Saturday, March 18, 2023

LAMULUNGU LA 04 MU NYENGO YA LENTI – CHAKA A

“Tiyende m’kuwala kwa Yesu Khristu.”

 

MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA SAMUELE; 01 SAMUELE 16: 01b, 06 – 07, 10 – 13a (Davide adzozedwa kukhala mfumu).

 

Chauta adauza Samuele kuti, “kodi udzakhala ukumulirabe Saulo mpaka liti, poti ndamkana kuti akhalenso mfumu yolamulira Aisraele? Dzaza mafuta m’nsupa yakoyi. Upite kwa Yese wa ku Betelehemu, poti ndadzipezera mfumu pakati pa ana ake aamuna.” Onsewo atafika, Samuele adayang’ana Eliyabu namaganiza kuti, “nthithudi amene Chauta adamsankha ndi uyu ali pamaso pakeyu.” Koma Chauta adauza Samuele kuti, “usayang’ane maonekedwe ake, ngakhale kutalika kwa msinkhu wake, poti ndamkana ameneyo. Chauta sapenya monga m’mene apenyera anthu. Anthu amapenya zakunja, koma Chauta amapenya zamumtima.” Tsono Yese adatumiza ana ake aamuna asanu ndi awiri kuti apite kwa Samuele. Koma Samuele yo adati, “Chauta sadawasankhe amenewa.” Tsono adafunsa Yese kuti, “kodi ana ako aamuna ndi okhawa?” Yese yo adati, “alipo wina wamng’ono, mzime, amene watsala, koma iyeyo akuweta nkhosa.” Apo Samuele adauza Yese kuti, “mtumireni munthu, akamtenge, pakuti sitipereka nsembe mpaka iyeyo atabwera pano.” Choncho adatuma munthu kukamutenga, ndipo adabwera naye.  Anali wofiira ndi wamaonekdwe okongola ochititsa kaso. Pamenepo Chauta adati, “ndi ameneyu, mdzoze.” Samuele adatenga nsupa yamafuta, namdzoza pamaso pa abale ake. Ndipo mzimu wa Chauta udamlowa Davide mwamphamvu kuyambira tsiku limenelo mpaka m’tsogolo mwake. Pambuyo pake Samuele adanyamuka napita ku Rama.

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 23: 01 – 30a, 03b – 04 – 06.

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu,

Amandigoneka pa busa lamsipu,

Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Amatsitsimutsa moyo wanga,

Amanditsogolera m’njira za chilungamo,

Malinga ndi ulemerero wa dzina lake,

Ngakhale ndiyende m’chigwa chamdima wabii,

Sindidzaopa choipa chilichonse,

Pakuti Inu Ambuye mumakhala nane,

Chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditeteza.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Inu mumandikonzera chakudya, adani anga akuwona,

Mumandilandira bwino podzoza mutu wanga ndi mafuta,

Mumadzaza chikho changa mpaka kusefukira.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

 

Zoonadi, zokoma zanu ndi chikondi chanu,

Zidzakhala ndi ine masiku onse a moyo wanga,

Ndidzakhala m’Nyumba mwanu moyo wanga wonse.

 

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AEFESO; AEFESO 05: 08 – 14 (Dzuka wam’tulo iwe, uka kwa akufa.).

 

Abale, inunso kale mudaali mu mdima, koma tsopano muli m’kuwala, popeza kuti ndinu ao a Ambuye. Tsono muziyenda ngati anthu okhala m’kuwala. Pajatu pamene pali kuwala, pamapezekanso ubwino wonse, chilungamo chonse ndi choona chonse. Muziyetsa kudziwa kwenikweni zimene zingakondweretse Ambuye. Musayanjane nawo anthu ochita zopanda pake za mdima, koma muwatsutse. Paja zimene iwo amachita mobisa, ngakhale kuzitchula komwe kumachititsa manyazi. Koma kuwala kumaunika zinthu, ndipo zonse zimaonekera poyera. Motero chilichonse choonekera poyera, chimasanduka kuwala. Nchifukwa chake amati, “dzuka wamtulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuwalira.”

 

Mau a Ambuye.......Tithokoze Mulungu.

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – YOHANE 08: 12.

 

Ulemerero ndi mayamiko kwa Inu, Khristu. – Ine ndine kuwala kounikira anthu onse. Munthu wotsata Ine, sadzayenda mumdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo. – Ulemerero ndi mayamiko kwa Inu, Khristu.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA; YOHANE 09: 01 – 41 (Munthuyo adapitadi, adakasamba, nabwerako akupenya).

 

Pamene Yesu ankayenda, adaona munthu wa Khungu lobadwa nalo. Ophunzira ake adamufunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi adachimwa ndani kuti munthu ameneyu abadwe wakhungu? Adachimwa ndi iyeyu kapena makolo ake?” Yesu adati, “sikuti iyeyu adachimwa kapena makolo ake ai. Koma adabadwa wakhungu kuti Mulungu aonentse ntchito zake mwa iye. Kukali usana tizigwira ntchito za Atate amene adandituma. Usiku ukudza pamene munthu sangathe kugwira ntchito.

Pamene ndili pansi pano, ndine kuwala kounikira anthu onse.” Atanena zimenezi, Yesu adalavulira malovu pansi, nakanda thope ndi malovuwo. Kenaka adapaka thopelo m’maso mwa munthuyo, namuuza kuti, “pita ukasambe ku dziwe la Siloamu.” (tanthauzo la Siloamu ndiye kuti, wotumidwa). Munthuyo adapitadi, adakasamba, nabwerako akupenya. Pamenepo anzake ndi anthu amene kale ankamuwona akupemphapempha adati, “kodi uyu si uja ankakhala pansi apa nkumangopempha?” Ena adati, “ndiye amene.” Ena nkumati, “iyai, akungofanana naye.” Koma mwini wakeyo adati, “ai ndithu, ndine amene.” Apo anthu aja adamufunsa kuti, “nanga maso ako akupenya bwanji?” Iyeyo adati, “munthu uja amati Yesu yu anakanda thope nalipaka m’maso mwangamu. Kenaka anadiwuza kuti, ‘pita, ukasambe ku Siloamu.’ Ndinapitadi, ndipo nditasamba, ndayamnba kupenya.’ Anthuwo adamfunsa kuti, “iyeyo ali kuti?” Munthu uja adati, “kaya, sindikudziwa.”

 

Tsono munthu uja kale sankapenyayu adapita naye kwa Afarisi. Tsiku limene Yesu adaakanda thope namchiritsalo linali la sabata. Tsono Afarisi nawonso adamufunsa munthu uja kuti, “iwe, wapenya bwanji?” Iye adawauza kuti, “anandipaka thope m’maso mwanga, ine nkukasamba, ndipo tsopano ndikupenya.” Afarisi ena adati, “munthu amene uja ngwosachokera kwa Mulungu, chifukwa satsata lamulo lokhuza tsiku la sabata.” Koma ena adati, “kodi inu, munthu wochimwa nkuchita zizindikiro zozizwitsa zotere?” Choncho panali kutsutsana. Choncho Afarisi aja adamufunsanso munthu uja kale sankapenyayu, adati, “kodi iweyo ukutipo chani za iyeyo, m’mene wakuchiritsamu?” Iye adati, “ndi mneneritu basi.” Koma akulu a Ayuda wo sadakhulupirire kuti munthu yo kale sankapenya ndipo tsopano akupenya, mpaka anaitanitsa makolo ake. Tsono adawafunsa kuti, “kodi inu, uyu ndi mwana wanu? Ndiye mukuti adaabadwadi wosapenya? Nanga zatani kuti tsopano akupenya?” Makolo ake adati, “chimene tikudziwa ife nchakuti ameneyu ndi mwana wathu, ndipo adaabadwadi wosapenya. Koma kuti tsopano akupenya, sitikudziwa m’mene zachitikira. Zoti wamupenyetsa ndani kaya, ife sitikudziwanso. Mufunseni mwiniwakeyo, ngwamkulu, afotokoze yekha.” Makolo akewo adaatero chifukwa ankaopa akulu a Ayuda. Pakuti Ayuda anali atapangana kale kuti, ngati munthu adzavomereza kuti Yesu ndiye Mpulumutsi wolonjezedwa uja, adzamdula ku mpingo. Nchifukwa chake makolo akewo adati, “ngwamkulu, mufunseni mwiniwakeyo.”

 

Pamenepo Ayuda aja adamuitana kachiwiri munthu uja kale sankapenyayu, namuuza kuti, “Lemekeza Mulungu, ndipo unene zoona. Ife tikudziwa kuti munthu uja ngwochimwa.” Iye adati, “zakuti iye ngwochimwa, ine sindikudziwa. Chinthu chimodzi chokha ndikudziwa, kuti kale ndinali wosapenya, koma tsopano ndikupenya.” Iwo adamufunsa kuti, “kodi anachita chiyani, pamene anakupenyetsa?” Iye adati, “ndakuuzani kale, koma simumasamalako. Nanga chifukwa chani mukufuna kuzimvanso? Kapenatu nanunso mukufuna kukhala ophunzira ake eti?” Pamenepo iwo adayamba kumlalatira, adati, “wophunzira wake ndi iweyo. Ife ndifetu ophunzira a Mose. Tikudziwa kuti Mulungu adalankhula ndi Mose, koma uyu sitikudziwa kumene wachokera.” Munthuyo adati, “pakudabwitsatu mpamenepa: kuti inuyo simukudziwa kumene iye wachokera, komabe wandipenyetsa. Timadziwa kuti Mulungu samvera anthu ochimwa. Koma munthu akasamala za Mulungu, nachita zimene Mulungu akufuna, Mulungu amamumvera. Nkale lomwe sikudamveke konse kuti wina adapenyetsa munthu wakhungu. Munthu ameneyu akadapanda kuchokera kwa Mulungu, sakadatha konse kuchita kanthu.” Iwo adati, “iwe udabadwa m’machimo okhaokha. Ndiye iweyo nkutiphunzitsa ife?” Atatero adamtulutsa nkumudula mu mpingo.

 

Yesu adamva kuti Ayuda amtulutsa ndi kumdula ku mpingo munthu uja. Tsono pamene adampeza, adamfunsa kuti, “kodi ukukhulupirira mwana wa munthu?” Iye adati, “Ambuye, mundiwuzetu ndani iyeyo, kuti ndimkhulupirire.” Yesu adamuuza kuti, “wamuona kale, ndiyemwe akulankhula nawe.” Iye adati, “Ambuye, ndikukhulupirira.” Atatero adamgwadira. Tsono Yesu adati, “ndidabwera pansi pano kudzaweruza, kuti osapenya apenye, ndipo openya achite Khungu.” Afarisi ena amene anali pafupi naye, atamva zimenezi adamufunsa kuti, “kodi monga ifenso ndife akhungu?” Yesu adati, “mukadakhala akhungu, bwezi mulibe mlandu. Koma chifukwa mukuti, ‘tikupenya,’ ndiye kuti mlandu wanu ulipobe.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

--------------------------------------

 

Mapemphero a Akhristu.

 

Abale, lero popempherera anthu onse, tiyeni tipemphe Atate a Kumwamba kuti kuwala kwa Yesu Khristu kuunike m’mitima yathu ndi ya anthu ena:

 

1.     Eklezia wa Mulungu aonetse anthu amafuko onse kuwala kwa Yesu Khristu, pakuwalalikira Mthenga Wabwino, ndi pakuwatumikira modzichepetsa.
Tikupemphani, mutivomereze.

2.     Akhristu onse aunikire anzawo pakuyenda molimbika m’njira yaungwiro, ndipo pakuwonetsana mtima waubale pa moyo wao wa tsiku ndi tsiku.
Tikupemphani, mutivomereze.

3.     Anthu akhungu, agonthi, odwala, ndi ena onse amene ali m’mavuto, azindikire chifundo cha Mulungu polandira chithandizo chochokera kwa anzao.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

4.     Ife tomwe tili muno, Mulungu atiwonjezere chikhulupiriro, tizipenya zinthu ndi maso a mu mtima ndi kufunafuna zimene zingakondweretse Iyeyo.
Tikupemphani, mutivomereze.

 

Mulungu Atate athu, Inu mumayan’gana mitima ya anthu, osati maonekedwe ao. Tikutula m’manja mwanu mapemphero athuwa potamanda Mwana wanu Yesu Khristu Ambuye athu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

No comments:

Post a Comment

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...