LAMULUNGU LACHISANU MU NYENGO YA PASAKA - CYCLE C
(Mukondane
monga momwe Ine ndidakukonderani)
MAWU WOYAMBA: MAWU A M'BUKU LA
NTCHITO ZA ATUMWI; NTCHITO 14: 21 – 27. (Adasonkhanitsa mpingo wonse,
naufotokezera zonse zimene Mulungu adaachita mwa iwo.)
NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 145: 08 – 09, 10 – 11, 12 – 13.
Chauta ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
Wosakwiya msanga, wodzaza ndi
chikondi chosasinthika.
Chauta ndi wabwino kwa onse,
Amachitira chifundo zamoyo zonse
zimene adazilenga.
Ndidzatamanda dzina lanu mpaka
muyaya, Inu Ambuye, Mfumu yanga.
Zamoyo zonse zidzakuthokozani, Inu
Chauta,
Anthu anu onse oyera mtima
adzakutamandani.
Adzalankhula za ulemerero wa ufumu
wanu,
Adzasimba za mphamvu, kutinso
asimbe za ulemerero ndi za ufumu wanu waukulu.
Ndidzatamanda dzina lanu mpaka
muyaya, Inu Ambuye, Mfumu yanga.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
ulamuliro wanu ndi wa pa mibadwo
yonse.
Ndidzatamanda dzina lanu mpaka
muyaya, Inu Ambuye, Mfumu yanga.
MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA:
MAWU A M’BUKU LA CHIVUMBULUTSO; CHIVUMBULUTSO 21: 01 – 05a. (Mulungu adzawapukuta
misozi yonse m’maso mwao.)
Ine Yohane ndidaona thambo latsopano ndi dziko lapansi la tsopano. Paja thambo loyamba lija zinali zitazimilira, ndipo nyanja padalibenso. Tsono ndidaona Mzinda Woyera, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu. Unali wokonzeka ngati mkwati wamkazi wokonzekera mwamuna wake. Ndidamva mawu amphamvu ochokera kumpando wa Chifumu uja. Mauwo adati, “Tsopano malo okhalamo Mulungu ali pakati pa anthu. Iye adzakhala nawo pamodzi, ndipo iwo adzakhala anthu akeake. Mulungu mwini adzakhala nawo, ndipo adzakhala Mulungu wao. Iye adzawapukuta misozi yonse m’maso mwao. Sipadzakhalanso imfa, chisoni, kulira, kapena kumva zowawa. Zakale zonse zapitiratu.” Pamenepo okhala pampando wachifumu uja adati, “Tsopano ndisandutsa zonse kuti zikhale zatsopano.”
Mau a Ambuye.................................Tithokoze Mulungu.
Alleluia, Alleluia!! Ndikukupatsani lamulo latsopano, lakuti muzikondana. Monga momwe Ine ndidakukonderani, inunso muzikondana. Alleluia, Alleluia!!
MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA YOHANE WOYERA; YOHANE 13: 31 – 33a, 34 – 35. (Ndikukupatsani lamulo latsopano, lakuti muzikondana.)
Yudasi atatuluka, Yesu adati, “Tsopano mwana wa Munthu walemekezedwa, ndipo mwa iyeyu Mulungu walemekezedwa. Ngati Mulungu walemekezedwa mwa iyeyu, Mulungu mwini nayenso adzamlemekeza iye, ndipo achita zimenezi tsopano apa. Ana anga, ndili nanube kanthawi pang’ono. Ndikukupatsani lamulo latsopano, lakuti muzikondana. Monga momwe ine ndidakukonderani, inunso muzikondana. Mukamakondana, anthu onse adzadziwa kuti ndinudi ophunzira anga.”
Mthenga
wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.
#Pax_et_Gaudium_in_Domino.
Facebook:
https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295
No comments:
Post a Comment