Saturday, September 24, 2022

 LAMULUNGU LA 26 PACHAKA (CYCLE C)

“Kalanga ine! Ndikadadziwa!”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MNENERI AMOSI; AMOSI 06: 1a, 04 – 07. (Inu anthu amene mumangoti lamzi pa mipando yanu nkumangoimba azeze, mudatsogoza ndinu kupita ku ukapolo.)

 

Tsoka kwa inu amene mumakhala mosateketseka ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mumakhala mosavutika ku Samariya. Tsoka kwa inu anthu otchuka pakati pa Israeli, inu amene anthu onse amafika kwanu. Tsoka kwa inu amene mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga yanjovu, inu amene mumangoti lamzi pa mipando yanu, nkumachita phwando la nyama la anaankhosa ndi anaang’ombe onenepa. Ntchito nkumangoimba azeze ngati Davide, ndikumangopeka nyimbo zoimbira pa zingw’enyengw’enye. Tsoka kwa inu amene mumamwera vinyo m’zipanda zodzadza, inu amene mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa dziko la Yosefe. Nchifukwa chake mudzatsogola ndinu kupita ku ukapolo, ndipo maphwando ndi zikondwerero zidzakutherani.

 

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 146: 06 – 10.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga.

 

Amasunga malonjezo ake nthawi zonse,

Amachitira anthu opsinjidwa zolungama,

Amawapatsa chakudya anthu anjala,

Chauta amamasula am’ndende.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga.

 

Chauta amatsekula maso a anthu osapenya,

Chauta amakweza anthu otsitsidwa,

Chauta amakonda anthu ochita chilungamo,

Chauta amateteza alendo.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga.

 

Amachirikiza mkazi wamasiye ndiponso mwana wa wamasiye,

Koma njira za anthu oipa amazipotoza,

Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako, iwe Ziyoni, adzalamulira ku mibadwo yonse.

 

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA TIMOTEO; 01 TIMOTEO 06: 11 – 16. (Utsate bwino zonse zimene udalamulidwa, mpaka Ambuye athu Yesu Khristu adzabwerenso.)

 

Koma iwe, munthu wa Mulungu, uzipewe zonsezi. Uzikhala ndi mtima wofunafuna chilungamo, wolemekeza Mulungu, wokhulupirika, wachikondi, wolimbika ndi wofatsa. Uzimenya nkhondo yabwino ya kusunga chikhulupiriro, mpaka ukalandire moyo wosatha. Paja Mulungu adakuitanira zimenezi, ndipo udavomera bwino chikhulupiriro chako pamaso pa mboni zambiri. Ndikukulamula pamaso pa Mulungu amene amapatsa moyo zinthu zonse, ndiponso pamaso pa Khristu Yesu amene popereka umboni pamaso pa Ponsio Pilato, adaanena zoona zenizeni. Ndikukulamula kuti, mopanda cholakwa kapena chokayikitsa, utsate bwino zonse zimene udalamulidwa, mpaka Ambuye athu Yesu Khristu adzabwerenso. Pa nthawi yake Mulungu adzamuonetsa kwa ife. Mulunguyo ngwodala ndipo Iye yekha ndiye wolamula, ndiye Mfumu ya mafumu onse, ndiponso Mbuye wa ambuye onse. Ndiye yekha wosafa, ndipo amakhala m’kuwala kosayandikizika. Chikhalire palibe munthu amene adamuona, palibenso amene angathe kumuona. Kwa iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Amen.

 

Mawu a Ambuye……………Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO. – 02 Akorinto 08: 09.

Alleluia, Alleluia –Ambuye athu Yesu Khristu anali wolemera, koma adakhala mmphawi chifukwa cha inu, kuti umphawi wakewo inu mukhale olemera. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 16: 19 – 31. (Kumbukira kuti udalaandiriratu zokondweretsa ukadali ndi moyo, pamene Lazaro adaalandira zowawa. Koma tsopano iye akusangalala kuno, pamene iwe ukuzunzika kwambiri.)

 

Yesu adauza Afarisi kuti, “panali munthu wina wachuma, amene ankavala zovala za mtengo wapatali, ndipo ankasangalala ndikudyerera masiku onse. Panalinso munthu wina, dzina lake Lazaro, amene ankangogona pakhomo la munthu wachuma uja. Iyeyu anali ndi zilonda m’thupi lonse. Ankalakalaka kudya nyenyeswa zimene zinkagwa pansi kuchokera pa tebulo la wachuma uja. Koma sipokhapo, ngakhale agalu ankabwera kumadzanyambita zilonda zake. Munthu osauka uja adamwalira, angelo nkumunyamula, nakamtula m’manja mwa Abrahamu. Munthu wachuma uja nayenso adamwalira, naikidwa m’manda. Pamene ankazunzika ku malo a anthu akufa, wachuma uja adayang’ana kumwamba naona Abrahamu ali patali, ndi Lazaro pambali pakepa. Pamenepo adaanena mokweza mau kuti, ‘Atate Abrahamu, mundichitire chifundo. Tumani Lazaro aviike nsonga ya chala chake m’madzi kuti adzidziritseko lilime langa, pakuti ndikuzunzika koopsa m’moto muno.’ Koma Abrahamu adati, ‘mwana wanga, kumbukira kuti udalaandiriratu zokondweretsa ukadali ndi moyo, pamene Lazaro adaalandira zowawa. Koma tsopano iye akusangalala kuno, pamene iwe ukuzunzika kwambiri. Ndipo pakati pa ife ndi inu pali chiphompho, kotero kuti ofuna kuchoka kuno kubwera kwanuko, sangathe ai. Chimodzimodzinso kuchoka kwanuko kuworokera kuno.’ Apo wachuma uja adati, ‘ndipotu ndikukupemphani Atate, kuti mumtume Lazaroyo apite ku nyumba ya bambo wanga. Kumeneko ndili ndi abale anga asanu. Akawachenjeze, kuwopa kuti iwonso angabwere ku malo ano amazunzo.’ Koma Abrahamu adati, ‘iwo ali ndi mabuku a Mose ndi a aneneri. Amvere za m’menemo.’  Iye adati, ‘iyai, atate Abrahamu, koma wina atauka kwa akufa nkupita kwa iwo, apo adzatembenuka mtima.’ Koma Abrahamu adamuuza kuti, ‘ngatitu iwo samvera Mose ndi aneneri, sangathekenso ngakhale wina auke kwa akufa.”’

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, September 17, 2022

LAMULUNGU LA 25 PACHAKA (CYCLE C)

“Nditani nacho chuma changa?”

 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MNENERI AMOSI; AMOSI 08: 04 – 07. (Imvani izi, inu amene mumapondereza osowa, amene mufuna kugula osauka ndi siliva.)

 

Amosi adati, “imvani izi, inu amene mumapondereza osowa, amene mufuna kuwononga anthu osauka a m’dzikomu. Inu mumazifunsa kuti, ‘kodi chikondwerero cha kukhala kwa mwezi chidzachitika liti, kuti tigulitse dzinthu? Kodi tsiku lopumula la sabata litha liti kuti tigulitsenso tirigu, kutinso tipeze mpata wochepetsera miyeso ndikukweza mitengo, ndiponso kuti tichenjeretse anthu ndi masikelo onama, kuti osauka tiwagule ndi siliva, amphawi tiwagule ndi nkhwawiro, kutinso tigulitse ndi mungu womwe wa tirigu?’” Chauta, Mulungu amene ana a Yakobe amamnyadira walumbira kuti, “Ndithudi, sindidzaiwala zochita zao zonse.”

 

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 113: 01 – 02, 04 – 08.

 

Tamandani Chauta, amene amatulutsa ku dzala anthu osowa.

 

Tamandani Chauta! Mtamandeni, inu atumiki ake,

Tamandani dzina la Chauta. Yamikani Chauta.

Dzina la Chauta litamandike,

Kuyambira tsopano mpaka muyaya.

 

Tamandani Chauta, amene amatulutsa ku dzala anthu osowa.

 

Chauta akulamulira anthu a mitundu yonse,

Ulemerero wake ndi waukulu kuposa wa mlengalenga,

Ndani angalingane ndi Chauta, Mulungu wathu,

Amene akukhala kumwamba, wochita kuweramira pansi,

Poyang’ana mlengalenga ndi dziko lapansi.

 

Tamandani Chauta, amene amatulutsa ku dzala anthu osowa.

 

Amakweza munthu wosauka kuchokera ku fumbi,

Ndipo amatulutsa ku dzala anthu osowa,

Amawakhazika pamodzi ndi mafumu,

Mafumu a Chauta.

 

Tamandani Chauta, amene amatulutsa ku dzala anthu osowa.

--------------------------------------

 

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA TIMOTEO; 01 TIMOTEO 02: 01 – 08. (Pakhale mapemphero opempherera anthu kwa Mulungu, amene afuna kuti anthu onse apulumuke.)

 

Abale, choyamba ndikukupemphani kuti pakhale mapemphero opempherera anthu onse. Mapemphero ake akhale opemba, opempha ndi othokoza Mulungu. Mudziwapempherera mafumu ndi onse amene ali ndi ulamuliro, kuti tikhale ndi moyo wabata ndi wamtendere, tizitamanda Mulungu pa zonse ndi kumadzilemekeza. Zimenezi nzabwino ndi zokondweretsa pamaso pa Mulungu, mpulumutsi wathu. Iye amafuna kuti anthu onse apulumuke ndipo kuti adziwe choona. Pajatu Mulungu ndi mmodzi yekha, Mkhalapakati mmodzi yekhanso pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja timati Khristu Yesu. Iyeyo adadzipereka kuti akhale momboli wa anthu onse. Umenewu unali umboni umene udaperekedwa pa nthawi yake. Nchifukwa chake ine adandiika kuti ndikhale mlaliki wake ndiponso mtumwi, wophunzitsa anthu amitundu ina mau a chikhulupiliro choona. Sindikunamatu ai, ndikunena zoona. Ndikufuna kuti paliponse amuna popemphera azikweza manja ao kwa Mulungu momchitira Ulemu, mopanda mkwiyo kapena kukangana.

 

Mawu a Ambuye……………Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

 

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO. – 02 Akorinto 08:09

 

Alleluia, Alleluia – Ambuye athu Yesu Khristu anali wolemera, koma adakhala mmphawi chifukwa cha inu, kuti ndi umphawi wakewo inu mukhale olemera. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

 

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 16: 01 – 13/ [16: 10 – 13] (Simungathe kutumikira onse awiri, Mulungu ndi chuma.)

 

Yesu adauza ophunzira ake kuti, “panali munthu wina wachuma amene anali ndi kapitao wake. Anthu adadzamneneza kapitawoyo kuti akumwaza chuma cha mbuye wake. Tsono mbuye wakeyo adamuitana, namufunsa kuti, ‘nchiyani chimene ndikumva za iwe? Undifotokozere za ukapitao wako, pakuti sungakhalenso kapitao ai’ Apo kapitaoyo adayamba kuganiza mumtima mwake kuti, ‘ndichite chiyani, popeza kuti mbuye wanga akundilanda ukapitao? Kulima ai, ndilibe mphamvu. Kupemphapempha, ainso kukundichititsa manyazi. Chabwino, tsopano ndadziwa choti ndichite, kuti anthu akandilandire ku nyumba zao, ukapitao ukandithera.’ Motero adaitana angongole a mbuye wake mmodzimmodzi. Adafunsa woyamba kuti, ‘kodi uli ndi ngongole yotani kwa mbuye wanga?’ Iye adati, ‘mafuta amuyeso wokwanira Mitsuko makumi khumi.’ Kapitaoyo adamuuza kuti, ‘nayi kalata yako ya ngongole, khala pansi msanga, ungolembapo Mitsuko makumi asanu.’ Adafunsanso wina kuti, ‘nanga iwe, ngongole yako ndiyotani?’ iye adati, ‘tirigu wamuyeso wokwanira matumba makumi khumi.’ Kapitaoyo adamuuza kuti, ‘nayi kalata yako ya ngongole, ungolembapo matumba makumi asanu ndi atatu.’ Apo mbuye wa kapitao wonyenga uja adamuyamikira chifukwa cha kuchenjera kwake. Pajatu pokhala ndi anzao, anthu okonda zapansi pano ngochenjera koposa anthu okhala m’kuwala kwa Mulungu.”’ Yesu popitiriza mau adati, “ndipo ine ndikukuuzani kuti mudzipezere abwenzi achuma chonyengachi. Apo chumacho chikadzakutherani, Mulungu adzakulandirani ku nyumba zamuyaya. Wokhulupirika pa zinthu zazing’ono, ngokhulupirikanso pa zazikulu. Ndipo wonyenga pa zazing’ono, amanyenganso pa zazikulu. Tsono ngati mwakhala osakhulupirika pa chuma chonyengachi, ndani nanga adzakusungizeni chuma chenicheni? Ndipo ngati mwakhala osakhulupirika ndi za wina, ndani adzakupatseni zimene zili zanuzanu? Palibe wantchito amene angathe kutumikira mabwana awiri, pakuti kapena adzadana ndi mmodzi nkukonda winayo, kapena adzadzipereka kwa mmodzi nkunyoza winayo. Simungathe kutumikira onse awiri, Mulungu ndi chuma.”

 

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, September 10, 2022

LAMULUNGU LA 24 PA CHAKA (CYCLE C)

“Ndinyamuka ndi kubwerera kwa bambo wanga” 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA EKISODO; EKISODO 32: 07 – 11, 13 – 14. (Choncho Chauta adaleka chilango choposa chimene adaati agwetsere anthu akewo.)

Chauta adauza Mose kuti, “fulumira, tsika phiri, chifukwa anthu ako amene udawatsogolera powatulutsa ku Ejipito aja, adziipitsa kwambiri. Asiya mwansanga zonse zija zimene ndidawalamula kuti azichita. Adzipangira fano la mwanawang’ombe wa golide wosungunula, ndipo alipembedza ndikuliphera nsembe, namanena kuti, ‘inu Aisraele, nayi milungu yanu imene idakutulutsani ku aejipito.”’ Ndipo Chauta adaonjeza kuti, “anthu amenewa ndikuwadziwa, ngokanika kwambiri. Nchifukwa chake tsono, undileke kuti ndiwaononge chifukwa ndili wokwiya kwambiri, koma iweyo ndidzakusandutsa mtundu waukulu wa anthu.” Koma Mose adapepesa Chauta wake, nati, “Inu Chauta, chifukwa chiyani mukukwiyira anthu anu chotero, anthu amene mudawatulutsa mu ukapolo ku Ejipito kuja ndi mphamvu zanu zazikulu ndi dzanja lanu lamphamvu? Kumbukirani atumiki anu aja Abrahamu, Isaki ndi Israele ndiponso zija mudawalonjezazi molumbira pa dzina lanu, pamene mudawauza kuti, ‘ndidzakupatsani zidzukulu zambiri, zochuluka ngati nyenyezi zakuthambo. Zidzukulu zanuzo ndidzazipatsa dziko lonse limene ndidalonjeza. Dziko limeneli lidzakhala lao mpaka muyaya.”’ Choncho Chauta adaleka chilango choopsa chimene adaati agwetsere anthu akewo.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 51: 03 – 04, 12 – 19.

 

Ndinyamuka, ndipita kwa bambo wanga.

 

Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, malinga ndi chikondi chanu chosasinthika.

Mufafanize machimo anga, malinga ndi chifundo chanu chachikulu,

Mundisambitse kwathunthu pochotsa kulakwa kwanga,

Mundiyeretse mtima pochotsa machimo anga.

 

Ndinyamuka, ndipita kwa bambo wanga.

 

Mundilengere mtima woyera, Inu Mulungu,

Muike mwa ine mtima watsopano ndi wokhazikika.

Musandipirikitse pamaso panu,

Musachotse Mzimu wanu woyera mwa ine.

 

Ndinyamuka, ndipita kwa bambo wanga.

 

Ambuye, tsekulani milomo yanga,

ndipo pakamwa panga padzalankhula zotamanda Inu.

Nsembe imene Inu Mulungu mumailandira ndi mtima wotswanyika,

Mtima wachisoni ndi wolapa, Inu Mulungu simudzanyoza.

 

Ndinyamuka, ndipita kwa bambo wanga.

--------------------------------------

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA TIMOTEO: 01 TIMOTEO 01: 12 – 17. (Yesu Khristu adabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa.)

Abale, ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene adandipatsa mphamvu pa ntchitoyi.  Ndikumthokoza pondiwona wokhulupirika nandipatsa ntchito yomtumikira, ngakhale kuti kale ndinkamuchita chipongwe, kumzunza ndi kumnyoza. Koma Mulungu adandichitira chifundo chifukwa ndinkadzichita mosadziwa, poti ndinali wopanda chikhulupiliro. Ambuye athu adandikomera mtima koposa, nkundipatsa chikhulupiliro ndi chikondi zimene tili nazo chifukwa chogwirizana ndi Khristu Yesu. Awa ndi mau otsimikizika, oyenera kuwavomereza ndi mtima wonse, akuti Khristu Yesu adabwera pansi pano kuti adzapulumutse anthu ochimwa. Ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwa koposa. Koma Mulungu adandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwa koposane, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse. Adafuna kuti ndikhale chitsanzo cha kuwalezera mtima onse amene adzamkhulupilire kuti alandire moyo wosatha. Kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Amen.

Mawu a Ambuye……………Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO. – 2 Akorinto 05: 19.

Alleluia, Alleluia – Mwa Khristu Mulungu ankayanjanitsa anthu a pa dziko lonse lapansi ndi Iye mwini, ndipo adatipatsa ifeyo mau onena za chiyanjanitsocho kuti tiwalalike. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 15: 01 – 10. (Kumwamba kudzakhala chimwemwe chifukwa cha munthu mmodzi wochimwa amene watembenuka mtima.)

Pa nthawi yomweyo, anthu onse okhometsa msonkho ndi Ayuda enanso onyozera Malamulo ankabwera kwa Yesu kudzamva mau ake. Tsono Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo adayamba kuwinya nkumanena kuti, “munthu uyu amalandira anthu ochimwa, nkumadya nawo pamodzi.” Tsono Yesu adawaphera fanizo ili, adati, “ndani mwa inu ali ndi nkhosa 100, imodzi itatayikapo, sangasiye nkhosa zina zonse 99 zija ku busa, nkukafunafuna yotayikayo mpaka ataipeza? Ndipo ataipeza, amaisenza pamapewa pake mokondwa. Pofika kwao, amasonkhanitsa abwenzi ake ndi anzake oyandikana nawo, nawauza kuti, mukondwere nane pamodzi, chifukwa ndaipeza nkhosa yanga idaatayika ija.” Yesu adapitiriza mau kuti, “ndithu ndikunenetsa kuti momwemonso Kumwamba kudzakhala chimwemwe chifukwa cha munthu mmodzi wochimwa amene watembenuka mtima, kuposa anthu olungama 99 amene alibe chifukwa chotembenukira mtima. Mwinanso mai amakhala ndi tindalama khumi, kamodzi nkutayika. Kodi suja amayatsa nyale nasesasesa m’nyumba nkufunafuna mosamala mpaka atakapeza? Atakapeza amasonkhanitsa abwenzi ake ndi anzake oyandikana nawo, nawauza kuti, ‘mukondwere nane pamodzi, chifukwa ndakapeza kandalama kanga kaja kadaatayikaka.”’ Yesu popitiriza mau adati, “ndikunenetsa kuti ndi m’menenso angelo a Mulungu amakondwerera munthu mmodzi wochimwa amene watembenuka mtima.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, September 3, 2022

 

LA MULUNGU LA 23 PA CHAKA (CYCLE C)

“Tiyambe takhala pansi.”

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA LUNTHA; LUNTHA 09: 13 – 18. (Ndani angathe kuzindikira zimene Ambuye akufuna?)

Kodi ndani angathe kudziwa maganizo a Mulungu?  Ndani angathe kuzindikira zimene Ambuye akufuna? Nzeru za anthu nzoperewera, zolinga zathu nzotha kulephera. Chifukwa thupi lodzafali limalemetsa mtima, nyumba yake yadothiyi imavuta mtima woganiza zambiri. Nkwapatali kale kwa ife kulota zimene zili pansi pano, ndipo timachita kuvutikira kuti timvetse ngakhale zimene zili pafupi nafe. Nanji tsono zimene zili kumwamba, angazitulukire ndani?  Ndani angathe kudziwa kufuna kwanu Ambuye, mutapanda kumupatsa luntha, kapena kumutumizira mzimu wanu woyera kuchokera kumwamba? Motero njira za anthu a pansi pano zidalungamitsidwa, anthu adaphunzira zimene zimakukomerani, ndipo adapulumuka chifukwa cha luntha.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 90: 03 – 06, 12 – 14, 17.

 

Inu Ambuye, ndinu kothawira kwathu pa mibadwo yonse.

 

Inu mumabwezera anthu ku fumbi,

Ndipo mumati, “bwerani inu ana a anthu.”

Pakuti zaka chikwi chimodzi pamaso panu zili ngati dzulo chabe,

Kapena ngati kamphindi chabe kausiku.

 

Inu Ambuye, ndinu kothawira kwathu pa mibadwo yonse.

 

Inu mumachotsa moyo wa anthu mwadzidzi,

Ali ngati maloto, ali ngati udzu wongotsitsimuka m’mawa,

M’mamawamo umatsitsimuka ndipo umakondwa,

Madzulo umafota ndi kuuma.

 

Inu Ambuye, ndinu kothawira kwathu pa mibadwo yonse.

 

Tsono tiphunzitseni kuwerenga masiku athu, kuti tikhale ndi mtima wanzeru,

Lezani mtima, Inu Chauta.

Nanga mudzatikwiyira mpaka liti?

Achitireni chifundo atumiki anu.

 

Inu Ambuye, ndinu kothawira kwathu pa mibadwo yonse.


Tidzazeni m’mawa mulimonse ndi chikondi chanu chosasinthika,

Kuti tizikondwa ndi kusangalala masiku athu onse.

Inu Ambuye, mutikomere mtima, ndipo mudalitse ntchito zonse za manja athu.

 

Inu Ambuye, ndinu kothawira kwathu pa mibadwo yonse.

--------------------------------------

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA FILEMONI: FILEMONI 09 – 10: 12 – 17. (Udzakhale naye ngati mbale wokondedwa.)

Iwe Filemoni, chifukwa cha chikondi makamaka ndingochita kukupempha, ine Paulo amene ndili nkhalamba, amenenso ndili m’ndende tsopano chifukwa cha Khristu Yesu. Ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga mwa Khristu, amene ndidachita ngati kumubala m’ndende muno. Iyeyu ndi Onesimo. Ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, ndipo pakutero ndikuchita ngati kukutumizira mtima wanga womwe. Ndikadakonda kuti akhalebe ndi ine kuno, kuti azinditumikira m’malo mwako, pokhala ndili m’ndende chifukwa cha Uthenga Wabwino. Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, kuwopa kuti ungandichitire chinthu chabwinochi mokakamizidwa, osati mwaufulu. Kapena Onesimo anangokusiya kanthawi pang’ono, kuti udzakhale naye nthawi zonse, osatinso ngati kapolo, koma kwenikweni ngati m’bale wokondeka. Ine ndimamkonda kwambiri, ndipo iweyo uyenera kumkonda koposa, popeza kuti ndi munthu m’nzako ndiponso mkhristu m’nzako. Tsono ngati umati ndine bwenzi lako, umlandire iyeyu monga momwe ukadandilandilira ineyo.

Mawu a Ambuye……………Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO. – SALIMO 119: 135.

Alleluia, Alleluia – Yang’anireni ine mtumiki wanu ndi chikondi chanu, ndipo mundiphunzitse malamulo anu. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 14: 25 – 33. (Aliyense mwa inu atha kukhala wophunzira wanga pokhapokha atagulitsa chuma chake chonse.)

Chikhamu cha anthu chinkatsagana ndi Yesu. Tsono Iye adatembenuka nawauza kuti, “aliyense wofuna kukhala wophunzira wanga, azikonda ine kuposa atate ake ndi amai ake, mkazi wake ndi ana ake, abale ake ndi alongo ake, ndiponso koposa ngakhale moyo wake womwe. Aliyense amene sasenza mtanda wake nkumanditsata, sangakhale wophunzira wanga. Wina mwa inu akafuna kumanga nyumba yosanja, kodi suja amayamba wakhala pansi nkuwerenga ndalama zofunika, kuti aone ngati ali nazo zokwanira kuitsiriza? Akapanda kutero, mwina adzaika maziko, nkulephera kuitsiriza. Apo anthu onse, poona zimenezi, adzayamba kumseka. Adzati, ‘mkulu uyu adaayamba kumanga nyumba, koma adalephera kuitsiriza.’ Chimodzimodzinso kodi ndi Mfumu iti, popita ku nkhondo kukamenya ndi mfumu ina, siiyamba yakhala pansi nkuganiza bwino? Imaganiziratu ngati ndi asilikali zikwi khumi ingathe kukamenyana ndi mfumu ina ija, imene ikubwera ndi asilikali zikwi makumi awiri. Tsono ngati siingathe, idzatuma nthumwi kukapempha mtendere, mfumu ina ija ikali kutali. Chonchonso aliyense mwa inu amene sasiya zonse zimene ali nazo, sangakhale ophunzira wanga.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

 

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...