LAMULUNGU LA 20 PA CHAKA – C.
“Ndinabwera kudzaponya moto pa dziko lapansi.”
MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA YEREMIYA; YEREMIYA 38: 04 – 06, 08 – 10. (Munandilera kukhala munthu wosokoneza pa dziko)
Tsono akuluakulu adauza Mfumu kuti, “munthuyu ayenera
kuphedwa. Akutayitsa mtima ankhondo ndi anthu onse otsatira mu mzinda, chifukwa
cha zolankhula zakezi. Munthu ameneyu sakuwafunira zabwino anthu, angofuna kuti
aonongedwe basi.’’ Mfumu Zedekiya adati, “suyu, ali m’manja mwanu. Ine
sindingakuletseni ai.’’ Choncho iwo aja adatenga Yeremiya, nakamponya m’chitsime
adaakumba Malakiya mwana wa Mfumu, m’bwalo la alonda a Mfumu. Adamtsitsira m’menemo
ndi chingwe. M’chitsimemo munalibe madzi, munali maotope okhaokha. Ndipo
Yeremiya adamira m’matopemo. Ebedemeleki adatuluka ku nyumba ya amfumu
kukaiwuza kuti, “Mfumu mbuyanga, anthu awa amchita zoipa kwambiri mneneri
Yeremiya. Amponya m’chitsime, ndipo poti buledi adatha mu mnzinda, adzafa ndi
njala mmenemu.’’ Tsono mfumu idalamula Mkusi Ebedemeleki kuti, “tenga anthu
atatu, mukamtulutse mneneri Yeremiya asanafe.’’
Mawu a
Ambuye.......Tithokoze Mulungu
---------------------------------------
NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 40: 02 – 04, 18.
Ambuye, bwerani kuti mudzandithandize.
Ine
ndidayembekeza Chauta ndi mtima wokhulupirira kuti adzandithandize,
Adaweramira
pansi kuyang’ana kwa ine, namva kulira kwanga.
Ambuye, bwerani
kuti mudzandithandize.
Adanditulutsa
m’dzenje la chiwonongeko, mchithaphwi chamatope,
Adapondetsa mapazi
anga pa thanthwe, nandiyetsa bwino lomwe.
Ambuye, bwerani
kuti mudzandithandize.
Mulungu waika
nyimbo yatsopano m’kamwa mwanga, nyimbo yake yotamanda Iye,
Anthu ambiri
adzaona zimenezi ndipo adzaopa, nadzakhulupirira Chauta.
Ambuye, bwerani
kuti mudzandithandize.
Inu Chauta, ine
ndine wolefuka ndi wosowa, koma simunandiiwale,
Inu ndinu
mthandizi wanga ndi mpulumutsi wanga.
Inu Mulungu
wanga, musachedwe kudzandithandiza.
Ambuye, bwerani
kuti mudzandithandize.
--------------------------------------
MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOLEMBERA AHEBERI; AHEBERI 12: 01 – 04. (Tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu.)
Popeza kuti ponse pozungulira pali mboni zambirimbiri chotere, tiyeni tichotse kalikonse kotichedwetsa, makamaka tchimo limene limatikangamira, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu. Maso athu azipenyetsetsa Yesu amene ali woyambitsa chikhulupiliro chathu, ndiponso wochifikitsa pake penipeni. Chifukwa cha chimwemwe chimene chinkamudikira, Iyeyo adapirira zowawa zapamtanda. Adawanyoza manyazi a imfa chotere, ndipo tsopano akukhala ku dzanja la lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu. Muziganiza za Iye amene adapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafookere ndi kutaya Mtima. Polimbana ndi uchimo, simudafike mpaka pokhetsa magazi. Mulungu amalanga ana ake.
Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu
--------------------------------------
NYIMBO YA MTHENGA WABWINO.
Alleluia, Alleluia – Nkhosa zanga zimamva mau anga, atero Ambuye. Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsatira. – Alleluia, Alleluia.
--------------------------------------
MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 12: 49 – 53. (Sindidabwera kudzapereka mtendere ai, koma kugawanikana.)
Yesu adawauza ophunzira ake kuti, “ndidabwera kudzaponya
moto pa dziko lapansi, ndipo ndikadakonda utayaka kale. Koma ndiyenera kuyamba
ndalowa m’masautso akulu, ndipo mtima wanga sukhazikika mpaka zitachitika. Kodi
mukuyetsa kuti ndidadzapereka mtendere pansi pano? Iyayi, kunena zoona, osati
mtendere koma kugawikana. Kuyambira tsopano m’banja limodzi mudzakhala anthu
asanu ogawikana, atatu adzakangana ndi awiri, ndipo awiri adzakangana ndi
atatu. Bambo adzakangana ndi mwana wake wamwamuna, mwana wamwamuna adzakangana
ndi bambo wake. Mai adzakangana ndi mwana wake wamkazi, mwana wamkazi
adzakangana ndi mai wake. Apongozi adzakangana ndi mkazi wamwana wao, ndipo
mkaziyo adzakangana ndi Apongozi akewo.”
Mthenga
wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.
#Pax_et_Gaudium_in_Domino.
Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295
No comments:
Post a Comment