidwa kuphwandoko kuti azibwera, anthuwo nkukana. Idatumanso antchito ena nkunena kuti, Kawauzeni oitanidwa aja kuti chakudya chakonzeka. Ndapha ng’ombe ndi nyama zina zonenepa. Zonse zakonzeka, bwerani ku phwando laukwati. Koma oitanidwawo sadalabadireko, adangopita ku zao: wina kumunda kwake, wina ku ntchito yake yamalonda. Enawo adagwira antchito a mfumu aja nawazunza, nkuwapha. Pamenepo mfumu idapsa mtima kwambiri, mwakuti idatuma ankhondo ake kuti akaononge opha anzao aja, ndi kutentha mudzi wao. Pambuyo pake idauza antchito ake kuti, ‘Phwando laukwati ndiye lakonzekatu, koma oitanidwa aja anali osayenera. Pitani tsono ku mphambano za miseu, mukaitane aliyense amene mukampeze, kuti abwere kuno ku phwando laukwati.’ Apo antchitowo adapitadi ku miseu nakasonkhanitsa onse amene adawapeza, abwino ndi oipa omwe, mwakuti nyumba yaphwando idadzaza ndi anthu. Pamene mfumu ija idalowa m’nyumbamo kukaona anthu odzadya phwando aja, idapezamo wina amene sadavale chovala chaukwati. Tsono idamufunsa kuti, ‘Kodi iwe, walowa bwanji muno opanda chovala chaukwati?’ Iye uja adangoti chete. Apo mfumuyo idauza anyamata ake kuti, ‘Mmangeni manja ndi miyendo, mukamponye kunja ku mdima. Kumeneko adzalira ndi kukukuta mano.’” Tsono Yesu adati, “Inde oitanidwa ngambiri, komatu osankhidwa ngowerengeka.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, popeza kuti Mulungu ngwa chuma chochuluka ndipo mwa Yesu Khristu amatipatsa zonse zimene timasowa, tiyeni tipempherere anthu onse:

 

1.     Akhristu onse avomere kuitanidwa kwao ndi kumavala makhalidwe oyenera pa moyo wao wa tsiku ndi tsiku poyembekezera tsiku lolowera m’nyumba yachaka.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Ayuda atsekule mitima yao ndi kuvomera Mthenga wa Yesu Khristu, ndipo choncho afikire ku chipulumutso cha Kumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu amafuko onse nawonso azindikire ndi kuvomera kuitanidwa kwao, mpaka alowe ndithu m’chikondwerero cha Kumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tili muno, tikhale oyera mtima posunga malonjezo a ubatizo wathu, kufikira tsiku limene Ambuye adzatitsekulira nyumba yachaka.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, mwa chifundo chanu mverani mapemphero athuwa pamodzi ndi madandaulo a anthu onse; ndipo mutifikitse tonse ku chikondwerero chosatha. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, October 7, 2023

LAMULUNGU LA 27 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 27 PA CHAKA – CHAKA A.

“Munda wa Ambuye ndife amene.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MPROFETI YESAYA; YESAYA 05: 01 – 07 (Tsonotu munda wamphesawo wa Chauta Wamphamvuzonse ndi dziko la Israele).

 

Ntamuimbirako bwenzi langa nyimbo yokamba za wokondedwa wanga ndi munda wake wamphesa. Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa pa phiri la nthaka yachonde. Adautipula nachotsa miyala yonse, ndipo adaokamo mipesa yabwino kwabasi. Adamanga nsanja pakati pa mundawo, nasema mopondera mphesa m’kati momwemo. Adaayembekeza kuti mundawo udzabala mphesa zabwino, koma ai, udabala mphesa zachabechabe. Ndiye wokondedwa wanga akuti, Inu amene mumakhala ku Yerusalemu, ndi inu anthu a ku Yuda, ndakupembani, taweruzani pakati pa ine ndi munda wanga wamphesawu. Kodi chilipo chinanso chimene ndidaayenera kuchitira munda wanga wamphesa, koma sindidachite? Pamene ndinkayembekeza kuti udzabala mphesa zabwino, bwanji udabala mphesa zachabechabe? Tsopano taimani nkuuzeni zimene ndidzauchite munda wanga wamphesawo. Ndidzazula mpanda wake, ndipo mundawo udzaonongeka. Ndidzagwetsa chipupa chake, ndipo nyama zidzapondapondamo. Ndidzausandutsa tsala, udzakhala wosatengulira ndi wosalimira, ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina. Ndidzalamula mitambo kuti isagwetse mvula pamundapo. Tsonotu munda wamphesawo wa Chauta Wamphamvuzonseyo ndi dziko la Israele, ndipo Ayuda ndiwo mipesa yake yokondweretsa. Iye ankayembekeza ntchito zabwino, koma adangoona kuphana. Ankayembekeza chilungamo, koma adangomva kulira kwa anthu

ozunzidwa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 80: 09. 12 – 16. 19 – 20.

 

Munda wamphesawo wa Chauta Wamphamvuzonse ndi dziko la Israele.

 

Mudatulutsa mpesa wanu Israele m’dziko la Ejipito,

Mudapirikitsa mitundu ina ya anthu kuti muubzale mpesawo,

Nthambizo zidafika mpaka ku nyanja yaikulu yakuzambwe,

Ndipo mphukira zake mpaka ku mtsinje waukulu wakuvuma.

 

Munda wamphesawo wa Chauta Wamphamvuzonse ndi dziko la Israele.

 

Nanga chifukwa chiyani mwagumula mpanda wake,

Kuti opita m’njira azithyola nawo zipatso zake?

Nguluwe zam’nkhalango zimauwononga,

Ndipo zonse zoyenda m’thengo zimaudya.

 

Munda wamphesawo wa Chauta Wamphamvuzonse ndi dziko la Israele.

 

Mutembenukirenso kwa ife, Inu Mulungu Wamphamvuzonse,

Muyang’ane Inu okhala kumwamba, ndipo muwone,

Samalani mpesawo, mtengo woyambirira,

Umene Inu mudaubzala ndi dzanja lanu lamanja.

 

Munda wamphesawo wa Chauta Wamphamvuzonse ndi dziko la Israele.

 

Tsono sitidzakusiyaninso, tipatseni moyo,

Ndipo tidzatama dzina lanu mopemba,

Inu Chauta, Mulungu Wamphamvuzonse, tibwezereni mwakale,

Mutiwonetse nkhope yowala, kuti ife tipulumuke.

 

Munda wamphesawo wa Chauta Wamphamvuzonse ndi dziko la Israele.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AFILIPI; AFILIPI 04: 06 – 09 (Mulungu amene amapatsa mtendere adzakhala nanu).

 

Abale, musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma m’mapemphero anu onse muzipempha Mulungu zimene zikusowani, ndipo nthawi zonse muzipemphe ndi mtima woyamika. Pamenepo mtendere wochokera kwa Mulungu, umene uli wopitirira nzeru zonse za anthu, udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu. Potsiriza, abale, muziika mtima pa zilizonse zabwino kwambiri ndi zotamandika, monga izi: zinthu zoona ndi zolemekezeka, zinthu zolungama, zoyera, zokongola, ndi zaulemu. Muzichita zimene mudaphunzira ndi kulandira kwa ine, ndiponso zimene mudamva kwa ine ndi kuwonera kwa ine. Pamenepo Mulungu amene amapatsa mtendere adzakhala nanu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 15: 16.

Alleluia, Alleluia – Ndidakupatulani kuti mukabereke zipatso, zipatso zake zokhalitsa, atero Ambuye. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 21: 33 – 43 (Munda uja nkuubwereka alimi ena amene adzampatsa

zipatso zake pa nyengo yake).

 

Yesu adawauza akulu a ansembe ndi akulu a Ayuda kuti: “Imvani fanizo lina. Munthu wina anali ndi munda wake. M’mundamo adaabzalamo mipesa, namanga mpanda kuzinga mundawo.

Adakumba nkhuti yoponderamo mphesa, namanga nsanja yolondera mundawo. Pambuyo pake munda uja adaubwereka alimi, iye nkunyamuka ulendo wa ku dziko lina. Nyengo yothyola zipatso itayandikira, munthu uja adatuma antchito ake kwa alimi aja, kuti akatengeko zipatso za m’munda muja. Koma alimiwo adawagwira antchito aja, wina kummenya, wina kumupha, wina kumponya miyala. Munthu uja adatumanso antchito ena, ochuluka koposa oyamba aja, ndipo alimi aja adawachita chimodzimodzi. Potsiriza pake adawatumira mwana wake, nanena kuti, ‘Mwana wanga yekhayu akamchitira ulemu.’ Koma pamene alimiwo adaona mwana wakeyo, adayamba kuuzana kuti, ‘Ameneyu ndiye amene ati adzamsiyire chumachi. Tiyeni timuphe kuti chidzakhale chathu? Tsono adamugwiradi, namuponya kunja kwa mundawo, nkumupha. Kodi mwini munda wamphesa uja akadzafika, adzawatani alimi aja?” Iwo adati, “Adzawapha mowazunza alimi oipawo, munda uja nkuubwereka alimi ena amene adzampatsa zipatso zake pa nyengo yake” Yesu adawafunsa kuti, “Kodi monga simudawerenge Malembo aja akuti, Mwala umene amisiri omanga nyumba adaaukana, womwewo wasanduka mwala wapangodya, wofunika koposa. Ambuye ndiwo adachita zimenezi, ndipo nzotidabwitsa kwambiri. Nchifukwa chake ndikunenetsa kuti Mulungu adzakulandani Ufumu wake ndi kuupereka kwa anthu ena amene adzabala zipatso zoyenera.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, monga atilangizira Paulo Woyera, tisade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma tipemphe Mulungu zimene timazisowa, ndipo tipemphe ndi mtima woyamika:

 

1.     Tipempherere Eklezia amene ali ngati munda wa Ambuye, kuti anthu ake alimbikitse kuchita ntchito zabwino ndi kubala zipatso zokondweretsa Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Tipempherere ansembe ndi atsogoleri a Mpingo kuti aonetse‚ changu pa ntchito zosamalira akhristu ao ndi zophunzitsira akatekumeni.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Tipempherere mabanja achikhristu kuti eni ake akondane ndi kumagwirizana pa ntchito yolera bwino ana ao monga Mulungu afunira.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tomwe tili muno tipemphererane kuti mau a Mulungu agwire ntchito mwa ife, ndipo moyo wathu ubale zipatso zokometsera Mpingo wa Ambuye.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, tikutula m’manja mwanu mapemphero athuwa pamodzi ndi zosowa za anthu onse, ndipo tikuyamika chifundo chanu chofuna kupulumutsa anthu onse. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...