Saturday, September 30, 2023

LAMULUNGU LA 26 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 26 PA CHAKA – CHAKA A.

“Tisamangoti ‘Ambuye, Ambuye!’”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MPROFETI EZEKIELE; EZEKIELE 18: 25 – 28 (Munthu woipa akaleka zoipa zake, adzakhala ndi moyo, sadzafa).

 

Chauta adandipatsira uthenga uwu wakuti: “Inu mumati, ‘A! Zimene Ambuye amachitazi nzopanda chilungamo.’ Tamvani tsono Aisraele inu: Kani zochita zanga ndiye zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene zili zosalungama? Ngati munthu wabwino aleka kuchita zoyenera, namachita zoipa, adzafa chifukwa cha zoipa zakezo. Komanso munthu woipa akaleka zoipa zake, namachita zoyenera, adzapulumutsa moyo wake. Poti adazindikira kuipa kwa zolakwa zake, nazileka, ndiye kuti adzakhala ndi moyo, sadzafa.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 25: 04 – 09.

 

Inu Chauta, kumbukirani chifundo chanu.

 

Mundidziwitse njira zanu, Inu Chauta,

Mundiphunzitse kuchita kufuna kwanu,

Munditsogolere m’choona chanu ndi kundilangiza,

Pakuti Inu ndinu Mulungu Mpulumutsi wanga.

 

Inu Chauta, kumbukirani chifundo chanu.

 

Inu Chauta, kumbukirani chifundo chanu ndi chikondi chanu chosasinthika,

Chifukwa mudaziwonetsa kuyambira kalekale,

Musakumbukire machimo a unyamata wanga,

Koma mundikomere mtima, Inu Chauta,

Chifukwa cha chikondi chanu, pakuti Inu ndinu abwino.

 

Inu Chauta, kumbukirani chifundo chanu.

 

Chauta ndi wabwino ndi wolungama,

Nchifukwa chake amaphunzitsa ochimwa njira zake,

Amatsogolera anthu odzichepetsa kuti achite zolungama,

Amawaphunzitsa njira zake.

 

Inu Chauta, kumbukirani chifundo chanu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AFILIPI; AFILIPI 02: 01 – 11 (Nonse mukhale ndi mtima womwe uja umene adaali nawonso Khristu Yesu).

Abale, mosapeneka, moyo wanu mwa Khristu umakulimbitsani mtima. Chikondi chake chimakuchotsani nkhawa. Mumakhala a mtima umodzi mwa Mzimu Woyera, ndipo mumamvera anzanu chifundo ndi chisoni. Nchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundikondweretse kwenikweni pakuvomerezana maganizo ndi kukondana chimodzimodzi, kukhala a mtima umodzi ndi a cholinga chimodzi. Musamachita kanthu ndi mtima wodzikonda, kapena wodzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa, ndipo aliyense aziwona anzake kuti ngomuposa iyeyo. Musamangofuna zokomera inu nokha, koma zokomeranso anzanu. Motero nonse mukhale ndi mtima womwe uja umene adaali nawonso Khristu Yesu: Iyeyu anali ndi umulungu chikhalire, komabe sadayese kuti kulingana ndi Mulungu ndi chinthu choti achigwiritsitse. Koma adadzitsitsa kotheratu pakudzitengera umphawi wa kapolo, ndi kukhala munthu wonga anthu onse. Ali munthu choncho adadzichepetsa, adakhala womvera mpaka imfa, imfa yake yapamtanda. Chifukwa cha chimenechi Mulungu adamkweza kopambana, nampatsa dzina lopambana dzina lina lililonse. Adachita zimenezi kuti pakumva dzina la Yesu, zolengedwa zonse kumwamba, pansi pano ndi pansi pa dziko, zidzagwade pansi mopembedza. Zonse zidzavomereze poyera kuti, Yesu Khristu ndi Ambuye, ndipo pakutero zilemekeze Mulungu Atate.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 10: 27.

Alleluia, Alleluia – Nkhosa zanga zimamva mau anga, atero Ambuye. Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsatira. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 21: 28 – 32 (Okhometsa msonkho ndi akazi adama akulowa mu Ufumu wa Mulungu inu nkumakusiyani m’mbuyo).

 

Yesu adawauza akulu a ansembe ndi akulu a Ayuda kuti: “Kodi inu, mukuganiza bwanji? Munthu wina anali ndi ana aamuna awiri. Adapita kwa woyamba, nakamuuza kuti, ‘Mwana wanga, pita ukagwire ntchito m’munda wamphesa lero.’ Iyeyo adati, ‘Toto ine.’ Koma pambuyo pake adasintha maganizo, napitadi. Bambo uja adapita kwa mwana wina uja, nakamuuza mau omwe aja. Iyeyo adati, ‘Chabwino atate,’ koma sadapite. Kodi mwa awiriwo, yemwe adachita zimene bambo wake ankafuna ndi uti?” Iwo adati, “Woyamba uja.” Yesu adawauza kuti, “Ndithu ndikunenetsa kuti okhometsa msonkho ndi akazi adama akulowa mu Ufumu wa Mulungu inu nkumakusiyani m’mbuyo. Paja Yohane Mbatizi adaabwera nadzakuwonetsani njira ya chilungamo, inu osamkhulupirira, m’menemo okhometsa msonkho ndi akazi adama adamkhulupirira. Inuyo ngakhale mudaziwona zimenezo, simudasinthe maganizo pambuyo pake kuti muzimkhulupirira.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, popeza kuti patokha timangofooka, tiyeni tikweze mitima yathu kumwamba kuti Mulungu atiwonjezere mphamvu ndi kuchirikiza anthu onse m’njira ya chipulumutso:

 

1.     Apapa, Aepiskopi ndi ansembe onse, atsogolere akhristu ao m’njira yaungwiro, pakuwaphunzitsa za kulapa ndi za kutsanzira Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Anthu amuna ndi akazi a m’zipani zamumpingo, alimbikire kusunga malonjezo ao ndi kuwonetsa anthu onse kuwala kwa Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu ofooka ndi okayikira alandire chithandizo kuchokera kwa akhristu anzao ndipo ayambe moyo watsopano wa kuyanjana ndi Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse tili muno tipitirize kuwongola makhalidwe athu ndi kukomera Mulungu ndi anthu omwe, potsanzira Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, mverani mapemphero athuwa ndipo mutilimbitse, kuti tiyende mokhulupirika m’njira ya malamulo anu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

 

Saturday, September 23, 2023

LAMULUNGU LA 25 PA CHAKA – CHAKA A

 
LAMULUNGU LA 25 PA CHAKA – CHAKA A.

“Kani chifundo cha Mulungu nchotero?”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MPROFETI YESAYA; YESAYA 55: 06 – 09 (Maganizo anga ndi maganizo anu si amodzimodzi).

 

Mufunefune Chauta pamene angathe kupezeka, mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi. Oipa asiye makhalidwe ao oipa, ndipo osalungama asinthe maganizo ao oipa. Abwerere kwa Chauta, kuti Iyeyo awachitire chifundo. Abwerere kwa Mulungu wathu, kuti Iye awakhululukire machimo ao mofewa mtima. Chauta akunena kuti, “Maganizo anga ndi maganizo anu si amodzimodzi, ndipo zochita zanga ndi zochita zanu si zimodzimodzi. Monga momwe mlengalenga uliri kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 145: 02 – 03, 08 – 09, 17 – 18.

 

Chauta ali pafupi ndi onse amene amamutama mopemba.

 

Ndidzakuyamikani, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga,

Ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse mpaka muyaya,

Chauta ndi wamkulu ndi woyenera kumtamanda kwambiri,

Ndipo ukulu wake sitingathe kuumvetsa.

 

Chauta ali pafupi ndi onse amene amamutama mopemba.

 

Chauta ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

Wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi chosasinthika,

Chauta ndi wabwino kwa onse,

Amachitira chifundo zamoyo zonse zimene adazilenga.

 

Chauta ali pafupi ndi onse amene amamutama mopemba.

 

Chauta ndi wolungama m’zochita zake zonse,

Ndi wachifundo pa zonse zimene achita,

Chauta ali pafupi ndi onse,

Amene amamutama mopemba.

 

Chauta ali pafupi ndi onse amene amamutama mopemba.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AFILIPI; AFILIPI 01: 20 – 24, 27 (Kwa inetu moyo ndi Khristu amene).

Abale, motero ndikuyembekeza ndi kukhulupirira ndi mtima wonse kuti sipadzakhala konse manyazi. Koma ndikuyembekeza kuti ndidzalimba mtima kulankhula poyera, kuti tsopanonso, monga nthawi zonse, Khristu alemekezedwe mwa ine, ngakhale ndikhale moyo, kapena ndimwalire. Kwa inetu moyo ndi Khristu amene, ndipo nayonso imfa ili ndi phindu. Koma ngati kukhalabe moyo kungandipatse mwai woti ndigwire ntchito yoonetsa zipatso, sindidziwa kaya ndingasankhe chiti. Ndagwira njakata. Kwinaku ndikulakalaka kuti ndisiye moyo uno ndikakhale pamodzi ndi Khristu, pakuti chimenechi ndiye chondikomera koposa. Koma kwinakunso nkofunika kwambiri kuti ndikhale moyo chifukwa cha inuyo. Chachikulu nchakuti mayendedwe anu akhale oyenerana ndi Uthenga Wabwino wonena za Khristu. Ngakhale ndibwere kudzakuwonani, kapena ndikhale kutali, ndikufuna kumva kuti mukulimbika ndi mtima umodzi. Ndikufunanso kumva kuti momvana ndi mothandizana mukumenya nkhondo chifukwa chokhulupirira Uthenga Wabwino.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – Cf. AKORINTO 16: 14b.

 

Alleluia, Alleluia – Ambuye tsekulani mitima yathu kuti mau a Mwana wanu akhale mwa ife. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 20:1-16 (Kapenatu ukuipidwa nawo ufulu wanga eti?).

 

Yesu adawauza ophunzira ake kuti: “Za Ufumu wakumwamba tingazifanizire motere: Munthu wina adaalawirira m’mamawa kukalemba anthu okagwira ntchito m’munda wake wamphesa.

Adaapangana nawo kuti adzawalipira ndalama imodzi yasiliva pa tsiku, nawatuma kumunda kwake. Pa nthawi ya 9 koloko adapitanso, nakapeza ena atangokhala khale pa msika, osagwira ntchito. Adawauza kuti, ‘Inunso pitani ku munda wanga wamphesa, ndidzakulipirani moyenerera.’ Iwowo adapitadi. Munthu uja adapitanso pa 12 koloko masana ndi pa 3 koloko, nakachita chimodzimodzi. Pafupi 5 koloko madzulo adapitanso nakapeza enanso akungokhala. Adawafunsa kuti, ‘Bwanji mwangokhala khale pano tsiku lonse osagwira ntchito?’ Iwowo adayankha kuti, ‘Chifukwa palibe amene watilemba.’ Iye uja adawauza kuti, ‘Inunso pitani ku munda wanga wamphesa.’ Dzuwa likulowa, mwinimunda uja adauza kapitao wake kuti, ‘Kawaitane antchito aja, uwalipire. Uyambire amene alembedwa potsirizawo, utsirizire oyamba aja.’ Pamene adabwera olembedwa pa 5 koloko yamadzulo aja, aliyense adalandira ndalama imodzi. Tsono pamene olembedwa poyamba aja adabwera, ankaganiza kuti alandira pakulu. Koma nawonso adangolandira aliyense ndalama imodzi. Ndiye iwowo polandira, adayamba kuwiringula, adati, ‘Aa! Anzathu otsirizirawa angogwira ntchito kanthawi pang’ono, bwanji mwawapatsa malipiro olingana ndi athu, pamene ifeyo tathyoka nayo ntchito tsiku lathunthu, ndi chidzuwa chonse chija?’ Koma mwinimunda uja adayankha mmodzi mwa iwo kuti, ‘Iwe, inetu sindidakubere ai. Kodi suja tinapangana ndalama yasiliva imodzi? Tenga malipiro ako, uzipita. Mwiniwakene ndafuna kuti ndipatse wolembedwa potsirizayu molingana ndi iwe. Kodi zinthu zanga ndisachite nazo monga ndifunira? Kapenatu ukuipidwa nawo ufulu wanga eti?”’ Tsono Yesu adati, “Choncho amene ali oyambirira adzakhala otsirizira. Ndipo amene ali otsirizira adzakhala oyambirira.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, Mulungu watitsimikizira chifundo chake chofuna kupulumutsa anthu onse. Tiyeni tipemphere mogwirizana ndi mosakayika:

 

1.     Atsogoleri a Mpingo alondoloze anthu awo m’njira yachikondi, pakuwasamala osauka ndi ena osowa chithandizo.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akulu olamulira maiko akhale otekeseka ndi ubwino wa anthu ao poteteza ufulu wao ndi kutsata chilungamo.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu odwala ndi ena onse amene akumva zowawa m’mitima mwao, alandire chisamaliro ndi chisangalalo kuchokera kwa anthu anzao.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse tili muno tilimbikire kuchita zachifundo modziwala ndi mopanda tsankho, monga momwe Mulungu amakondera anthu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, tili kuyamika ufulu wanu chifukwa mumasamala anthu onse ndipo mumatichitira zabwino koposa m’mene tingayembekezere. Mwa Yesu Khristu Ambuye anthu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 


 

Saturday, September 16, 2023

LAMULUNGU LA 24 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 24 PA CHAKA – CHAKA A.

“Uzikhululukira anzako monga Mulungu amakukhululukira.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MPHUNZITSI; MPHUNZITSI 27: 30 – 28: 07 (Ukakhululukira mnzako amene wakuchimwira, nawenso Ambuye ukawapempha adzakukhululukira machimo ako).

 

Mkwiyo ndi ukali, nazonso nzoipa zazikulu, munthu wochimwa amakhala nazo ziwiri zonsezo. Munthu wokonda kulipsira anzake, nayenso adzamulipsira Ambuye amene amawerenga machimo ake. Ukakhululukira mnzako amene wakuchimwira, nawenso Ambuye ukawapempha adzakukhululukira machimo ako. Ngati munthu asungira chiwembu mnzake angayembekeze bwanji kuti Ambuye adzamumvera chisoni? Ngati sachitira chifundo munthu mnzake, angapemphe bwanji Ambuye kuti amkhululukire machimo ake? Ngati amene ali munthu chabe asunga mkwiyo, osafuna kukhululukira mnzake, iyeyo ndani adzamkhululukira zolakwa zake? Kumbukira kutha kwa moyo wako, ndipo lekeratu chidani. Kumbukira kuti udzafa ndi kuwola, ndipo sunga Malamulo mokhulupirika. Ganiza za Malamulo ndipo usakwiyire mnzako. Kumbukira chipangano cha Wopambanazonse, ndipo ukhululukire mnzako.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 103: 01 – 04, 09 – 12.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima, ndi wosakwiya msanga.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,

Moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera,

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,

Ndipo usaiwale zabwino zake zonse.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima, ndi wosakwiya msanga.

 

Ndiye amene amakhululukira machimo ako onse, ndi kuchiritsa matenda ako onse.

Ndiye amene amapulumutsa moyo wako ku manda,

Amakuveka chikondi chake chosasinthika,

Ndiponso chifundo chake ngati chisoti chaufumu.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima, ndi wosakwiya msanga.

 

Chauta ndi wosakwiya msanga,

Akatikalipira, mkwiyo wake sudzakhala woyaka mpakampaka,

Satilanga moyenerera machimo athu,

Satibwezera molingana ndi zolakwa zathu.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima, ndi wosakwiya msanga.

 

Monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi,

Ndi momwenso chidakulira chikondi chake chosasinthika kwa anthu oopa Chauta.

Monga kuvuma kuli kutali ndi kuzambwe,

Ndi momwenso amachotsera zolakwa zathu kuti zikhale kutali ndi ife.

 

Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima, ndi wosakwiya msanga.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA 14: 07 – 09 (Ngakhale tikhale ndi moyo kapena tife, ndife ao a Ambuye).

 

Abale, palibe ndi mmodzi yemwe mwa ife amene amakhala moyo chifukwa cha iye yekha, kapena kufa chifukwa cha iye yekha. Tikakhala ndi moyo, moyowo ndi wa Ambuye, tikafa, timafera Ambuye. Nchifukwa chake, ngakhale tikhale ndi moyo kapena tife, ndife ao a Ambuye. Paja Khristu adamwalira nakhalanso ndi moyo, kuti akhale Mbuye wa anthu akufa ndiponso wa anthu amoyo.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 13: 34.

 

Alleluia, Alleluia – Ndikukupatsani lamulo latsopano, lakuti muzikondana; monga momwe Ine ndidakukonderani, inunso muzikondana, atero Ambuye.  – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 18: 21 – 35 (Kodi ndikuti kasanunkawiri kokha ngati, iyai, koma maka kasanunkawiri kuchulukitsa ndi makumi asanu ndi awiri).

 

Pamenepo Petro adadzafunsa Yesu kuti, “Ambuye, kodi m’bale wanga atamandichimwira, ndidzamkhululukire kangati? Kodi ndidzachite kufikitsa kasanu nkawiri?” Yesu adamuyankha kuti, “Kodi ndikuti kasanu nkawiri kokha ngati, iyai, koma mpaka kasanu nkawiri kuchulukitsa ndi makumi asanu ndi awiri. Tsono Ufumu wakumwamba tingaufanizire motere: Panali mfumu ina imene idaaitanitsa antchito ake kuti iwonenso bwino ngongole zao. Atangoyamba kumene, adabwera ndi wantchito wina amene anali ndi ngongole ya ndalama zochuluka kwabasi. Ndiye popeza kuti adaasowa chobwezera ngongoleyo, mbuye wake uja adalamula kuti amgulitse wantchitoyo pamodzi ndi mkazi wake ndi ana ake ndi zake zonse, kuti ngongole ija ibwezedwe. Apo wantchito uja adamgwadira nati, ‘Pepani, ndakupembani, lezereni mtima, ndidzakubwezerani ndithu zonse.’ Mbuye wake uja adamumveradi chifundo, ndipo adamkhululukira ngongole ija, namlola kuti apite. Koma pamene wantchitoyo ankatuluka, adakumana ndi m’modzi mwa antchito anzake, yemwe iye adaamkongoza ndalama zochepa.

Adamgwira pa khosi mwaukali namuuza kuti, ‘bweza ngongole yako ija.’ Apo wantchito mnzake uja adadzigwetsa pansi ku mapazi ake nati, ‘Pepani, ndakupembani, lezereni mtima, ndidzakubwezerani.’ Koma iye adakana, nakamponyetsa m’ndende kuti mpaka abweze ndithu ngongoleyo. Antchito anzake ena ataona zimenezi, adamva chisoni kwambiri. Adapita kukafotokozera mbuye wao zonsezo. Tsono mbuye wakeyo adamuitana namuuza kuti, ‘Wantchito woipa iwe, ine ndinakukhululukira ngongole yonse ija pamene unandidandaulira.

Kodi sunayenera kuti iwenso umchitire chifundo wantchito mnzako, monga ndinakuchitira iwe chifundo?’ Motero mbuye wakeyo adapsa mtima kwambiri, nampereka kuti akamzunze mpaka atabweza ngongole yonse ija. Inunsotu Atate anga akumwamba adzakuchitani zomwezo, aliyense mwa inu akapanda kukhululukira m’bale wake ndi mtima wonse.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, popereka mapemphero athu kwa Atate athu a Kumwamba, tiyeni tipempherere anthu onse ndi mtima umodzi:

 

1.     Akhristu onse atsimikize kuti ndiwodi ake a Yesu Khristu pokhala nawo mtima wodziwa kukhululuka nthawi zonse.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Anthu amene akusowa mtendere m’mabanja mwao, ayesetse kuyanjana ndi kukhulupirirana, pokumbukira chifundo cha Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu amene akusunga udani kapena mkwiyo m’mitima mwao, azindikire kulakwa kwao ndipo akhululukire anzao mwaubale.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ifenso amene tili muno tipemphererane kuti tikhale oyanjana ndi anthu onse ngakhale iwo atinyoze ndi kutichimwira chotani.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, Inu mumatikhululukira kosalekeza, mutithandize kuwonetsa anzathu mtima womwewo, pakuwachitira chifundo, kuti tifanane ndi Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, September 9, 2023

LAMULUNGU LA 23 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 23 PA CHAKA – CHAKA A.

“M’bale wako akachimwa, mumdzudzule.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU MPROFETI EZEKIELE; EZEKIELE 33: 07 – 09 (Ukapanda kumchenjeza kuti aleke makhalidwe oipa, iweyo ndidzakuzenga mlandu chifukwa cha imfa yake).

 

Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuika kuti ukhale mlonda wa Aisraele. Ukamva mau anga, uwachenjeze. Ndikauza munthu woipa kuti, Munthu woipa iwe, udzafa, iwe nupanda kumchenjeza kuti aleke makhalidwe oipa, kuti akhalebe ndi moyo, munthuyo adzafadi ali wochimwa, koma iweyo ndidzakuzenga mlandu chifukwa cha imfa yake. Koma munthu woipa ukamchenjeza kuti asiye njira zake zoipa, iye nkupitiriza makhalidwe ake oipawo, adzafa ali wochimwa, koma iweyo udzapulumutsa moyo wako.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 95: 01 – 02, 06 – 09.

 

Lero mukadamverako mau ake! Musaumitse mitima yanu.

 

Bwerani, timuimbire Chauta,

Tiyeni tifuule ndi chimwemwe kwa Iye, thanthwe lotipulumutsa,

Tiyeni, tikafike pamaso pake,

Tikamthokoze, timuimbire nyimbo zotamanda.

 

Lero mukadamverako mau ake! Musaumitse mitima yanu.

 

Bwerani, timpembedze ndi kumlambira,

Tiyeni tigwade pamaso pa Chauta Mlengi wathu,

Pakuti ndiye Mulungu wathu, ndipo ife ndife anthu a pa busa lake,

Ndife nkhosa zodyera m’manja mwake.

 

Lero mukadamverako mau ake! Musaumitse mitima yanu.

 

Lero mukadamverako mau ake!

Musaumitse mitima yanu monga ku Meriba kuja,

Monganso tsiku lija ku Masa m’chipululu muja,

Pamene makolo anu adandiputa mondiyesa ngakhale anali ataona ntchito zanga.

 

Lero mukadamverako mau ake! Musaumitse mitima yanu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA 13: 08 – 10 (Amene amakonda mnzake, wasunga zonse zimene

Malamulo a Mulungu akunena).

Abale, musakhale ndi ngongole ina iliyonse kwa munthu wina aliyense, koma kukondana kokha. Wokonda mnzake, watsata zonse zimene Malamulo a Mulungu akunena. Pajatu malamulo amene amati, ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usasirire,’ ndiponso malamulo ena onse, amaundidwa mkota m’lamulo ili lakuti, ‘Uzikonda mnzako monga momwe umadzikondera iwe wemwe.’ Ngati munthu akonda mnzake, sangamchite choipa ai. Nchifukwa chake amene amakonda mnzake, wasunga zonse zimene Malamulo a Mulungu akunena.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – 02 AKORINTO 05: 19.

 

Alleluia, Alleluia – Mwa Khristu Mulungu ankayanjanitsa anthu a pa dziko lonse lapansi ndi Iye mwini, ndipo adatipatsa ifeyo mau onena za chiyanjanitsocho kuti tiwalalike. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 18: 15 – 20 (Mbale wako akakumvera, wamkonza mbale wakoyo).

 

Yesu adawauza ophunzira ake kuti: “Mbale wako akakuchimwira, pita ukamdzudzule muli awiri nokha. Akakumvera, wamkonza mbale wakoyo. Koma akapanda kukumvera, utengerepo wina mmodzi kapena ena awiri, kuti mau onse akatsimikizike ndi mboni ziwiri kapena zitatu. Akapanda kuwamvera iwowo, ukauze Mpingo. Ndipo akapanda kumveranso ndi Mpingo womwe, umuyese munthu wakunja kapena wokhometsa msonkho. Ndithu ndikunenetsa kuti chilichonse chimene mudzamanga pansi pano, chidzamangidwa ndi Kumwamba komwe, ndipo chilichonse chimene mudzamasula pansi pano, chidzamasulidwa ndi Kumwamba komwe.

Ndikunenetsanso kuti awiri mwa inu mutavomerezana pansi pano popempha kanthu kalikonse, Atate anga akumwamba adzakupatsani. Pajatu pamene awiri kapena atatu asonkhana m’dzina langa, Ineyo ndili nao pomwepo.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, podziwa kuti Yesu Khristu ali nafe pompano, tiyeni, pamodzi naye, tikweze mapemphero athu kwa Atate athu a Kumwamba.

 

1.     Ansembe ndi atsogoleri onse a Mpingo aonetse anthu ao mtima wachifundo pokonza milandu yao ndi powalangiza mofatsa ndi modzichepetsa.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akhristu onse akhale otekeseka ndi chipulumutso cha anthu anzawo powaongolera m’njira ya ungwiro ndi yachikondi.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Akhristu otaika ndi ena onse amene ali pa milandu apeze njira yoyanjananso ndi Mulungu polandira malangizo abwino kuchokera kwa anthu anzawo.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse tili muno, mau athu ndi mayendedwe athu abweretse umodzi ndi chiyanjano pakati pa anthu onse.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, mumvere mapemphero athuwa ndi kulunzitsa anthu onse M’chikondi chanu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...