Saturday, August 27, 2022

 

LA MULUNGU LA 22 PA CHAKA (CYCLE C)

“Tipewe khalidwe lakunyada ndi lakudzikonda.” 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA MPHUNZITSI; MPHUNZITSI 03: 17 – 19, 28 – 29. (Udzichepetse, ukatero udzapeza kuyanja pamaso pa Ambuye.)

Mwana wanga, ukhale wodekha pa zonse zimene umachita, ndipo anthu okomera Ambuye adzakukonda. Ngati ndiwe wotchuka kwambiri, udzichepetse, ukatero udzapeza kuyanja pamaso pa Ambuye. Pali anthu ambiri otchuka ndi amphamvu, koma Ambuye amaulula zinsinsi zao kwa anthu odzichepetsa. Tsoka likagwera onyada, palibe mankhwala, pakuti kuipa kumakhala kutazika mizu mwa iye. Munthu wochenjera amalingalira bwino fanizo, munthu wanzeru amafunitsitsa kukhala ndi makutu atcheru.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO: 68: 04 – 07, 10 – 11.


Mwakukoma mtima kwanu, Inu Chauta, mwakonza malo okhala anthu ovutika.

 

Anthu anu Mulungu, akondwere,

Asangalale pamaso panu,

Inde, asekere ndi chimwemwe,

Muimbireni Mulungu, imbani nyimbo zotamanda dzina lake.

 

Mwakukoma mtima kwanu, Inu Chauta, mwakonza malo okhala anthu ovutika.

 

Atate a ana amasiye ndiponso Mtetezi wa azimai amasiye,

Ndi Mulungu amene amakhala m’malo ake oyera,

Anthu osiyidwa, Mulungu amawapatsa malo okhalamo,

Am’ndende amawatulutsa kuti akhale pa ufulu.

 

Mwakukoma mtima kwanu, Inu Chauta, mwakonza malo okhala anthu ovutika.

 

Inu Mulungu, mudagwetsa mvula yokwanira pa dziko,

Mudalimbitsanso dziko, pamene lidaali lofooka,

Anthu anu adapezamo malo okhala,

Inu Mulungu, mudapatsa anthu osauka zao mwa ubwino wanu.

 

Mwakukoma mtima kwanu, Inu Chauta, mwakonza malo okhala anthu ovutika.

--------------------------------------

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOLEMBERA AHEBERI; AHEBERI 12: 18 – 19, 22 – 24a. (Inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ndiponso ku mzinda wa Mulungu wamoyo.)

Inu simudachite monga Aisraele aja, amene adaafika ku chinthu chimene adaatha kuchikhudza, ndiye kuti ku Phiri la Sinai, lija linali loyaka moto, lamdima wa bii, la mphepo yamkuntho; limene panali kulira kwa lipenga, ndiponso kumveka kwa mau. Anthu atamva mauwo, adaapempha kuti asawamvenso konse. Koma inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ndiponso ku mzinda wa Mulungu wamoyo, ndiye kuti Yerusalemu wa Kumwamba, m’mene muli Angelo osawerengeka. Mwafika kuchikondwelero kumene kwasonkhana ana oyamba a Mulungu, amene maina ao adalembedwa Kumwamba. Mwafika kwa Mulungu, mweruzi wa anthu onse, ndiponso kwa mizimu ya anthu olungama, amene Mulungu wawasandutsa angwiro kwenikweni. Mwafika kwa Yesu, Nkhoswe yokonza za chipangano chatsopano, ndiponso mwafika ku magazi okhetsedwa, amene akutilonjeza zinthu zabwino koposa m’mene magazi a Abele ankachitira.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO. – MATEYO 11: 29ab

Alleluia, Alleluia – Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wa mtima wodzichepetsa. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 14: 01, 07 – 14. (Aliyense wodzikuza adzamchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamkuza.)

Pa tsiku lina la sabata Yesu adakadya kwa mkulu wina wa m’gulu la Afarisi, ndipo Afarisi anzake ankamupenyetsetsa. Yesu adaaona kuti anthu amene adaaitanidwa kudzadya nao ankadzisankhira malo aulemu. Tsono adawaphera fanizo, adati, “wina akakuitana ku phwando la ukwati, usamakhala pa malo aulemu ai, chifukwa mwina kapena adaitananso wina waulemu kuposa iwe. Ndiye iye uja amene adaitana awiri nonsenu nkudzakuuza kuti, ‘pepani, patsani awa malowa.’ Apo iweyo udzachita manyazi pokakhala pa malo otsika. Koma akakuitana, kakhale pa malo otsika, kuti amene adakuitana uja adzakuuze kuti, ‘bwezi langa, dzakhale pa malo aulemu pano.’ Apo udzalandira ulemu pamaso pa onse amene uli nao podyera. Pajatu aliyense wodzikuza adzamchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamkuza.” Yesu adauzanso Mfarisi uja amene adaamuitana kudzadya naye kuti, “ukamakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamaitana abwenzi ako, kapena abale ako, kapena a fuko lako, kapena anzako achuma, chifukwa mwina iwonso adzakuitanako, motero udzalandiriratu mphoto yako. Koma iwe ukamakonza phwando, uziitana amphawi, otsimphina, opunduka ndi akhungu. Apo udzakhala wodala, chifukwa iwo alibe kanthu koti nkukubwezera. Mulungu ndiye adzakubwezera, pamene anthu olungama adzauka kwa akufa.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, August 20, 2022

 

LAMULUNGU LA 21 PA CHAKA – C.

“Yesetsani kolowera pa khomo lophaphatiza.” 

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA YESAYA; YESAYA 66: 18 – 21. (Adzabwera nawo abale anu onse kuchokera kwa anthu a mitundu yonse.)

Chauta akunena kuti, “ndikudziwa ntchito zawo ndi maganizo ao. Ndikubwera kudzasonkhanitsa anthu amitundu yonse ndi a zilankhulo zonse. Adzabweradi ndipo adzaona ulemelero wanga. Ndidzaika chizindikiro pakati pao. Mwa iwowo padzakhala ena opulumukako amene ndidzawatuma kwa anthu a mitundu ina, monga a ku Tarisisi, a ku Puti ndi aku Ludi, akatswiri a mauta, ndiponso Tubala, ku Yavani, ndi ku maiko akutali amene sadamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemelero wanga. Iwowo adzalalika za ulemelero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. Ndipo adzabwera nawo abale anu onse kuchokera kwa anthu a mitundu yonse, kuti akhale mphatso kwa ine. Adzabwera nawo monga momwe Aisraele amabwerera ndi zopereka za chakudya ku Nyumba ya Mulungu, atazitenga m’ziwiya zotsukatsuka. Ndipo ena mwa iwo ndidzawasandutsa ansembe ndi Alevi.”

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO: 117: 01 – 02

Pitani ku dziko lonse lapansi, kalalikireni uthenga wabwino.

 

Tamandani Chauta, Inu mitundu yonse ya anthu,

Mlemekezeni kwambiri, inu anthu a m’maiko onse.

 

Pitani ku dziko lonse lapansi, kalalikireni uthenga wabwino.

 

Pakuti chikondi chake kwa ife nchachikulu,

Kukhulupirika kwa Chauta nkwamuyaya.

 

Pitani ku dziko lonse lapansi, kalalikireni uthenga wabwino.

--------------------------------------

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOLEMBERA AHEBERI; AHEBERI 12: 05 – 07, 11 – 13. (Ambuye amamlanga aliyense amene amamkonda.)

Mwaiwala kodi mau olimbitsa mtima aja, amene Mulungu amakulankhulani ngati ana ake? Mauwo ndi awa: “mwana wanga, usanyozere malangizo a Ambuye, kapena kutaya mtima pamene Iwo akudzudzula. Paja Ambuye amamlanga aliyense amene amamkonda, amakwapula mwana aliyense amene iwo amamlandira.” Muzipirira masautso kuti muphunzirepo makhalidwe oyenera. Mulungu amakutengani ngati ana ake m’zochita zake zonse. Kodi nkale lonse analipo mwana wake amene bambo wake sadamlange?  Pamene munthu akulandira chilango, kwa iye chilangocho chimaoneka ngati chinthu chomvetsa chisoni, ndi chosakondweretsa. Koma anthu amene adaleredwa mwa njira imeneyi, pambuyo pake amapata mtendere umene uli chipatso cha moyo olungama. Limbitsani tsono manja anu ofooka ndiponso maondo anu ofooka. Muziyenda m’njira zoongoka, kuti miyendo yopunduka isagweduke, koma ichiritsidwe.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – Yohane 14: 06.

Alleluia, Alleluia – Ineyo ndine njira, ndine choona ndiponso moyo. Palibe munthu angafike kwa Atate ngati sadzera mwa Ine. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 13: 22 – 30. (Adzachokera kuvuma ndi kuzambwe, nadzakhala podyera mu Ufumu wa Mulungu.)

Pa ulendo wake wopita ku Yerusalemu, Yesu ankayendera mizinda ndi midzi akuphunzitsa. Munthu wina adamufunsa kuti, “Ambuye, kodi adzapulumuka ndi anthu owerengeka okha?” Yesu adayankha kuti, “yesetsani kulowera pa khomo lophaphatiza, pakuti kunena zoona anthu ambiri adzafuna kulowa, koma adzalephera. Mwini nyumba adzanyamuka nkutseka pakhomo. Pamenepo okhala panjanu mudzayamba kugogoda nkumanena kuti, ‘Ambuye, titsekulireni.’  Koma iye adzakuyankhani kuti, ‘sindikudziwa kumene mukuchokera.’ Apo inuyo mudzayamba kunena kuti, ‘pajatu tinkadya ndi kumamwa nanu pamodzi, ndipo inuyo munkaphunzitsa m’misewu ya m’zinda mwathu.’ Koma iye adzakauuzani kuti, ‘pepani, sindikudziwa kumene mukuchokera. Chokani apa nonsenu, anthu ochita zoipa.’ Apo mudzayamba kulira ndi kukukuta mano, pamene mudzaona Abrahamu ndi Isaki ndi Yakobe ndi aneneri onse mu Ufumu wa Mulungu, inuyo mukuponyedwa kunja. Anthu adzachokera kuvuma ndi kuzambwe, kumpoto ndi kumwera, nadzakhala podyera mu ufumu wa Mulungu. Pamenepo amene ali otsirizira adzakhala oyambirira, ndipo amene anali oyambirira adzakhala otsirizira.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-10982647706729

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

Saturday, August 13, 2022


                                                       LAMULUNGU LA 20 PA CHAKA – C.

“Ndinabwera kudzaponya moto pa dziko lapansi.”

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA YEREMIYA; YEREMIYA 38: 04 – 06, 08 – 10. (Munandilera kukhala munthu wosokoneza pa dziko)

Tsono akuluakulu adauza Mfumu kuti, “munthuyu ayenera kuphedwa. Akutayitsa mtima ankhondo ndi anthu onse otsatira mu mzinda, chifukwa cha zolankhula zakezi. Munthu ameneyu sakuwafunira zabwino anthu, angofuna kuti aonongedwe basi.’’ Mfumu Zedekiya adati, “suyu, ali m’manja mwanu. Ine sindingakuletseni ai.’’ Choncho iwo aja adatenga Yeremiya, nakamponya m’chitsime adaakumba Malakiya mwana wa Mfumu, m’bwalo la alonda a Mfumu. Adamtsitsira m’menemo ndi chingwe. M’chitsimemo munalibe madzi, munali maotope okhaokha. Ndipo Yeremiya adamira m’matopemo. Ebedemeleki adatuluka ku nyumba ya amfumu kukaiwuza kuti, “Mfumu mbuyanga, anthu awa amchita zoipa kwambiri mneneri Yeremiya. Amponya m’chitsime, ndipo poti buledi adatha mu mnzinda, adzafa ndi njala mmenemu.’’ Tsono mfumu idalamula Mkusi Ebedemeleki kuti, “tenga anthu atatu, mukamtulutse mneneri Yeremiya asanafe.’’

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 40: 02 – 04, 18.

Ambuye, bwerani kuti mudzandithandize.

 

Ine ndidayembekeza Chauta ndi mtima wokhulupirira kuti adzandithandize,

Adaweramira pansi kuyang’ana kwa ine, namva kulira kwanga.

 

Ambuye, bwerani kuti mudzandithandize.

 

Adanditulutsa m’dzenje la chiwonongeko, mchithaphwi chamatope,

Adapondetsa mapazi anga pa thanthwe, nandiyetsa bwino lomwe.

 

Ambuye, bwerani kuti mudzandithandize.

 

Mulungu waika nyimbo yatsopano m’kamwa mwanga, nyimbo yake yotamanda Iye,

Anthu ambiri adzaona zimenezi ndipo adzaopa, nadzakhulupirira Chauta.

 

Ambuye, bwerani kuti mudzandithandize.

 

Inu Chauta, ine ndine wolefuka ndi wosowa, koma simunandiiwale,

Inu ndinu mthandizi wanga ndi mpulumutsi wanga.

Inu Mulungu wanga, musachedwe kudzandithandiza.

 

Ambuye, bwerani kuti mudzandithandize.

--------------------------------------

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA YOLEMBERA AHEBERI; AHEBERI 12: 01 – 04. (Tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu.)

Popeza kuti ponse pozungulira pali mboni zambirimbiri chotere, tiyeni tichotse kalikonse kotichedwetsa, makamaka tchimo limene limatikangamira, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu. Maso athu azipenyetsetsa Yesu amene ali woyambitsa chikhulupiliro chathu, ndiponso wochifikitsa pake penipeni. Chifukwa cha chimwemwe chimene chinkamudikira, Iyeyo adapirira zowawa zapamtanda. Adawanyoza manyazi a imfa chotere, ndipo tsopano akukhala ku dzanja la lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu. Muziganiza za Iye amene adapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafookere ndi kutaya Mtima. Polimbana ndi uchimo, simudafike mpaka pokhetsa magazi. Mulungu amalanga ana ake.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO.

Alleluia, Alleluia – Nkhosa zanga zimamva mau anga, atero Ambuye. Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsatira. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 12: 49 – 53. (Sindidabwera kudzapereka mtendere ai, koma kugawanikana.)

Yesu adawauza ophunzira ake kuti, “ndidabwera kudzaponya moto pa dziko lapansi, ndipo ndikadakonda utayaka kale. Koma ndiyenera kuyamba ndalowa m’masautso akulu, ndipo mtima wanga sukhazikika mpaka zitachitika. Kodi mukuyetsa kuti ndidadzapereka mtendere pansi pano? Iyayi, kunena zoona, osati mtendere koma kugawikana. Kuyambira tsopano m’banja limodzi mudzakhala anthu asanu ogawikana, atatu adzakangana ndi awiri, ndipo awiri adzakangana ndi atatu. Bambo adzakangana ndi mwana wake wamwamuna, mwana wamwamuna adzakangana ndi bambo wake. Mai adzakangana ndi mwana wake wamkazi, mwana wamkazi adzakangana ndi mai wake. Apongozi adzakangana ndi mkazi wamwana wao, ndipo mkaziyo adzakangana ndi Apongozi akewo.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Saturday, August 6, 2022


                                                 LAMULUNGU LA 19 PA CHAKA – C.

(Tilimbike m’chikhulupiriro poyembekeza kudza kwa Ambuye.)

MAU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAU A M’BUKU LA LUNTHA; LUNTHA 18: 06 – 09. (Njira yomwe mudalangira adani athu, idakhala njira yoti mutichitire ife zaulemu potiitana kwa Inu.)

Usiku umenewo makolo athu anali ataudziwiratu kuti azilimba mtima ndi kukondwa podziwa kuti apherezera malumbiro aja ankawakhulupirirawa. Choncho anthu anu ankayembekeza chipulumutso cha olungama ndiponso chiwonongeko cha adani ao. Njira yomwe mudalangira adani athu, idakhala njira yoti mutichitire ife zaulemu potiitana kwa Inu. Adzukulu oyera mtima a ulungama aja ankapereka nsembe mobisala. Ankavomerezana kuti adzasunga ndi kugawana molingana zinthu zimodzimodzi, kaya zikhale madalitso, kaya zoopsa. Motero adaayambiziratu kuimba nyimbo zotamanda za makolo ao.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

---------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 33: 01, 12, 18 – 22.

 

Ngwodala mtundu wa anthu amene Mulungu wao ndi Chauta.

 

Kondwerani mwa Chauta, inu anthu ake,

Zoonadi ochita zolungama azitamanda,

Ngwodala mtundu wa anthu amene Mulungu wao ndi Chauta,

Anthu amene Chauta wawasankha akeake.

 

Ngwodala mtundu wa anthu amene Mulungu wao ndi Chauta.

 

Chauta amayang’ana anthu omumvera,

Ndi odalira chikondi chake chosasinthika,

Iye amachita izi kuti awapulumutse ku imfa,

Ndi kuwasungira moyo anthuwo pa nthawi ya njala.

 

Ngwodala mtundu wa anthu amene Mulungu wao ndi Chauta.

 

Mitima yathu ikuyembekeza Chauta,

Chifukwa Iye ndiye chithandizo ndi chishango chathu,

Mitima yathu imasangalala mwa Chauta,

Popeza kuti timadalira dzina lake loyera.

 

Ngwodala mtundu wa anthu amene Mulungu wao ndi Chauta.

--------------------------------------

MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAU A M’KALATA KWA AHEBRI; AHEBRI 11: 01 – 02, 08 – 12. (Abrahamu adayang’ana maso kutsogolo ku mzinda umene Mulungu adaumanga mwakaso.)

Tikati kukhulupirira, ndiye kuti kusakayika konse pa zinthu zimene tikuziyembekeza, ndiponso kutsimikiza kuti zinthu zimene sitikuziwona zilipo ndithu. Pokhala ndi chikhulupiriro, makolo athu akale aja Mulungu adaonetsa kuti ankakondwera nawo. Pokhala ndi chikhulupiriro, Abrahamu adamvera pamene Mulungu adamuitana kuti apite ku dziko lina limene adaamlonjeza kuti lidzakhala lake. Ngakhale sankadziwa kumene ankapita, adapitabe. Pokhala ndi chikhulupiriro chomwecho, ankakhala ngati mlendo m’dzikolo limene Mulungu adaamlonjeza. Ankakhala m’mahema pamodzi ndi Isaki ndi Yakobo, amene nawonso anali atalandira lonjezo lomwelo la Mulungu. Monsemo Abrahamu ankadikira mzinda wa maziko okhazikika. Mzindawo, Mmisiri woganiziratu mamangidwe ake ndiponso woumanga, ndi Mulungu. Pokhala ndi chikhulupiriro, Sara yemwe adalandira mphamvu zakutenga pathupi, ngakhale zaka zake zakubala mwana zinali zitapita kale. Zimenezi zidatheka chifukwa adaavomera kuti amene adazilonjezayo ngwokhulupirika. Nchifukwa chake mwa munthu mmodzi, wotinso anali ngati wakufa, mudatuluka mibadwo yochuluka ngati nyenyezi, ndi yosawerengeka ngati mchenga wa pa gombe la nyanja.

Mawu a Ambuye.......Tithokoze Mulungu

--------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO.

Alleluia, Alleluia – Khalani maso, chifukwa simudziwa tsiku limene Mwana wa Munthu adzabwera. – Alleluia, Alleluia.

--------------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA; LUKA 12: 32 – 48 (Khalani okonzeka kutumikira.)

Yesu anawauza ophunzira ake kuti. “Inu nkhosa zanga, ngakhale muli owerengeka, musaope, pakuti kudakomera Atate anu kuti akupatseni Ufumu wake. Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupatse amphawi. Mudzipezere matumba a ndalama amene safwifwa, ndi kudziwunjikira chuma chokhalitsa Kumwamba; kumeneko mbala sizingafikeko, ndipo njenjete sizingachiwononge. Pajatu kumene kuli chuma chako, mtima wakonso kokhala nkomweko. Khalani okonzeka kutumikira, ndipo nyale zanu zikhale zoyaka. Khalani ngati antchito amene akudikira mbuye wao wochokera ku phwando la ukwati, kuti pamene afike ndi kugogoda, iwo amtsekulire msanga. Ngodala antchito amene mbuye wao pofika, awapeza ali maso. Ndithu ndikunenetsa kuti adzadzikonzekera, nadzawakhazika podyera, ndipo adzabwera nkumawatumikira. Ngodala antchitowo mbuye waoyo akadzawapeza ali choncho pamene iye adzafike, ngakhale pakati pa usiku kapena kuli pafupi kucha. Koma kumbukirani kuti, mwini nyumba akadadziwiratu nthawi yoti mbala ifika, sibwenzi atalola kuti ithyole nyumba yake. Choncho inunso khalani okonzeka, pakuti Mwana wa Munthu adzabwera pa nthawi imene simukuyembekeza.” Pamenepo Petro adati, “Ambuye, kodi fanizoli mukuphera ife tokha, kapena mukuuza onse?” Yesu adati, “tsono kapitao wokhulupirika ndi wanzeru ndani, amene mbuye wake adzamuike kuti aziyang’anira onse a m’nyumba mwake, nkumawagawira chakudya chao pa nthawi yake? Ngwodala wantchito ameneyo, ngati mbuye wake pofika adzampeza akuchitadi zimenezi. Ndithu ndikunenetsa kuti adzamuika woyang’anira chuma chake chonse. Koma ngati ndi wantchito woipa, mumtima mwake azidzati, ‘mbuye wanga akuchedwa kubwera.’ Ndiye adzayamba kumenya antchito anzake, amuna ndi akazi, ndiponso kumadya, kumamwa ndi kuledzera. Tsono mbuye wake adzangoti mbwe mwadzidzidzi, pa tsiku limene iye sakumuyembekeza. Choncho adzamlanga koopsa, ndipo adzamtaya ku malo a anthu osakhulupirika. Wantchito amene akudziwa zimene mbuye wake amafuna, koma osakonzekera kuzichita, adzamkwapula kwambiri. Koma wantchito amene sadziwa zimene mbuye wake amafuna, tsono nkumachita zoyenera kumlanga nazo, adzamkwapula pang’ono. Aliyense amene adalandira zambiri, adzayenera kubweza zambiri. Ndipo amene adamsungiza zambiri, adzamlamula kuti abweze zochuluka koposa.

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...