Saturday, March 26, 2022



LAMULUNGU LA 04 MU LENTI - C

(Tibwerere kwa Mulungu Atate athu.)

MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA YOSWA: YOSWA 05: 09 – 12 (Pamene Aisraele anali m’zithando ku Giligala m’chigwa cha ku Yeriko, adachita Pasaka madzulo)

Tsono Chauta adauza Yoswa kuti, “lero ndakuchotserani manyazi a ukapolo wanu uja umene munali nawo ku Ejipito.” Nchifukwa chake malowo adawatcha Giligala, ndipo mpaka lero lino malo amenewa akudziwika ndi dzina limeneli. Pamene Aisraele anali m’zithando ku Giligala m’chigwa cha ku Yeriko, adachita Pasaka madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo. M’mawa mwake mpamene anthu aja adayamba kudya chakudya cha ku Kanani. Adakazinga tirigu, naphikanso buledi wosatupitsa tsiku limenelo. Zitangotero, mana uja adaleka kugwa, ndipo sadapezekenso pakati pa Aisraele. Kuyambira nthawi imeneyo adayamba kudya chakudya cha ku Kanani.

Mau a Ambuye.................................Tithokoze Mulungu.

 

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 34: 02 – 07.

Tiyeni kwa Mulungu ndipo tidzaona kuti ndi wabwino.

 

Ndidzayamika Chauta nthawi zonse.

Pakamwa panga padzatamanda Iye kosalekeza.

Moyo wanga umanyadira Chauta.

Anthu ozunzika amve ndipo akondwere.

 

Tiyeni kwa Mulungu ndipo tidzaona kuti ndi wabwino.

 

Lalikani pamodzi nane ukulu wa Chauta,

Tiyeni limodzi tiyamike dzina lake.

Ndidapemphera kwa Chauta ndipo adandiyankha.

Adandipulumutsa kwa zonse zimene ndinkaziwopa.

 

Tiyeni kwa Mulungu ndipo tidzaona kuti ndi wabwino.

 

Ozunzikawo atayang’ana kwa Chauta,

Nkhope zao zidasangalala, sadachite manyazi.

Munthu wosaukayu adalira, ndipo Chauta adamumva,

Nampulumutsa m’mavuto ake onse.


Tiyeni kwa Mulungu ndipo tidzaona kuti ndi wabwino.


MAWU ACHIWIRI A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’KALATA YACHIWIRI YA PAULO WOYERA KWA AKORINTO: 02 AKORINTO 05: 17 – 21 (Mwa Khristu Mulungu ankayanjanitsa anthu a pa dziko lonse lapansi.)

Abale, ngati munthu ali mwa Khristu, ngwolengedwa kwatsopano. Zakale zapita, zimene zilipo nzatsopano. Wochita zonsezi ndi Mulungu, amene mwa Khristu adatiyanjanitsa ndi Iye mwini, ndipo adatipatsa ntchito yolalikira anthu chiyanjanitsocho. Ndiye kuti mwa Khristu Mulungu ankayanjanitsa anthu a pa dziko lonse lapansi ndi Iye mwini, osawawerengera machimo ao. Ndipo adatipatsa ifeyo mau onena za chiyanjanitsocho kuti tiwalalike. Tsono ndife akazembe oimirira Khristu, ndipo kudzera mwa ifeyo Mulungu mwini ndiye akulankhula nanu mokudandaulirani. Tikukupemphani m’dzina la Khristu kuti muvomere kuyanjananso ndi Mulungu. Khristu sadachimwe konse, koma Mulungu adamsandutsa uchimo chifukwa cha ife, kuti mwa Iyeyo ife tisanduke olungama pamaso pa Mulungu.

Mau a Ambuye.................................Tithokoze Mulungu.

NYIMBO YA MTHENGA WABWINO – LUKA 15: 18.

Ulemerero ndi mayamiko kwa Inu, Khristu.

Ndipita kwa bambo wanga, ndipo ndikanena kuti; “Atate, ndidachimwira Mulungu wakumwamba, ndi inu nomwe.”

Ulemerero ndi mayamiko kwa Inu, Khristu!

MTHENGA WABWINO: MAU A MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA LUKA WOYERA: LUKA 15: 01 – 03, 11 – 32. (Mng’ono wakoyu adaafa, koma tsopano wakhalanso moyo.)

Anthu onse okhometsa msonkho ndi Ayuda enanso onyozera Malamulo ankabwera kwa Yesu kudzamva mau ake. Tsono Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo adayamba kuwinya nkumanena kuti, “Munthu uyu amalandira anthu ochimwa, nkumadya nawo pamodzi.” Tsono Yesu adawaphera fanizo ili, adati, “Munthu wina adaali ndi ana aamuna awiri, wamng’ono adapempha bambo wake kuti. ‘Atate, bwanji mugawiretu tsopano chuma chanu, ine mundipatsiretu chigawo changa.’ Bamboyo adawagawiradi ana ake aja chuma chake. Patangopita masiku owerengeka wamng’ono uja adagulitsa chigawo chake chonse, nachoka kwaoko ndi ndalama zake kupita ku dziko lakutali. Kumeneko adamwaza chuma chakecho ndi mayendedwe oipa. Chitamthera chuma chake chonse, mudalowa njala yaikulu m’dziko limeneli, mwakuti iye yemwe adayamba kusauka. Pamenepo adapita kukakhala nao kwa nzika ina ya m’dzikomo. Nzikayo idamtuma ku busa kukaweta nkhumba zake. Mnyamata uja ankalakalaka kudya makoko amene nkhumba zinkadya, koma panalibe munthu wompatsako ngakhale makokowo. Atakhalakhala adadzidzimuka mumtima mwake, ndipo adati, ‘achulukirenji antchito a bambo wanga amene ali ndi chakudya chokwanira mpaka kutsalako, pamene ine kuno ndikufa ndi njala. Basi ndinyamuka, ndipita kwa bambo wanga, ndipo ndikanena kuti: Atate, ndidachimwira Mulungu wakumwamba, ndi inu nomwe. Sindili woyenera kutchedwanso mwana wanu. Mundilole ndisanduke mmodzi mwa antchito anu.’ Choncho adanyamukadi napita kwa bambo wake. Koma akubwera patali, bambo wake adamuwona, namumvera chisoni. Adamthamangira, namkumbatira, nkumamumpsompsona. Mwanayo adati, ‘Atate, ndidachimwira Mulungu wakumwamba, ndi inu nomwe. Sindili woyenera kutchedwanso mwana wanu.’ Koma bambo wake adauza antchito ake kuti ‘thamangani mukatenge mkanjo wabwino kwambiri, mumuveke. Mumuvekenso mphete ku chala, ndi nsapato ku mapazi. Ndipo katengeni mwanawang’ombe wonenepa uja, muphe kuti tidye, tikondwere. Chifukwa mwana wangayu adaafa, koma tsopano wakhalanso moyo; adaatayika, koma tsopano wapezeka: Ndiye pompo chikondwerero chidayamba. Koma mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Pochokera kumundako, atafika pafupi ndi nyumba, adamva anthu akuimba ndi kuvina. Adaitana wantchito mmodzi namufunsa kuti, ‘kodi kwagwanji?' Iye adati, Mng’ono wanu uja wabwera, ndiye bambo apha mwanawang'ombe wonenepa uja chifukwa amlandira ali wamoyo. Atamva zimenezo mwana wamkuluyo adapsa mtima, nakana kulowa. Apo bambo wake adatuluka, nkumupempha mopemba kuti alowe. Koma iye adayankha bambo akewo kuti, ‘ine zaka zonsezi ndakhala ndikukugwirirani ntchito ndipo sindidalakwirepo lamulo lanu. Komabe inu simudandipatsepo ndi katonde komwe kuti ndikondwere pamodzi ndi anzanga. Koma mwana wanuyu, chuma chanu chonse adaonongera akazi achiwerewere, ndipo pamene wabwera, mwamuphera mwanawang’ombe wonenepa uja!’ Bambo wakeyo adamuyankha kuti, ‘mwana wanga, iwe uli ndi ine nthawi zonse, ndipo zanga zone nzako. Kunayenera kuti tikondwere ndi kusangalala, chifukwa mng’ono wakoyu adaafa, koma tsopano wakhalanso moyo; adaatayika, koma tsopano wapezeka.”

Mthenga wa Ambuye…Ulemu kwa Inu Ambuye Yesu Khristu.

#Pax_et_Gaudium_in_Domino.

Facebook: https://www.facebook.com/Mawu-a-Lamulungu-Lililonse-a-Chikatolika-mu-Chichewa-109826477067295

Blog: https://mkatolikamw.blogspot.com/

 

No comments:

Post a Comment

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C

Chaka cha Ukaristia [Corpus Christi]—C “Muzichita zimenezi kuti mundikumbukire.”   MAWU WOYAMBA A M’BUKU LOYERA: MAWU A M’BUKU LA GENESIS (...