Saturday, January 22, 2022

LAMULUNGU LA 03 PA CHAKA C


LAMULUNGU LA 03 PA CHAKA C (Mau anu ndi opatsa moyo wosatha.)

MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA NEHEMIYA: NEHEMIYA 08: 02 – 06, 08 – 10. (Ezara adawerenga buku la Malamulo, ndipo adatanthauzira mauwo kuti anthu amvetse bwino.)

Pamenepo Ezarayo adabwera ndi buku la Malamulo, pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, ku msonkhano wa amuna ndi akazi ndi ana amene ankatha kumvetsa zinthu bwino. Tsono Ezara adawerenga bukulo atayang’ana bwalo la chipata cha madzi, kuyambira m’mamawa mpaka pa masana, pamaso pa amuna ndi akazi omwe, ndiponso onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino. Ndipo anthu onsewo ankatchera makutu kuti amve zowerengazo. Mlembi Ezara adaaimirira pa nsanja yamitengo, imene anthuwo adaamanga chifukwa cha msonkhanowo. Ku dzanja lake lamanja kudaaimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseiya. Kudzanja lake lamanzere kudaaimirira Pedaya, Misaele, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndiponso Mesulamu. Tsono ataimirira pansanjapo, Ezara adafutukula buku, anthu onse akupenya. Pomwepo anthu onse adaimirira. Kenaka Ezara adati, “atamandike Chauta, Mulungu wamkulu!” Ndipo anthu onse adakweza manja nayankha kuti, “inde momwemo, inde momwemo.” Pambuyo pake adaweramitsa mitu pansi ndipo adapembedza Chauta ali chizyolikire. Aleviwo adawerenga buku la Malamulo a Mulungu momveka bwino, ndipo adatanthauzira mauwo kuti anthu amvetse bwino. Tsono bwanamkubwa Nehemiya, pamodzi ndi Ezara wansembe ndi Mphunzitsi wa malamulo, kudzanso Alevi amene ankaphunzitsa anthu, adauza anthu onse aja kuti, “lero ndi tsiku loyera kwa Chauta, Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Ndiye kuti anthu onse ankalira atamva mau a Malamulowo. Tsono Nehemiya adapititriza nati, “kazipitani, mukachite phwando ku nyumba, kenaka muwapetseko anzanu amene sadakonze kanthu. Pakuti lero ndi tsiku loyera kwa Chauta, Mulungu wathu. Tsono musakhale ndi chisoni, popeza kuti chimwemwe chimene Chauta amakupatsani, chimakulimbikitsani.”

Mawu a Ambuye…Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------------------------------------------------------------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 19: 08 – 10, 15.

 

Mau anu ndi mzimu, Ambuye, ndipo ndi moyo.

 

Mau a Chauta ngangwiro,

Amapatsa munthu moyo watsopano,

Umboni wa Chauta ndi wokhulupirika,

Umawapatsa nzeru amene alibe.

 

Mau anu ndi mzimu, Ambuye, ndipo ndi moyo.

 

Malangizo a Chauta ndi olungama,

Amasangalatsa mtima,

Malamulo a Chauta ndi olungama,

Amapatsa mtima womvetsa.

 

Mau anu ndi mzimu, Ambuye, ndipo ndi moyo.

 

Kuwopa Chauta ndiye chinthu changwiro,

Chimakhala mpaka muyaya,

Chiweruzo cha Chauta nchoona,

Ncholungama nthawi zonse.

 

Mau anu ndi mzimu, Ambuye, ndipo ndi moyo.

 

Mau anga ndi maganizo anga,

Avomerezeke pamaso panu,

Inu Chauta, thanthwe langa,

Ndi Mpulumutsi wanga.

 

Mau anu ndi mzimu, Ambuye, ndipo ndi moyo.

----------------------------------------------------------------------------------------------------------------

MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 1 AKORINTO 12: 12 – 21, 27. (Inuyo nonse pamodzi ndinu thupi la Khristu, ndipo aliyense mwa inu ndi chiwalo cha thupilo.)

Abale, Khristu ali ngati thupi limene lili ndi ziwalo zambiri. Ngakhale ziwalozo nzambiri, komabe thupilo ndi limodzi lokha. Pajatu ngakhale ndife Ayuda kapena a mitundu ina, akapolo kapena mfulu, tidabatizidwa mwa Mzimu Woyera mmodzimodzi kuti tikhale thupi limodzi. Ndipo tonse tidalandira nao Mzimu Woyera mmodzi yemweyo. Thupitu si chiwalo chimodzi chokha ai, koma lili ndi ziwalo zambiri. Nanga phazi litanena kuti, “poti sindine dzanja, ndiye kuti sindine chiwalo cha thupi”, kodi silikhala chiwalo cha thupi chifukwa cha chimenecho? Nanga khutu litanena kuti, “poti sindine diso, ndiye kuti sindine chiwalo cha thupi”, kodi silikhala chiwalo cha thupi chifukwa cha chimenecho? Kodi thupi lonse likadakhala diso lokha, bwenzi munthu akumva bwanji? Kapena thupi lonse likadakhala khutu lokha, bwenzi munthu akuninkhiza bwanji? Koma m’mene ziliri Mulungu adaika chiwalo chilichonse pamalo pake m’thupi, monga momwe adafunira. Ziwalo zonse zikadangokhala chiwalo chimodzi, sipakadakhala thupi konse. Komatu ziwalo nzambiri, ngakhale thupi ndi limodzi lokha. Motero diso silingauze dzanja kuti, “ndilibe nawe ntchito.” Ndiponso mutu sungauze mapazi kuti, “ndilibe nanu ntchito.” Tsono inuyo nonse pamodzi ndinu thupi la Khristu, ndipo aliyense mwa inu ndi chiwalo cha thupilo.

Mawu a Ambuye…Tithokoze Mulungu.

---------------------------------------------------------------------------------------------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO: LUKA 04: 18.

Alleluia, Alleluia – Ambuye wandidzoza kuti ndikalalikire amphawi Uthenga Wabwino. Wandituma kuti ndikalengeze kwa am’ndende kuti adzamasulidwa. – Alleluia, Alleluia.

-----------------------------------------------------------------------------------------------------------------MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 01: 01 – 04; 04: 14 – 21. (Lero zachitikadi zimene adaaneneratu Malembo amene mwawamva.)

Ateofilo olemekezeka, anthu ambiri adayesa kulongosola mbiri ya zinthu zimene zidachitika pakati pathu. Iwo adalemba zimene adaatisimbira anthu oziwona chamaso kuyambira pachiyambi pake, nakhala akuzilalika. Tsono popeza kuti inenso ndalondola mosamala kwambiri m’mene zonsezo zidaachitikira kuyambira pa chiyambi, ndaganiza kuti nkwabwino kuti ndikulembereni zimenezo mwatsatanetsatane. Ndatero kuti mudziwe ndithu kuti zimene adakuphunzitsanizo nzoonadi. Yesu adabwereranso ku Galileya ndi mphamvu za Mzimu Woyera. Mbiri yake idawanda kuzungulira dziko lonseli. Ankaphunzitsa m’nyumba zao zamapemphero, ndipo anthu onse ankamutamanda. Nthawi ina Yesu adafika ku Nazerete kumene adaaleredwa. Ndipo pa tsiku la Sabata adalowa m’nyumba yamapemphero, monga adazolowera, naimirira kuti awerenge mau. Adampatsa buku la mneneri Yesaya. Tsono Iye adafutukula bukulo, napeza pamene padalembedwa kuti, “Mzimu wa Chauta wadzaza mwa Ine. Wandidzoza kuti ndikalalikire amphawi Uthenga Wabwino. Wandituma kuti ndikalengeze kwa am’ndende kuti adzamasulidwa, ndi kwa akhungu kuti adzapenyanso. Wandituma kuti ndikawapatse ufulu anthu osautsidwa, ndi kukalalika za nthawi imene Ambuye adzapulumutsa anthu ao.” Yesu adatseka bukulo nkulipereka kwa mtumiki wa nyumba yamapemphero, nakhala pansi. Anthu onse amene adaasonkhana m’nyumbamo ankangomupenyetsetsa. Tsono Yesu adawauza kuti, “lero zachitikadi zimene adaaneneratu Malembo amene mwamvawa.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Mkatolikamw

 

 

No comments:

Post a Comment

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...