LAMULUNGU LA PASAKA –
CYCLE C
“Yesu Khristu ndiye
moyo wathu.”
MAWU OYAMBA: MAWU A BUKU LA NTCHITO ZA ATUMWI: NTCHITO 10: 34, 37 – 43. (Adaonekera kwa ife,
amene tinkadya ndi kumwa naye pamodzi atauka kwa akufa.)
Petro adayamba
kulankhula, adati, "Zoonadi ndazindikira tsopano kuti Mulungu alibe
tsankho. Mukudziwa zimene zidachitika ku Yudeya konse, kuyambira ku Galileya
pambuyo pa nthawi imene Yohane ankalalika za ubatizo wake. Mukudziwa za Yesu wa
ku Nazarete, kuti Mulungu adaamudzoza ndi Mzimu Woyera nampatsa mphamvu. Tsono
popeza kuti Mulungu anali naye, adapita ponseponse akuchita ntchito zabwino ndi
kuchiritsa onse osautsidwa ndi Satana. Ife ndife mboni za zonse zimene Iye
adachita mu Yerusalemu ndi m'dziko lonse la Ayuda. Iwo adamupha pakumpachika pa
mtanda. Komabe mkucha wake Mulungu adamuukitsa kwa akufa, nalola kuti aonekere
poyera. Sadaonekere kwa anthu onse ai, koma kwa mboni zimene Mulungu
adazisankhiratu. Ndiye kuti adaonekera kwa ife, amene tinkadya ndi kumwa naye
pamodzi atauka kwa akufa. Ndipo adatilamula kuti tikalalikire anthu onse, ndi
kuchita umboni kuti Iyeyo ndiye amene Mulungu adamsankha kukhala Woweruza anthu
amoyo ndi akufa omwe. Aneneri onse adamchitira umboni, ndi kunena kuti chifukwa
cha dzina lake, Mulungu adzakhululukira machimo a munthu aliyense wokhulupirira
Iyeyu.”
Mawu a
Ambuye…………...Tithokoze Mulungu.
NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 118: 01 – 02, 16 – 17, 22 – 23.
Lero ndiye
tsiku limene Chauta adalipanga. Tiyeni tikondwe ndi kusangalala pa tsiku
limeneli. / Alleluia, alleluia, alleluia!!
Thokozani
Chauta chifukwa ngwabwino,
ndipo chikondi
chake nchamuyaya.
Aisraele anene
kuti,
“Chikondi
chake nchamuyaya.”
Lero ndiye
tsiku limene Chauta adalipanga. Tiyeni tikondwe ndi kusangalala pa tsiku
limeneli. / Alleluia, alleluia, alleluia!!
Dzanja lamanja
la Chauta lapambana,
dzanja lamanja
la Chauta limagonjetsa mwamphamvu.”
Sindidzafa,
ndidzakhala moyo,
ndipo
ndidzalalika ntchito za Chauta.
Lero ndiye
tsiku limene Chauta adalipanga. Tiyeni tikondwe ndi kusangalala pa tsiku limeneli.
/ Alleluia, alleluia, alleluia!!
Mwala umene
amisiri omanga nyumba adaukana,
womwewo
wasanduka mwala wapangodya.
Chauta ndiye
amene wachita zimenezi,
zimenezi
nzodabwitsa pamaso pathu.
Lero ndiye
tsiku limene Chauta adalipanga. Tiyeni tikondwe ndi kusangalala pa tsiku
limeneli. / Alleluia, alleluia, alleluia!!
MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YA PAULO WOYERA
KWA AKOLOSE: AKOLOSE 03: 01 – 04
(Muzifunafuna za Kumwamba, osati zapansipano.)
Tsono ngati
mudaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mtima pa zinthu za Kumwamba, kumene
Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu. Muzifunafuna za Kumwamba, osati
zapansipano. Pakuti kunena za moyo wakalewo mudafa, ndipo moyo wanu watsopano
ndi wobisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu. Khristu ndiye moyo wanu weniweni
tsopano, choncho pamene Iye adzaonekerenso, inunso mudzaonekera mu ulemerero
pamodzi naye.
Mau a Ambuye.................................Tithokoze
Mulungu.
NYIMBO YA MTHENGA WABWINO
Alleluia,
Alleluia!!
Kankhosa kathu
ka Pasaka ndiye Yesu Khristu amene waphedwa ngati nsembe. Tiyeni tsopano,
tichite chikondwerero choyamikira Ambuye.
Alleluia,
Alleluia!!
MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA:
YOHANE 20: 01 – 09 (Yesu
adzayenera kuuka kwa akufa.)
Pa tsiku
lotsatira Sabata ya Ayuda, m’mamaŵa ndithu kudakali kamdima, Maria wa ku
Magadala adadza ku manda a Yesu. Adaona kuti chimwala chija chachotsedwa kale
pa khomo la mandawo. Choncho adathamanga nakafika kwa Simoni Petro, ndi kwa
wophunzira wina uja amene Yesu ankamukonda kwambiri. Adaŵauza kuti, “Aŵachotsa
Ambuye m'manda muja, ndipo sitikudziŵa kumene akaŵaika.” Pamenepo Petro ndi
wophunzira wina uja adatuluka napita ku manda. Onse aŵiri adathamanga pamodzi,
koma wophunzira wina uja adathamanga kopambana Petro, nkuyambira ndiye kufika
kumandako. Adaŵerama naona nsalu zija zili chikhalire, koma iye sadaloŵemo.
Simoni Petro atafika akumutsatira, adaloŵa m'mandamo. Adaona nsalu zija zili
chikhalire, ndiponso kansalu kamene kanali kumutu kwake. Kansaluko sikanali
pamodzi ndi nsalu zina zija, koma padera pakokha, kali chipindire. Pamenepo
wophunzira wina uja, amene adaayambira kufika ku manda, nayenso adaloŵa; ndipo
ataona zimenezi, adakhulupirira. Mpaka nthaŵi imeneyo iwo aja anali asanamvetse
Malembo akuti Yesu adzayenera kuuka kwa akufa.
Mthenga
wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.
#Pax_et_Gaudium_in_Domino.
Facebook:
https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295
Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/
No comments:
Post a Comment