LAMULUNGU LA 3 MU NYENGO YA LENTI – C
“Mtengo wosabereka adzaudula.”
MAU OYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA EKSODO: EKSODO 3:1-8.13-15 (NDILIPO wandituma).
Mose ankaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina adatenga ziwetozo, nayenda nazo chakuzambwe kwa chipululu, mpaka kukafika ku phiri la Mulungu dzina lake Horebu. Mngelo wa Chauta adamuwonekera ngati malawi a moto umene unkayaka m'chitsamba. Mose atapenya, adaona kuti chitsamba chili moto lawilawi, koma osapsa. Tsono mumtima mwake adati, “ndipita pafupi, kuti ndikaonetsetse zozizwitsa ndikupenyazi. Chifukwa chiyani chitsambacho sichilikupsa?” Chauta ataona kuti Mose akuyandikira, adamuitana m'chitsambamo kuti, “Mose, Mose!” Mose adayankha kuti, “wawa.” Mulungu adati, “usayandikire pafupi. Vula nsapato zakozo, chifukwa malo waimapowo ngoyera.” Adapitirira kunena kuti. “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isaki, Mulungu wa Yakobo.” Pompo Mose adadziphimba kumaso chifukwa adaopa kupenya Mulungu. Kenaka Chauta adati, “ndaona m’mene anthu anga akuzunzikira ku Ejipito. Ndamva kulira kwao kofuna chithandizo, chifukwa cha anthu amene akuwapsinja. Ndikudziwa bwino kuzunzika kwao. Ndabwera kuti ndiwapulumutse kwa Aejipito ndi kuwatulutsa m’dziko limenelo, kuti ndikawalowetse m’dziko lalikulu lachonde. Dziko limenelo ndi lamwanaalirenji. Amene akukhala m’dziko limenelo ndi Akanani, Ahiti, Aamori, Aperizi, Ahivi ndi Ayebusi.” Mose adayankha kuti, “tsono ine ndikapita kwa Aisraelewo kukawauza kuti Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu, iwowo akakandifunsa kuti, ‘dzina lake ndani?’ Ndiye ineyo ndikawauze chiyani?” Mulungu adamuuza kuti, “Dzina langa ndine NDILIPO. Aisraelewo ukawauze kuti, NDILIPO wandituma kwa inu.” Ndipo Mulungu adamuuzanso Mose kuti, “Aisraele ukawauze kuti, Chauta, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isaki, Mulungu wa Yakobo, ndiye amene wandituma kwa inu. Tsono limeneli ndilo dzina langa mpaka muyaya. Limeneli ndilo dzina limene idzanditchula mibadwo yonse yam’tsogolo.”
Mau a Ambuye... Tithokoze Mulungu.
--------------------------------------
NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 103:1-4, 6-8, 11.
Chauta ndi wokoma mtima ndi wachikondi.
Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,
Moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera.
Tamanda Chauta, iwe mtima wanga,
Ndipo usaiwale zabwino zake zonse.
Chauta ndi wokoma mtima ndi wachikondi.
Ndiye amene amakhululukira machimo ako onse,
Ndi kuchiritsa matenda ako onse.
Ndiye amene amapulumutsa moyo wako ku manda.
Amakuveka chikondi chake chosasinthika,
Ndiponso chifundo chake ngati chisoti chaufumu.
Chauta ndi wokoma mtima ndi wachikondi.
Chauta amaweruza mwachilungamo one opsinjidwa,
Amawachitira zolungama.
Adadziwitsa Mose njira zake,
Adaonetsa Aisraele ntchito zake.
Chauta ndi wokoma mtima ndi wachikondi.
Chauta ndi wachifundo ndi wokoma mtima,
Ndi wosakwiya msanga, ndipo chikondi chake chosasinthika nchachikulu.
Monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi,
Ndi momwenso chidakulira chikondi chake chosasinthika
Kwa anthu oopa Chauta.
Chauta ndi wokoma mtima ndi wachikondi.
---------------------------------------------------------------
MAU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YOYAMBA YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 1 AKORINTO 10:1-6, 10-12 (Moyo umene makolo athu amakhala pansi pa ulamuliro wa Mose, zidalembedwa kuti tipezepo phunziro ifeyo).
Abale, ndifuna kuti mudziwe zimene zidawachitikira makolo athu akale aja. Onse adayenda mu mthunzi wa mtambo, ndipo onse adaoloka Nyanja Yofiira. Motero mumtambomo ndi n’nyanjamo onsewo adachita ngati kubatizidwa ndi kukhala amodzi ndi Mose. Onse ankadya chakudya chauzimu chimodzimodzi. Onse ankamwanso chakumwa chauzimu chimodzimodzi, pakuti analikumwa m’thanthwe lauzimu limene linkawatsatira. Thanthwelo linali Khristu yemwe. Komabe ambirimbiri mwa iwo Mulungu sadakondwere nawo, kotero kuti adafera m'chipululu. Tsono zimene zidachitikazi ndi zitsanzo zotichenjeza ife, kuti tisamasirira zoipa monga adaachitira iwowo. Musadandaule monga momwe adaadandaulira ena mwa iwo: paja adaphedwa ndi mngelo wodzetsa imfa. Zonsezi zidawagwera makolo athuwo kuti zikhale zowachenjeza. Ndipo zidalembedwa kuti tipezepo phunziro ifeyo, amene tikuyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. Tsono amene akuganiza kuti waimirira molimba, achenjere kuti angagwe.
Mau a Ambuye... Tithokoze Mulungu.
--------------------------------------
NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – MATEYO 4:17.
Ulemerero ndi mayamiko kwa Inu, Khristu—Tembenukani mtima, chifukwa ufumu wakumwamba wayandikira.—Ulemerero ndi mayamiko kwa Inu, Khristu.
--------------------------------------
MTHENGA WABWINO: MTHENGA WABWINO MONGA ANALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 13: 01 – 09. (Mukapanda kutembenuka mtima, inunso mudzaonongedwa ngati iwo aja).
Anthu ena amene anali pomwepo adadza kwa Yesu, nayamba kumsimbira za Agalileya amene Pilato adaalamula kuti aphedwe, pamene iwo ankapereka nsembe zao kwa Mulungu. Tsono Yesu
adawafunsa kuti, “Kodi mukuyesa kuti Agalileyawo anali ochimwa koposa Agalileya ena onse, popeza kuti adaphedwa motere? Iyai. koma mukapanda kutembenuka mtima, inunso mudzaonongedwa ngati iwo aja. Nanga anthu aja 18 amene nyumba yosanja idawagwera ku Siloamu nkuwapha? Kodi mukuyesa kuti iwowo anali ophwanya malamulo koposa anthu ena onse okhala m’Yerusalemu? Iyai, koma mukapanda kutembenuka mtima, inunso mudzaonongedwa ngati iwo aja.” Yesu adawaphera fanizo, adati, “Munthu wina anali ndi mkuyu
wobzalidwa m’munda wake wamphesa. Adakafunamo zipatso, koma osazipeza. Tsono adauza wosamala mundawo kuti, ‘papita zaka zitatu tsopano ndikufuna zipatso mu mkuyu uwu, koma osazipeza. Udule tsono. Ukugugitsiranji nthaka?’ Koma iye adati. ‘Ambuye, baulekani chaka chino chokha. Ndiukumbira pa tsinde nkuuthira manyowa. Ukadzabala zipatso chaka chamawa, zidzakhala bwino. Koma ukakapanda kubala, apo mudzaudule.’”
Mthenga wa Ambuye… Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.
--------------------------------------
Mapemphero a Akhristu.
Abale, popeza kuti Mulungu akuwamvera chifundo anthu onse, ifenso tiyeni tiwaonetse onse mtima wachikondi, pakuwapempherera:
1. Akulu a Mpingo atsogolere akhristu ao m’njira ya kulapa, pakuwasonyeza kukoma mtima kwa Mulungu.
Tikupemphani, mutivomereze.
2. Anthu amene ali m’mavuto aakulu chifukwa cha ngozi, nkhondo kapena zoipa zina, asataye mtima koma akhulupirire Mulungu ndithu.
Tikupemphani, mutivomereze.
3. Tipempherere odwala onse kuti apirire mavuto ao mosataya mtima pokhulupirira Yesu Khristu.
Tikupemphani, mutivomereze.
4. Akhristu ofooka ndi osokera adzidzimuke m'mitima mwao pa nthawi ino ya Lenti ndipo abwerere kwa Mulungu Atate ao.
Tikupemphani, mutivomereze.
5. Ife tomwe tili muno, moyo wathu ukhale wodziletsa ndi wobala zipatso pakuchita ntchito zabwino.
Tikupemphani, mutivomereze.
Atate okoma mtima, Inu mukudziwa umphawi wathu ndi kufooka kwathu. Mverani madandaulo athu ndipo musaleke kutiwongolera, kuti tibale zipatso za chilungamo. Mwa Yesu Khristu Ambuye athu.
#Pax_et_Gaudium_in_Domino.
Facebook: https://business.facebook.com/latest/home?asset_id=109826477067295&business_id=1326098184199637&nav_ref=profile_plus_profile_left_nav_button Blog: https://www.blogger.com/blog/posts/2477989519106302629?hl=en-GB
No comments:
Post a Comment