Saturday, January 15, 2022

LAMULUNGU LA 02 PA CHAKA C


 LAMULUNGU LA 02 PA CHAKA C

(Ophunzira ake adamkhulupirira)

MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA MPROFETI YESAYA: YESAYA 62: 01 – 05. (Mkwati wamwamuna amakondwerera mkwati wamkazi.)

Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndipo chipulumutso chake chitaoneka ngati muuni woyaka. Iwe Yerusalemu, mitundu ya anthu idzakuwona utapambana pa nkhondo, mafumu ao onse adzaona ulemerero wako. Adzakuitanira dzina latsopano, limene adzakutcha ndi Chauta yemwe. Udzakhala ngati chisoti chaufumu chokongola m’manja mwa Chauta, ngati msangamutu yaulemerero m’manja mwa Mulungu wako. Sudzatchedwanso ‘wosiyidwa’, dziko lako silidzatchedwanso ‘chipululu’. Dzina lako latsopanolo lidzakhala ‘ndikukondwera naye’. Dziko lako lidzatchedwa ‘wokwatiwa mwachimwemwe’, chifukwa choti Chauta akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako. Monga mnyamata amakwatira namwali, chonchonso mmisiri wodzakumanganso adzakukwatira. Monganso mkwati wamwamuna amakondwerera mkwati wamkazi, chonchonso Mulungu adzasangalala nawe.

Mawu a Ambuye…Tithokoze Mulungu.

-----------------------------------------

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 96: 01 – 03, 07 – 10.

Lalikani za ntchito zodabwitsa za Ambuye kwa anthu a m’maiko onse.

Imbirani Chauta nyimbo yatsopano!

Imbirani Chauta, anthu a m’dziko lonse lapansi!

Imbirani Chauta, tamandani dzina lake!

Lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

Lalikani za ntchito zodabwitsa za Ambuye kwa anthu a m’maiko onse.

Lengezani za ulemerero wake,

Kwa anthu a mitundu yonse,

Simbani za ntchito zake zodabwitsa,

Kwa anthu a m’maiko onse.

Lalikani za ntchito zodabwitsa za Ambuye kwa anthu a m’maiko onse.

Tamandani, inu anthu a mitundu yonse,

Vomerezani kuti ulemerero ndi mphamvu, zonse nzake,

Tamandani ulemerero wa dzina la Chauta.

Lalikani za ntchito zodabwitsa za Ambuye kwa anthu a m’maiko onse.

Pembedzani Chauta waulemerero ndi woyera,

Njenjemerani pamaso pake, inu anthu onse a pa dziko lapansi,

Uzani mitundu ya anthu kuti, “Chauta ndiye Mfumu.”

Adzaweruza mitundu yonse ya anthu mwachilungamo.

Lalikani za ntchito zodabwitsa za Ambuye kwa anthu a m’maiko onse.

------------------------------

MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 1 AKORINTO 12: 04 – 11. (Mzimu Woyera mmodzi yemweyo amagawira munthu aliyense monga momwe Iye afuna kumgawira.)

Abale, pali mphatso zamitundumitundu, koma wozipereka ndi Mzimu Woyera mmodzimodzi. Pali njira zosiyanasiyana zotumikira, koma Ambuye amene timawatumikira ndi amodzimodzi. Pali mphamvu zosiyasiyana, koma Mulungu ndi mmodzimodzi amene amagwiritsa ntchito mphamvu zonsezo mwa munthu aliyense. Mzimu Woyera amapatsa munthu aliyense mphatso yakutiyakuti yoti aigwiritse ntchito yopindulitsa anthu onse. Mzimu Woyera yemweyo amapatsa wina mphatso ya kulankhula mau olangiza anthu. Mzimu Woyera yemweyo amapatsa wina mphatso ya kukhulupirira, ndipo Mzimu Woyera mmodzi yemweyo amapatsa wina mphatso ya kuchiritsa matenda. Amapatsa wina mphamvu zochitira zozizwitsa, wina mphatso ya kulalika mau a Mulungu, wina nzeru za kusiyanitsa pakati pa zinthu zochokera kwa Mzimu Woyera ndi zochokera kwina. Amapatsa wina mphatso ya kulankhula zilankhulo zosadziwika, ndipo amapatsa wina mphatso za kutanthauzira zilankhulozo. Amene amachititsa anthu zonsezi ndi Mzimu Woyera mmodzi yemweyo. Amagawira munthu aliyense monga momwe Iye afuna kumgawira.

Mawu a Ambuye…Tithokoze Mulungu.

-----------------------------

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO: 2 ATESALONIKA 02: 14.

Alleluia, Alleluia – Mulungu adakuitanani kudzera mwa Uthenga Wabwino kuti mulandire nao ulemerero wa Ambuye athu Yesu Khristu. – Alleluia, Alleluia.

-------------------------------

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA: YOHANE 02: 01 – 11. (Yesu adaonetsa chizindikiro chake choyambachi m’mudzi wa Kana m’dera la Galileya.)

Kunali Ukwati ku mudzi wa Kana m’dera la Galileya. Amai ake a Yesu anali komweko. Yesu nayenso pamodzi ndi ophunzira ake adaaitanidwa kuukwatiko. Pamene vinyo adatha, amai ake a Yesu adamuuza kuti, “wawathera vinyo.” Yesu adayankha kuti, “Mai kodi mukuti nditani? Nthawi yangatu siinafike.” Apo mai ake adauza anyamata amene ankatumukira kuti, “chilichonse chimene akuuzeni, muchite.” Pamenepo panali mbiya zamwala zisanu ndi imodzi, zimene adaaziikapo chifukwa cha mwambo wa kudziyeretsa wa Ayuda. M’mbiya iliyonse munkalowa madzi okwanira malita zana limodzi kapena kupitirirapo. Tsono Yesu adauza anyamata aja kuti, “dzadzani mbiyazi ndi madzi.” Ndipo adazidzadza mpaka m’milomo. Pambuyo pake adawauza kuti, “tsopano tungani, kaperekeni kwa mkulu wa mphwando.” Iwowo adakaperekadi. Mkulu wa phwandoyo adalawa madzi osanduka vinyoyo osadziwa kumene achokera. (Koma anyamata aja amene adaatunga madziwo ankadziwa.) Tsono mkulu wa mphwandoyo adaitana mkwati, namuuza kuti, “anzanu amapereka vinyo wabwino kwambiri poyamba, kenaka anthu atakhuta, amawapatsa vinyo wokoma pang’ono. Koma inu mwasunga vinyo wabwino kwambiri kufikira tsopano.” Yesu adaonetsa chizindikiro chake choyambachi m’mudzi wa Kana m’dera la Galileya. Pamenepo adaonetsa ulemerero wake, ndipo ophunzira ake adamkhulupirira.

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: Mkatolikamw

No comments:

Post a Comment

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...