Saturday, August 26, 2023

LAMULUNGU LA 21 PA CHAKA – CHAKA A

 

LAMULUNGU LA 21 PA CHAKA – CHAKA A.

“Ndidzakupatsa makii a Ufumu wakumwamba.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MPROFETI YESAYA; YESAYA 22: 19 – 23 (Ndidzampatsa makii a ulamuliro wa pa banja la mfumu Davide).

 

Chauta Wamphamvuzonse adamuuza Sebina, kapitao woyang’anira nyumba yaufumu, kuti: “Ndidzakuchotsa pa ukapitao wako, ndipo ndidzakutsitsa pakuthetsa udindo wako. Tsiku limenelo ndidzaitana mtumiki wanga Eliyakimu, mwana wa Hilikiya. Ndidzam’veka mkanjo wako ndi lamba wako ndi kumpatsa ulamuliro wako. Tsono adzalamulira anthu onse okhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda. Ndidzampatsa makii a ulamuliro wa pa banja la mfumu Davide. Akadzatsekula, palibe amene adzatseke. Ndipo adzatseka, popanda wina wotsekula. Ndidzamulimbitsa ngati chikhomo pa udindo wakewo, ndipo adzakhala wopatsa ulemu kwa banja la atate ake.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 138: 01 – 03, 06, 08.

 

Chikondi chanu, Inu Chauta, nchamuyaya. Muipitirize ntchito imene mwaiyambayo.

 

Ndikukuthokozani Inu Chauta ndi mtima wanga wonse,

Ndikuimba nyimbo zokutamandani pamaso pa milungu,

Ndikugwada mowerama kumaso kwa Nyumba yanu yoyera.

 

Chikondi chanu, Inu Chauta, nchamuyaya. Muipitirize ntchito imene mwaiyambayo.

 

Ndikutamanda dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika,

Chifukwanso cha kukhulupirika kwanu,

Pa tsiku limene ndidakuitanani, Inu mudandiyankha,

Mumandilimbitsa mtima ndi mphamvu zanu.

 

Chikondi chanu, Inu Chauta, nchamuyaya. Muipitirize ntchito imene mwaiyambayo.

 

Ngakhale Chauta ndi wamphamvu, amasamalira anthu otsika,

Koma anthu odzikuza amawadziwira chapatali,

Chikondi chanu, Inu Chauta, nchamuyaya,

Muipitirize ntchito imene mwaiyambayo.

 

Chikondi chanu, Inu Chauta, nchamuyaya. Muipitirize ntchito imene mwaiyambayo.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA  11: 33 – 36 (Zinthu zonse nzochokera kwa Iye, nzolengedwa ndi Iye

ndipo zimalinga kwa Iye).

 

Abale, chuma cha Mulungu nchachikulu zedi. Nzeru zake ndikudziwa kwake nzozama kwambiri. Ndani angamvetse maweruzidwe ake, ndipo njira zake ndani angazitulukire? Ndi monga mau a Mulungu anenera kuti, Ndani amadziwa maganizo a Chauta, ndani angamupatse malangizo? Ndani adaayamba waperekapo kanthu kwa Mulungu, kuti Mulunguyo amubwezereko kanthu? Paja zinthu zonse nzochokera kwa Iye, nzolengedwa ndi Iye ndipo

zimalinga kwa Iye. Ulemerero ukhale wake mpaka muyaya. Amen.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 16: 18.

 

Alleluia, Alleluia – Ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe limeneli ndidzamanga Mpingo wanga. Ndipo ngakhale mphamvu za imfa sizidzaugonjetsa. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 16: 13 – 20 (Ndiwe Petro, ndipo ndidzakupatsa makii a Ufumu wakumwamba).

 

Pamene Yesu adafika ku madera a ku Kesareya Filipi, adafunsa ophunzira ake kuti, “Kodi anthu amati Mwana wa Munthune ndine yani?” Iwo adati, “Ena amati ndinu Yohane Mbatizi, ena amati ndinu Eliya, enanso amati ndinu Yeremiya kapena mmodzi mwa aneneri.” Apo Yesu adawafunsa kuti, “Nanga inuyo, mumati ndine yani?” Simoni Petro adayankha kuti, “Inu ndinu Mpulumutsi wolonjezedwa uja, Mwana wa Mulungu wamoyo.” Yesu adamuuza kuti, “Ndiwe wodala, Simoni mwana wa Yona, pakuti si munthu wakuululira zimenezi ai, koma ndi Atate anga amene ali Kumwamba. Ndipo Ine ndikuti, Ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe limeneli

ndidzamanga Mpingo wanga. Ndipo ngakhale mphamvu za imfa sizidzaugonjetsa. Ndidzakupatsa makii a Ufumu wakumwamba, kotero kuti zimene udzamange pansi pano, zidzamangidwa ndi Kumwamba komwe, ndipo zimene udzamasule pansi pano, zidzamasulidwa ndi Kumwamba komwe.” Yesu atanena zimenezi, adalamula ophunzira aja kuti asauze munthu aliyense kuti Iye ndiye Mpulumutsi wolonjezedwa uja.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, tigwirizane nawo akhristu onse popereka mapemphero athu kwa Atate athu a Kumwamba, podziwa kuti Yesu Khristu akutitsogolera:

 

1.     Apapa ndi Aepiskopi onse asenze udindo wao molimbika ndi mogwirizana, ndipo ayendetse Mpingo m’njira yaungwiro ndi yachikondi.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Ansembe onse asamalire akhristu ao ndi kuwalimbikitsa, pakuwadyetsa Mau a Mulungu ndi kuwagawira Chakudya cha Kumwamba.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Abale athu a mipingo ina, Mulungu awaunikire ndi Kuwakhazikitsa m’chikondi chake, mpaka tidzalumikizane tonse m’chikhulupiriro chimodzi.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tonse a m’Parishi yathu ino, tithandizane kuti ntchito zathu zotumikira Mpingo ziwawonetse anthu onse kuwala kwa Yesu Khristu Ambuye athu.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, tikukuyamikani chifukwa mwatisonkhanitsa tonse m’mbumba yanu kuti tikhale amodzi m’chikondi chanu. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu. Amen.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, August 19, 2023

LAMULUNGU LA 20 PA CHAKA – CHAKA A

LAMULUNGU LA 20 PA CHAKA – CHAKA A.

“Chikhulupiriro chako nchachikulu ndithu.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MPROFETI YESAYA; YESAYA 56: 01, 06 – 07 (Ndidzabweretsa akunja onse ku phiri langa lopatulika).

 

Chauta akuuza anthu ake kuti, “Muzichita zabwino ndi zolungama, chifukwa ndikuwombolani posachedwa, chipulumutso changa chiwoneka.” Chauta akutinso, “Akunja amene amaphatikana ndi Chauta mpaka kumgwirira ntchito, kumkonda, ndi kumtumikira, amenenso amalemekeza tsiku la Sabata, osaliwononga, nasunga bwino chipangano changa, Ine ndidzawafikitsa ku Ziyoni, phiri langa lopatulika. Ndidzawapatsa chimwemwe m’nyumba yanga yopemphereramo. Zopereka zao zootcha ndiponso nsembe zao zinanso ndidzazilandira pa guwa langa. Paja Nyumba yanga idzatchedwa nyumba yopemphereramo anthu a mitundu yonse.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 67: 02 – 03, 05 – 06, 08.

 

Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu, mitundu yonse ya anthu ikuyamikeni.

 

Inu Mulungu mutikomere mtima ndi kutidalitsa,

Mutiwunikire ndi chikondi chanu,

Njira yanu idziwike pa dziko lonse lapansi,

chipulumutso chanu chidziwike pakati pa mitundu yonse.

 

Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu, mitundu yonse ya anthu ikuyamikeni.

 

Mitundu ya anthu isangalale ndi kuimba ndi chimwemwe,

Chifukwa Inu mumaweruza anthu mwachilungamo,

Ndi kuwatsogolera pa dziko lapansi.

 

Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu, mitundu yonse ya anthu ikuyamikeni.

 

Mitundu yonse ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu,

Mitundu yonse ya anthu ikuyamikeni,

Inde, Mulungu watidalitsa,

Anthu onse a ku mathero a dziko lapansi apembedze Iye.

 

Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu, mitundu yonse ya anthu ikuyamikeni.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA  11: 13 – 15, 29 – 32 (Mulungu sasinthanso ataitana munthu ndi kumpatsa mphatso).

 

Abale, tsopano ndifuna kukuuzani kanthu, inu amene simuli Ayuda. Malinga nkuti ndine wotumidwa kwa anthu a mitundu ina, ndimaunyadira utumiki wanga umenewu. Koma ndimakhumba kuti ndichititse nsanje anthu a mtundu wanga, ndi kupulumutsa ena mwa iwo. Ngati anthu a pa dziko lonse lapansi adayanjanitsidwa ndi Mulungu chifukwa Iye adawaika pambali Ayuda, nanga kudzatani Iye akadzawalandiranso? Kudzakhala monga ngati anthu akufa akuuka! Pakuti Mulungu sasinthanso ataitana munthu ndi kumpatsa mphatso. Kale inu a mitundu ina simunkamvera Mulungu, koma tsopano Mulungu akukuchitirani chifundo chifukwa cha kusamvera kwa Ayuda. Momwemonso Ayuda tsopano samvera Mulungu, koma cholinga chake nchakuti iwonso adzalandire chifundo pa nthawi yake, chifukwa cha chifundo mwalandira inuchi. Mulungu adasandutsa anthu onse akaidi a kusamvera, kuti Iye athe kuchitira onse chifundo.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO

 

Alleluia, Alleluia – Yesu adalalika Uthenga Wabwino wonena za ufumu wakumwamba. Ankachiritsanso nthenda zonse za anthu ndi zofooka zao zam'thupi. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 15: 21 – 28 (Inu mai, chikhulupiriro chanu nchachikulu).

 

Yesu adachoka kumeneko, napita ku madera a ku Tiro ndi Sidoni. Mai wina wachikanani, wa ku madera amenewo, adadza kwa Yesu. Adafuula kuti, “Mundichitire chifundo, Inu Ambuye, Mwana wa Davide. Mwana wanga wamkazi ngwogwidwa koopsa ndi mzimu woipa.” Koma Yesu sadamuyankhe mau ndi amodzi omwe. Ophunzira ake adadza nampempha kuti, “Muuzeni azipita, onani akubwera natisokosera.” Yesu adati, “Inetu Mulungu adandituma kwa amene ali ngati nkhosa zotayika pa mtundu wa Aisraele.” Mai uja adadzamgwadira nati, “Ambuye, ndithu thandizeni.” Yesu adamuuza kuti, “Sibwino kutenga chakudya cha ana nkuponyera agalu.” Maiyo adati, “Nzoonadi, Ambuye, koma suja ngakhale agalu omwe amadyako nyenyeswa zimene zimagwa pansi kuchokera pa tebulo la mbuye ao?” Apo Yesu adati, “Inu mai, chikhulupiriro chanu nchachikulu. Zichitikedi zimene mukufuna.” Pompo mwana wake wamkazi uja adachira.

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, pakuti Yesu Khristu adadzaitana anthu a mitundu yonse, tiyeni tiwapempherere kuti Mulungu awaunikire ndi kuwafikitsa ku chikhulupiriro choona:

 

1.     Eklezia, Mpingo wa Yesu Khristu, alimbikire pa ntchito yake yofalitsa Mthenga Wabwino mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akhristu a mipingo yosiyanasiyana aleke kutsutsana kopanda phindu ndipo aphunzire kudziwana, kukondana ndi kulemekezana.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu amene adakali padera adziwe kukhulupirira Mulungu ndi kupemphera, maka adzazindikire kuwala kwa Yesu Khristu, Mpulumutsi wao.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife tomwe osonkhana pano tizitekeseka ndi chipulumutso cha anthu onse, pakuwapempherera ndi kuwathandiza m’mavuto ao.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, popereka kwa Inu mapemphero athuwa, tikuyamika chifundo chanu chofuna kusonkhanitsa anthu onse mu Ufumu wanu waulemerero. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, August 12, 2023

LAMULUNGU LA 19 PA CHAKA – CHAKA A.

LAMULUNGU LA 19 PA CHAKA – CHAKA A.

“Adakapemphera ali yekhayekha.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LOYAMBA LA MAFUMU; 01 MAFUMU 19: 09, 11 – 13 (Tuluka, ukaime pa phiri, pamaso panga).

 

Eliya adayenda mpaka adakafika ku Sinai, phiri la Mulungu. Kumeneko adafikira m’phanga, nagona momwemo. Apo Chauta adati, “Tuluka, ukaime pa phiri, pamaso panga.” Tsono Chauta adadutsa pamenepo, ndipo mphepo yamphamvu idaomba ning’amba mapiri ndi kuswa matanthwe, koma Chauta sanali m’mphepomo. Itapita mphepoyo, padachita chivomezi, koma Chauta sanali m’chivomezimo. Chitapita chivomezi chija, padafika moto, koma Chauta sanali m’motomo. Utapita motowo, padamveka kamphepo kongoti wii. Eliya atakamva, adafunda kumutu, ndipo adatuluka, nakaima pa khomo la phanga.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 85: 09 – 14.

 

Tiwone chifundo chanu, Ambuye, ndipo mutipulumutse ife ku zoipa.

 

Ndimve zimene Chauta adzalankhula,

Chifukwa adzalankhula za mtendere kwa anthu ake,

Kuti apulumutse amene amamuwopa,

Kuti ulemerero wake ukhale m’dziko lathu.

 

Tiwone chifundo chanu, Ambuye, ndipo mutipulumutse ife ku zoipa.

 

Chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika zidzakumana,

Chilungamo ndi mtendere zidzagwirizana,

Anthu ake adzakhala okhulupirika pansi pano,

Ndipo Mulungu wakumwamba adzawalungamitsa.

 

Tiwone chifundo chanu, Ambuye, ndipo mutipulumutse ife ku zoipa.

 

Inde, Chauta adzapereka zabwino,

Ndipo dziko lathu lidzabereka zokolola zambiri,

Mulungu ndi wolungama chikhalire,

Chilungamo chake chimaongolera zochita zake zonse.

 

Tiwone chifundo chanu, Ambuye, ndipo mutipulumutse ife ku zoipa.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AROMA; AROMA 09: 01 – 05 (Chifukwa cha abale anga, ndikadakonda kuti m’malo mwao, ineyo ndikhale wotembereredwa).

Abale, ndithudi ndikunena zoona ine amene ndili wake wa Khristu, ndipo sindikunama ai. Mtima wanga, umene Mzimu Woyera amautsogolera, ukundichitira umboni kuti ndili ndi chisoni chachikulu. Ndipo ukundipweteka kosalekeza chifukwa cha abale anga, anthu a mtundu wangawa. Ndikadakonda kuti m’malo mwao, ineyo ndikhale wotembereredwa, osakhalanso wake wa Khristu. Iwowa ndi Aisraele, amene Mulungu adawasankha kuti akhale ana ake, ndipo adawapatsa ulemerero. Mulungu adachita nawo mapangano, ndipo adawapatsa

Malamulo ake. Adawaphunzitsa mwambo wachipembedzo, ndipo adawapatsa malonjezo ake. Iwowa ndi zidzukulu za makolo athu akale aja, ndipo Mpulumutsi wolonjezedwa uja ndi wa mtundu wao, kunena za umunthu wake. Mulungu amene amalamulira zonse, alemekezeke mpaka muyaya. Amen.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – SALIMO 130: 05.

 

Alleluia, Alleluia – Ndimayembekeza ndi mtima wonse chithandizo cha Ambuye,

ndipo ndimakhulupirira mau ake. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 14: 22 – 33 (“Tandiwuzani kuti ndibwere kwa Inu pamadzipo.”)

 

Madzulo omwewo Yesu adalamula ophunzira ake kuti alowe m’chombo, atsogole kupita ku tsidya, pamene Iye akuuza anthu kuti azipita kwao. Tsono atatsazikana nawo anthu aja, Iye adakwera ku phiri yekha kukapemphera. M’mene kunkayamba kuda, nkuti ali komweko yekhayekha. Pamenepo nkuti chombo chija chili kutalitali ndi mtunda, chikuvutika ndi mafunde, chifukwa chinali chitayang’anana ndi mphepo. M’mamawa kukali mbuu, Yesu adadza kwa iwo Iye akuyenda pa madzi. Pamene ophunzira aja adamuwona akuyenda pa madzi, adaopsedwa nati, “Ndi mzukwa!” Ndipo adayamba kukuwa chifukwa cha mantha. Koma nthawi yomweyo Yesu adawauza kuti, “Khazikani mtima pansi, ndine; musaope.” Apo Petro adati, “Ambuye, ngati ndinudi, tandiwuzani kuti ndibwere kwa Inu pamadzipo.” Yesu adati, “Chabwino, bwera.” Tsono Petro adatuluka m’chombo nayamba kuyenda pa madzi kupita kwa Yesu. Koma ataona m’mene ikuwombera mphepo, adachita mantha, nkuyamba kumira. Tsono adafuula kuti, “Ambuye, pulumutseni!” Pompo Yesu adatambalitsa dzanja nkumugwira nati, “Iwe wa chikhulupiriro chochepawe, unakayikiranji?” Pambuyo pake awiriwo adalowa m’chombo muja, mphepo nkuleka. Apo amene anali m’chombo aja adamgwadira Yesu nati, “Ndithudi, ndinu Mwana wa Mulungu.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

 

Abale, lero Mulungu watiwonetsanso chifundo chake chofuna kupulumutsa anthu onse. Tiyeni titule m’manja mwake mapemphero athu:

 

1.     Ansembe ndi atsogoleri onse apitirize ntchito yao molimbika, pokhala okonda kupemphera.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Ayuda, Mulungu awalitse nkhope yake pa iwo, kuti nawonso avomere Mpulumutsi wa anthu onse, Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu onse amene ali paulendo, Mulungu awatsogolere ndi kuwateteza, mpaka akafike bwino kumene alikulinga.
Tikupemphani, mutivomereze.

4.     Ife amene timakhala otanganidwa ndi ntchito zosiyanasiyana, tidziwe kucheza ndi Ambuye masiku onse, timange moyo wathu pa chikondi chao.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Atate, tikukuyamikani kuti simulephera kumvera madandaulo athu. Mulimbitse chikhulupiriro chathu, mutipatse mtima wokonda kucheza nanu masiku onse. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, August 5, 2023

CHAKA CHA KUSANDULIKA KWA AMBUYE YESU – CHAKA A. [TRANSFIGURATION OF THE LORD]

CHAKA CHA KUSANDULIKA KWA AMBUYE YESU – CHAKA A.

[TRANSFIGURATION OF THE LORD]

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MPROFETI DANIELE; DANIELE 07: 09 – 10, 13 – 14 (Zovala zake zinali zambee ngati chipale).

 

Ine ndikuyang’ana, ndidaona mipando yaufumu ikuikidwa pa malowo, ndipo Mkulu amene analipo chikhalire adakhala pa mpando umodzi. Zovala zake zinali zambee ngati chipale, ndipo tsitsi lake linali loyera ngati ubweya wa nkhosa. Mpando wake unali wonga wa malawi a moto, mikombero yake ngati moto woyaka. Mtsinje wa moto udatuluka nkumayenda patsogolo pake. Panali chinamtindi cha anthu omtumikira, panalinso chinamtindi china chochuluka kupambana chinacho. Chimenechi chidaima pamaso pake. Tsono bwalo lidayamba kuweruza, ndipo mabuku adatsekulidwa. Pamene ndinkaonabe zinthu m’masomphenya usiku, ndidaona wina ngati mwana wa munthu akutsika ndi mitambo yakumwamba. Atayandikira Mkulu amene analipo chikhalire uja, ena adamperekeza kwa Mkuluyo. Pamenepo adampatsa ulamuliro, ulemerero ndi ufumu, kuti anthu a mitundu yonse, a mafuko onse ndi a zilankhulo zosiyanasiyana azimtumikira. Ulamuliro wake ndi wamuyaya, sudzatha. Ufumu wake ndi wosagawikana, ndipo sudzaonongedwa.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 97: 01 – 02, 05 – 06, 09.

 

Chauta ndiye Mfumu, Chauta ndinu Wopambanazonse, wolamulira dziko lonse lapansi.

 

Chauta ndiye Mfumu,

Anthu a pa dziko lapansi akondwere,

Anthu onse a m’mbali mwa nyanja asangalale.

 

Chauta ndiye Mfumu, Chauta ndinu Wopambanazonse, wolamulira dziko lonse lapansi.

 

Mitambo ndi mdima waukulu zamzinga Chauta,

Amalamulira molungama,

Mu ufumu wake mulibe tsankho.

 

Chauta ndiye Mfumu, Chauta ndinu Wopambanazonse, wolamulira dziko lonse lapansi.

 

Mapiri amasungunuka ngati sera pamaso pa Chauta,

Ndiye wolamulira dziko lonse lapansi,

Zakumwamba zimalalika za kulungama kwake,

Ndipo anthu a mitundu yonse amaona ulemerero wake.

 

Chauta ndiye Mfumu, Chauta ndinu Wopambanazonse, wolamulira dziko lonse lapansi.

 

Pakuti Inu Chauta ndinu Wopambanazonse,

Wolamulira dziko lonse lapansi,

Ndinu amphamvu kupambana milungu yonse.

 

Chauta ndiye Mfumu, Chauta ndinu Wopambanazonse, wolamulira dziko lonse lapansi.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YACHIWIRI YA PETRO WOYERA; 02 PETRO 01: 16 – 19 (Mau amenewa ifeyo tidawamva kuchokera kumwamba).

 

Abale, ife sitidatsate nthano zongopeka chabe, pamene tidakudziwitsani za mphamvu zao ndi za kubweranso kwao kwa Ambuye athu Yesu Khristu. Koma tidachita kuwona ndi maso athu ukulu wake. Iye adalandira ulemu ndi ulemerero kwa Mulungu Atate, ndipo adamufikira mau ochokera kwa Atate aulemererowo akuti, “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa, amene ndimakondwera naye.” Ndipo mau amenewa ifeyo tidawamva kuchokera kumwamba chifukwa tidaali naye pamodzi pa phiri loyera lija. Motero tikudziwa ndithu tsopano kuti mau aja a aneneriwa ngoona. Nkwabwino tsono kuti muwayang’anitsitse ngati nyale yowala m’malo amdima, kufikira nthawi imene kudzayambe kucha, pamene nyenyezi yam’mamawa idzayambe kuwala m’mitima mwanu.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 17: 05c.

 

Alleluia, Alleluia – Uyu ndiye Mwana wanga amene ndimamkonda, ndipo ndimakondwera naye kwambiri. Muzimumvera. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA MATEYO WOYERA; MATEYO 17: 01 – 09 (Nkhope yake idawala ngati dzuwa).

 

Patapita masiku asanu ndi limodzi, Yesu adatenga Petro, Yakobo ndi Yohane, mbale wa Yakobo yo, nakwera nawo ku phiri lalitali, kwaokha. Tsono maonekedwe a Yesu adasinthika iwo akuwona. Nkhope yake idawala ngati dzuwa, ndipo zovala zake zidachita kuti mbee kuyera. Nthawi yomweyo ophunzira aja adaona Mose ndi Eliya akulankhula naye. Petro adauza Yesu kuti, “Ambuye, ndi bwino kuti ife tili nao pano. Ngati mukufuna, ndimanga misasa itatu pano, wina wanu, wina wa Mose, wina wa Eliya.” Akulankhula choncho, kudadza mtambo wowala nuwaphimba. Mumtambomo mudamveka mau akuti, “Uyu ndiye Mwana wanga amene ndimamkonda, ndipo ndimakondwera naye kwambiri. Muzimumvera.” Ophunzira aja atamva zimenezi, adachita mantha kwambiri nadzigwetsa chafufumimba. Koma Yesu adabwera, nawakhudza nkunena kuti, “Dzukani, musachite mantha.” Iwo aja poweramuka, adangoona kuti palibe munthu winanso, koma Yesu yekha. Pamene ankatsika phiri lija, Yesu adawalamula kuti, “Zimene mwaona m’masomphenyazi musakauze wina aliyense mpaka Mwana wa Munthu atauka kwa akufa.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...