
LAMULUNGU LA KANJEDZA
(CHIYAMBI CHA MLUNGU WOYERA) CYCLE C
MTHENGA WABWINO (KU
M’DIPITI): MAWU A
MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 19: 28 – 40 (Ngwodala amene
alikudza m’dzina la Ambuye)
Yesu
adatsogolera ophunzira ake kupita ku Yerusalemu. Atafika pafupi ndi midzi ya
Betefage ndi Betaniya, pafupi ndi phiri lotchedwa Phiri la Olivi, adatuma
ophunzira awiri, nawauza kuti, “pitani m’mudzi
mukuwonawo. Mukakangolowamo mukapeza mwanawabulu ali chimangire, amene munthu
sanakwerepo chikhalire. Mukam’masule, nkubwera naye kuno. Wina akakakufunsani
kuti, ‘mukum’masuliranji?’ Mukati, ‘Ambuye ali naye ntchito.”’ Awiriwo adapita,
nakapezadi monga momwe Yesu adaawauzira. Pamene ankamasula mwanawabuluyo, eni
ake adawafunsa kuti, “mukum’masuliranji, mwanawabuluyu?” Iwo adati, “Ambuye ali
naye ntchito.” Tsono adapita naye kwa Yesu, nayamba kuyala zovala zao pa
buluyo, nakwezapo Yesu. Pamene Yesu ankapita, anthu adamchitira ulemu pakuyala
zovala zao mu mseu. Pamene ankayandikira Yerusalemu, pa matsitso a Phiri la
Olivi, gulu lonse la omutsatira aja lidayamba kukondwerera. Adakweza mau,
natamanda Mulungu chifukwa cha ntchito zonse zamphamvu zimene iwo adaziwona.
Adati, “ndi yodala Mfumu imene ilikudza m’dzina la Ambuye. Mtendere Kumwamba,
ulemu kwa Mulungu kumwambamwamba.” Apo Afarisi ena amene adaali m'khamumo
adauza Yesu kuti. “Aphunzitsi, auzeni ophunzira anuwa aleke zimenezi.” Iye adati,
“ndikutitu iwowa akangokhala chete, ifuula ndi miyalayi?”
Mthenga wa
Ambuye................. Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.
PAMBUYO PA
M’DIPITI.
MAWU OYAMBA:
MAWU A BUKU LA MPROFETI YESAYA: YESAYA 50: 04 – 07. (Sindidawabisire nkhope ondinyoza.
Ndikudziwa kuti Chauta sadzandichititsa manyazi.)
Ambuye Chauta
andiphunzitsa zoyenera kunena, kuti ndidziwe mau olimbitsa mtima anthu ofooka.
M’mawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa makutu anga kuti ndimve, monga
amachitira amene akuphunzira. Ambuye Chauta anditsekula makutu, ndipo
sindidawanyoze kapena kuwapandukira. Ndidaperekera msana wanga kwa ondimenya,
ndiponso masaya anga kwa ondimwetula ndevu. Sindidawabisire nkhope ondinyoza
ndi ondithira malovu. Koma kunyoza kwawo sindikuvutika nako, chifukwa Ambuye
Chauta amandithandiza. Nchifukwa chake ndalimbitsa mtima wanga ngati mwala.
Ndikudziwa kuti sadzandichititsa manyazi.
Mawu a
Ambuye…………...Tithokoze Mulungu.
NYIMBO YA SALIMO: SALIMO
22: 08 – 09, 17 – 18, 19 – 20, 23 – 24.
Mulungu wanga,
Mulungu wanga, mwandisiyiranji?
Onse ondiwona
amandiseka,
Amandikwenzulira
ndi kupukuta mitu two.
Amati, “unkadalira
Chauta, Chauta yemweyo akupulumutse.
Akulanditsetu
tsono, popeza kuti amakukonda.”
Mulungu wanga,
Mulungu wanga, mwandisiyiranji?
Anthu ankhanza
andizinga ngati mimbulu.
Aboola manja
anga ndi mapazi anga.
Mafupa anga
akuwonekera, koma anthu aja akungondiyang’anitsitsa,
Akukondwera
poona kuti ndikuvutika.
Mulungu wanga,
Mulungu wanga, mwandisiyiranji?
Agawana zovala
zanga, ndipo achitira malaya anga maere.
Koma Inu Chauta
musakhale kutali.
Inu, mphamvu
zanga, fulumirani kudzandithandiza.
Mulungu wanga,
Mulungu wanga, mwandisiyiranji?
Ndidzasimbira
abale anga za dzina lanu.
Ndidzatamanda
dzina lanu pa msonkhano wa anthu anu.
Ndidzati, ‘Inu
omvera Chauta, mtamandeni Iye.
Inu nonse ana a
Yakobe mlemekezeni Iye,
inu nonse ana a
Israele, mchitireni Iye ulemu.’
Mulungu wanga,
Mulungu wanga, mwandisiyiranji?
MAWU ACHIWIRI A
M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YA PAULO WOYERA KWA AFILIPI: AFILIPI 02: 06 –
11. (Ali munthu choncho adadzichepetsa, koma Mulungu adamkweza kopambana.)
Abale, Yesu
Khristu anali ndi umulungu chikhalire, komabe sadayese kuti kulingama ndi
Mulungu ndi chinthu choti achigwiritsitse. Koma adadzitsitsa kotheratu
pakudzitengera umphawi wa kapolo, ndi kukhala munthu monga anthu onse. Ali
munthu choncho adadzichepetsa, adakhala womvera mpaka imfa, imfa yake
yapamtanda. Chifukwa cha chimenechi Mulungu adamkweza kopambana, nampatsa dzina
lopambana dzina lina lililonse. Adachita zimenezi kuti pakumva dzina la Yesu,
zolengedwa zonse kumwamba, pansi pano ndi pansi pa dziko, zidzagwade pansi
mopembedza. Zonse zidzavomereze poyera kuti, “Yesu Khristu ndi Ambuye,” ndipo
pakutero zilemekeze Mulungu Atate.
Mau a Ambuye.................................Tithokoze
Mulungu.
NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – AFILIPI
02: 08 – 09.
Ulemerero ndi
mayamiko kwa Inu, Khristu!
Ambuye,
adadzichepetsa, adakhala womvera mpaka imfa, imfa yake yapamtanda. Nchifukwa
chake chimene Mulungu adamkweza kopambana nampatsa dzina lopambana dzina lina
lililonse.
Ulemerero ndi
mayamiko kwa Inu, Khristu!
MTHENGA WABWINO: KUSAUKA KWA
YESU KHRISTU AMBUYE ATHU MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 22: 14 –– 23:56
W. – Wowerenga.
Y. – Yesu.
M. – Munthu.
A. – Anthu ena.
1. YESU ADACHITA PHWANDO LA
PASAKA NAPANGA UKARISTIA.
W. Nthawi itakwana, Yesu
adakakhala podyera pamodzi ndi atumwi ake aja. Tsono adawauza kuti:
Y. Ndafunitsitsa kudya phwando
ili la Pasaka pamodzi ndi inu ndisanayambe kumva zowawa. Pakuti kunena zoona,
sindidzadyanso konse Pasaka, mpaka Pasakayi itadzafika pake penipeni mu Ufumu
wa Mulungu.
W. Atatero Yesu adatenga chikho,
ndipo atathokoza Mulungu adati:
Y. Kwayani, imwani nonsenu.
Ndithu ndikunenetsa kuti kuyambira tsopano sindidzamwanso konse chakumwa cha
mtengo wamphesa, mpaka Mulungu atadzakhazikitsa ufumu wake.
W. Kenaka Yesu adatenga mkate,
nathokoza Mulungu, nkuunyemanyema, nagawira ophunzira aja, ndipo adati:
Y. Ili ndi thupi langa limene
likuperekedwa chifukwa cha inu muzichita zimenezi kuti muzindikumbukira.
W. Atatha kudya, adawapatsanso
chikho, nati:
Y. Chikhochi ndi chipangano
chatsopano chimene magazi anga, omwe akukhetsedwa chifukwa cha inu,
akuchitsimikizira. Koma ndithudi wondipereka kwa adani akudya nane pamodzi
pompano. Mwana wa Munthu akukaphedwadi, monga momwe Mulungu adazikonzeratu
kale. Komabe ali ndi tsoka munthu amene akukapereka Mwana wa Munthuyo.
W. Apo onse adayamba kumafunsana
kuti:
A. Kodi ndani mwa ife angachite
zotere?
W. Tsono ophunzira aja adayamba
kutsutsana kuti:
A. Kodi mwa ife amati wamkulu
ndani?
W. Yesu adawauza kuti:
Y. Pakati pa anthu akunja,
mafumu amadyera anthu ao masuku pa mutu, ndipo amene amawaonetsa mphamvu zao,
amatchedwa mfulu zopatsa. Koma pakati pa inu zisamatero ai. Kwenikweni wamkulu
mwa inu azikhala ngati wamng'ono mwa onse, ndipo mtsogoleri azikhala ngati
wotumikira. Kodi wamkulu ndani? Ndi amene alikudya, kapena amene akumtumikira?
Si amene alikudyayo nanga? Koma Ine ndili pakati panu ngati wotumukira. Inu
ndinu amene mwakhala ndi Ine pa masautso anga onse. Nchifukwa chake, monga
Atate anga adandipatsa ufumu, Inenso ndikukupatsani ufumu. Ndikadzalowa mu
ufumu wanga, muzidzadya ndi kumwa pamodzi nane, ndipo mudzakhala pa mipando
yachifumu nkumaweruza mafuko khumi ndi awiri a Israele. Simoni, Simoni,
chenjera! Mulungu walola Satana kuti akupeteni nonse ngati tirigu. Koma Ine
ndakupempherera, kuti usaleke kundikhulupirira. Ndipo iweyo utatembenuka mtima,
ukawalimbitse abale akowa.
W. Apo Petro adati:
M. Ambuye, ndili wokonzeka
kupita nanu ku ndende, ngakhale kufa kumene.
W. Koma Yesu adamuyankha kuti:
Y. Ndikukuuza, iwe Petro, kuti
lero lomwe lino, tambala asanalire, ukhala utandikana katatu kuti Ine
sundidziwa.
W. Yesu adawafunsa kuti:
Y. Nthawi ina ndidaakutumani
opanda thumba la ndalama, kapena thumba lapaulendo, kapenanso nsapato. Kodi
pamene paja mudaasowapo kanthu?
W. Iwo adati:
A. Iyai.
W. Yesu adawauza kuti:
Y. Koma tsopano amene ali ndi
thumba la ndalama, asalisiye. Chimodzimodzinso thumba lake lapaulendo. Ndipo
amene alibe lupanga, agulitse mwinjiro wake nkugula lupanga. Ndithu
ndikunenetsa kuti ziyenera kuchitikadi mwa Ine zimene Malembo adanena kuti, “Ankamuyesa
mmodzi mwa anthu ophwanya malamulo.” Ndipo zonse zimene zidalembedwa za Ine
zikuchitikadi.
W. Ophunzirawo adati:
A. Ambuye, awa malupanga, tili
nawo kale awiri.
W. Yesu adawauza kuti:
Y. Chabwino. basi.
Kanyimbo
2. YESU ADAKAPEMPHERA KU MUNDA
WA GETSEMANI.
W. Pambuyo pake Yesu adatuluka
mu mzinda napita ku Phiri la Olivi monga adaazolowera. Ndipo ophunzira ake
adapita naye. Pamene adafika kumeneko, Yesu adawauza kuti:
Y. Pempherani, kuti mungagwe
m'zokuyesani.
W. Tsono adapatukana nawo
kadera, kutalika kwake ngati pamene mwala ungafike munthu atauponya. Apo
adagwada pansi nayamba kupemphera. Adati:
Y. Atate, ngati mukufuna,
mundichotsere chikho chamasautso chi. Komabe muchite zimene mukufuna Inu, osati
zimene ndikufuna Ine ai.
W. Pamenepo mngelo wochokera
Kumwamba adamuwonekera namlimbitsa mtima. Koma Yesu adavutikabe koopsa mu
mtima, nkumapemphera kolimba kuposa kale. Ndipo thukuta limene linkadza linali
ngati madontho akuluakulu a magazi ogwera pansi. Atapemphera, adaimirira napita
kwa ophunzira ake. Adawapeza ali m'tulo chifukwa cha chisoni, ndipo adawafunsa
kuti:
Y. Bwanji mukugona? Dzukani ndi
kumapemphera, kuti mungagwe m'zokuyesani.
W. Yesu akulankhula choncho,
padabwera khamu la anthu. Amene ankawatsogolera anali Yudasi, mmodzi mwa
ophunzira khumi ndi awiri aja. Iyeyu adadza pafupi ndi Yesu kuti amumpsompsone.
Koma Yesu adamufunsa kuti:
Y. Yudasi, mongadi ukupereka
Mwana wa Munthu kwa adani pakumumpsompsona?
W. Ophunzira amene anali pafupi
ndi Yesu ataona zimene zinali kuchitika, adafunsa Yesu kuti:
A. Ambuye, kodi tiwateme ndi
lupanga?
W. Apo m’modzi mwa iwo adatemadi
wantchito wa mkulu wa ansembe onse, mpaka kumusenga khutu la ku dzanja lamanja.
Koma Yesu adati:
Y. Basi, lekani zimenezi.
W. Atatero adakhudza khutu la
munthuyo namchiritsa. Kenaka Yesu adalankhula nawo onse amene adaabwera kudzamugwira,
akulu a ansembe ndi atsogoleri a alonda a ku Nyumba ya Mulungu, ndiponso akulu
a Ayuda. Adawafunsa kuti:
Y. Bwanji mwachita kunditengera
malupanga ndi zibonga ngati kuti ndine chigawenga? Tsiku ndi tsiku ndidaali
nanu m’Nyumba ya Mulungu, inuyo osandigwira. Koma ino ndi nthawi yanu ndiponso
ya mphamvu za mdima.
Kanyimbo.
3. ANTHU AJA ADAPITA NDI YESU KU
BWALO LA AYUDA.
W. Anthu aja adamugwira Yesu,
napita naye ku nyumba ya mkulu wa ansembe onse. Petro ankawatsatira chapatali.
Iwo adasonkha moto m'kati mwa bwalo la nyumbayo, nakhala pansi pamodzi. Petro
nayenso adakakhala pakati pao. Mtsikana wina wantchito adamuwona atakhala nao
pamotopo. Adamuyang'anitsitsa, nati:
M. Awansotu anali naye.
W. Koma Petro adakana, adati:
M. Mai iwe, sindimdziwa ameneyu,
W. Patapita kanthawi pang'ono,
munthu wina pomuwona adati:
M. Akulu inu, ndinunso mmodzi
mwa iwo aja.
W. Koma Petro adati:
M. Munthu iwe, ai ndithu
sindine.
W. Patapita ngati ora limodzi,
munthu winanso adanenetsa kuti:
M. Ndithudi akulu awanso anali
naye, pakuti ndi a ku Galileya.
W. Koma Petro adati:
M. Munthu iwe, sindikuzidziwa
zimene ukunenazi.
W. Ndipo pompo, akulankhulabe,
tambala adalira. Ambuye adacheuka nayang'ana Petro. Pamenepo Petro adakumbukira
mau aja amene Ambuye adaamuuza kuti, ‘lero lomwe lino, tambala asanalire,
ukhala utandikana katatu.’ Pamenepo adatuluka, nakalira kwambiri chifukwa cha
chisoni chachikulu. Tsono anthu amene ankalonda Yesu aja adayamba kumseka ndi
kumammenya. Adammanga nsalu
m'maso nkumamufunsa kuti:
A. Lota, wakumenya ndani?
W. Ndipo adamnenanso mau ena
ambiri achipongwe. Kutacha, a m'Bungwe Lalikulu la Ayuda adasonkhana, ndiye
kuti akulu a ansembe ndi aphunzitsi a Malamulo. Adatenga Yesu napita
naye ku Bwalo lao. Adamuuza kuti:
A. Ngati ndiwe Mpulumutsi
wolonjezedwa uja, utiwuze mosabisa.
W. Koma Iye adawayankha kuti:
Y. Ngakhale ntakuuzani,
simungandikhulupirire konse, ndipo nditakufunsani funso, inu simungaliyankhe.
Koma kuyambira tsopano Mwana wa Munthune ndidzakhala ku dzanja lamanja la
Mulungu Wamphamvuzonse.
W. Apo onse aja adati:
A. Tsono ndiye kutitu ndiwe
Mwana wa Mulungu, ati?
W. Yesu adati:
Y. Mwanena nokha kuti ndine
amene.
W. Pamenepo iwo aja adati:
A. Tikufuniranji umboni wina?
Tadzimvera tokha mau akewa.
Kanyimbo
4. AKULU A AYUDA ADAPITA NAYE
YESU KWA PILATO.
W. Gulu lonse lija lidanyamuka
nkupita naye Yesu kwa Pilato. Iwo adayamba kuneneza Yesu kuti:
A. Munthu uyu tidampeza
akusokeza anthu a mtundu wathu. Amatiletsa kuti tisamakhome msonkho kwa Mfumu
ya ku Roma. Amanenanso kuti ati Iyeyu ndi Mpulumutsi wolonjezedwa uja ndiponso
mfumu.
W. Pilato adafunsa Yesu kuti:
M. Kodi iwe, ndiwe Mfumu ya
Ayuda?
W. Yesu adati:
Y. Mwanena nokha.
W. Pamenepo Pilato adauza akulu
a ansembe ndi anthu onse aja kuti:
M. Sindikumpeza mlandu munthuyu.
W. Koma iwo adaumirira nati:
A. Ameneyu amautsa mitima ya
anthu ndi zimene amaphunzitsa m'dziko lonse la Yudeya. Adayambira ku Galileya,
mpaka konse kuno.
W. Pamene Pilato adamva
zimenezi, adawafunsa kuti:
M. Kodi munthuyu ndi wa ku
Galileya?
W. Tsono atamva kuti
ngwochokeradi ku dera limene Herode amalamulira, adamtumiza kwa Herodeyo, amene
nayenso anali m' Yerusalemu masiku omwewo. Herode poona Yesu, adakondwa
kwambiri, chifukwa ankamva za Iye, mwakuti kwa nthawi yaitali ankafuna
atamuwona. Ankayembekeza kuti aone Yesu akuchita chozizwitsa china. Herode
adamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sadamuyankhe kanthu. Akulu a ansembe ndi
aphunzitsi a Malamulo adaimirira pomwepo nkumaneneza Yesu kwambiri. Herode
pamodzi ndi asilikali ake adayamba kumseka Yesu ndi kumamnyoza. Adamuveka
chovala chachifumu, namubwezera kwa Pilato. Tsiku lomwelo Herode ndi Pilato
adayamba kuyanjana, chonsecho kale ankadana. Pilato adasonkhanitsa akulu a
ansembe ndi akulu a Ayuda ndi anthu wamba. Adawauza kuti:
M. Mwadzampereka munthuyu kwa
ine kuti ndi munthu wosokoneza anthu. Ndipo onani, ine ndamufunsa pamaso panu,
koma sindikumpeza mlandu pa zonse zimene mukumnenezazi.
Herode yemwe sadampeze mlandu,
nchifukwa chake wamubweza kwa ife. Ameneyu sadachite kanthu koyenera kumuphera.
Motero ndingomukwapula kenaka nkumumasula.
W: Pilatoyo ankayenera
kuwamasulira mkaidi m’modzi pa nthawi ya chikondwerero cha Pasaka. Koma anthu
onse aja adayamba kufuula pamodzi kuti:
A. Mchotseni ameneyu,
mutimasulire Barabasi.
W. Barabasi anali atamponya m’ndende
chifukwa cha kuyambitsa chipolowe mu mzinda, ndiponso kupha munthu. Pilato
adafuna kumasula Yesu, motero adakakamba nawonso anthu aja. Koma iwo
adafuulirafuulira kuti:
A. Mpachikeni! Mpachikeni!
W. Pilato adawafunsa kachitatu
kuti:
M. Koma wachimwanji Iyeyu?
Sindikumpeza mlandu woyenera kumuphera. Motero ndingomukwapula kenaka
ndimmasula.
W. Koma iwo adamuumiriza mokweza
mau kuti Yesu apachikidwe. kufuula kwao kunkakulirakulira. Tsono Pilato
adagamula kuti zimene anthu aja ankapempha zichitike. Adawamasulira munthu
amene ankamupempha uja, amene adaaponyedwa m’ndende chifukwa cha chipolowe ndi
kupha munthu. Koma Yesu adampereka kwa iwo kuti akamchite zimene ankafuna.
Kanyimbo.
5. ASIRIKALI ADAPITA NAYE KU
GOLOGOTA KUTI AKAMPACHIKE PA MTANDA.
W. Asilikali adamtenga Yesu
napita naye kuti akampachike. Pa njira adagwira munthu wina wa ku Kirene, dzina
lake Simoni. Iye ankachokera ku midzi. Adamsenzetsa mtanda wa Yesu kuti
aunyamule, azitsatira pambuyo pa Yesuyo. Anthu ambirimbiri ankamutsatira.
Pakati pao panalinso akazi amene ankadzigunda pa chifuwa ndi chisoni nkumalira
chifukwa cha Iye. Koma Yesu adawacheukira nawauza kuti:
Y. Inu azimai a ku Yerusalemu,
musandilire Ine ai, koma mulire chifukwa cha inu nomwe ndi ana anu. Pakuti
masiku akubwera pamene anthu azidzati, “ngodala azimai ouma, azimai osabala,
azimai amene sadayamwitseko mwana.” Nthawi imeneyo adzapempha mapiri kuti, “tigwereni,”
ndiponso magomo kuti, “tiphimbeni.” Pakuti ngati mtengo wauwisi auchita
zimenezi, nanga mtengo wouma ndiye adzauchita zotani?
W. Asilikali aja adaatenganso
anthu ena awiri, amene anali zigawenga kuti akaphedwe pamodzi ndi Yesu. Pamene
adafika ku malo otchedwa Chibade cha Mutu, adapachika Yesu komweko pa mtanda.
Komwekonso adapachika zigawenga zija, china ku dzanja lamanja, china ku dzanja
lamanzere. Yesu adati:
Y. Atate, muwakhululukire
anthuwa, chifukwa sakudziwa zimene akuchita.
W. Iwo aja adagawana zovala zake
pakuchita maere. Anthu ena onse adaimirira pomwepo nkumaonerera. Komanso akulu a
Ayuda ankamunyodola nkumanena kuti:
A. Adapulumutsa ena,
adzipulumutse yekha ngati ndiyedi Mpulumutsi uja amene Mulungu adamsankha.
W. Nawonso asilikali adayamba
kumseka. Adadza pafupi ndi Iye, nampatsa vinyo wosasa kuti amwe. Adati:
A. Ngati ndiwedi mfumu ya Ayuda,
dzipulumutse wekha.
W. Pamwamba pa mtanda panali
kalata yolembedwa m’Chigriki, m’Chilatini, ndi m’Chiyuda. Mau ake anali akuti, “Uyu
ndi mfumu ya Ayuda.” Chigawenga chimodzi chimene chidaapachikidwa nao,
chidayamba kunyoza Yesu nkumanena kuti:
M. Ha! Kodi iwe sindiwe
Mpulumutsi Wolonjezedwa uja? Udzipulumutse wekha ndi ife tomwe.
W. Koma mnzake uja adamdzudzula,
adati:
M. Kodi iwe, suwopa ndi Mulungu
yemwe, chidziwirecho kuti nawenso ukulandira chilango chomwechi? Tsonotu ife
zikutiyeneradi zimenezi, tikulandira zolingana ndi zimene tidachita. Koma awa
sadachite cholakwa chilichonse.
W. Ndipo adati:
M. Inu, mukandikumbikire
mukakafika mu Ufumu wanu.
W. Yesu adamuyankha kuti:
Y. Ndithu ndikunenetsa kuti lero
lomwe lino ukhala nane ku Malo a Chisangalalo, Kumwamba.
W. Nthawi itakwana ngati 12
koloko masana, padaagwa mdima pa dziko lonse mpaka pa 3 koloko, dzuwa litangoti
bi kuda. Pamenepo chinsalu chotchinga chija cha m’Nyumba ya Mulungu chidang’ambika
pakatimpakati. Tsono Yesu adanena mokweza mau kuti:
Y. Atate ndikupereka mzimu wanga
m’manja mwanu.
W. Atanena zimenezi,
adatsirizika.
“Onse agwade ndikukhala chete
kwa kanthawi.”
Kanyimbo
W. Mkulu wa asilikali ataona
zimene zidaachitikazo, adatamanda Mulungu, adati:
M. Ndithudi munthuyu adaalidi
wosalakwa konse.
W. Anthu onse amene adaasonkhana
kudzaonerera zimene zinkachitikazo, ataona zonsezi, adabwerera kwao akudzigunda
pa chifuwa ndi chisoni. Anthu onse amene ankadziwana ndi Yesu, ndiponso azimai
amene adaamtsatira kuchokera ku Galileya, adaima patali nkumaona zimenezi.
Panali munthu wina, dzina lake Yosefe, wa ku Arimatea, mudzi wina wa Ayuda.
Anali munthu wabwino ndi wolungama, ndipo anali wa m’Bungwe Lalikulu la Ayuda.
Komatu sankavomereza zimene anzake a m'Bungweli ankapangana, iye ankayembekeza
kudza kwa Ufumu wa Mulungu. Iyeyu adapita
kwa Pilato kukapempha mtembo wa Yesu. Tsono adautsitsa naukulunga m’nsalu
yoyera yabafuta, nkuuika m’manda. Mandawo anali asanaikemo munthu wina
aliyense. Linali tsiku la chikonzero, tsiku la Sabata likuti liziyamba kumene.
Azimai aja amene adaabwera ndi Yesu kuchokera ku Galileya, adatsatira Yosefe,
naona manda ndi m’mene adaaikira mtembo wa Yesu. Kenaka adabwerera nakayamba
kukonza zonunkhira ndiponso mafuta abwino. Tsono pa tsiku la Sabata adapumula
malinga ndi Malamulo a Mose.
Mthenga wa Ambuye......Ulemu kwa
Inu Ambuye Yesu Khristu.
#Pax_et_Gaudium_in_Domino.
Facebook:
https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295
Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/